Exodus 5 (BOGWICC)

1 Zitachitika izi, Mose ndi Aaroni anapita kwa Farao ndipo anati, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Aloleni anthu anga apite, kuti akachite chikondwerero cha Ine mʼchipululu.’ ” 2 Koma Farao anati, “Yehova ndani kuti ine ndimumvere ndi kulola Aisraeli kuti apite? Ine Yehova sindikumudziwa ndipo sindilola kuti Aisraeli apite.” 3 Ndipo iwo anati, “Mulungu wa Ahebri anakumana nafe. Chonde tiloleni tipite ulendo wa masiku atatu ku chipululu kuti tikapereke nsembe kwa Yehova Mulungu wathu, ngati sititero iye adzatipweteka ndi miliri kapena lupanga.” 4 Koma mfumu ya Igupto inati, “Mose ndi Aaroni, chifukwa chiyani mukuchititsa anthuwa kuti asagwire ntchito zawo? Bwererani ku ntchito zanu!” 5 Ndiponso Farao anati, “Taonani, anthuwa mʼdziko muno alipo ochuluka, ndipo inu mukuwaletsa kugwira ntchito.” 6 Pa tsiku lomwelo Farao analamulira akapitawo a thangata ndi anzawo a Chiisraeli amene ankayangʼanira anthu kuti 7 “Inu musawapatsenso udzu wopangira njerwa monga mumachitira kale, iwo azipita ndi kukatenga udzu wawo. 8 Koma musawachepetsere chiwerengero cha njerwa chomwe munawalamulira kale kuti aziwumba. Iwowa ndi aulesi. Nʼchifukwa chake akulira kuti, ‘Tiloleni tipite tikapereke nsembe kwa Mulungu wathu.’ 9 Muwakhawulitse ndi ntchito anthu amenewa kuti azitanganidwa, asakhale ndi mpata omvera zabodza.” 10 Choncho akapitawo a thangata ndi anzawo a Chiisraeli amene ankayangʼanira anthu anapita kwa anthu aja nati, “ ‘Farao akuti sadzakupatsaninso udzu. 11 Mʼmalo mwake mupite mukadzimwetere udzu kulikonse kumene mungawupeze. Komabe ntchito yanu sichepetsedwa.’ ” 12 Kotero anthuwo anamwazikana mʼdziko lonse la Igupto kukamweta udzu. 13 Akapitawo a thangata aja anawafulumiza anthu aja nati, “Malizani kugwira ntchito yanu ya tsiku ndi tsiku monga mmene zinalili pamene munkapatsidwa udzu.” 14 Akapitawo a thangata a Farao ankawamenya oyangʼanira anzawo a Chiisraeli aja nawapanikiza kuti, “Chifukwa chiyani lero simunawumbe chiwerengero chovomerezeka cha njerwa monga chakale chija?” 15 Pamenepo oyangʼanira anzawo a Chiisraeli aja anapita kukadandaula kwa Farao kuti, “Chifukwa chiyani mwachitira antchito anu zotere? 16 Antchito anu sakupatsidwa udzu, komabe akutiwuza kuti, ‘Umbani njerwa!’ Antchito anu akumenyedwa, koma cholakwa sichili ndi anthu anu.” 17 Farao anati, “Ulesi, inu ndinu alesi! Nʼchifukwa chake mukumanena kuti, ‘Mutilole tipite kukapereka nsembe kwa Yehova.’ 18 Pitani tsopano kuntchito. Simudzapatsidwanso udzu komabe muyenera kuwumba muyeso wanu wovomerezeka wa njerwa.” 19 Oyangʼanira anzawo a Chiisraeli anazindikira kuti ali pa mavuto pamene anawuzidwa kuti, “Musachepetse chiwerengero cha njerwa chimene muyenera kuwumba tsiku lililonse.” 20 Atachoka pamaso pa Farao, anakumana ndi Mose ndi Aaroni akuwadikira, 21 ndipo iwo anati, “Yehova akupenyeni ndi kukuweruzani popeza mwachititsa Farao ndi nduna zake kuti anyansidwe nafe ndipo mwayika lupanga mʼmanja mwawo kuti atiphe.” 22 Mose anabwerera kwa Yehova ndipo anati, “Chonde Ambuye, chifukwa chiyani mukuzunza anthu anu? Kodi munanditumira zimenezi? 23 Chipitireni changa kwa Farao kukamuyankhula mʼdzina lanu, iye wakhala akuzunza anthuwa, ndipo inu simunawapulumutse konse anthu anu.”

