Ezekiel 10 (BOGWICC)

1 Ine nditayangʼana ku thambo limene lili pamwamba pa mitu ya akerubi ndinangoona chinthu chooneka ngati mpando waufumu wa mwala wa safiro. 2 Tsono Yehova anawuza munthu wovala chovala chabafuta uja kuti, “Pita pakati pa mikombero kunsi kwa akerubi. Udzaze manja ako ndi makala oyaka amene ali pakati pa akerubiwo ndipo uwawaze mu mzinda.” Iye anachita zimenezi ine ndikuona. 3 Apa akerubiwo anali atayima mbali ya kummwera kwa Nyumba ya Mulungu pamene munthuyo ankalowa. Tsono mtambo unadzaza bwalo lamʼkati. 4 Ndipo ulemerero wa Yehova unachoka pamwamba pa akerubi ndipo unafika ku chiwundo cha Nyumba ya Mulungu. Mtambo unadzaza Nyumba ya Mulungu, ndipo kuwala kwa ulemerero wa Yehova kunadzaza bwalolo. 5 Phokoso la mapiko a akerubi limamveka mpaka ku bwalo lakunja, monga momwe linamvekera liwu la Mulungu Wamphamvuzonse akamayankhula. 6 Kenaka Yehova analamula munthu wovala chovala chabafuta uja kuti, “Pala moto pakati pa mikombero, pakati pa akerubi.” Munthu uja anapitadi nakayima pa mbali pa mkombero umodzi. 7 Ndipo mmodzi wa akerubi anatambalitsa dzanja lake mpaka pa moto umene unali pakati pawo. Iye anapalako motowo ndipo anapatsa munthu wovala chovala chabafuta uja. Tsono iye anawulandira natuluka. 8 Ndiye kuti kunsi kwa mapiko akerubi kumaoneka zinthu zooneka ngati manja a munthu. 9 Ine nditayangʼanitsitsa ndinaona mikombero inayi pambali pa akerubi. Pambali pa kerubi aliyense panali mkombero umodzi; mikomberoyo inkanyezimira ngati miyala yokongola ya krizoliti. 10 Maonekedwe a mikombero inayi ija anali ofanana. Mkombero uliwonse umaoneka ngati mkombero wolowana ndi unzake. 11 Poyenda akerubiwo, amapita mbali iliyonse ya mbali zinayizo kumene akerubiwo amayangʼana. Mikomberoyo simatembenuka pamene akerubiwo ankayenda. Kulikonse kumene mutu walunjika nʼkumene ankapita popanda kutembenuka. 12 Matupi awo onse, misana yawo, manja awo ndi mapiko awo zinali ndi maso okhaokha, monganso mʼmene inalili mikombero yawo inayi ija. 13 Ine ndinamva mikombero ikutchedwa kuti, “mikombero yakamvuluvulu.” 14 Kerubi aliyense anali ndi nkhope zinayi. Nkhope yoyamba inali ya Kerubi, nkhope yachiwiri inali ya munthu, nkhope yachitatu inali ya mkango ndipo nkhope yachinayi inali ya chiwombankhanga. 15 Tsono akerubi aja anawuluka. Izi zinali zamoyo zija zimene ndinaziona ku mtsinje wa Kebara. 16 Pamene akerubi ankayenda, nayonso mikombero ya mʼmbali mwawo inkayenda. Akerubiwo ankati akatambasula mapiko awo kuti auluke mikombero sinkachoka mʼmbali mwawo. 17 Akerubiwo ankati akayima, mikombero inkayimanso. Ngati akerubiwo auluka, mikomberoyo inkapita nawo chifukwa mzimu wa zamoyozo ndiwo unkayendetsa mikomberoyo. 18 Pamenepo ulemerero wa Yehova unachoka pa chiwundo cha Nyumba ya Mulungu ndi kukakhala pamwamba pa akerubi. 19 Ine ndikuona akerubi, anatambasula mapiko awo ndi kuwuluka. Pamene ankapita, mikombero inapita nawo pamodzi. Akerubi anakayima pa khomo la chipata cha kummawa cha Nyumba ya Yehova. Tsono ulemerero wowala wa Mulungu wa Israeli unali pamwamba pawo. 20 Izi ndizo zamoyo ndinaziona pansi pa Mulungu wa Israeli ku mtsinje wa Kebara, ndipo ndinazindikira kuti anali akerubi. 21 Kerubi aliyense anali ndi nkhope zinayi ndi mapiko anayi, ndipo kunsi kwa mapiko awo kunali chinthu chimene chimaoneka ngati manja a munthu. 22 Nkhope zawo zinali zofanana ndi zomwe ndinaziona ku mtsinje wa Kebara. Kerubi aliyense amayenda molunjika.

