Leviticus 4 (BOGWICC)

1 Yehova anayankhula ndi Mose kuti, 2 “Awuze Aisraeli kuti, ‘Munthu akachimwa mosadziwa ndi kuchita chilichonse chimene Yehova walamula kuti asachite, azichita izi: 3 “ ‘Ngati wansembe wodzozedwa achimwa, ndi kuchimwitsa anthu onse, iyeyu ayenera kupereka mwana wangʼombe wamphongo wopanda chilema chifukwa cha tchimo limene wachitalo. Imeneyi ndi nsembe ya Yehova yopepesera tchimo lake. 4 Wansembeyo abwere nayo ngʼombeyo pa khomo la tenti ya msonkhano pamaso pa Yehova. Asanjike dzanja lake pamutu pa ngʼombeyo ndipo ayiphe pamaso pa Yehova. 5 Kenaka wansembe wodzozedwa atengeko magazi a ngʼombeyo ndi kulowa nawo mu tenti ya msonkhano. 6 Iye aviyike chala chake mʼmagazi, ndipo awawaze kasanu ndi kawiri pamaso pa Yehova, patsogolo pa katani yotchinga malo wopatulika. 7 Kenaka wansembe apake magaziwo pa nyanga za guwa lofukizira lubani limene lili pamaso pa Yehova mu tenti ya msonkhano. Magazi ena otsalawo awathire pa tsinde pa guwa lansembe zopsereza, limene lili pa khomo la tenti ya msonkhano. 8 Pambuyo pake achotse mafuta onse a ngʼombe yayimuna yopepesera machimoyo: mafuta okuta zamʼkati kapena mafuta onse amʼkatimo. 9 Achotsenso ndi kubwera ndi impsyo zonse ziwiri pamodzi ndi mafuta onse ndiponso mafuta onse amene aphimba chiwindi ndi impsyo 10 monga momwe amachotsera mafuta a ngʼombe yoperekedwa kuti ikhale chopereka chachiyanjano. Tsono wansembe atenthe zimenezi pa guwa lansembe zopsereza. 11 Koma chikopa cha ngʼombe yayimunayo ndi mnofu wake wonse, pamodzi ndi mutu ndi miyendo, zamʼkati ndi matumbo, 12 kapena kuti ngʼombe yonse yotsalayo apite nayo kunja kwa msasa ku malo woyeretsedwa, kumene amatayako phulusa ndi kuyitentha pa nkhuni, pa phulusapo. 13 “ ‘Ngati gulu lonse la Aisraeli lichimwa mosadziwa, nachita chomwe ndi choletsedwa ndi Yehova, ngakhale kuti gulu lonselo silikudziwa kuti lachimwa, anthuwo ndi olakwa ndithu. 14 Akazindikira tchimo limene achita, gulu lonse lipereke mwana wangʼombe wamphongo kuti akhale chopereka chopepesera tchimo ndipo abwere naye pa khomo la tenti ya msonkhano. 15 Akuluakulu a anthuwo asanjike manja awo pa mutu pa ngʼombe pamaso pa Yehova, ndipo ayiphe pomwepo pamaso pa Yehova. 16 Tsono wansembe wodzozedwa atengeko magazi a ngʼombeyo ndi kulowa nawo mu tenti ya msonkhano. 17 Aviyike chala chake mʼmagaziwo ndi kuwawaza pamaso pa Yehova kasanu ndi kawiri patsogolo pa nsalu yotchinga. 18 Pambuyo pake iye apake magaziwo pa nyanga za guwa limene lili pamaso pa Yehova mu tenti ya msonkhano. Magazi ena otsalawo awathire pa tsinde pa guwa lansembe zopsereza limene lili pa khomo la tenti ya msonkhano. 