Ezekiel 4 (BOGWICC)

1 Mulungu anati, “Iwe mwana wa munthu, tsopano tenga njerwa, uliyike pamaso pako ndipo ujambulepo chithunzi cha mzinda wa Yerusalemu. 2 Ndipo uwuzinge mzindawo motere: uwumangire nsanja zowuzinga, uwumbire mitumbira ya nkhondo, uwumangire misasa ya nkhondo ndipo uyike zida zogumulira kuzungulira mzindawo. 3 Kenaka utenge chiwaya chachitsulo uchiyike ngati khoma lachitsulo pakati pa iwe ndi mzindawo. Uyangʼanitsitse mzindawo ndipo udzakhala wozingidwa ndi nsanja za nkhondo. Choncho umangire nsanja zankhondo. Chimenechi chidzakhala chizindikiro kwa Aisraeli. 4 “Tsono iwe ugonere kumanzere kwako ndipo ndidzayika pa iwe tchimo la Aisraeli. Iwe udzasenza tchimolo masiku onse amene udzagonere mbali imeneyo. 5 Ine ndakuyikira masiku okwana 390 malingana ndi zaka za machimo awo. Umu ndi mmene udzasenzere machimo a Aisraeli. 6 “Utatha zimenezo udzagonerenso mbali ya kudzanja lamanja, ndipo udzasenza machimo a anthu a ku Yuda masiku makumi anayi, tsiku lililonse kuyimira chaka chimodzi. 7 Tsono udzayangʼanitsitse nsanja za nkhondo zozinga. Dzanja la mkanjo wako utalikwinya ndi dzanja lako utakweza, udzalosere modzudzula Yerusalemu. 8 Ine ndidzakumanga ndi zingwe kotero kuti sudzatha kutembenukira uku ndi uku mpaka utatsiriza masiku akuzingidwa ako. 9 “Tsono tenga tirigu ndi barele, nyemba ndi mphodza, mapira ndi mchewere; ndipo uyike zonsezi mʼmbale imodzi ndipo upange buledi wako. Uzidya pa masiku 390 amene udzakhala ukugonera mbali imodzi. 10 Uyeze theka la kilogalamu la chakudyacho kuti uzidya tsiku lililonse kamodzi kokha. 11 Uyezenso zikho ziwiri zamadzi ndipo uzimwa tsiku ndi tsiku. 12 Uzidya chakudya chako ngati momwe amadyera keke ya barele. Uzidzaphika chakudyacho anthu akuona pogwiritsa ntchito ndowe ya munthu ngati nkhuni.” 13 Yehova anati, “Chimodzimodzi anthu a Israeli adzadya chakudya chodetsedwa ku mayiko achilendo kumene Ine ndidzawapirikitsira.” 14 Koma ine ndinati, “Zisatero, Ambuye Yehova! Ine sindinadziyipitsepo pa zachipembedzo. Kuyambira ubwana wanga mpaka tsopano, sindinadyepo kanthu kalikonse kopezeka katafa kapena kophedwa ndi zirombo za kutchire. Palibe nyama yodetsedwa pa zachipembedzo imene inalowa pakamwa panga.” 15 Iye anati, “Chabwino, ndidzakulola kuti uphike buledi wako ndi ndowe za ngʼombe mʼmalo mwa ndowe za munthu.” 16 Pambuyo pake anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, anthu a ku Yerusalemu ndidzawachepetsera chakudya. Anthuwo adzadya chakudya chochita kuyeza ndipo azidzadya mwa nkhawa. Azidzamwanso madzi ochita kuyeza ndiponso mwa mantha. 17 Ndidzachita zimenezi kuti adzasowe chakudya ndi madzi. Choncho adzachita nkhawa akumapenyana ndipo adzatheratu ndi kuwonda chifukwa cha machimo awo.”