In Other Versions

Ezekiel 10 in the ANGEFD

Ezekiel 10 in the ANTPNG2D

Ezekiel 10 in the AS21

Ezekiel 10 in the BAGH

Ezekiel 10 in the BBPNG

Ezekiel 10 in the BBT1E

Ezekiel 10 in the BDS

Ezekiel 10 in the BEV

Ezekiel 10 in the BHAD

Ezekiel 10 in the BIB

Ezekiel 10 in the BLPT

Ezekiel 10 in the BNT

Ezekiel 10 in the BNTABOOT

Ezekiel 10 in the BNTLV

Ezekiel 10 in the BOATCB

Ezekiel 10 in the BOATCB2

Ezekiel 10 in the BOBCV

Ezekiel 10 in the BOCNT

Ezekiel 10 in the BOECS

Ezekiel 10 in the BOHCB

Ezekiel 10 in the BOHCV

Ezekiel 10 in the BOHLNT

Ezekiel 10 in the BOHNTLTAL

Ezekiel 10 in the BOICB

Ezekiel 10 in the BOILNTAP

Ezekiel 10 in the BOITCV

Ezekiel 10 in the BOKCV

Ezekiel 10 in the BOKCV2

Ezekiel 10 in the BOKHWOG

Ezekiel 10 in the BOKSSV

Ezekiel 10 in the BOLCB

Ezekiel 10 in the BOLCB2

Ezekiel 10 in the BOMCV

Ezekiel 10 in the BONAV

Ezekiel 10 in the BONCB

Ezekiel 10 in the BONLT

Ezekiel 10 in the BONUT2

Ezekiel 10 in the BOPLNT

Ezekiel 10 in the BOSCB

Ezekiel 10 in the BOSNC

Ezekiel 10 in the BOTLNT

Ezekiel 10 in the BOVCB

Ezekiel 10 in the BOYCB

Ezekiel 10 in the BPBB

Ezekiel 10 in the BPH

Ezekiel 10 in the BSB

Ezekiel 10 in the CCB

Ezekiel 10 in the CUV

Ezekiel 10 in the CUVS

Ezekiel 10 in the DBT

Ezekiel 10 in the DGDNT

Ezekiel 10 in the DHNT

Ezekiel 10 in the DNT

Ezekiel 10 in the ELBE

Ezekiel 10 in the EMTV

Ezekiel 10 in the ESV

Ezekiel 10 in the FBV

Ezekiel 10 in the FEB

Ezekiel 10 in the GGMNT

Ezekiel 10 in the GNT

Ezekiel 10 in the HARY

Ezekiel 10 in the HNT

Ezekiel 10 in the IRVA

Ezekiel 10 in the IRVB

Ezekiel 10 in the IRVG

Ezekiel 10 in the IRVH

Ezekiel 10 in the IRVK

Ezekiel 10 in the IRVM

Ezekiel 10 in the IRVM2

Ezekiel 10 in the IRVO

Ezekiel 10 in the IRVP

Ezekiel 10 in the IRVT

Ezekiel 10 in the IRVT2

Ezekiel 10 in the IRVU

Ezekiel 10 in the ISVN

Ezekiel 10 in the JSNT

Ezekiel 10 in the KAPI

Ezekiel 10 in the KBT1ETNIK

Ezekiel 10 in the KBV

Ezekiel 10 in the KJV

Ezekiel 10 in the KNFD

Ezekiel 10 in the LBA

Ezekiel 10 in the LBLA

Ezekiel 10 in the LNT

Ezekiel 10 in the LSV

Ezekiel 10 in the MAAL

Ezekiel 10 in the MBV

Ezekiel 10 in the MBV2

Ezekiel 10 in the MHNT

Ezekiel 10 in the MKNFD

Ezekiel 10 in the MNG

Ezekiel 10 in the MNT

Ezekiel 10 in the MNT2

Ezekiel 10 in the MRS1T

Ezekiel 10 in the NAA

Ezekiel 10 in the NASB

Ezekiel 10 in the NBLA

Ezekiel 10 in the NBS

Ezekiel 10 in the NBVTP

Ezekiel 10 in the NET2

Ezekiel 10 in the NIV11

Ezekiel 10 in the NNT

Ezekiel 10 in the NNT2

Ezekiel 10 in the NNT3

Ezekiel 10 in the PDDPT

Ezekiel 10 in the PFNT

Ezekiel 10 in the RMNT

Ezekiel 10 in the SBIAS

Ezekiel 10 in the SBIBS

Ezekiel 10 in the SBIBS2

Ezekiel 10 in the SBICS

Ezekiel 10 in the SBIDS

Ezekiel 10 in the SBIGS

Ezekiel 10 in the SBIHS

Ezekiel 10 in the SBIIS

Ezekiel 10 in the SBIIS2

Ezekiel 10 in the SBIIS3

Ezekiel 10 in the SBIKS

Ezekiel 10 in the SBIKS2

Ezekiel 10 in the SBIMS

Ezekiel 10 in the SBIOS

Ezekiel 10 in the SBIPS

Ezekiel 10 in the SBISS

Ezekiel 10 in the SBITS

Ezekiel 10 in the SBITS2

Ezekiel 10 in the SBITS3

Ezekiel 10 in the SBITS4

Ezekiel 10 in the SBIUS

Ezekiel 10 in the SBIVS

Ezekiel 10 in the SBT

Ezekiel 10 in the SBT1E

Ezekiel 10 in the SCHL

Ezekiel 10 in the SNT

Ezekiel 10 in the SUSU

Ezekiel 10 in the SUSU2

Ezekiel 10 in the SYNO

Ezekiel 10 in the TBIAOTANT

Ezekiel 10 in the TBT1E

Ezekiel 10 in the TBT1E2

Ezekiel 10 in the TFTIP

Ezekiel 10 in the TFTU

Ezekiel 10 in the TGNTATF3T

Ezekiel 10 in the THAI

Ezekiel 10 in the TNFD

Ezekiel 10 in the TNT

Ezekiel 10 in the TNTIK

Ezekiel 10 in the TNTIL

Ezekiel 10 in the TNTIN

Ezekiel 10 in the TNTIP

Ezekiel 10 in the TNTIZ

Ezekiel 10 in the TOMA

Ezekiel 10 in the TTENT

Ezekiel 10 in the UBG

Ezekiel 10 in the UGV

Ezekiel 10 in the UGV2

Ezekiel 10 in the UGV3

Ezekiel 10 in the VBL

Ezekiel 10 in the VDCC

Ezekiel 10 in the YALU

Ezekiel 10 in the YAPE

Ezekiel 10 in the YBVTP

Ezekiel 10 in the ZBP