Jeremiah 37 (BOGWICC)

1 Nebukadinezara mfumu ya Babuloni, inakhazika pa mpando waufumu Zedekiya mwana wa Yosiya kukhala mfumu ya Yuda. Iye analowa mʼmalo mwa Yehoyakini mwana wa Yehoyakimu. 2 Koma Zedekiya kapena atumiki ake ngakhalenso anthu a mʼdzikomo sanasamalire mawu a Yehova amene anayankhula kudzera mwa mneneri Yeremiya. 3 Tsono Zedekiya anatuma Yehukali mwana wa Selemiya ndi wansembe Zefaniya mwana wa Maseya kwa mneneri Yeremiya ndi uthenga uwu: “Chonde tipempherereni kwa Yehova Mulungu wathu.” 4 Nthawi imeneyinso nʼkuti Yeremiya ali ndi ufulu woyenda pakati pa anthu chifukwa anali asanaponyedwe mʼndende. 5 Nthawi imeneyinso nʼkuti gulu lankhondo la Farao litatuluka mʼdziko la Igupto. Ndipo Ababuloni amene anali atazinga Yerusalemu atamva zimenezi, anachoka ku Yerusalemuko. 6 Tsono Yehova anawuza mneneri Yeremiya kuti, 7 “Uyiwuze mfumu ya Yuda imene inakutuma kuti udzapemphe nzeru kwa ine kuti Ine Yehova, Mulungu wa Israeli ndikuti, gulu lankhondo la Farao limene linatuluka kuti lidzakuthandize lidzabwerera kwawo ku Igupto. 8 Ndipo Ababuloni adzabwerera kudzathira nkhondo mzinda uno. Iwo adzawugonjetsa ndi kuwutentha. 9 “Yehova akuti: Musadzinyenge, nʼkumaganiza kuti, ‘Ndithu Ababuloni adzatisiya.’ Ndithudi sadzakusiyani! 10 Ngakhale mutagonjetsa gulu lonse lankhondo la Ababuloni limene likukuthirani nkhondo ndipo mʼmatenti mwawo ndikutsala anthu ovulala okhaokha, amenewo adzabwera ndi kudzatentha mzinda uno.” 11 Gulu lankhondo la Ababuloni litaleka kuthira nkhondo mzinda wa Yerusalemu chifukwa choopa gulu lankhondo la Farao, 12 Yeremiya ananyamuka kuchoka ku Yerusalemu ndi kumapita ku dziko la Benjamini kuti akalandire gawo lake la minda ya makolo ake. 13 Koma atafika pa Chipata cha Benjamini, mkulu wa alonda amene dzina lake linali Iriya mwana wa Selemiya, mwana wa Hananiya, anagwira mneneri Yeremiyayo ndipo anati, “Iwe ukuthawira kwa Ababuloni!” 14 Yeremiya anati, “Zimenezo si zoona! Ine sindikuthawira kwa Ababuloni.” Koma Iriya sanamumvere. Mʼmalo mwake anagwira Yeremiya nʼkupita naye kwa akuluakulu. 15 Akuluakuluwo anamupsera mtima Yeremiya ndipo anamukwapula ndi kumuyika mʼnyumba ya mlembi Yonatani, imene anayisandutsa ndende. 16 Yeremiya anayikidwa mʼndende ya pansi pa nthaka, kumene anakhalako nthawi yayitali. 17 Kenaka Mfumu Zedekiya inatuma anthu kuti akayitane Yeremiya ndipo anabwera naye ku nyumba ya mfumu. Atafika mfumu inamufunsa mwamseri kuti, “Kodi pali mawu ena amene Yehova wakuwuza?”Yeremiya anayankha kuti, “Inde. Inu mfumu mudzaperekedwa kwa mfumu ya ku Babuloni.” 18 Pamenepo Yeremiya anafunsa Mfumu Zedekiya kuti, “Kodi ndakulakwirani chiyani inuyo kapena akuluakulu anu kapenanso anthu awa, kuti mundiyike mʼndende? 19 Kodi ali kuti aneneri anu amene anakuloserani kuti, ‘Mfumu ya ku Babuloni sidzakuthirani nkhondo pamodzi ndi dziko lino’? 20 Koma tsopano, mbuye wanga mfumu, chonde tamverani. Loleni ndinene pempho langa pamaso panu: Musandibwezere ku nyumba ya mlembi Yonatani, kuopa kuti ndingakafere kumeneko.” 21 Tsono Mfumu Zedekiya analamula kuti Yeremiya asungidwe mʼbwalo la alonda. Ankamupatsa buledi tsiku ndi tsiku amene ankamugula kwa ophika buledi. Anapitiriza kutero mpaka buledi yense anatha mu mzindamo. Choncho Yeremiya anapitirira kukhala mʼbwalo la alonda.

