Genesis 50 (BOGWICC)

1 Kenaka Yosefe anadzigwetsa pa nkhope ya abambo ake, nawapsompsona kwinaku akulira. 2 Ndipo Yosefe analamula antchito ake a chipatala kuti akonze thupi la Israeli ndi mankhwala kuti lisawole. Kotero antchitowo anakonzadi thupilo. 3 Antchito aja zinawatengera masiku 40 kuti akonze mtembo uja popeza ntchito ngati imeneyi inafunikira masiku monga amenewa. Ndipo Aigupto anamulira Yakobo kwa masiku makumi asanu ndi awiri. 4 Yosefe atatha kulira maliro a abambo ake, anayankhula kwa nduna za Farao nati, “Ngati mungandikomere mtima, chonde mundiyankhulire kwa Farao kumuwuza kuti, 5 ‘Abambo anga anandilumbiritsa ndipo anati, ‘Ndatsala pangʼono kumwalira, ukandiyike mʼmanda amene ndinakumba ndekha mʼdziko la Kanaani.’ Tsono mundilole ndikayike abambo anga, ndipo ndikabweranso.’ ” 6 Farao anati, “Pita ukayike abambo ako monga anakulumbiritsa kuti uchite.” 7 Kotero Yosefe anapita kukayika abambo ake. Nduna zonse za Farao, akuluakulu a bwalo lake ndi akuluakulu a ku Igupto, anapita naye pamodzi. 8 Anapitanso onse a pa banja la Yosefe ndi abale ake ndi onse amene anali a pa banja la abambo ake. Ana awo okha, nkhosa ndi ngʼombe zinatsala ku Goseni 9 Asilikali okwera pa magaleta ndi asilikali a pa akavalo anapita nayenso pamodzi. Linali gulu lalikulu. 10 Atafika pa Goreni ha-Atadi, pafupi ndi Yorodani, anachita mwambo waukulu wa maliro. Choncho Yosefe analira maliro a abambo ake masiku asanu ndi awiri. 11 Akanaani amene ankakhala ku Goreni ha-Atadi ataona mwambo wa maliro anati, “Aigupto ali ndi mwambo wa maliro a akulu.” Ndi chifukwa chake malo amenewo a pafupi ndi Yorodani amatchedwa Abeli-Mizraimu. 12 Choncho ana a Yakobo anachita monga momwe abambo awo anawalamula: 13 Ndiye kuti ana a Yakobo anamunyamula kupita naye ku Kanaani kuti akamuyike mʼphanga limene lili mʼmunda wa Makipela pafupi ndi Mamre. Abrahamu anagula mundawo kwa Efroni Mhiti kuti pakhale manda. 14 Atatha kuyika abambo ake, Yosefe anabwerera ku Igupto, pamodzi ndi abale ake ndi onse amene anapita nawo kukayika abambo ake. 15 Abale ake a Yosefe ataona kuti abambo awo amwalira, anati, “Nanga tidzatani ngati Yosefe anatisungira mangawa nafuna kutibwezera pa zoyipa zonse zimene tinamuchitira?” 16 Motero anatumiza mawu kwa Yosefe kuti, “Abambo anu anasiya malangizo asanafe nati: 17 ‘Zimene mudzayenera kunena kwa Yosefe ndi izi: Ndikukupempha kuti uwakhululukire abale ako cholakwa chawo ndi machimo awo, popeza anakuchitira zoyipa.’ Ndiye tsopano chonde tikhululukireni zolakwa zimene ife akapolo a Mulungu wa abambo anu tinachita.” Yosefe atangomva mawu amenewa anayamba kulira. 18 Kenaka abale ake anabwera nadzigwetsa pansi pamaso pake, nati, “Ife ndife akapolo anu.” 19 Koma Yosefe anawawuza kuti, “Musachite mantha. Kodi ine ndalowa mʼmalo mwa Mulungu? 20 Inu munafuna kundichitira zoyipa, koma Mulungu anasandutsa zoyipazo kuti zikhale zabwino kuti zikwaniritsidwe zimene zikuchitika panozi, zopulumutsa miyoyo yambiri. 21 Kotero, musachite mantha. Ine ndidzasamalira inu pamodzi ndi ana anu omwe.” Tsono iye anawalimbitsa mtima powayankhula moleza mtima. 22 Yosefe anakhala mu Igupto pamodzi ndi banja lonse la abambo ake. Anakhala ndi moyo zaka 110 23 ndipo anaona mʼbado wachitatu wa ana a Efereimu. Yosefe anatenganso ana a Makiri, mwana wa Manase kukhala ngati ana a mʼbanja lake. 24 Kenaka Yosefe anati kwa abale ake, “Ine ndatsala pangʼono kufa. Koma mosakayika Mulungu adzakuyangʼanirani nadzakutengani kukutulutsani mʼdziko lino kupita ku dziko limene Iye analonjeza kwa Abrahamu, Isake ndi Yakobo.” 25 Ndipo Yosefe analumbiritsa ana a Israeli lumbiro nati, “Lonjezani kuti Mulungu akadzakusungani mudzanyamula mafupa anga kuwachotsa ku malo kuno.” 26 Choncho Yosefe anafa ali ndi zaka 110. Motero iwo atakonza thupi lake ndi mankhwala kuti lisawole, analiyika mʼbokosi ku Igupto.

