Genesis 8 (BOGWICC)

1 Tsono Mulungu anakumbukira Nowa ndi nyama zonse zakuthengo ndi ziweto zimene anali nazo mu chombo. Yehova anatumiza mphepo pa dziko lapansi ndipo madzi anaphwera. 2 Tsono akasupe a madzi ambiri a pansi pa dziko ndi zitseko za madzi a kumwamba zinatsekedwa, ndipo mvula inaleka kugwa. 3 Madzi amaphwabe pa dziko lapansi. Pakutha pa masiku 150, madzi anatsika, 4 ndipo pa tsiku la 17 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, chombo chija chinakakhazikika pa mapiri a Ararati. 5 Madzi anapitirira kuphwa mpaka mwezi wa khumi, ndipo pa tsiku loyamba la mwezi wa khumiwo msonga za mapiri zinayamba kuonekera. 6 Patapita masiku makumi anayi, Nowa anatsekula zenera limene anapanga mʼchombomo 7 natulutsa khwangwala, koma khwangwalayo ankangowuluka uku ndi uku mpaka madzi anawuma pa dziko lapansi. 8 Kenaka anatulutsa nkhunda kuti aone ngati madzi aphwa pa dziko. 9 Koma nkhunda sinapeze poti nʼkutera chifukwa panali madzi ponseponse pa dziko lapansi. Choncho inabwerera kwa Nowa mʼchombo. Nowa anatulutsa dzanja lake kunja ndi kutenga nkhundayo kuyibwezera mʼchombo mmene iye anali. 10 Choncho anadikirabe masiku ena asanu ndi awiri ndipo anatulutsanso nkhundayo mʼchombo muja. 11 Pamene nkhunda inabwerera madzulo ake, inali itanyamula tsamba laliwisi la mtengo wa olivi. Motero Nowa anadziwa kuti madzi aphwadi pa dziko lapansi. 12 Iye anadikira masiku ena asanu ndi awiri ndipo anatumizanso nkhunda ija, koma nthawi imeneyi sinabwererenso kwa iye. 13 Pofika tsiku loyamba la mwezi woyamba wa chaka chimene Nowa anakwanitsa zaka 601, madzi anawuma pa dziko lapansi. Ndipo Nowa anachotsa denga la chombo ndipo anaona kuti kunja kwawuma. 14 Pokwana tsiku la 27 la mwezi wachiwiri dziko lapansi linawumiratu. 15 Tsono Mulungu anawuza Nowa kuti, 16 “Iwe, mkazi wako, ana ako pamodzi ndi akazi awo tulukani mʼchombomo. 17 Tulutsa zamoyo zonse zili ndi iwe, mbalame, nyama ndi zokwawa zonse kuti ziswane ndi kuchulukana pa dziko lapansi.” 18 Nowa anatuluka pamodzi ndi ana ake aamuna, mkazi wake ndi akazi a ana ake. 19 Nyama zonse, zokwawa zonse, mbalame zonse, chilichonse choyenda pa dziko lapansi, zinatuluka mʼchombo motsogozana monga mwa mitundu yawo. 20 Pamenepo Nowa anamanga guwa lansembe la Yehova ndipo anatengako mtundu uliwonse wa nyama zoti nʼkudya ndi mbalame zoti nʼkudya naperekapo nsembe yopsereza. 21 Yehova atamva fungo labwino anati mu mtima mwake: “Sindidzatembereranso nthaka chifukwa cha munthu, ngakhale kuti maganizo a mu mtima mwake ndi oyipa kuyambira ubwana wake. Ndipo sindidzawononganso zolengedwa zonse zamoyo monga ndachitiramu. 22 “Nthawi zonse mmene dziko lapansi lidzakhalire,nthawi yodzala ndi nthawi yokololayozizira ndi yotentha,dzinja ndi chilimwe,usana ndi usiku,sizidzatha.”

