Zechariah 1 (BOGWICC)

1 Mwezi wachisanu ndi chitatu, mʼchaka chachiwiri cha ulamuliro wa Dariyo, Yehova anayankhula ndi mneneri Zekariya mwana wa Berekiya, mwana wa Ido, kuti: 2 “Yehova anakwiya kwambiri ndi makolo anu. 3 Choncho awuze anthuwa kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Bwererani kwa Ine,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse. ‘Ndipo Ine ndidzabwerera kwa inu,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse. 4 Musakhale ngati makolo anu, amene aneneri akale anawalalikira kuti: Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Tsopano lekani njira zanu zoyipa ndi machitidwe anu oyipawo.’ Koma iwo sanamvere kapena kulabadira za Ine, akutero Yehova. 5 Kodi makolo anuwo ali kuti tsopano? Nanga aneneri, kodi amakhalapo mpaka muyaya? 6 Kodi mawu anga ndi malangizo anga, amene ndinawawuza atumiki anga aneneri, suja anawachitira makolo anu?“Tsono iwo analapa ndi kunena kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse watichitira zomwe zikuyenera njira zathu ndi machitidwe athu, monga anatsimikiza kuti adzachita.’ ” 7 Tsiku la 24 la mwezi wa 11, mwezi wa Sebati, chaka chachiwiri cha ulamuliro wa Dariyo, Yehova anayankhula ndi Zekariya mwana wa Berekiya, mwana wa Ido. 8 Nthawi ya usiku ndinaona masomphenya. Ndinaona munthu atakwera pa kavalo wofiira. Iye anayima pakati pa mitengo ya mchisu mʼchigwa. Kumbuyo kwake kunali akavalo ofiira, akhofi ndi oyera. 9 Ine ndinafunsa kuti, “Mbuye wanga, kodi zimenezi ndi chiyani?”Mngelo amene amayankhula nane anayankha kuti, “Ndidzakuonetsa kuti zimenezi ndi chiyani.” 10 Pamenepo munthu amene anayima pakati pa mitengo ya mchisu anafotokoza kuti, “Amenewa ndiwo amene Yehova wawatuma kuti ayendere dziko lonse lapansi.” 11 Ndipo okwera pa akavalo enawo anafotokoza kwa mngelo wa Yehova, amene anayima pakati pa mitengo ya mchisu kuti, “Ife tayendera dziko lonse lapansi ndipo tapeza kuti dziko lonselo lili pa bata ndi mtendere.” 12 Tsono mngelo wa Yehova anati, “Yehova Wamphamvuzonse, kodi mpaka liti mudzakhala osaonetsa chifundo chanu kwa Yerusalemu ndi mizinda ya Yuda, amene mwawakwiyira kwa zaka izi 70?” 13 Choncho Yehova anayankhula mawu abwino ndi achitonthozo kwa mngelo amene ankayankhula nane. 14 Pamenepo mngelo amene ankayankhula nane anati, “Lengeza mawu awa: Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Ine ndikuchitira nsanje Yerusalemu ndi Ziyoni, 15 koma ndakwiya kwambiri ndi anthu a mitundu ina amene akuganiza kuti ali pa mtendere. Ndinakwiyira anthu anga pangʼono pokha, koma iwo anawonjeza kuzunza anthu angawo.’ 16 “Choncho, Yehova akuti, ‘Ndidzabwerera ku Yerusalemu ndi mtima wachifundo, nyumba yanga adzayimanganso kumeneko. Ndipo adzatenganso chingwe choyezera kuti amange Yerusalemu,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse. 17 “Lengezanso kuti, Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Mizinda yanga idzakhalanso ndi zokoma zosefukira ndipo Yehova adzatonthoza Ziyoni ndi kusankhanso Yerusalemu.’ ” 18 Kenaka ndinayangʼananso, ndipo patsogolo panga panali nyanga zinayi. 19 Ndinamufunsa mngelo amene amayankhula nane kuti, “Kodi zimenezi ndi chiyani?”Iye anandiyankha kuti, “Izi ndi nyanga zimene zinabalalitsa Yuda, Israeli ndi Yerusalemu.” 20 Kenaka Yehova anandionetsa amisiri azitsulo anayi. 21 Ndinafunsa kuti, “Amisiri a zitsulowa akudzachita chiyani?”Iye anayankha kuti, “Izi ndi nyanga zimene zinabalalitsa Yuda kotero kuti panalibe wina amene akanalimbana nazo, koma amisiri a zitsulowa abwera kudzaziopseza ndi kugwetsa nyanga zimenezi za mitundu ya anthu amene analimbana ndi dziko la Yuda ndi kubalalitsa anthu ake.”