19 Kenaka achotse mafuta onse a ngʼombeyo ndi kuwatentha pa guwa, 20 ndipo achite ndi ngʼombe yayimunayi monga anachitira ndi ngʼombe yayimuna yopepesera machimo. Potero, wansembe adzapereka nsembe yopepesera anthu, ndipo machimo awo adzakhululukidwa. 21 Kenaka atulutse ngʼombeyo kunja kwa msasa ndi kuyitentha monga anatenthera ngʼombe yoyamba ija. Imeneyi ndiyo nsembe yopepesera machimo a gulu lonse. 22 “ ‘Ngati mtsogoleri achimwa mosadziwa nachita zimene ndi zoletsedwa ndi Yehova Mulungu wake, ndiye kuti wapalamula. 23 Ndipo ngati wauzidwa za tchimo limene wachita, iye abwere ndi mbuzi yayimuna yopanda chilema kuti ikhale chopereka chake. 24 Asanjike dzanja lake pa mutu wa mbuziyo ndi kuyiphera pamalo pamene amaphera zopereka zopsereza pamaso pa Yehova. Ichi ndi chopereka chopepesera tchimo. 25 Pambuyo pake wansembe atengeko magazi a chopereka chopepesera tchimocho ndi chala chake, ndipo awapake pa nyanga za guwa lansembe zopsereza. Athire magazi otsalawo pa tsinde la guwalo. 26 Wansembeyo atenthe mafuta onse pa guwapo monga amatenthera chopereka chachiyanjano. Pochita zimenezi, wansembe adzapereka nsembe yopepesera tchimo la munthuyo, ndipo adzakhululukidwa. 27 “ ‘Ngati munthu wamba achimwa mosadziwa nachita zimene ndi zoletsedwa ndi Yehova, ndiye kuti wapalamula. 28 Ndipo ngati wauzidwa za tchimo limene wachita, abweretse mbuzi yayikazi yopanda chilema kuti ikhale chopereka chopepesera tchimo. 29 Asanjike dzanja lake pamutu pa mbuziyo ndipo ayiphe pamalo pamene amaphera chopereka chopsereza. 30 Ndipo wansembe atenge magazi ndi chala chake ndi kuwapaka pa nyanga za guwa lansembe zopsereza ndi kuthira magazi wotsalawo pa tsinde la guwalo. 31 Kenaka iye achotse mafuta onse monga momwe anachotsera mafuta a chopereka chachiyanjano, ndipo awatenthe pa guwa kuti akhale fungo lokomera Yehova. Potero, wansembe adzapereka nsembe yopepesera tchimo la munthuyo ndipo adzakhululukidwa. 32 “ ‘Ngati munthu apereka mwana wankhosa ngati chopereka chopepesera tchimo lake, abwere ndi mwana wankhosa wamkazi wopanda chilema. 33 Asanjike dzanja lake pa mutu wa mwana wankhosayo ndipo amuphe pamalo pamene amaphera chopereka chopsereza. 34 Kenaka wansembe atengeko ndi chala chake magazi a mwana wankhosa uja ndi kuwapaka pa nyanga za guwa lansembe zopsereza. Magazi otsalawo athire pa tsinde la guwalo. 35 Iye achotse mafuta onse, monga amachotsera mafuta a mwana wankhosa wa chopereka chachiyanjano, ndipo wansembe awatenthe pa guwa pamodzi ndi zopereka zina zopsereza za Yehova. Potero, wansembe adzapereka nsembe yopepesera tchimo limene munthuyo anachita ndipo adzakhululukidwa.

