Genesis 28 (BOGWICC)

1 Choncho Isake anayitanitsa Yakobo namudalitsa nʼkumuwuzitsa kuti, “Usakwatire mkazi wa kuno ku Kanaani. 2 Panopo upite ku Padanaramu, ku nyumba kwa Betueli abambo a amayi akowa, kumeneko ukakwatire mmodzi mwa ana aakazi a Labani, mlongo wa amayi akowa. 3 Mulungu Wamphamvuzonse akudalitse iwe nakupatse ana ambiri mpaka udzasanduke gulu lalikulu la mitundu ya anthu. 4 Mulunguyo akudalitse iwe monga mmene anamudalitsira Abrahamu kuti zidzukulu zako zidzalandira dziko limene ukukhalamo ngati mlendo kuti lidzakhale lawo. Ili ndi dziko limene Mulungu anapereka kwa Abrahamu.” 5 Ndipo Isake anamulola Yakobo kuti anyamuke kupita ku Padanaramu kwa Labani mwana wa Betueli Mwaramu. Labani anali mlongo wa Rebeka, mayi wa Yakobo ndi Esau. 6 Tsopano Esau anadziwa kuti Isake anadalitsa Yakobo ndi kumutumiza ku Padanaramu kuti akakwatire kumeneko. Anawuzidwanso kuti, “Usakwatire mkazi wa ku Kanaani.” 7 Yakobo anamvera abambo ake ndi amayi ake ndi kupita ku Padanaramu. 8 Ndiye pamenepo Esau anazindikira kuti abambo ake Isake sankakondwera ndi akazi a ku Kanaani; 9 anapita kwa Ismaeli mwana wa Abrahamu nakwatira Mahalati mwana wa Ismaeli, mlongo wake wa Nebayoti. Anatero kuwonjezera akazi amene anali nawo kale. 10 Yakobo ananyamuka pa ulendo kuchoka ku Beeriseba kupita ku Harani. 11 Atafika pa malo pena, anayima kuti agonepo chifukwa dzuwa linali litalowa. Anatenga mwala wina pomwepo natsamiritsapo mutu wake, ndipo anagona. 12 Mʼmaloto, anaona makwerero oyimikidwa pansi ndipo anakafika kumwamba. Angelo a Mulungu amakwera ndi kutsika pa makwereropo. 13 Tsono Yehova anayimirira pambali pake, nati, “Ine ndine Yehova, Mulungu wa Abrahamu kholo lake la Isake abambo ako. Ndidzakupatsa iwe ndi zidzukulu zako dziko limene ukugonamolo. 14 Zidzukulu zako zidzachuluka ngati fumbi la pa dziko lapansi ndipo zidzabalalikira kumadzulo ndi kummawa, kumpoto ndi kummwera. Anthu onse adzalandira madalitso kudzera mwa iwe ndi zidzukulu zako. 15 Ine ndili nawe pamodzi ndipo ndidzakuyangʼanira kulikonse upiteko, ndipo ndidzakubwezera ku dziko lino. Sindidzakusiya mpaka nditachita zimene ndakulonjezazi.” 16 Yakobo atadzidzimuka, anati, “Zoonadi Yehova ali pa malo ano, ndipo ine sindinadziwe.” 17 Tsono anachita mantha ndipo anati, “Malo ano ndi woopsa ndithu. Zoonadi pano ndi pa nyumba ya Mulungu ndi khomo la kumwamba.” 18 Mmamawa mwake Yakobo anatenga mwala umene anatsamira mutu wake uja nawuyimika ngati chipilala ndi kuthira mafuta pamwamba pake 19 Iye anawatcha malowo Beteli, ngakhale kuti poyamba mzindawo ankawutcha Luzi. 20 Pamenepo Yakobo analumbira kwa Yehova nati, “Ngati inu Mulungu mukhala ndi ine, kundiyangʼanira pa ulendo wangawu ndi kundipatsa chakudya ndi chovala; 21 ngati inu mudzandibweretsa kwathu mu mtendere, ndiye kuti mudzakhala Mulungu wanga, 22 ndipo mwala uwu ndawuyimikawu udzakhala Nyumba ya Mulungu. Ine ndidzakupatsani chakhumi cha zinthu zonse zimene mudzandipatse.”

