Proverbs 16 (BOGWICC)

1 Zolinga za mu mtima ndi za munthu,koma kwa Yehova ndiye kumachokera yankho. 2 Zochita zonse za munthu zimaoneka zabwino pamaso pake,koma Yehova ndiye amasanthula zolinga zako. 3 Pereka ntchito zako zonse mʼmanja mwa Yehova,ndipo zolinga zako zidzachitikadi. 4 Yehova amachita zonse ndi cholinga chake,ngakhale anthu oyipa kuti aone tsiku latsoka. 5 Munthu aliyense wodzikuza amamunyansa Yehova.Koma dziwani izi: Iwo sadzakhala osalangidwa. 6 Chifukwa cha chikondi chosasinthika ndi kukhulupirika, munthu amakhululukidwa machimo ake;chifukwa cha kuopa Yehova munthu amapewa zoyipa. 7 Pamene makhalidwe a munthu akondweretsa Yehova,ngakhale adani ake amakhala naye mwa mtendere. 8 Kuli bwino kukhala ndi zinthu pangʼono zozipeza mwachilungamo,kusiyana ndi kukhala ndi zinthu zambiri zozipeza popanda chilungamo. 9 Mtima wa munthu umalingalira zochita,koma Yehova ndiye amakhazikitsa njira zake. 10 Mawu a mfumu ali ngati mawu ochokera kwa Mulungu;ndipo pakamwa pake sipalakwa poweruza mlandu. 11 Miyeso ndi masikelo achilungamo zimachokera kwa Yehova;miyala yonse yoyesera ya mʼthumba anayipanga ndi Yehova. 12 Kuchita zoyipa kumanyansa mafumu,pakuti chilungamo ndiye maziko a ufumu wake. 13 Mawu owona amakondweretsa mfumu.Iyo imakonda munthu woyankhula choonadi. 14 Ukali wa mfumu ndi mthenga wa imfa,koma munthu wanzeru amawupepesa ukaliwo. 15 Kuwala kwa nkhope ya mfumu kumapatsa moyo;ndipo kukoma mtima kwake kuli ngati mitambo ya mvula nthawi ya chilimwe. 16 Nʼkwabwino kwambiri kupeza nzeru kupambana golide.Kukhala womvetsa bwino zinthu nʼkwabwino kupambana ndi kukhala ndi siliva. 17 Msewu wa munthu wowongoka mtima umapewa zoyipa;wopenyetsetsa kumene akupita amasunga moyo wake. 18 Kunyada kumafikitsa ku chiwonongeko,ndipo munthu wodzikuza adzagwa. 19 Nʼkwabwino kukhala ndi mtima wodzichepetsa pakati pa anthu oponderezedwa,kusiyana ndi kugawana zolanda ndi anthu onyada. 20 Munthu womvera malangizo zinthu zimamuyendera bwino,ndipo wodala ndi amene amadalira Yehova. 21 A mtima wanzeru amatchedwa ozindikira zinthu,ndipo mawu ake okoma amawonjezera nzeru. 22 Kumvetsa zinthu ndi kasupe wa moyo kwa iwo amene ali nako,koma uchitsiru umabweretsa chilango kwa zitsiru. 23 Mtima wanzeru umathandiza munthu kuyankhula mwa nzeru,ndipo mawu ake amawonjezera nzeru. 24 Mawu okometsera ali ngati chisa cha njuchi,amakoma mu mtima ndipo amalimbitsa thupi. 25 Pali njira ina yooneka ngati yowongoka kwa munthukoma kumatsiriziro kwake ndi imfa. 26 Njala ya munthu wantchito imamuthandiza kulimbikira;njalayo imamukakamiza kuchitapo kanthu. 27 Munthu wopanda pake amakonzekera kuchita zoyipandipo mawu ake ali ngati moto wopsereza. 28 Munthu woyipa mtima amayambitsa mikangano,ndipo miseche imalekanitsa anthu okondana kwambiri. 29 Munthu wandewu amakopa mnansi wake,ndipo amamuyendetsa njira imene si yabwino. 30 Amene amatsinzinira maso ake amalingalira zinthu zokhota;amene amachita msunamo amakonzeka kuchita zoyipa. 31 Imvi zili ngati chipewa chaufumu chaulemerero;munthu amazipeza akakhala moyo wolungama. 32 Munthu wosapsa mtima msanga amaposa munthu wankhondo,munthu wowugwira mtima wake amaposa amene amalanda mzinda. 33 Maere amaponyedwa pa mfunga,koma ndiye Yehova amene amalongosola zonse.

