Deuteronomy 19 (BOGWICC)

1 Yehova Mulungu wanu akadzawononga anthu amene dziko lawo akukupatsani, ndipo inu mukawapirikitsa ndi kukhazikika mʼmizinda ndi mʼnyumba zawo, 2 mukapatule mizinda itatu imene ili pakati pa dziko lomwe Yehova Mulungu akukupatsani kukhala lanu. 3 Mudzakonze misewu ndi kuligawa patatu dzikolo limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ngati cholowa chanu, kuti aliyense wopha munthu akhoza kuthawirako. 4 Ili ndi lamulo lokhudza munthu amene wapha mnzake mosazindikira osati mwadala, nathawira kumeneko kupulumutsa moyo wake. Ndi munthu amene wapha mnzake mosazindikira, popanda maganizo oyipa. 5 Mwachitsanzo, munthu atapita ku nkhalango ndi mnzake kukadula mitengo, ndiye posamula nkhwangwa kuti adule mtengo, nkhwangwa ikhoza kuguluka nʼkukagwera mnzake uja nʼkumupha. Munthu ameneyo akhoza kuthawira ku umodzi mwa mizindayo napulumutsa moyo wake. 6 Kupanda kutero ndiye kuti wolipsira akhoza kumuthamangitsa mwaukali ndi kumugwira ngati mtunda utalika, ndipo akhoza kumupha ngakhale kuti sanayenera kufa popeza sanaphe mnzake mwadala. 7 Ichi ndi chifukwa chake ndikukulamulani kuti mudzipatulire nokha mizinda itatu. 8 Ngati Yehova Mulungu wanu akulitsa malire anu monga analonjezera pa malumbiro ndi makolo anu, nakupatsani dziko lonse monga analonjezera, 9 chifukwa chotsatira bwino malamulo onse amene ndikukuwuzani lero, kukonda Yehova Mulungu wanu ndi kuyenda mʼnjira zake nthawi zonse, ndiye kuti mukuyenera kupatula mizinda itatu yowonjezera. 10 Muchite zimenezi kuti musakhetse magazi wosalakwa mʼdziko lanu limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ngati cholowa, ndipo kuti musapezeke ndi mlandu wokhetsa magazi. 11 Koma ngati munthu adana ndi mnzake namubisalira panjira nʼkumuvulaza mpaka kumupha, nathawira ku umodzi mwa mizindayi, 12 akuluakulu a mu mzinda wake akamugwire ndi kumubwezera ku mzinda wake namupereka kwa wolipsira kuti aphedwe. 13 Osamumvera chisoni. Muyenera kuchotsa tchimo lokhetsa magazi wosalakwa mu Israeli kuti zinthu zizikuyenderani bwino. 14 Musamasunthe mwala wa malire anu ndi mnzanu amene anayikidwa ndi makolo anu pa cholowa chimene mulandire mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani. 15 Mboni imodzi siyokwanira kupeza munthu kuti ndi wolakwa pa mlandu uliwonse umene wapalamula. Nkhani itsimikizike ndi umboni wa anthu awiri kapena atatu. 16 Ngati mboni yonama ifuna kunamizira munthu mlandu, 17 anthu awiri okhudzidwa ndi mlanduwo ayenera kuyima pamaso pa Yehova pali ansembe ndi oweruza amene ali pa ntchito pa nthawiyo. 18 Oweruza afufuze bwinobwino, ndipo ngati zatsimikizika kuti mboniyo ndi yabodza, yopereka umboni wonama pa mʼbale wake, 19 ndiye kuti amuchitire iyeyo zimene anafuna kuchitira mʼbale wakezo. Muyenera kuchotsa choyipa pakati panu. 20 Anthu ena onse adzamva zimenezi nachita mantha, ndipo choyipa choterechi sichidzachitikanso pakati panu. 21 Osachita chisoni, moyo uzilipira moyo, diso kulipira diso, dzino kulipira dzino, dzanja kulipira dzanja ndi phazi kulipira phazi.