In Other Versions

Exodus 5 in the ANGEFD

Exodus 5 in the ANTPNG2D

Exodus 5 in the AS21

Exodus 5 in the BAGH

Exodus 5 in the BBPNG

Exodus 5 in the BBT1E

Exodus 5 in the BDS

Exodus 5 in the BEV

Exodus 5 in the BHAD

Exodus 5 in the BIB

Exodus 5 in the BLPT

Exodus 5 in the BNT

Exodus 5 in the BNTABOOT

Exodus 5 in the BNTLV

Exodus 5 in the BOATCB

Exodus 5 in the BOATCB2

Exodus 5 in the BOBCV

Exodus 5 in the BOCNT

Exodus 5 in the BOECS

Exodus 5 in the BOHCB

Exodus 5 in the BOHCV

Exodus 5 in the BOHLNT

Exodus 5 in the BOHNTLTAL

Exodus 5 in the BOICB

Exodus 5 in the BOILNTAP

Exodus 5 in the BOITCV

Exodus 5 in the BOKCV

Exodus 5 in the BOKCV2

Exodus 5 in the BOKHWOG

Exodus 5 in the BOKSSV

Exodus 5 in the BOLCB

Exodus 5 in the BOLCB2

Exodus 5 in the BOMCV

Exodus 5 in the BONAV

Exodus 5 in the BONCB

Exodus 5 in the BONLT

Exodus 5 in the BONUT2

Exodus 5 in the BOPLNT

Exodus 5 in the BOSCB

Exodus 5 in the BOSNC

Exodus 5 in the BOTLNT

Exodus 5 in the BOVCB

Exodus 5 in the BOYCB

Exodus 5 in the BPBB

Exodus 5 in the BPH

Exodus 5 in the BSB

Exodus 5 in the CCB

Exodus 5 in the CUV

Exodus 5 in the CUVS

Exodus 5 in the DBT

Exodus 5 in the DGDNT

Exodus 5 in the DHNT

Exodus 5 in the DNT

Exodus 5 in the ELBE

Exodus 5 in the EMTV

Exodus 5 in the ESV

Exodus 5 in the FBV

Exodus 5 in the FEB

Exodus 5 in the GGMNT

Exodus 5 in the GNT

Exodus 5 in the HARY

Exodus 5 in the HNT

Exodus 5 in the IRVA

Exodus 5 in the IRVB

Exodus 5 in the IRVG

Exodus 5 in the IRVH

Exodus 5 in the IRVK

Exodus 5 in the IRVM

Exodus 5 in the IRVM2

Exodus 5 in the IRVO

Exodus 5 in the IRVP

Exodus 5 in the IRVT

Exodus 5 in the IRVT2

Exodus 5 in the IRVU

Exodus 5 in the ISVN

Exodus 5 in the JSNT

Exodus 5 in the KAPI

Exodus 5 in the KBT1ETNIK

Exodus 5 in the KBV

Exodus 5 in the KJV

Exodus 5 in the KNFD

Exodus 5 in the LBA

Exodus 5 in the LBLA

Exodus 5 in the LNT

Exodus 5 in the LSV

Exodus 5 in the MAAL

Exodus 5 in the MBV

Exodus 5 in the MBV2

Exodus 5 in the MHNT

Exodus 5 in the MKNFD

Exodus 5 in the MNG

Exodus 5 in the MNT

Exodus 5 in the MNT2

Exodus 5 in the MRS1T

Exodus 5 in the NAA

Exodus 5 in the NASB

Exodus 5 in the NBLA

Exodus 5 in the NBS

Exodus 5 in the NBVTP

Exodus 5 in the NET2

Exodus 5 in the NIV11

Exodus 5 in the NNT

Exodus 5 in the NNT2

Exodus 5 in the NNT3

Exodus 5 in the PDDPT

Exodus 5 in the PFNT

Exodus 5 in the RMNT

Exodus 5 in the SBIAS

Exodus 5 in the SBIBS

Exodus 5 in the SBIBS2

Exodus 5 in the SBICS

Exodus 5 in the SBIDS

Exodus 5 in the SBIGS

Exodus 5 in the SBIHS

Exodus 5 in the SBIIS

Exodus 5 in the SBIIS2

Exodus 5 in the SBIIS3

Exodus 5 in the SBIKS

Exodus 5 in the SBIKS2

Exodus 5 in the SBIMS

Exodus 5 in the SBIOS

Exodus 5 in the SBIPS

Exodus 5 in the SBISS

Exodus 5 in the SBITS

Exodus 5 in the SBITS2

Exodus 5 in the SBITS3

Exodus 5 in the SBITS4

Exodus 5 in the SBIUS

Exodus 5 in the SBIVS

Exodus 5 in the SBT

Exodus 5 in the SBT1E

Exodus 5 in the SCHL

Exodus 5 in the SNT

Exodus 5 in the SUSU

Exodus 5 in the SUSU2

Exodus 5 in the SYNO

Exodus 5 in the TBIAOTANT

Exodus 5 in the TBT1E

Exodus 5 in the TBT1E2

Exodus 5 in the TFTIP

Exodus 5 in the TFTU

Exodus 5 in the TGNTATF3T

Exodus 5 in the THAI

Exodus 5 in the TNFD

Exodus 5 in the TNT

Exodus 5 in the TNTIK

Exodus 5 in the TNTIL

Exodus 5 in the TNTIN

Exodus 5 in the TNTIP

Exodus 5 in the TNTIZ

Exodus 5 in the TOMA

Exodus 5 in the TTENT

Exodus 5 in the UBG

Exodus 5 in the UGV

Exodus 5 in the UGV2

Exodus 5 in the UGV3

Exodus 5 in the VBL

Exodus 5 in the VDCC

Exodus 5 in the YALU

Exodus 5 in the YAPE

Exodus 5 in the YBVTP

Exodus 5 in the ZBP