2 Kings 6 (BOGWICC)

1 Ana a aneneri anati kwa Elisa, “Taonani malo amene timakhala ndi inu atichepera kwambiri. 2 Tiloleni tipite ku Yorodani kumene aliyense wa ife akadule mtengo umodzi, kuti timange malo woti tizikhalamo.”Ndipo Elisa anati, “Pitani.” 3 Mmodzi wa iwo anati, “Chonde mulole kutsagana nawo atumiki anu.”Elisa anayankha kuti, “Ndipita nanu.” 4 Ndipo anapita nawo.Anapita ku Yorodani nayamba kudula mitengo. 5 Pamene wina ankadula mtengo, nkhwangwa yake inaguluka nigwera mʼmadzi. Iye anafuwula kuti, “Mayo! Mbuye wanga! Popeza ndi yobwereka!” 6 Ndipo munthu wa Mulungu uja anafunsa, “Yagwera pati?” Pamene anamuonetsa malowo, Elisa anadula kamtengo nakaponya pamenepo, ndipo nkhwangwayo inayandama. 7 Elisa anati, “Itenge.” Ndipo munthuyo anatambalitsa dzanja lake nayitenga. 8 Tsono mfumu ya ku Aramu inali pa nkhondo ndi Israeli. Itakambirana ndi atsogoleri ake ankhondo inati, “Ndidzamanga misasa yanga pamalo akutiakuti.” 9 Munthu wa Mulungu anatumiza mawu kwa mfumu ya ku Israeli kuti “Musamale podutsa malo akuti, chifukwa Aaramu akupita kumeneko.” 10 Choncho mfumu ya ku Israeli inatuma anthu kumalo kumene munthu wa Mulunguyo ananena. Nthawi ndi nthawi Elisa ankachenjeza mfumu, kotero kuti ankakhala tcheru ku malo amenewo. 11 Zimenezi zinakwiyitsa kwambiri mfumu ya ku Aramu. Mfumuyo inayitanitsa atsogoleri ake ankhondo ndipo inawafunsa kuti, “Kodi simungandiwuze munthu amene pakati pathu pano ali mbali ya mfumu ya ku Israeli?” 12 Mmodzi mwa atsogoleri a ankhondowo anati, “Palibe ndi mmodzi yemwe pakati pathu, inu mbuye wanga, koma Elisa mneneri amene ali ku Israeli amawuza mfumu ya ku Israeli mawu enieni amene inu mumayankhula ku chipinda kwanu.” 13 Choncho mfumu inalamula kuti, “Pitani, kafufuzeni kumene akukhala kuti ine nditume anthu kukamugwira.” Anthuwo anabweretsa mawu oti, “Taonani, Elisa ali ku Dotani.” 14 Ndipo mfumu inatumizako magaleta ndi akavalo ndiponso gulu lankhondo lamphamvu. Anapita usiku nakawuzungulira mzindawo. 15 Mtumiki wa munthu wa Mulungu atadzuka mmamawa ndi kutuluka panja, gulu la ankhondo pamodzi ndi akavalo ndi magaleta anali atazungulira mzindawo. Mtumikiyo anafunsa kuti, “Kalanga mbuye wanga, tidzachita chiyani?” 16 Mneneri anamuyankha kuti, “Usachite mantha. Amene ali mbali yathu ndi ambiri kupambana amene ali mbali yawo.” 17 Ndipo Elisa anapemphera kuti, “Inu Yehova tsekulani maso ake kuti aone.” Pamenepo Yehova anatsekula maso a mtumikiyo, ndipo anayangʼana naona kuti phiri lonse linali lodzaza ndi akavalo ndi magaleta a moto atazungulira Elisa. 18 Pamene adaniwo ankabwera kudzalimbana naye, Elisa anapemphera kwa Yehova kuti, “Achititseni khungu anthu awa.” Kotero Yehova anawachititsa khungu monga anapemphera Elisa. 