Galatians 1 (BOGWICC)
1 Paulo mtumwi, osati wosankhidwa ndi anthu kapena kutumidwa ndi munthu ayi, koma Yesu Khristu, ndi Mulungu Atate amene anamuukitsa Yesuyo kwa akufa, 2 pamodzi ndi abale onse amene ali nane,Kulembera mipingo ya ku Galatiya: 3 Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu zikhale nanu. 4 Yesuyo anadzipereka yekha chifukwa cha machimo athu kuti atipulumutse ku njira za moyo woyipa uno, molingana ndi chifuniro cha Mulungu ndi Atate athu. 5 Ulemerero ukhale kwa Mulunguyo mpaka muyaya. Ameni. 6 Ine ndikudabwa kuti mukusiya mwamsangamsanga chotere Mulungu amene anakuyitanani mwachisomo cha Khristu ndipo mwatembenuka ndi kutsatira uthenga wina wosiyana, 7 umene si Uthenga Wabwino konse. Pali anthu ena amene akukusokonezani komanso akufuna kupotoza Uthenga Wabwino wa Khristu. 8 Ngakhale ife kapena mngelo wochokera kumwamba, akalalikira Uthenga Wabwino wosiyana ndi umene tinakulalikirani uja, iyeyo akhale wotembereredwa! 9 Monga tanena kale, tsopano ndikubwereza kunenanso kuti, “Ngati wina aliyense akulalikirani Uthenga Wabwino wosiyana ndi umene munawulandira, iyeyo akhale wotembereredwa.” 10 Kodi tsopano ndikufuna kukopa anthu kuti andivomereze, kapena Mulungu? Kapena ndikufuna kukondweretsa anthu? Ngati ine ndikanakhala kuti ndikufunabe kukondweretsa anthu, sindikanakhala mtumiki wa Khristu. 11 Abale, ine ndikufuna kuti mudziwe, kuti Uthenga Wabwino umene ndinalalikira si ochokera kwa munthu ayi. 12 Ine sindinawulandire kuchokera kwa munthu aliyense, kapena kuphunzitsidwa; koma ndinawulandira mwa vumbulutso lochokera kwa Khristu. 13 Pakuti inu munamva za moyo wanga wakale mʼChiyuda, mmene ndinkazunzira mpingo wa Mulungu koopsa ndi kuyesetsa kuwuwononga. 14 Ine ndinkapambana Ayuda ambiri a msinkhu wanga pochita za Chiyuda, ndipo ndinali wachangu koposa pa miyambo ya makolo athu. 15 Koma Mulungu, amene anandipatula ine ndisanabadwe, ndi kundiyitana mwachisomo chake, atakondweretsedwa 16 kuvumbulutsa Mwana wake mwa ine, kuti ndikalalikire Khristuyo pakati pa anthu a mitundu ina, ine sindinapemphe nzeru kwa munthu aliyense. 17 Ine sindinapite ku Yerusalemu kukaonana ndi amene anali atumwi ine ndisanakhale mtumwi. Mʼmalo mwake nthawi yomweyo ndinapita ku Arabiya ndi kubwereranso ku Damasiko. 18 Pambuyo pake, patatha zaka zitatu, ndinapita ku Yerusalemu kukaonana ndi Petro ndikukhala naye masiku khumi ndi asanu. 19 Ine sindinaonane ndi atumwi enawo koma Yakobo yekha, mʼbale wa Ambuye. 20 Ine ndikutsimikizira inu pamaso pa Mulungu kuti zimene ndikukulemberani si zonama ayi. 21 Pambuyo pake ndinapita ku Siriya ndi ku Kilikiya. 22 Koma sindimadziwika ndi nkhope ku mipingo ya ku Yudeya imene ili mwa Khristu. 23 Iwo anangomva mbiri yokha yakuti, “Munthu amene poyamba anatizunza ife, tsopano akulalikira chikhulupiriro chimene iyeyo nthawi ina anafuna kuchiwononga.” 24 Ndipo iwo anayamika Mulungu chifukwa cha ine.
