Genesis 48 (BOGWICC)

1 Patapita kanthawi Yosefe anawuzidwa kuti, “Abambo ako akudwala.” Choncho anatenga ana ake awiri aja Manase ndi Efereimu ndi kupita nawo kwa Yakobo. 2 Yakobo atawuzidwa kuti, “Mwana wanu Yosefe wabwera,” Israeli anadzilimbitsa nadzuka kukhala tsonga pa bedi pake. 3 Yakobo anati kwa Yosefe, “Mulungu Wamphamvuzonse anandionekera ku Luzi mʼdziko la Kanaani, ndipo anandidalitsa, 4 nati kwa ine, ‘Ndidzakupatsa ana ambiri ndipo zidzukulu zako zidzasanduka mitundu yambiri ya anthu. Ndidzapereka dziko ili kwa zidzukulu zako zobwera pambuyo pako kuti likhale lawo mpaka muyaya.’ 5 “Tsopano ana ako aamuna awiri amene anabadwa ine ndisanabwere kuno adzakhala ana anga. Efereimu ndi Manase adzakhala anga monga mmene alili Rubeni ndi Simeoni. 6 Koma amene ati adzabadwe pambuyo pa iwowa adzakhala ako ndipo cholowa chawo chidzadziwika ndi mayina a abale awo. 7 Pamene ndimabwerera kuchoka ku Parani, mwachisoni Rakele, amayi ako anamwalira mʼdziko la Kanaani, tikanali mʼnjira, mtunda wokafika ku Efurata ukanalipo. Ndipo ndinawayika kumeneko mʼmphepete mwa msewu wa ku Efurata” (amene ndi Betelehemu). 8 Israeli ataona ana a Yosefe anafunsa kuti, “Anyamatawa ndi a yani?” 9 Yosefe anati kwa abambo ake, “Awa ndi ana anga amene Mulungu wandipatsa kuno.”Ndipo Israeli anati, “Bwera nawo kuno kuti ndiwadalitse.” 10 Koma maso a Israeli anali ofowoka chifukwa cha kukalamba moti sankaona nʼkomwe. Tsono Yosefe anabwera nawo ana ake aja pafupi ndi abambo ake ndipo abambo ake anawapsompsona nawakumbatira. 11 Israeli anati kwa Yosefe, “Ine sindinali kuyembekeza kuti nʼkudzaonanso nkhope yako, ndipo tsopano Mulungu wandilola kuti ndionenso ngakhale ana ako.” 12 Tsono Yosefe anawachotsa ana aja pa mawondo a Israeli ndipo anamuweramira nkhope pansi. 13 Yosefe anawagwira ana onse awiri padzanja, Efereimu ku dzanja lake lamanja kulunjika dzanja lamanzere la Israeli ndipo Manase ku dzanja lamanzere kulunjikitsa dzanja lamanja la Israeli, ndipo anawayandikiza kwa Yakobo. 14 Koma Israeli anapinganitsa mikono motero kuti anayika dzanja lake lamanja pamutu pa Efereimu ngakhale kuti iyeyo anali wamngʼono ndi dzanja lake lakumanzere analisanjika pamutu pa Manase ngakhale kuti iyeyu ndiye anali mwana woyamba. 15 Kenaka anadalitsa Yosefe nati,“Mulungu amene makolo angaAbrahamu ndi Isake anamutumikira,Mulungu amene wakhala ali mʼbusa wangamoyo wanga wonse kufikira lero, 16 mngelo amene wandipulumutsa ine ku zovuta zonse,ameneyo adalitse anyamata awa.Kudzera mwa iwowadzina langa ndi mayina a makolo anga, Abrahamu ndi Isake, adzamveka.Iwowa adzakhala ndi ana ambiri nadzasanduka mtundu waukulupa dziko lapansi.” 17 Yosefe ataona kuti abambo ake ayika dzanja lamanja pa Efereimu, sanakondwere. Choncho anagwira dzanja la abambo ake kuti alichotse pamutu pa Efereimu ndi kuliyika pamutu pa Manase, 18 nati kwa abambo ake, “Ayi, abambo anga, uyu ndiye woyamba kubadwa, ikani dzanja lanu lamanja pamutu pake.” 19 Koma abambo ake anakana nati, “Ndikudziwa, mwana wanga, ndikudziwa. Adzukulu a iyeyunso adzakhala mtundu waukulu. Komabe mʼbale wake wamngʼonoyu adzakhala wamkulu kuposa iye, ndipo zidzukulu zake zidzakhala mitundu yayikulu ya anthu.” 20 Tsono iye anawadalitsa tsiku limenelo nati,“Aisraeli adzagwiritsa ntchito dzina lanu podalitsa nadzati:Mulungu akudalitseni monga Efereimu ndi Manase.”Choncho anayika Efereimu patsogolo pa Manase. 21 Kenaka Israeli anati kwa Yosefe, “Ine ndatsala pangʼono kufa, koma Mulungu adzakhala ndipo adzakutenganinso kubwerera nanu ku dziko la makolo anu. 22 Ndiponso iwe wekha ndikupatsa moposera abale ako, malo woonjezera, Sekemu, malo amene ndinalanda kwa Aamori ndi lupanga ndi uta wanga.”

