Proverbs 31 (BOGWICC)

1 Nawa mawu a mfumu Lemueli wa ku Massa amene anamuphunzitsa amayi ake: 2 Nʼchiyani mwana wanga? Nʼchiyani mwana wa mʼmimba mwanga?Nʼchiyani iwe mwana wanga amene ndinachita kupempha ndi malumbiro? 3 Usapereke mphamvu yako kwa akazi.Usamayenda nawo amenewa popeza amawononga ngakhale mafumu. 4 Iwe Lemueli si choyenera kwa mafumu,mafumu sayenera kumwa vinyo.Olamulira asamalakalake chakumwa choledzeretsa 5 kuopa kuti akamwa adzayiwala malamulo a dziko,nayamba kukhotetsa zinthu zoyenera anthu osauka. 6 Perekani chakumwa choledzeretsa kwa amene ali pafupi kufa,vinyo kwa amene ali pa mavuto woopsa; 7 amwe kuti ayiwale umphawi wawoasakumbukirenso kuvutika kwawo. 8 Yankhula mʼmalo mwa amene sangathe kudziyankhulira okha.Uwayankhulire anthu onse osiyidwa pa zonse zowayenera. 9 Yankhula ndi kuweruza mwachilungamo.Uwateteze amphawi ndi osauka. 10 Kodi mkazi wangwiro angathe kumupeza ndani?Ndi wokwera mtengo kuposa miyala yamtengowapatali. 11 Mtima wa mwamuna wake umamukhulupirirandipo mwamunayo sasowa phindu. 12 Masiku onse a moyo wakemkaziyo amachitira mwamuna wake zabwino zokhazokha osati zoyipa. 13 Iye amafunafuna ubweya ndi thonje;amagwira ntchito ndi manja ake mwaufulu. 14 Iye ali ngati sitima zapamadzi za anthu amalonda,amakatenga chakudya chake kutali. 15 Iye amadzuka kusanache kwenikweni;ndi kuyamba kukonzera a pa banja pake chakudyandi kuwagawira ntchito atsikana ake antchito. 16 Iye amalingalira za munda ndi kuwugula;ndi ndalama zimene wazipeza amalima munda wamphesa. 17 Iye amavala zilimbenagwira ntchito mwamphamvu ndi manja ake. 18 Iye amaona kuti malonda ake ndi aphindu,choncho nyale yake sizima usiku wonse. 19 Iye amadzilukira thonjendipo yekha amagwira chowombera nsalu. 20 Iye amachitira chifundo anthu osaukandipo amapereka chithandizo kwa anthu osowa. 21 Iye saopa kuti banja lake lifa ndi kuzizira pa nyengo yachisanu;pakuti onse amakhala atavala zovala zofunda. 22 Iye amadzipangira yekha zoyala pa bedi pake;amavala zovala zabafuta ndi zapepo. 23 Mwamuna wake ndi wodziwika pa chipata cha mzinda,ndipo amakhala pakati pa akuluakulu a mʼdzikomo. 24 Iye amasoka nsalu zabafuta nazigulitsa;amaperekanso mipango kwa anthu amalonda. 25 Mphamvu ndi ulemu zimakhala ngati chovala chake;ndipo amaseka osaopa zamʼtsogolo. 26 Iye amayankhula mwanzeru,amaphunzitsa anthu mwachikondi. 27 Iye amayangʼanira makhalidwe a anthu a pa banja lakendipo sachita ulesi ndi pangʼono pomwe. 28 Ana ake amamunyadira ndipo amamutcha kuti wodala;ndipo mwamuna wake, amamuyamikira nʼkumati, 29 “Pali akazi ambiri amene achita zinthu zopambanakoma iwe umawaposa onsewa.” 30 Nkhope yachikoka ndi yonyenga, ndipo kukongola nʼkosakhalitsa;koma mkazi amene amaopa Yehova ayenera kutamandidwa. 31 Mupatseni mphotho chifukwa cha zimene iye wachitandipo ntchito zake zimutamande ku mabwalo.