In Other Versions

Genesis 50 in the ANGEFD

Genesis 50 in the ANTPNG2D

Genesis 50 in the AS21

Genesis 50 in the BAGH

Genesis 50 in the BBPNG

Genesis 50 in the BBT1E

Genesis 50 in the BDS

Genesis 50 in the BEV

Genesis 50 in the BHAD

Genesis 50 in the BIB

Genesis 50 in the BLPT

Genesis 50 in the BNT

Genesis 50 in the BNTABOOT

Genesis 50 in the BNTLV

Genesis 50 in the BOATCB

Genesis 50 in the BOATCB2

Genesis 50 in the BOBCV

Genesis 50 in the BOCNT

Genesis 50 in the BOECS

Genesis 50 in the BOHCB

Genesis 50 in the BOHCV

Genesis 50 in the BOHLNT

Genesis 50 in the BOHNTLTAL

Genesis 50 in the BOICB

Genesis 50 in the BOILNTAP

Genesis 50 in the BOITCV

Genesis 50 in the BOKCV

Genesis 50 in the BOKCV2

Genesis 50 in the BOKHWOG

Genesis 50 in the BOKSSV

Genesis 50 in the BOLCB

Genesis 50 in the BOLCB2

Genesis 50 in the BOMCV

Genesis 50 in the BONAV

Genesis 50 in the BONCB

Genesis 50 in the BONLT

Genesis 50 in the BONUT2

Genesis 50 in the BOPLNT

Genesis 50 in the BOSCB

Genesis 50 in the BOSNC

Genesis 50 in the BOTLNT

Genesis 50 in the BOVCB

Genesis 50 in the BOYCB

Genesis 50 in the BPBB

Genesis 50 in the BPH

Genesis 50 in the BSB

Genesis 50 in the CCB

Genesis 50 in the CUV

Genesis 50 in the CUVS

Genesis 50 in the DBT

Genesis 50 in the DGDNT

Genesis 50 in the DHNT

Genesis 50 in the DNT

Genesis 50 in the ELBE

Genesis 50 in the EMTV

Genesis 50 in the ESV

Genesis 50 in the FBV

Genesis 50 in the FEB

Genesis 50 in the GGMNT

Genesis 50 in the GNT

Genesis 50 in the HARY

Genesis 50 in the HNT

Genesis 50 in the IRVA

Genesis 50 in the IRVB

Genesis 50 in the IRVG

Genesis 50 in the IRVH

Genesis 50 in the IRVK

Genesis 50 in the IRVM

Genesis 50 in the IRVM2

Genesis 50 in the IRVO

Genesis 50 in the IRVP

Genesis 50 in the IRVT

Genesis 50 in the IRVT2

Genesis 50 in the IRVU

Genesis 50 in the ISVN

Genesis 50 in the JSNT

Genesis 50 in the KAPI

Genesis 50 in the KBT1ETNIK

Genesis 50 in the KBV

Genesis 50 in the KJV

Genesis 50 in the KNFD

Genesis 50 in the LBA

Genesis 50 in the LBLA

Genesis 50 in the LNT

Genesis 50 in the LSV

Genesis 50 in the MAAL

Genesis 50 in the MBV

Genesis 50 in the MBV2

Genesis 50 in the MHNT

Genesis 50 in the MKNFD

Genesis 50 in the MNG

Genesis 50 in the MNT

Genesis 50 in the MNT2

Genesis 50 in the MRS1T

Genesis 50 in the NAA

Genesis 50 in the NASB

Genesis 50 in the NBLA

Genesis 50 in the NBS

Genesis 50 in the NBVTP

Genesis 50 in the NET2

Genesis 50 in the NIV11

Genesis 50 in the NNT

Genesis 50 in the NNT2

Genesis 50 in the NNT3

Genesis 50 in the PDDPT

Genesis 50 in the PFNT

Genesis 50 in the RMNT

Genesis 50 in the SBIAS

Genesis 50 in the SBIBS

Genesis 50 in the SBIBS2

Genesis 50 in the SBICS

Genesis 50 in the SBIDS

Genesis 50 in the SBIGS

Genesis 50 in the SBIHS

Genesis 50 in the SBIIS

Genesis 50 in the SBIIS2

Genesis 50 in the SBIIS3

Genesis 50 in the SBIKS

Genesis 50 in the SBIKS2

Genesis 50 in the SBIMS

Genesis 50 in the SBIOS

Genesis 50 in the SBIPS

Genesis 50 in the SBISS

Genesis 50 in the SBITS

Genesis 50 in the SBITS2

Genesis 50 in the SBITS3

Genesis 50 in the SBITS4

Genesis 50 in the SBIUS

Genesis 50 in the SBIVS

Genesis 50 in the SBT

Genesis 50 in the SBT1E

Genesis 50 in the SCHL

Genesis 50 in the SNT

Genesis 50 in the SUSU

Genesis 50 in the SUSU2

Genesis 50 in the SYNO

Genesis 50 in the TBIAOTANT

Genesis 50 in the TBT1E

Genesis 50 in the TBT1E2

Genesis 50 in the TFTIP

Genesis 50 in the TFTU

Genesis 50 in the TGNTATF3T

Genesis 50 in the THAI

Genesis 50 in the TNFD

Genesis 50 in the TNT

Genesis 50 in the TNTIK

Genesis 50 in the TNTIL

Genesis 50 in the TNTIN

Genesis 50 in the TNTIP

Genesis 50 in the TNTIZ

Genesis 50 in the TOMA

Genesis 50 in the TTENT

Genesis 50 in the UBG

Genesis 50 in the UGV

Genesis 50 in the UGV2

Genesis 50 in the UGV3

Genesis 50 in the VBL

Genesis 50 in the VDCC

Genesis 50 in the YALU

Genesis 50 in the YAPE

Genesis 50 in the YBVTP

Genesis 50 in the ZBP