19 Elisa anawawuza ankhondowo kuti, “Njira si imeneyi ndipo mzinda sumenewunso. Tsateni, ndipo ndidzakutengerani kwa munthu amene mukumufunayo.” Ndipo anawatengera ku Samariya. 20 Atalowa mu mzinda wa Samariya, Elisa anati, “Yehova tsekulani maso a anthu awa kuti aone.” Choncho Yehova anatsekula maso awo ndipo anangoona kuti ali mʼkati mwenimweni mwa Samariya. 21 Mfumu ya ku Israeli itawaona, inafunsa Elisa kuti, “Abambo anga, kodi ndiwaphe? Kodi ndiwaphe?” 22 Elisa anayankha kuti, “Musawaphe. Kodi mungaphe anthu amene munawagwira pogwiritsa ntchito lupanga ndi uta? Apatseni chakudya ndi madzi kuti adye ndi kumwa kenaka apite kwa mbuye wawo.” 23 Choncho anawakonzera mphwando lalikulu, ndipo atatsiriza kudya ndi kumwa, anawatumiza kwawo ndipo anabwerera kwa mbuye wawo. Kotero magulu a ankhondo a ku Aramu analeka kuthira nkhondo dziko la Israeli. 24 Patapita nthawi, Beni-Hadadi mfumu ya Aramu anasonkhanitsa gulu lake lonse la ankhondo, napita kukazungulira mzinda wa Samariya. 25 Mu mzinda wa Samariya munali njala yoopsa. Ndipo taonani, Aaramu anazungulira mzindawu kwa nthawi yayitali kotero kuti mutu wa bulu ankawugulitsa ndalama za siliva 80, ndipo magalamu 200 a zitosi za nkhunda ankawagulitsa pa mtengo wa masekeli asanu. 26 Pamene mfumu inkayenda pa khoma la mzindawo, mayi wina anafuwulira mfumuyo kuti, “Thandizeni mbuye wanga mfumu!” 27 Mfumu inayankha kuti, “Ngati Yehova sakuthandiza iwe, ine thandizo lako ndingalipeze kuti? Kuchokera ku malo opunthira tirigu kodi? Kuchokera kumalo opsinyira mphesa kodi?” 28 Pamenepo mfumuyo inafunsa mayiyo kuti, “Kodi chakuvuta nʼchiyani?”Iye anayankha kuti, “Mayi uyu anandiwuza kuti, ‘Bweretsa mwana wako kuti timudye lero, ndipo mawa tidzadya mwana wangayu.’ 29 Choncho tinaphika mwana wanga ndi kumudya. Tsiku lotsatira lakelo ine ndinati, ‘Bweretsa mwana wako kuti timudye,’ koma iye anabisa mwana wakeyo.” 30 Mfumu itamva mawu a mayiyo, inangʼamba mkanjo wake. Pamene inkayenda pa khoma, anthu anayangʼana, ndipo anaona zovala zamʼkati, pakuti anavala chiguduli. 31 Mfumuyo inati, “Mulungu andilange, andilange kwambiri ndikapanda kudula mutu wa Elisa mwana wa Safati lero!” 32 Tsono Elisa nʼkuti atakhala mʼnyumba mwake, ndipo akuluakulu anali naye limodzi. Mfumu inatuma munthu wina kuti imutsogolere, koma asanafike, Elisa anawuza akuluakuluwo kuti, “Kodi simukuona momwe wopha munthu uja watumizira munthu wina kuti adzadule mutu wanga? Taonani mthengayo akafika, mutseke chitseko ndipo muchigwiritsitse kuti asalowe. Kodi ndikumvawo pambuyo pake si mgugu wa mbuye wake?” 33 Elisa akuyankhulabe ndi anthuwo, taonani, wamthengayo anafika kwa iye. Ndipo mfumu inati, “Mavuto amenewa ndi ochokera kwa Yehova. Kodi nʼchifukwa chiyani ine ndiyenera kudikira thandizo lochokera kwa Yehova?”