In Other Versions

Genesis 28 in the ANGEFD

Genesis 28 in the ANTPNG2D

Genesis 28 in the AS21

Genesis 28 in the BAGH

Genesis 28 in the BBPNG

Genesis 28 in the BBT1E

Genesis 28 in the BDS

Genesis 28 in the BEV

Genesis 28 in the BHAD

Genesis 28 in the BIB

Genesis 28 in the BLPT

Genesis 28 in the BNT

Genesis 28 in the BNTABOOT

Genesis 28 in the BNTLV

Genesis 28 in the BOATCB

Genesis 28 in the BOATCB2

Genesis 28 in the BOBCV

Genesis 28 in the BOCNT

Genesis 28 in the BOECS

Genesis 28 in the BOHCB

Genesis 28 in the BOHCV

Genesis 28 in the BOHLNT

Genesis 28 in the BOHNTLTAL

Genesis 28 in the BOICB

Genesis 28 in the BOILNTAP

Genesis 28 in the BOITCV

Genesis 28 in the BOKCV

Genesis 28 in the BOKCV2

Genesis 28 in the BOKHWOG

Genesis 28 in the BOKSSV

Genesis 28 in the BOLCB

Genesis 28 in the BOLCB2

Genesis 28 in the BOMCV

Genesis 28 in the BONAV

Genesis 28 in the BONCB

Genesis 28 in the BONLT

Genesis 28 in the BONUT2

Genesis 28 in the BOPLNT

Genesis 28 in the BOSCB

Genesis 28 in the BOSNC

Genesis 28 in the BOTLNT

Genesis 28 in the BOVCB

Genesis 28 in the BOYCB

Genesis 28 in the BPBB

Genesis 28 in the BPH

Genesis 28 in the BSB

Genesis 28 in the CCB

Genesis 28 in the CUV

Genesis 28 in the CUVS

Genesis 28 in the DBT

Genesis 28 in the DGDNT

Genesis 28 in the DHNT

Genesis 28 in the DNT

Genesis 28 in the ELBE

Genesis 28 in the EMTV

Genesis 28 in the ESV

Genesis 28 in the FBV

Genesis 28 in the FEB

Genesis 28 in the GGMNT

Genesis 28 in the GNT

Genesis 28 in the HARY

Genesis 28 in the HNT

Genesis 28 in the IRVA

Genesis 28 in the IRVB

Genesis 28 in the IRVG

Genesis 28 in the IRVH

Genesis 28 in the IRVK

Genesis 28 in the IRVM

Genesis 28 in the IRVM2

Genesis 28 in the IRVO

Genesis 28 in the IRVP

Genesis 28 in the IRVT

Genesis 28 in the IRVT2

Genesis 28 in the IRVU

Genesis 28 in the ISVN

Genesis 28 in the JSNT

Genesis 28 in the KAPI

Genesis 28 in the KBT1ETNIK

Genesis 28 in the KBV

Genesis 28 in the KJV

Genesis 28 in the KNFD

Genesis 28 in the LBA

Genesis 28 in the LBLA

Genesis 28 in the LNT

Genesis 28 in the LSV

Genesis 28 in the MAAL

Genesis 28 in the MBV

Genesis 28 in the MBV2

Genesis 28 in the MHNT

Genesis 28 in the MKNFD

Genesis 28 in the MNG

Genesis 28 in the MNT

Genesis 28 in the MNT2

Genesis 28 in the MRS1T

Genesis 28 in the NAA

Genesis 28 in the NASB

Genesis 28 in the NBLA

Genesis 28 in the NBS

Genesis 28 in the NBVTP

Genesis 28 in the NET2

Genesis 28 in the NIV11

Genesis 28 in the NNT

Genesis 28 in the NNT2

Genesis 28 in the NNT3

Genesis 28 in the PDDPT

Genesis 28 in the PFNT

Genesis 28 in the RMNT

Genesis 28 in the SBIAS

Genesis 28 in the SBIBS

Genesis 28 in the SBIBS2

Genesis 28 in the SBICS

Genesis 28 in the SBIDS

Genesis 28 in the SBIGS

Genesis 28 in the SBIHS

Genesis 28 in the SBIIS

Genesis 28 in the SBIIS2

Genesis 28 in the SBIIS3

Genesis 28 in the SBIKS

Genesis 28 in the SBIKS2

Genesis 28 in the SBIMS

Genesis 28 in the SBIOS

Genesis 28 in the SBIPS

Genesis 28 in the SBISS

Genesis 28 in the SBITS

Genesis 28 in the SBITS2

Genesis 28 in the SBITS3

Genesis 28 in the SBITS4

Genesis 28 in the SBIUS

Genesis 28 in the SBIVS

Genesis 28 in the SBT

Genesis 28 in the SBT1E

Genesis 28 in the SCHL

Genesis 28 in the SNT

Genesis 28 in the SUSU

Genesis 28 in the SUSU2

Genesis 28 in the SYNO

Genesis 28 in the TBIAOTANT

Genesis 28 in the TBT1E

Genesis 28 in the TBT1E2

Genesis 28 in the TFTIP

Genesis 28 in the TFTU

Genesis 28 in the TGNTATF3T

Genesis 28 in the THAI

Genesis 28 in the TNFD

Genesis 28 in the TNT

Genesis 28 in the TNTIK

Genesis 28 in the TNTIL

Genesis 28 in the TNTIN

Genesis 28 in the TNTIP

Genesis 28 in the TNTIZ

Genesis 28 in the TOMA

Genesis 28 in the TTENT

Genesis 28 in the UBG

Genesis 28 in the UGV

Genesis 28 in the UGV2

Genesis 28 in the UGV3

Genesis 28 in the VBL

Genesis 28 in the VDCC

Genesis 28 in the YALU

Genesis 28 in the YAPE

Genesis 28 in the YBVTP

Genesis 28 in the ZBP