In Other Versions
Galatians 1 in the ANGEFD
Galatians 1 in the ANTPNG2D
Galatians 1 in the AS21
Galatians 1 in the BAGH
Galatians 1 in the BBPNG
Galatians 1 in the BBT1E
Galatians 1 in the BDS
Galatians 1 in the BEV
Galatians 1 in the BHAD
Galatians 1 in the BIB
Galatians 1 in the BLPT
Galatians 1 in the BNT
Galatians 1 in the BNTABOOT
Galatians 1 in the BNTLV
Galatians 1 in the BOATCB
Galatians 1 in the BOATCB2
Galatians 1 in the BOBCV
Galatians 1 in the BOCNT
Galatians 1 in the BOECS
Galatians 1 in the BOHCB
Galatians 1 in the BOHCV
Galatians 1 in the BOHLNT
Galatians 1 in the BOHNTLTAL
Galatians 1 in the BOICB
Galatians 1 in the BOILNTAP
Galatians 1 in the BOITCV
Galatians 1 in the BOKCV
Galatians 1 in the BOKCV2
Galatians 1 in the BOKHWOG
Galatians 1 in the BOKSSV
Galatians 1 in the BOLCB
Galatians 1 in the BOLCB2
Galatians 1 in the BOMCV
Galatians 1 in the BONAV
Galatians 1 in the BONCB
Galatians 1 in the BONLT
Galatians 1 in the BONUT2
Galatians 1 in the BOPLNT
Galatians 1 in the BOSCB
Galatians 1 in the BOSNC
Galatians 1 in the BOTLNT
Galatians 1 in the BOVCB
Galatians 1 in the BOYCB
Galatians 1 in the BPBB
Galatians 1 in the BPH
Galatians 1 in the BSB
Galatians 1 in the CCB
Galatians 1 in the CUV
Galatians 1 in the CUVS
Galatians 1 in the DBT
Galatians 1 in the DGDNT
Galatians 1 in the DHNT
Galatians 1 in the DNT
Galatians 1 in the ELBE
Galatians 1 in the EMTV
Galatians 1 in the ESV
Galatians 1 in the FBV
Galatians 1 in the FEB
Galatians 1 in the GGMNT
Galatians 1 in the GNT
Galatians 1 in the HARY
Galatians 1 in the HNT
Galatians 1 in the IRVA
Galatians 1 in the IRVB
Galatians 1 in the IRVG
Galatians 1 in the IRVH
Galatians 1 in the IRVK
Galatians 1 in the IRVM
Galatians 1 in the IRVM2
Galatians 1 in the IRVO
Galatians 1 in the IRVP
Galatians 1 in the IRVT
Galatians 1 in the IRVT2
Galatians 1 in the IRVU
Galatians 1 in the ISVN
Galatians 1 in the JSNT
Galatians 1 in the KAPI
Galatians 1 in the KBT1ETNIK
Galatians 1 in the KBV
Galatians 1 in the KJV
Galatians 1 in the KNFD
Galatians 1 in the LBA
Galatians 1 in the LBLA
Galatians 1 in the LNT
Galatians 1 in the LSV
Galatians 1 in the MAAL
Galatians 1 in the MBV
Galatians 1 in the MBV2
Galatians 1 in the MHNT
Galatians 1 in the MKNFD
Galatians 1 in the MNG
Galatians 1 in the MNT
Galatians 1 in the MNT2
Galatians 1 in the MRS1T
Galatians 1 in the NAA
Galatians 1 in the NASB
Galatians 1 in the NBLA
Galatians 1 in the NBS
Galatians 1 in the NBVTP
Galatians 1 in the NET2
Galatians 1 in the NIV11
Galatians 1 in the NNT
Galatians 1 in the NNT2
Galatians 1 in the NNT3
Galatians 1 in the PDDPT
Galatians 1 in the PFNT
Galatians 1 in the RMNT
Galatians 1 in the SBIAS
Galatians 1 in the SBIBS
Galatians 1 in the SBIBS2
Galatians 1 in the SBICS
Galatians 1 in the SBIDS
Galatians 1 in the SBIGS
Galatians 1 in the SBIHS
Galatians 1 in the SBIIS
Galatians 1 in the SBIIS2
Galatians 1 in the SBIIS3
Galatians 1 in the SBIKS
Galatians 1 in the SBIKS2
Galatians 1 in the SBIMS
Galatians 1 in the SBIOS
Galatians 1 in the SBIPS
Galatians 1 in the SBISS
Galatians 1 in the SBITS
Galatians 1 in the SBITS2
Galatians 1 in the SBITS3
Galatians 1 in the SBITS4
Galatians 1 in the SBIUS
Galatians 1 in the SBIVS
Galatians 1 in the SBT
Galatians 1 in the SBT1E
Galatians 1 in the SCHL
Galatians 1 in the SNT
Galatians 1 in the SUSU
Galatians 1 in the SUSU2
Galatians 1 in the SYNO
Galatians 1 in the TBIAOTANT
Galatians 1 in the TBT1E
Galatians 1 in the TBT1E2
Galatians 1 in the TFTIP
Galatians 1 in the TFTU
Galatians 1 in the TGNTATF3T
Galatians 1 in the THAI
Galatians 1 in the TNFD
Galatians 1 in the TNT
Galatians 1 in the TNTIK
Galatians 1 in the TNTIL
Galatians 1 in the TNTIN
Galatians 1 in the TNTIP
Galatians 1 in the TNTIZ
Galatians 1 in the TOMA
Galatians 1 in the TTENT
Galatians 1 in the UBG
Galatians 1 in the UGV
Galatians 1 in the UGV2
Galatians 1 in the UGV3
Galatians 1 in the VBL
Galatians 1 in the VDCC
Galatians 1 in the YALU
Galatians 1 in the YAPE
Galatians 1 in the YBVTP
Galatians 1 in the ZBP