In Other Versions

2 Kings 6 in the ANGEFD

2 Kings 6 in the ANTPNG2D

2 Kings 6 in the AS21

2 Kings 6 in the BAGH

2 Kings 6 in the BBPNG

2 Kings 6 in the BBT1E

2 Kings 6 in the BDS

2 Kings 6 in the BEV

2 Kings 6 in the BHAD

2 Kings 6 in the BIB

2 Kings 6 in the BLPT

2 Kings 6 in the BNT

2 Kings 6 in the BNTABOOT

2 Kings 6 in the BNTLV

2 Kings 6 in the BOATCB

2 Kings 6 in the BOATCB2

2 Kings 6 in the BOBCV

2 Kings 6 in the BOCNT

2 Kings 6 in the BOECS

2 Kings 6 in the BOHCB

2 Kings 6 in the BOHCV

2 Kings 6 in the BOHLNT

2 Kings 6 in the BOHNTLTAL

2 Kings 6 in the BOICB

2 Kings 6 in the BOILNTAP

2 Kings 6 in the BOITCV

2 Kings 6 in the BOKCV

2 Kings 6 in the BOKCV2

2 Kings 6 in the BOKHWOG

2 Kings 6 in the BOKSSV

2 Kings 6 in the BOLCB

2 Kings 6 in the BOLCB2

2 Kings 6 in the BOMCV

2 Kings 6 in the BONAV

2 Kings 6 in the BONCB

2 Kings 6 in the BONLT

2 Kings 6 in the BONUT2

2 Kings 6 in the BOPLNT

2 Kings 6 in the BOSCB

2 Kings 6 in the BOSNC

2 Kings 6 in the BOTLNT

2 Kings 6 in the BOVCB

2 Kings 6 in the BOYCB

2 Kings 6 in the BPBB

2 Kings 6 in the BPH

2 Kings 6 in the BSB

2 Kings 6 in the CCB

2 Kings 6 in the CUV

2 Kings 6 in the CUVS

2 Kings 6 in the DBT

2 Kings 6 in the DGDNT

2 Kings 6 in the DHNT

2 Kings 6 in the DNT

2 Kings 6 in the ELBE

2 Kings 6 in the EMTV

2 Kings 6 in the ESV

2 Kings 6 in the FBV

2 Kings 6 in the FEB

2 Kings 6 in the GGMNT

2 Kings 6 in the GNT

2 Kings 6 in the HARY

2 Kings 6 in the HNT

2 Kings 6 in the IRVA

2 Kings 6 in the IRVB

2 Kings 6 in the IRVG

2 Kings 6 in the IRVH

2 Kings 6 in the IRVK

2 Kings 6 in the IRVM

2 Kings 6 in the IRVM2

2 Kings 6 in the IRVO

2 Kings 6 in the IRVP

2 Kings 6 in the IRVT

2 Kings 6 in the IRVT2

2 Kings 6 in the IRVU

2 Kings 6 in the ISVN

2 Kings 6 in the JSNT

2 Kings 6 in the KAPI

2 Kings 6 in the KBT1ETNIK

2 Kings 6 in the KBV

2 Kings 6 in the KJV

2 Kings 6 in the KNFD

2 Kings 6 in the LBA

2 Kings 6 in the LBLA

2 Kings 6 in the LNT

2 Kings 6 in the LSV

2 Kings 6 in the MAAL

2 Kings 6 in the MBV

2 Kings 6 in the MBV2

2 Kings 6 in the MHNT

2 Kings 6 in the MKNFD

2 Kings 6 in the MNG

2 Kings 6 in the MNT

2 Kings 6 in the MNT2

2 Kings 6 in the MRS1T

2 Kings 6 in the NAA

2 Kings 6 in the NASB

2 Kings 6 in the NBLA

2 Kings 6 in the NBS

2 Kings 6 in the NBVTP

2 Kings 6 in the NET2

2 Kings 6 in the NIV11

2 Kings 6 in the NNT

2 Kings 6 in the NNT2

2 Kings 6 in the NNT3

2 Kings 6 in the PDDPT

2 Kings 6 in the PFNT

2 Kings 6 in the RMNT

2 Kings 6 in the SBIAS

2 Kings 6 in the SBIBS

2 Kings 6 in the SBIBS2

2 Kings 6 in the SBICS

2 Kings 6 in the SBIDS

2 Kings 6 in the SBIGS

2 Kings 6 in the SBIHS

2 Kings 6 in the SBIIS

2 Kings 6 in the SBIIS2

2 Kings 6 in the SBIIS3

2 Kings 6 in the SBIKS

2 Kings 6 in the SBIKS2

2 Kings 6 in the SBIMS

2 Kings 6 in the SBIOS

2 Kings 6 in the SBIPS

2 Kings 6 in the SBISS

2 Kings 6 in the SBITS

2 Kings 6 in the SBITS2

2 Kings 6 in the SBITS3

2 Kings 6 in the SBITS4

2 Kings 6 in the SBIUS

2 Kings 6 in the SBIVS

2 Kings 6 in the SBT

2 Kings 6 in the SBT1E

2 Kings 6 in the SCHL

2 Kings 6 in the SNT

2 Kings 6 in the SUSU

2 Kings 6 in the SUSU2

2 Kings 6 in the SYNO

2 Kings 6 in the TBIAOTANT

2 Kings 6 in the TBT1E

2 Kings 6 in the TBT1E2

2 Kings 6 in the TFTIP

2 Kings 6 in the TFTU

2 Kings 6 in the TGNTATF3T

2 Kings 6 in the THAI

2 Kings 6 in the TNFD

2 Kings 6 in the TNT

2 Kings 6 in the TNTIK

2 Kings 6 in the TNTIL

2 Kings 6 in the TNTIN

2 Kings 6 in the TNTIP

2 Kings 6 in the TNTIZ

2 Kings 6 in the TOMA

2 Kings 6 in the TTENT

2 Kings 6 in the UBG

2 Kings 6 in the UGV

2 Kings 6 in the UGV2

2 Kings 6 in the UGV3

2 Kings 6 in the VBL

2 Kings 6 in the VDCC

2 Kings 6 in the YALU

2 Kings 6 in the YAPE

2 Kings 6 in the YBVTP

2 Kings 6 in the ZBP