In Other Versions

Proverbs 16 in the ANGEFD

Proverbs 16 in the ANTPNG2D

Proverbs 16 in the AS21

Proverbs 16 in the BAGH

Proverbs 16 in the BBPNG

Proverbs 16 in the BBT1E

Proverbs 16 in the BDS

Proverbs 16 in the BEV

Proverbs 16 in the BHAD

Proverbs 16 in the BIB

Proverbs 16 in the BLPT

Proverbs 16 in the BNT

Proverbs 16 in the BNTABOOT

Proverbs 16 in the BNTLV

Proverbs 16 in the BOATCB

Proverbs 16 in the BOATCB2

Proverbs 16 in the BOBCV

Proverbs 16 in the BOCNT

Proverbs 16 in the BOECS

Proverbs 16 in the BOHCB

Proverbs 16 in the BOHCV

Proverbs 16 in the BOHLNT

Proverbs 16 in the BOHNTLTAL

Proverbs 16 in the BOICB

Proverbs 16 in the BOILNTAP

Proverbs 16 in the BOITCV

Proverbs 16 in the BOKCV

Proverbs 16 in the BOKCV2

Proverbs 16 in the BOKHWOG

Proverbs 16 in the BOKSSV

Proverbs 16 in the BOLCB

Proverbs 16 in the BOLCB2

Proverbs 16 in the BOMCV

Proverbs 16 in the BONAV

Proverbs 16 in the BONCB

Proverbs 16 in the BONLT

Proverbs 16 in the BONUT2

Proverbs 16 in the BOPLNT

Proverbs 16 in the BOSCB

Proverbs 16 in the BOSNC

Proverbs 16 in the BOTLNT

Proverbs 16 in the BOVCB

Proverbs 16 in the BOYCB

Proverbs 16 in the BPBB

Proverbs 16 in the BPH

Proverbs 16 in the BSB

Proverbs 16 in the CCB

Proverbs 16 in the CUV

Proverbs 16 in the CUVS

Proverbs 16 in the DBT

Proverbs 16 in the DGDNT

Proverbs 16 in the DHNT

Proverbs 16 in the DNT

Proverbs 16 in the ELBE

Proverbs 16 in the EMTV

Proverbs 16 in the ESV

Proverbs 16 in the FBV

Proverbs 16 in the FEB

Proverbs 16 in the GGMNT

Proverbs 16 in the GNT

Proverbs 16 in the HARY

Proverbs 16 in the HNT

Proverbs 16 in the IRVA

Proverbs 16 in the IRVB

Proverbs 16 in the IRVG

Proverbs 16 in the IRVH

Proverbs 16 in the IRVK

Proverbs 16 in the IRVM

Proverbs 16 in the IRVM2

Proverbs 16 in the IRVO

Proverbs 16 in the IRVP

Proverbs 16 in the IRVT

Proverbs 16 in the IRVT2

Proverbs 16 in the IRVU

Proverbs 16 in the ISVN

Proverbs 16 in the JSNT

Proverbs 16 in the KAPI

Proverbs 16 in the KBT1ETNIK

Proverbs 16 in the KBV

Proverbs 16 in the KJV

Proverbs 16 in the KNFD

Proverbs 16 in the LBA

Proverbs 16 in the LBLA

Proverbs 16 in the LNT

Proverbs 16 in the LSV

Proverbs 16 in the MAAL

Proverbs 16 in the MBV

Proverbs 16 in the MBV2

Proverbs 16 in the MHNT

Proverbs 16 in the MKNFD

Proverbs 16 in the MNG

Proverbs 16 in the MNT

Proverbs 16 in the MNT2

Proverbs 16 in the MRS1T

Proverbs 16 in the NAA

Proverbs 16 in the NASB

Proverbs 16 in the NBLA

Proverbs 16 in the NBS

Proverbs 16 in the NBVTP

Proverbs 16 in the NET2

Proverbs 16 in the NIV11

Proverbs 16 in the NNT

Proverbs 16 in the NNT2

Proverbs 16 in the NNT3

Proverbs 16 in the PDDPT

Proverbs 16 in the PFNT

Proverbs 16 in the RMNT

Proverbs 16 in the SBIAS

Proverbs 16 in the SBIBS

Proverbs 16 in the SBIBS2

Proverbs 16 in the SBICS

Proverbs 16 in the SBIDS

Proverbs 16 in the SBIGS

Proverbs 16 in the SBIHS

Proverbs 16 in the SBIIS

Proverbs 16 in the SBIIS2

Proverbs 16 in the SBIIS3

Proverbs 16 in the SBIKS

Proverbs 16 in the SBIKS2

Proverbs 16 in the SBIMS

Proverbs 16 in the SBIOS

Proverbs 16 in the SBIPS

Proverbs 16 in the SBISS

Proverbs 16 in the SBITS

Proverbs 16 in the SBITS2

Proverbs 16 in the SBITS3

Proverbs 16 in the SBITS4

Proverbs 16 in the SBIUS

Proverbs 16 in the SBIVS

Proverbs 16 in the SBT

Proverbs 16 in the SBT1E

Proverbs 16 in the SCHL

Proverbs 16 in the SNT

Proverbs 16 in the SUSU

Proverbs 16 in the SUSU2

Proverbs 16 in the SYNO

Proverbs 16 in the TBIAOTANT

Proverbs 16 in the TBT1E

Proverbs 16 in the TBT1E2

Proverbs 16 in the TFTIP

Proverbs 16 in the TFTU

Proverbs 16 in the TGNTATF3T

Proverbs 16 in the THAI

Proverbs 16 in the TNFD

Proverbs 16 in the TNT

Proverbs 16 in the TNTIK

Proverbs 16 in the TNTIL

Proverbs 16 in the TNTIN

Proverbs 16 in the TNTIP

Proverbs 16 in the TNTIZ

Proverbs 16 in the TOMA

Proverbs 16 in the TTENT

Proverbs 16 in the UBG

Proverbs 16 in the UGV

Proverbs 16 in the UGV2

Proverbs 16 in the UGV3

Proverbs 16 in the VBL

Proverbs 16 in the VDCC

Proverbs 16 in the YALU

Proverbs 16 in the YAPE

Proverbs 16 in the YBVTP

Proverbs 16 in the ZBP