In Other Versions

Proverbs 31 in the ANGEFD

Proverbs 31 in the ANTPNG2D

Proverbs 31 in the AS21

Proverbs 31 in the BAGH

Proverbs 31 in the BBPNG

Proverbs 31 in the BBT1E

Proverbs 31 in the BDS

Proverbs 31 in the BEV

Proverbs 31 in the BHAD

Proverbs 31 in the BIB

Proverbs 31 in the BLPT

Proverbs 31 in the BNT

Proverbs 31 in the BNTABOOT

Proverbs 31 in the BNTLV

Proverbs 31 in the BOATCB

Proverbs 31 in the BOATCB2

Proverbs 31 in the BOBCV

Proverbs 31 in the BOCNT

Proverbs 31 in the BOECS

Proverbs 31 in the BOHCB

Proverbs 31 in the BOHCV

Proverbs 31 in the BOHLNT

Proverbs 31 in the BOHNTLTAL

Proverbs 31 in the BOICB

Proverbs 31 in the BOILNTAP

Proverbs 31 in the BOITCV

Proverbs 31 in the BOKCV

Proverbs 31 in the BOKCV2

Proverbs 31 in the BOKHWOG

Proverbs 31 in the BOKSSV

Proverbs 31 in the BOLCB

Proverbs 31 in the BOLCB2

Proverbs 31 in the BOMCV

Proverbs 31 in the BONAV

Proverbs 31 in the BONCB

Proverbs 31 in the BONLT

Proverbs 31 in the BONUT2

Proverbs 31 in the BOPLNT

Proverbs 31 in the BOSCB

Proverbs 31 in the BOSNC

Proverbs 31 in the BOTLNT

Proverbs 31 in the BOVCB

Proverbs 31 in the BOYCB

Proverbs 31 in the BPBB

Proverbs 31 in the BPH

Proverbs 31 in the BSB

Proverbs 31 in the CCB

Proverbs 31 in the CUV

Proverbs 31 in the CUVS

Proverbs 31 in the DBT

Proverbs 31 in the DGDNT

Proverbs 31 in the DHNT

Proverbs 31 in the DNT

Proverbs 31 in the ELBE

Proverbs 31 in the EMTV

Proverbs 31 in the ESV

Proverbs 31 in the FBV

Proverbs 31 in the FEB

Proverbs 31 in the GGMNT

Proverbs 31 in the GNT

Proverbs 31 in the HARY

Proverbs 31 in the HNT

Proverbs 31 in the IRVA

Proverbs 31 in the IRVB

Proverbs 31 in the IRVG

Proverbs 31 in the IRVH

Proverbs 31 in the IRVK

Proverbs 31 in the IRVM

Proverbs 31 in the IRVM2

Proverbs 31 in the IRVO

Proverbs 31 in the IRVP

Proverbs 31 in the IRVT

Proverbs 31 in the IRVT2

Proverbs 31 in the IRVU

Proverbs 31 in the ISVN

Proverbs 31 in the JSNT

Proverbs 31 in the KAPI

Proverbs 31 in the KBT1ETNIK

Proverbs 31 in the KBV

Proverbs 31 in the KJV

Proverbs 31 in the KNFD

Proverbs 31 in the LBA

Proverbs 31 in the LBLA

Proverbs 31 in the LNT

Proverbs 31 in the LSV

Proverbs 31 in the MAAL

Proverbs 31 in the MBV

Proverbs 31 in the MBV2

Proverbs 31 in the MHNT

Proverbs 31 in the MKNFD

Proverbs 31 in the MNG

Proverbs 31 in the MNT

Proverbs 31 in the MNT2

Proverbs 31 in the MRS1T

Proverbs 31 in the NAA

Proverbs 31 in the NASB

Proverbs 31 in the NBLA

Proverbs 31 in the NBS

Proverbs 31 in the NBVTP

Proverbs 31 in the NET2

Proverbs 31 in the NIV11

Proverbs 31 in the NNT

Proverbs 31 in the NNT2

Proverbs 31 in the NNT3

Proverbs 31 in the PDDPT

Proverbs 31 in the PFNT

Proverbs 31 in the RMNT

Proverbs 31 in the SBIAS

Proverbs 31 in the SBIBS

Proverbs 31 in the SBIBS2

Proverbs 31 in the SBICS

Proverbs 31 in the SBIDS

Proverbs 31 in the SBIGS

Proverbs 31 in the SBIHS

Proverbs 31 in the SBIIS

Proverbs 31 in the SBIIS2

Proverbs 31 in the SBIIS3

Proverbs 31 in the SBIKS

Proverbs 31 in the SBIKS2

Proverbs 31 in the SBIMS

Proverbs 31 in the SBIOS

Proverbs 31 in the SBIPS

Proverbs 31 in the SBISS

Proverbs 31 in the SBITS

Proverbs 31 in the SBITS2

Proverbs 31 in the SBITS3

Proverbs 31 in the SBITS4

Proverbs 31 in the SBIUS

Proverbs 31 in the SBIVS

Proverbs 31 in the SBT

Proverbs 31 in the SBT1E

Proverbs 31 in the SCHL

Proverbs 31 in the SNT

Proverbs 31 in the SUSU

Proverbs 31 in the SUSU2

Proverbs 31 in the SYNO

Proverbs 31 in the TBIAOTANT

Proverbs 31 in the TBT1E

Proverbs 31 in the TBT1E2

Proverbs 31 in the TFTIP

Proverbs 31 in the TFTU

Proverbs 31 in the TGNTATF3T

Proverbs 31 in the THAI

Proverbs 31 in the TNFD

Proverbs 31 in the TNT

Proverbs 31 in the TNTIK

Proverbs 31 in the TNTIL

Proverbs 31 in the TNTIN

Proverbs 31 in the TNTIP

Proverbs 31 in the TNTIZ

Proverbs 31 in the TOMA

Proverbs 31 in the TTENT

Proverbs 31 in the UBG

Proverbs 31 in the UGV

Proverbs 31 in the UGV2

Proverbs 31 in the UGV3

Proverbs 31 in the VBL

Proverbs 31 in the VDCC

Proverbs 31 in the YALU

Proverbs 31 in the YAPE

Proverbs 31 in the YBVTP

Proverbs 31 in the ZBP