In Other Versions

Genesis 48 in the ANGEFD

Genesis 48 in the ANTPNG2D

Genesis 48 in the AS21

Genesis 48 in the BAGH

Genesis 48 in the BBPNG

Genesis 48 in the BBT1E

Genesis 48 in the BDS

Genesis 48 in the BEV

Genesis 48 in the BHAD

Genesis 48 in the BIB

Genesis 48 in the BLPT

Genesis 48 in the BNT

Genesis 48 in the BNTABOOT

Genesis 48 in the BNTLV

Genesis 48 in the BOATCB

Genesis 48 in the BOATCB2

Genesis 48 in the BOBCV

Genesis 48 in the BOCNT

Genesis 48 in the BOECS

Genesis 48 in the BOHCB

Genesis 48 in the BOHCV

Genesis 48 in the BOHLNT

Genesis 48 in the BOHNTLTAL

Genesis 48 in the BOICB

Genesis 48 in the BOILNTAP

Genesis 48 in the BOITCV

Genesis 48 in the BOKCV

Genesis 48 in the BOKCV2

Genesis 48 in the BOKHWOG

Genesis 48 in the BOKSSV

Genesis 48 in the BOLCB

Genesis 48 in the BOLCB2

Genesis 48 in the BOMCV

Genesis 48 in the BONAV

Genesis 48 in the BONCB

Genesis 48 in the BONLT

Genesis 48 in the BONUT2

Genesis 48 in the BOPLNT

Genesis 48 in the BOSCB

Genesis 48 in the BOSNC

Genesis 48 in the BOTLNT

Genesis 48 in the BOVCB

Genesis 48 in the BOYCB

Genesis 48 in the BPBB

Genesis 48 in the BPH

Genesis 48 in the BSB

Genesis 48 in the CCB

Genesis 48 in the CUV

Genesis 48 in the CUVS

Genesis 48 in the DBT

Genesis 48 in the DGDNT

Genesis 48 in the DHNT

Genesis 48 in the DNT

Genesis 48 in the ELBE

Genesis 48 in the EMTV

Genesis 48 in the ESV

Genesis 48 in the FBV

Genesis 48 in the FEB

Genesis 48 in the GGMNT

Genesis 48 in the GNT

Genesis 48 in the HARY

Genesis 48 in the HNT

Genesis 48 in the IRVA

Genesis 48 in the IRVB

Genesis 48 in the IRVG

Genesis 48 in the IRVH

Genesis 48 in the IRVK

Genesis 48 in the IRVM

Genesis 48 in the IRVM2

Genesis 48 in the IRVO

Genesis 48 in the IRVP

Genesis 48 in the IRVT

Genesis 48 in the IRVT2

Genesis 48 in the IRVU

Genesis 48 in the ISVN

Genesis 48 in the JSNT

Genesis 48 in the KAPI

Genesis 48 in the KBT1ETNIK

Genesis 48 in the KBV

Genesis 48 in the KJV

Genesis 48 in the KNFD

Genesis 48 in the LBA

Genesis 48 in the LBLA

Genesis 48 in the LNT

Genesis 48 in the LSV

Genesis 48 in the MAAL

Genesis 48 in the MBV

Genesis 48 in the MBV2

Genesis 48 in the MHNT

Genesis 48 in the MKNFD

Genesis 48 in the MNG

Genesis 48 in the MNT

Genesis 48 in the MNT2

Genesis 48 in the MRS1T

Genesis 48 in the NAA

Genesis 48 in the NASB

Genesis 48 in the NBLA

Genesis 48 in the NBS

Genesis 48 in the NBVTP

Genesis 48 in the NET2

Genesis 48 in the NIV11

Genesis 48 in the NNT

Genesis 48 in the NNT2

Genesis 48 in the NNT3

Genesis 48 in the PDDPT

Genesis 48 in the PFNT

Genesis 48 in the RMNT

Genesis 48 in the SBIAS

Genesis 48 in the SBIBS

Genesis 48 in the SBIBS2

Genesis 48 in the SBICS

Genesis 48 in the SBIDS

Genesis 48 in the SBIGS

Genesis 48 in the SBIHS

Genesis 48 in the SBIIS

Genesis 48 in the SBIIS2

Genesis 48 in the SBIIS3

Genesis 48 in the SBIKS

Genesis 48 in the SBIKS2

Genesis 48 in the SBIMS

Genesis 48 in the SBIOS

Genesis 48 in the SBIPS

Genesis 48 in the SBISS

Genesis 48 in the SBITS

Genesis 48 in the SBITS2

Genesis 48 in the SBITS3

Genesis 48 in the SBITS4

Genesis 48 in the SBIUS

Genesis 48 in the SBIVS

Genesis 48 in the SBT

Genesis 48 in the SBT1E

Genesis 48 in the SCHL

Genesis 48 in the SNT

Genesis 48 in the SUSU

Genesis 48 in the SUSU2

Genesis 48 in the SYNO

Genesis 48 in the TBIAOTANT

Genesis 48 in the TBT1E

Genesis 48 in the TBT1E2

Genesis 48 in the TFTIP

Genesis 48 in the TFTU

Genesis 48 in the TGNTATF3T

Genesis 48 in the THAI

Genesis 48 in the TNFD

Genesis 48 in the TNT

Genesis 48 in the TNTIK

Genesis 48 in the TNTIL

Genesis 48 in the TNTIN

Genesis 48 in the TNTIP

Genesis 48 in the TNTIZ

Genesis 48 in the TOMA

Genesis 48 in the TTENT

Genesis 48 in the UBG

Genesis 48 in the UGV

Genesis 48 in the UGV2

Genesis 48 in the UGV3

Genesis 48 in the VBL

Genesis 48 in the VDCC

Genesis 48 in the YALU

Genesis 48 in the YAPE

Genesis 48 in the YBVTP

Genesis 48 in the ZBP