In Other Versions

Ezekiel 4 in the ANGEFD

Ezekiel 4 in the ANTPNG2D

Ezekiel 4 in the AS21

Ezekiel 4 in the BAGH

Ezekiel 4 in the BBPNG

Ezekiel 4 in the BBT1E

Ezekiel 4 in the BDS

Ezekiel 4 in the BEV

Ezekiel 4 in the BHAD

Ezekiel 4 in the BIB

Ezekiel 4 in the BLPT

Ezekiel 4 in the BNT

Ezekiel 4 in the BNTABOOT

Ezekiel 4 in the BNTLV

Ezekiel 4 in the BOATCB

Ezekiel 4 in the BOATCB2

Ezekiel 4 in the BOBCV

Ezekiel 4 in the BOCNT

Ezekiel 4 in the BOECS

Ezekiel 4 in the BOHCB

Ezekiel 4 in the BOHCV

Ezekiel 4 in the BOHLNT

Ezekiel 4 in the BOHNTLTAL

Ezekiel 4 in the BOICB

Ezekiel 4 in the BOILNTAP

Ezekiel 4 in the BOITCV

Ezekiel 4 in the BOKCV

Ezekiel 4 in the BOKCV2

Ezekiel 4 in the BOKHWOG

Ezekiel 4 in the BOKSSV

Ezekiel 4 in the BOLCB

Ezekiel 4 in the BOLCB2

Ezekiel 4 in the BOMCV

Ezekiel 4 in the BONAV

Ezekiel 4 in the BONCB

Ezekiel 4 in the BONLT

Ezekiel 4 in the BONUT2

Ezekiel 4 in the BOPLNT

Ezekiel 4 in the BOSCB

Ezekiel 4 in the BOSNC

Ezekiel 4 in the BOTLNT

Ezekiel 4 in the BOVCB

Ezekiel 4 in the BOYCB

Ezekiel 4 in the BPBB

Ezekiel 4 in the BPH

Ezekiel 4 in the BSB

Ezekiel 4 in the CCB

Ezekiel 4 in the CUV

Ezekiel 4 in the CUVS

Ezekiel 4 in the DBT

Ezekiel 4 in the DGDNT

Ezekiel 4 in the DHNT

Ezekiel 4 in the DNT

Ezekiel 4 in the ELBE

Ezekiel 4 in the EMTV

Ezekiel 4 in the ESV

Ezekiel 4 in the FBV

Ezekiel 4 in the FEB

Ezekiel 4 in the GGMNT

Ezekiel 4 in the GNT

Ezekiel 4 in the HARY

Ezekiel 4 in the HNT

Ezekiel 4 in the IRVA

Ezekiel 4 in the IRVB

Ezekiel 4 in the IRVG

Ezekiel 4 in the IRVH

Ezekiel 4 in the IRVK

Ezekiel 4 in the IRVM

Ezekiel 4 in the IRVM2

Ezekiel 4 in the IRVO

Ezekiel 4 in the IRVP

Ezekiel 4 in the IRVT

Ezekiel 4 in the IRVT2

Ezekiel 4 in the IRVU

Ezekiel 4 in the ISVN

Ezekiel 4 in the JSNT

Ezekiel 4 in the KAPI

Ezekiel 4 in the KBT1ETNIK

Ezekiel 4 in the KBV

Ezekiel 4 in the KJV

Ezekiel 4 in the KNFD

Ezekiel 4 in the LBA

Ezekiel 4 in the LBLA

Ezekiel 4 in the LNT

Ezekiel 4 in the LSV

Ezekiel 4 in the MAAL

Ezekiel 4 in the MBV

Ezekiel 4 in the MBV2

Ezekiel 4 in the MHNT

Ezekiel 4 in the MKNFD

Ezekiel 4 in the MNG

Ezekiel 4 in the MNT

Ezekiel 4 in the MNT2

Ezekiel 4 in the MRS1T

Ezekiel 4 in the NAA

Ezekiel 4 in the NASB

Ezekiel 4 in the NBLA

Ezekiel 4 in the NBS

Ezekiel 4 in the NBVTP

Ezekiel 4 in the NET2

Ezekiel 4 in the NIV11

Ezekiel 4 in the NNT

Ezekiel 4 in the NNT2

Ezekiel 4 in the NNT3

Ezekiel 4 in the PDDPT

Ezekiel 4 in the PFNT

Ezekiel 4 in the RMNT

Ezekiel 4 in the SBIAS

Ezekiel 4 in the SBIBS

Ezekiel 4 in the SBIBS2

Ezekiel 4 in the SBICS

Ezekiel 4 in the SBIDS

Ezekiel 4 in the SBIGS

Ezekiel 4 in the SBIHS

Ezekiel 4 in the SBIIS

Ezekiel 4 in the SBIIS2

Ezekiel 4 in the SBIIS3

Ezekiel 4 in the SBIKS

Ezekiel 4 in the SBIKS2

Ezekiel 4 in the SBIMS

Ezekiel 4 in the SBIOS

Ezekiel 4 in the SBIPS

Ezekiel 4 in the SBISS

Ezekiel 4 in the SBITS

Ezekiel 4 in the SBITS2

Ezekiel 4 in the SBITS3

Ezekiel 4 in the SBITS4

Ezekiel 4 in the SBIUS

Ezekiel 4 in the SBIVS

Ezekiel 4 in the SBT

Ezekiel 4 in the SBT1E

Ezekiel 4 in the SCHL

Ezekiel 4 in the SNT

Ezekiel 4 in the SUSU

Ezekiel 4 in the SUSU2

Ezekiel 4 in the SYNO

Ezekiel 4 in the TBIAOTANT

Ezekiel 4 in the TBT1E

Ezekiel 4 in the TBT1E2

Ezekiel 4 in the TFTIP

Ezekiel 4 in the TFTU

Ezekiel 4 in the TGNTATF3T

Ezekiel 4 in the THAI

Ezekiel 4 in the TNFD

Ezekiel 4 in the TNT

Ezekiel 4 in the TNTIK

Ezekiel 4 in the TNTIL

Ezekiel 4 in the TNTIN

Ezekiel 4 in the TNTIP

Ezekiel 4 in the TNTIZ

Ezekiel 4 in the TOMA

Ezekiel 4 in the TTENT

Ezekiel 4 in the UBG

Ezekiel 4 in the UGV

Ezekiel 4 in the UGV2

Ezekiel 4 in the UGV3

Ezekiel 4 in the VBL

Ezekiel 4 in the VDCC

Ezekiel 4 in the YALU

Ezekiel 4 in the YAPE

Ezekiel 4 in the YBVTP

Ezekiel 4 in the ZBP