In Other Versions

Jeremiah 37 in the ANGEFD

Jeremiah 37 in the ANTPNG2D

Jeremiah 37 in the AS21

Jeremiah 37 in the BAGH

Jeremiah 37 in the BBPNG

Jeremiah 37 in the BBT1E

Jeremiah 37 in the BDS

Jeremiah 37 in the BEV

Jeremiah 37 in the BHAD

Jeremiah 37 in the BIB

Jeremiah 37 in the BLPT

Jeremiah 37 in the BNT

Jeremiah 37 in the BNTABOOT

Jeremiah 37 in the BNTLV

Jeremiah 37 in the BOATCB

Jeremiah 37 in the BOATCB2

Jeremiah 37 in the BOBCV

Jeremiah 37 in the BOCNT

Jeremiah 37 in the BOECS

Jeremiah 37 in the BOHCB

Jeremiah 37 in the BOHCV

Jeremiah 37 in the BOHLNT

Jeremiah 37 in the BOHNTLTAL

Jeremiah 37 in the BOICB

Jeremiah 37 in the BOILNTAP

Jeremiah 37 in the BOITCV

Jeremiah 37 in the BOKCV

Jeremiah 37 in the BOKCV2

Jeremiah 37 in the BOKHWOG

Jeremiah 37 in the BOKSSV

Jeremiah 37 in the BOLCB

Jeremiah 37 in the BOLCB2

Jeremiah 37 in the BOMCV

Jeremiah 37 in the BONAV

Jeremiah 37 in the BONCB

Jeremiah 37 in the BONLT

Jeremiah 37 in the BONUT2

Jeremiah 37 in the BOPLNT

Jeremiah 37 in the BOSCB

Jeremiah 37 in the BOSNC

Jeremiah 37 in the BOTLNT

Jeremiah 37 in the BOVCB

Jeremiah 37 in the BOYCB

Jeremiah 37 in the BPBB

Jeremiah 37 in the BPH

Jeremiah 37 in the BSB

Jeremiah 37 in the CCB

Jeremiah 37 in the CUV

Jeremiah 37 in the CUVS

Jeremiah 37 in the DBT

Jeremiah 37 in the DGDNT

Jeremiah 37 in the DHNT

Jeremiah 37 in the DNT

Jeremiah 37 in the ELBE

Jeremiah 37 in the EMTV

Jeremiah 37 in the ESV

Jeremiah 37 in the FBV

Jeremiah 37 in the FEB

Jeremiah 37 in the GGMNT

Jeremiah 37 in the GNT

Jeremiah 37 in the HARY

Jeremiah 37 in the HNT

Jeremiah 37 in the IRVA

Jeremiah 37 in the IRVB

Jeremiah 37 in the IRVG

Jeremiah 37 in the IRVH

Jeremiah 37 in the IRVK

Jeremiah 37 in the IRVM

Jeremiah 37 in the IRVM2

Jeremiah 37 in the IRVO

Jeremiah 37 in the IRVP

Jeremiah 37 in the IRVT

Jeremiah 37 in the IRVT2

Jeremiah 37 in the IRVU

Jeremiah 37 in the ISVN

Jeremiah 37 in the JSNT

Jeremiah 37 in the KAPI

Jeremiah 37 in the KBT1ETNIK

Jeremiah 37 in the KBV

Jeremiah 37 in the KJV

Jeremiah 37 in the KNFD

Jeremiah 37 in the LBA

Jeremiah 37 in the LBLA

Jeremiah 37 in the LNT

Jeremiah 37 in the LSV

Jeremiah 37 in the MAAL

Jeremiah 37 in the MBV

Jeremiah 37 in the MBV2

Jeremiah 37 in the MHNT

Jeremiah 37 in the MKNFD

Jeremiah 37 in the MNG

Jeremiah 37 in the MNT

Jeremiah 37 in the MNT2

Jeremiah 37 in the MRS1T

Jeremiah 37 in the NAA

Jeremiah 37 in the NASB

Jeremiah 37 in the NBLA

Jeremiah 37 in the NBS

Jeremiah 37 in the NBVTP

Jeremiah 37 in the NET2

Jeremiah 37 in the NIV11

Jeremiah 37 in the NNT

Jeremiah 37 in the NNT2

Jeremiah 37 in the NNT3

Jeremiah 37 in the PDDPT

Jeremiah 37 in the PFNT

Jeremiah 37 in the RMNT

Jeremiah 37 in the SBIAS

Jeremiah 37 in the SBIBS

Jeremiah 37 in the SBIBS2

Jeremiah 37 in the SBICS

Jeremiah 37 in the SBIDS

Jeremiah 37 in the SBIGS

Jeremiah 37 in the SBIHS

Jeremiah 37 in the SBIIS

Jeremiah 37 in the SBIIS2

Jeremiah 37 in the SBIIS3

Jeremiah 37 in the SBIKS

Jeremiah 37 in the SBIKS2

Jeremiah 37 in the SBIMS

Jeremiah 37 in the SBIOS

Jeremiah 37 in the SBIPS

Jeremiah 37 in the SBISS

Jeremiah 37 in the SBITS

Jeremiah 37 in the SBITS2

Jeremiah 37 in the SBITS3

Jeremiah 37 in the SBITS4

Jeremiah 37 in the SBIUS

Jeremiah 37 in the SBIVS

Jeremiah 37 in the SBT

Jeremiah 37 in the SBT1E

Jeremiah 37 in the SCHL

Jeremiah 37 in the SNT

Jeremiah 37 in the SUSU

Jeremiah 37 in the SUSU2

Jeremiah 37 in the SYNO

Jeremiah 37 in the TBIAOTANT

Jeremiah 37 in the TBT1E

Jeremiah 37 in the TBT1E2

Jeremiah 37 in the TFTIP

Jeremiah 37 in the TFTU

Jeremiah 37 in the TGNTATF3T

Jeremiah 37 in the THAI

Jeremiah 37 in the TNFD

Jeremiah 37 in the TNT

Jeremiah 37 in the TNTIK

Jeremiah 37 in the TNTIL

Jeremiah 37 in the TNTIN

Jeremiah 37 in the TNTIP

Jeremiah 37 in the TNTIZ

Jeremiah 37 in the TOMA

Jeremiah 37 in the TTENT

Jeremiah 37 in the UBG

Jeremiah 37 in the UGV

Jeremiah 37 in the UGV2

Jeremiah 37 in the UGV3

Jeremiah 37 in the VBL

Jeremiah 37 in the VDCC

Jeremiah 37 in the YALU

Jeremiah 37 in the YAPE

Jeremiah 37 in the YBVTP

Jeremiah 37 in the ZBP