In Other Versions

Deuteronomy 19 in the ANGEFD

Deuteronomy 19 in the ANTPNG2D

Deuteronomy 19 in the AS21

Deuteronomy 19 in the BAGH

Deuteronomy 19 in the BBPNG

Deuteronomy 19 in the BBT1E

Deuteronomy 19 in the BDS

Deuteronomy 19 in the BEV

Deuteronomy 19 in the BHAD

Deuteronomy 19 in the BIB

Deuteronomy 19 in the BLPT

Deuteronomy 19 in the BNT

Deuteronomy 19 in the BNTABOOT

Deuteronomy 19 in the BNTLV

Deuteronomy 19 in the BOATCB

Deuteronomy 19 in the BOATCB2

Deuteronomy 19 in the BOBCV

Deuteronomy 19 in the BOCNT

Deuteronomy 19 in the BOECS

Deuteronomy 19 in the BOHCB

Deuteronomy 19 in the BOHCV

Deuteronomy 19 in the BOHLNT

Deuteronomy 19 in the BOHNTLTAL

Deuteronomy 19 in the BOICB

Deuteronomy 19 in the BOILNTAP

Deuteronomy 19 in the BOITCV

Deuteronomy 19 in the BOKCV

Deuteronomy 19 in the BOKCV2

Deuteronomy 19 in the BOKHWOG

Deuteronomy 19 in the BOKSSV

Deuteronomy 19 in the BOLCB

Deuteronomy 19 in the BOLCB2

Deuteronomy 19 in the BOMCV

Deuteronomy 19 in the BONAV

Deuteronomy 19 in the BONCB

Deuteronomy 19 in the BONLT

Deuteronomy 19 in the BONUT2

Deuteronomy 19 in the BOPLNT

Deuteronomy 19 in the BOSCB

Deuteronomy 19 in the BOSNC

Deuteronomy 19 in the BOTLNT

Deuteronomy 19 in the BOVCB

Deuteronomy 19 in the BOYCB

Deuteronomy 19 in the BPBB

Deuteronomy 19 in the BPH

Deuteronomy 19 in the BSB

Deuteronomy 19 in the CCB

Deuteronomy 19 in the CUV

Deuteronomy 19 in the CUVS

Deuteronomy 19 in the DBT

Deuteronomy 19 in the DGDNT

Deuteronomy 19 in the DHNT

Deuteronomy 19 in the DNT

Deuteronomy 19 in the ELBE

Deuteronomy 19 in the EMTV

Deuteronomy 19 in the ESV

Deuteronomy 19 in the FBV

Deuteronomy 19 in the FEB

Deuteronomy 19 in the GGMNT

Deuteronomy 19 in the GNT

Deuteronomy 19 in the HARY

Deuteronomy 19 in the HNT

Deuteronomy 19 in the IRVA

Deuteronomy 19 in the IRVB

Deuteronomy 19 in the IRVG

Deuteronomy 19 in the IRVH

Deuteronomy 19 in the IRVK

Deuteronomy 19 in the IRVM

Deuteronomy 19 in the IRVM2

Deuteronomy 19 in the IRVO

Deuteronomy 19 in the IRVP

Deuteronomy 19 in the IRVT

Deuteronomy 19 in the IRVT2

Deuteronomy 19 in the IRVU

Deuteronomy 19 in the ISVN

Deuteronomy 19 in the JSNT

Deuteronomy 19 in the KAPI

Deuteronomy 19 in the KBT1ETNIK

Deuteronomy 19 in the KBV

Deuteronomy 19 in the KJV

Deuteronomy 19 in the KNFD

Deuteronomy 19 in the LBA

Deuteronomy 19 in the LBLA

Deuteronomy 19 in the LNT

Deuteronomy 19 in the LSV

Deuteronomy 19 in the MAAL

Deuteronomy 19 in the MBV

Deuteronomy 19 in the MBV2

Deuteronomy 19 in the MHNT

Deuteronomy 19 in the MKNFD

Deuteronomy 19 in the MNG

Deuteronomy 19 in the MNT

Deuteronomy 19 in the MNT2

Deuteronomy 19 in the MRS1T

Deuteronomy 19 in the NAA

Deuteronomy 19 in the NASB

Deuteronomy 19 in the NBLA

Deuteronomy 19 in the NBS

Deuteronomy 19 in the NBVTP

Deuteronomy 19 in the NET2

Deuteronomy 19 in the NIV11

Deuteronomy 19 in the NNT

Deuteronomy 19 in the NNT2

Deuteronomy 19 in the NNT3

Deuteronomy 19 in the PDDPT

Deuteronomy 19 in the PFNT

Deuteronomy 19 in the RMNT

Deuteronomy 19 in the SBIAS

Deuteronomy 19 in the SBIBS

Deuteronomy 19 in the SBIBS2

Deuteronomy 19 in the SBICS

Deuteronomy 19 in the SBIDS

Deuteronomy 19 in the SBIGS

Deuteronomy 19 in the SBIHS

Deuteronomy 19 in the SBIIS

Deuteronomy 19 in the SBIIS2

Deuteronomy 19 in the SBIIS3

Deuteronomy 19 in the SBIKS

Deuteronomy 19 in the SBIKS2

Deuteronomy 19 in the SBIMS

Deuteronomy 19 in the SBIOS

Deuteronomy 19 in the SBIPS

Deuteronomy 19 in the SBISS

Deuteronomy 19 in the SBITS

Deuteronomy 19 in the SBITS2

Deuteronomy 19 in the SBITS3

Deuteronomy 19 in the SBITS4

Deuteronomy 19 in the SBIUS

Deuteronomy 19 in the SBIVS

Deuteronomy 19 in the SBT

Deuteronomy 19 in the SBT1E

Deuteronomy 19 in the SCHL

Deuteronomy 19 in the SNT

Deuteronomy 19 in the SUSU

Deuteronomy 19 in the SUSU2

Deuteronomy 19 in the SYNO

Deuteronomy 19 in the TBIAOTANT

Deuteronomy 19 in the TBT1E

Deuteronomy 19 in the TBT1E2

Deuteronomy 19 in the TFTIP

Deuteronomy 19 in the TFTU

Deuteronomy 19 in the TGNTATF3T

Deuteronomy 19 in the THAI

Deuteronomy 19 in the TNFD

Deuteronomy 19 in the TNT

Deuteronomy 19 in the TNTIK

Deuteronomy 19 in the TNTIL

Deuteronomy 19 in the TNTIN

Deuteronomy 19 in the TNTIP

Deuteronomy 19 in the TNTIZ

Deuteronomy 19 in the TOMA

Deuteronomy 19 in the TTENT

Deuteronomy 19 in the UBG

Deuteronomy 19 in the UGV

Deuteronomy 19 in the UGV2

Deuteronomy 19 in the UGV3

Deuteronomy 19 in the VBL

Deuteronomy 19 in the VDCC

Deuteronomy 19 in the YALU

Deuteronomy 19 in the YAPE

Deuteronomy 19 in the YBVTP

Deuteronomy 19 in the ZBP