In Other Versions

Leviticus 4 in the ANGEFD

Leviticus 4 in the ANTPNG2D

Leviticus 4 in the AS21

Leviticus 4 in the BAGH

Leviticus 4 in the BBPNG

Leviticus 4 in the BBT1E

Leviticus 4 in the BDS

Leviticus 4 in the BEV

Leviticus 4 in the BHAD

Leviticus 4 in the BIB

Leviticus 4 in the BLPT

Leviticus 4 in the BNT

Leviticus 4 in the BNTABOOT

Leviticus 4 in the BNTLV

Leviticus 4 in the BOATCB

Leviticus 4 in the BOATCB2

Leviticus 4 in the BOBCV

Leviticus 4 in the BOCNT

Leviticus 4 in the BOECS

Leviticus 4 in the BOHCB

Leviticus 4 in the BOHCV

Leviticus 4 in the BOHLNT

Leviticus 4 in the BOHNTLTAL

Leviticus 4 in the BOICB

Leviticus 4 in the BOILNTAP

Leviticus 4 in the BOITCV

Leviticus 4 in the BOKCV

Leviticus 4 in the BOKCV2

Leviticus 4 in the BOKHWOG

Leviticus 4 in the BOKSSV

Leviticus 4 in the BOLCB

Leviticus 4 in the BOLCB2

Leviticus 4 in the BOMCV

Leviticus 4 in the BONAV

Leviticus 4 in the BONCB

Leviticus 4 in the BONLT

Leviticus 4 in the BONUT2

Leviticus 4 in the BOPLNT

Leviticus 4 in the BOSCB

Leviticus 4 in the BOSNC

Leviticus 4 in the BOTLNT

Leviticus 4 in the BOVCB

Leviticus 4 in the BOYCB

Leviticus 4 in the BPBB

Leviticus 4 in the BPH

Leviticus 4 in the BSB

Leviticus 4 in the CCB

Leviticus 4 in the CUV

Leviticus 4 in the CUVS

Leviticus 4 in the DBT

Leviticus 4 in the DGDNT

Leviticus 4 in the DHNT

Leviticus 4 in the DNT

Leviticus 4 in the ELBE

Leviticus 4 in the EMTV

Leviticus 4 in the ESV

Leviticus 4 in the FBV

Leviticus 4 in the FEB

Leviticus 4 in the GGMNT

Leviticus 4 in the GNT

Leviticus 4 in the HARY

Leviticus 4 in the HNT

Leviticus 4 in the IRVA

Leviticus 4 in the IRVB

Leviticus 4 in the IRVG

Leviticus 4 in the IRVH

Leviticus 4 in the IRVK

Leviticus 4 in the IRVM

Leviticus 4 in the IRVM2

Leviticus 4 in the IRVO

Leviticus 4 in the IRVP

Leviticus 4 in the IRVT

Leviticus 4 in the IRVT2

Leviticus 4 in the IRVU

Leviticus 4 in the ISVN

Leviticus 4 in the JSNT

Leviticus 4 in the KAPI

Leviticus 4 in the KBT1ETNIK

Leviticus 4 in the KBV

Leviticus 4 in the KJV

Leviticus 4 in the KNFD

Leviticus 4 in the LBA

Leviticus 4 in the LBLA

Leviticus 4 in the LNT

Leviticus 4 in the LSV

Leviticus 4 in the MAAL

Leviticus 4 in the MBV

Leviticus 4 in the MBV2

Leviticus 4 in the MHNT

Leviticus 4 in the MKNFD

Leviticus 4 in the MNG

Leviticus 4 in the MNT

Leviticus 4 in the MNT2

Leviticus 4 in the MRS1T

Leviticus 4 in the NAA

Leviticus 4 in the NASB

Leviticus 4 in the NBLA

Leviticus 4 in the NBS

Leviticus 4 in the NBVTP

Leviticus 4 in the NET2

Leviticus 4 in the NIV11

Leviticus 4 in the NNT

Leviticus 4 in the NNT2

Leviticus 4 in the NNT3

Leviticus 4 in the PDDPT

Leviticus 4 in the PFNT

Leviticus 4 in the RMNT

Leviticus 4 in the SBIAS

Leviticus 4 in the SBIBS

Leviticus 4 in the SBIBS2

Leviticus 4 in the SBICS

Leviticus 4 in the SBIDS

Leviticus 4 in the SBIGS

Leviticus 4 in the SBIHS

Leviticus 4 in the SBIIS

Leviticus 4 in the SBIIS2

Leviticus 4 in the SBIIS3

Leviticus 4 in the SBIKS

Leviticus 4 in the SBIKS2

Leviticus 4 in the SBIMS

Leviticus 4 in the SBIOS

Leviticus 4 in the SBIPS

Leviticus 4 in the SBISS

Leviticus 4 in the SBITS

Leviticus 4 in the SBITS2

Leviticus 4 in the SBITS3

Leviticus 4 in the SBITS4

Leviticus 4 in the SBIUS

Leviticus 4 in the SBIVS

Leviticus 4 in the SBT

Leviticus 4 in the SBT1E

Leviticus 4 in the SCHL

Leviticus 4 in the SNT

Leviticus 4 in the SUSU

Leviticus 4 in the SUSU2

Leviticus 4 in the SYNO

Leviticus 4 in the TBIAOTANT

Leviticus 4 in the TBT1E

Leviticus 4 in the TBT1E2

Leviticus 4 in the TFTIP

Leviticus 4 in the TFTU

Leviticus 4 in the TGNTATF3T

Leviticus 4 in the THAI

Leviticus 4 in the TNFD

Leviticus 4 in the TNT

Leviticus 4 in the TNTIK

Leviticus 4 in the TNTIL

Leviticus 4 in the TNTIN

Leviticus 4 in the TNTIP

Leviticus 4 in the TNTIZ

Leviticus 4 in the TOMA

Leviticus 4 in the TTENT

Leviticus 4 in the UBG

Leviticus 4 in the UGV

Leviticus 4 in the UGV2

Leviticus 4 in the UGV3

Leviticus 4 in the VBL

Leviticus 4 in the VDCC

Leviticus 4 in the YALU

Leviticus 4 in the YAPE

Leviticus 4 in the YBVTP

Leviticus 4 in the ZBP