In Other Versions

Zechariah 1 in the ANGEFD

Zechariah 1 in the ANTPNG2D

Zechariah 1 in the AS21

Zechariah 1 in the BAGH

Zechariah 1 in the BBPNG

Zechariah 1 in the BBT1E

Zechariah 1 in the BDS

Zechariah 1 in the BEV

Zechariah 1 in the BHAD

Zechariah 1 in the BIB

Zechariah 1 in the BLPT

Zechariah 1 in the BNT

Zechariah 1 in the BNTABOOT

Zechariah 1 in the BNTLV

Zechariah 1 in the BOATCB

Zechariah 1 in the BOATCB2

Zechariah 1 in the BOBCV

Zechariah 1 in the BOCNT

Zechariah 1 in the BOECS

Zechariah 1 in the BOHCB

Zechariah 1 in the BOHCV

Zechariah 1 in the BOHLNT

Zechariah 1 in the BOHNTLTAL

Zechariah 1 in the BOICB

Zechariah 1 in the BOILNTAP

Zechariah 1 in the BOITCV

Zechariah 1 in the BOKCV

Zechariah 1 in the BOKCV2

Zechariah 1 in the BOKHWOG

Zechariah 1 in the BOKSSV

Zechariah 1 in the BOLCB

Zechariah 1 in the BOLCB2

Zechariah 1 in the BOMCV

Zechariah 1 in the BONAV

Zechariah 1 in the BONCB

Zechariah 1 in the BONLT

Zechariah 1 in the BONUT2

Zechariah 1 in the BOPLNT

Zechariah 1 in the BOSCB

Zechariah 1 in the BOSNC

Zechariah 1 in the BOTLNT

Zechariah 1 in the BOVCB

Zechariah 1 in the BOYCB

Zechariah 1 in the BPBB

Zechariah 1 in the BPH

Zechariah 1 in the BSB

Zechariah 1 in the CCB

Zechariah 1 in the CUV

Zechariah 1 in the CUVS

Zechariah 1 in the DBT

Zechariah 1 in the DGDNT

Zechariah 1 in the DHNT

Zechariah 1 in the DNT

Zechariah 1 in the ELBE

Zechariah 1 in the EMTV

Zechariah 1 in the ESV

Zechariah 1 in the FBV

Zechariah 1 in the FEB

Zechariah 1 in the GGMNT

Zechariah 1 in the GNT

Zechariah 1 in the HARY

Zechariah 1 in the HNT

Zechariah 1 in the IRVA

Zechariah 1 in the IRVB

Zechariah 1 in the IRVG

Zechariah 1 in the IRVH

Zechariah 1 in the IRVK

Zechariah 1 in the IRVM

Zechariah 1 in the IRVM2

Zechariah 1 in the IRVO

Zechariah 1 in the IRVP

Zechariah 1 in the IRVT

Zechariah 1 in the IRVT2

Zechariah 1 in the IRVU

Zechariah 1 in the ISVN

Zechariah 1 in the JSNT

Zechariah 1 in the KAPI

Zechariah 1 in the KBT1ETNIK

Zechariah 1 in the KBV

Zechariah 1 in the KJV

Zechariah 1 in the KNFD

Zechariah 1 in the LBA

Zechariah 1 in the LBLA

Zechariah 1 in the LNT

Zechariah 1 in the LSV

Zechariah 1 in the MAAL

Zechariah 1 in the MBV

Zechariah 1 in the MBV2

Zechariah 1 in the MHNT

Zechariah 1 in the MKNFD

Zechariah 1 in the MNG

Zechariah 1 in the MNT

Zechariah 1 in the MNT2

Zechariah 1 in the MRS1T

Zechariah 1 in the NAA

Zechariah 1 in the NASB

Zechariah 1 in the NBLA

Zechariah 1 in the NBS

Zechariah 1 in the NBVTP

Zechariah 1 in the NET2

Zechariah 1 in the NIV11

Zechariah 1 in the NNT

Zechariah 1 in the NNT2

Zechariah 1 in the NNT3

Zechariah 1 in the PDDPT

Zechariah 1 in the PFNT

Zechariah 1 in the RMNT

Zechariah 1 in the SBIAS

Zechariah 1 in the SBIBS

Zechariah 1 in the SBIBS2

Zechariah 1 in the SBICS

Zechariah 1 in the SBIDS

Zechariah 1 in the SBIGS

Zechariah 1 in the SBIHS

Zechariah 1 in the SBIIS

Zechariah 1 in the SBIIS2

Zechariah 1 in the SBIIS3

Zechariah 1 in the SBIKS

Zechariah 1 in the SBIKS2

Zechariah 1 in the SBIMS

Zechariah 1 in the SBIOS

Zechariah 1 in the SBIPS

Zechariah 1 in the SBISS

Zechariah 1 in the SBITS

Zechariah 1 in the SBITS2

Zechariah 1 in the SBITS3

Zechariah 1 in the SBITS4

Zechariah 1 in the SBIUS

Zechariah 1 in the SBIVS

Zechariah 1 in the SBT

Zechariah 1 in the SBT1E

Zechariah 1 in the SCHL

Zechariah 1 in the SNT

Zechariah 1 in the SUSU

Zechariah 1 in the SUSU2

Zechariah 1 in the SYNO

Zechariah 1 in the TBIAOTANT

Zechariah 1 in the TBT1E

Zechariah 1 in the TBT1E2

Zechariah 1 in the TFTIP

Zechariah 1 in the TFTU

Zechariah 1 in the TGNTATF3T

Zechariah 1 in the THAI

Zechariah 1 in the TNFD

Zechariah 1 in the TNT

Zechariah 1 in the TNTIK

Zechariah 1 in the TNTIL

Zechariah 1 in the TNTIN

Zechariah 1 in the TNTIP

Zechariah 1 in the TNTIZ

Zechariah 1 in the TOMA

Zechariah 1 in the TTENT

Zechariah 1 in the UBG

Zechariah 1 in the UGV

Zechariah 1 in the UGV2

Zechariah 1 in the UGV3

Zechariah 1 in the VBL

Zechariah 1 in the VDCC

Zechariah 1 in the YALU

Zechariah 1 in the YAPE

Zechariah 1 in the YBVTP

Zechariah 1 in the ZBP