In Other Versions

Genesis 8 in the ANGEFD

Genesis 8 in the ANTPNG2D

Genesis 8 in the AS21

Genesis 8 in the BAGH

Genesis 8 in the BBPNG

Genesis 8 in the BBT1E

Genesis 8 in the BDS

Genesis 8 in the BEV

Genesis 8 in the BHAD

Genesis 8 in the BIB

Genesis 8 in the BLPT

Genesis 8 in the BNT

Genesis 8 in the BNTABOOT

Genesis 8 in the BNTLV

Genesis 8 in the BOATCB

Genesis 8 in the BOATCB2

Genesis 8 in the BOBCV

Genesis 8 in the BOCNT

Genesis 8 in the BOECS

Genesis 8 in the BOHCB

Genesis 8 in the BOHCV

Genesis 8 in the BOHLNT

Genesis 8 in the BOHNTLTAL

Genesis 8 in the BOICB

Genesis 8 in the BOILNTAP

Genesis 8 in the BOITCV

Genesis 8 in the BOKCV

Genesis 8 in the BOKCV2

Genesis 8 in the BOKHWOG

Genesis 8 in the BOKSSV

Genesis 8 in the BOLCB

Genesis 8 in the BOLCB2

Genesis 8 in the BOMCV

Genesis 8 in the BONAV

Genesis 8 in the BONCB

Genesis 8 in the BONLT

Genesis 8 in the BONUT2

Genesis 8 in the BOPLNT

Genesis 8 in the BOSCB

Genesis 8 in the BOSNC

Genesis 8 in the BOTLNT

Genesis 8 in the BOVCB

Genesis 8 in the BOYCB

Genesis 8 in the BPBB

Genesis 8 in the BPH

Genesis 8 in the BSB

Genesis 8 in the CCB

Genesis 8 in the CUV

Genesis 8 in the CUVS

Genesis 8 in the DBT

Genesis 8 in the DGDNT

Genesis 8 in the DHNT

Genesis 8 in the DNT

Genesis 8 in the ELBE

Genesis 8 in the EMTV

Genesis 8 in the ESV

Genesis 8 in the FBV

Genesis 8 in the FEB

Genesis 8 in the GGMNT

Genesis 8 in the GNT

Genesis 8 in the HARY

Genesis 8 in the HNT

Genesis 8 in the IRVA

Genesis 8 in the IRVB

Genesis 8 in the IRVG

Genesis 8 in the IRVH

Genesis 8 in the IRVK

Genesis 8 in the IRVM

Genesis 8 in the IRVM2

Genesis 8 in the IRVO

Genesis 8 in the IRVP

Genesis 8 in the IRVT

Genesis 8 in the IRVT2

Genesis 8 in the IRVU

Genesis 8 in the ISVN

Genesis 8 in the JSNT

Genesis 8 in the KAPI

Genesis 8 in the KBT1ETNIK

Genesis 8 in the KBV

Genesis 8 in the KJV

Genesis 8 in the KNFD

Genesis 8 in the LBA

Genesis 8 in the LBLA

Genesis 8 in the LNT

Genesis 8 in the LSV

Genesis 8 in the MAAL

Genesis 8 in the MBV

Genesis 8 in the MBV2

Genesis 8 in the MHNT

Genesis 8 in the MKNFD

Genesis 8 in the MNG

Genesis 8 in the MNT

Genesis 8 in the MNT2

Genesis 8 in the MRS1T

Genesis 8 in the NAA

Genesis 8 in the NASB

Genesis 8 in the NBLA

Genesis 8 in the NBS

Genesis 8 in the NBVTP

Genesis 8 in the NET2

Genesis 8 in the NIV11

Genesis 8 in the NNT

Genesis 8 in the NNT2

Genesis 8 in the NNT3

Genesis 8 in the PDDPT

Genesis 8 in the PFNT

Genesis 8 in the RMNT

Genesis 8 in the SBIAS

Genesis 8 in the SBIBS

Genesis 8 in the SBIBS2

Genesis 8 in the SBICS

Genesis 8 in the SBIDS

Genesis 8 in the SBIGS

Genesis 8 in the SBIHS

Genesis 8 in the SBIIS

Genesis 8 in the SBIIS2

Genesis 8 in the SBIIS3

Genesis 8 in the SBIKS

Genesis 8 in the SBIKS2

Genesis 8 in the SBIMS

Genesis 8 in the SBIOS

Genesis 8 in the SBIPS

Genesis 8 in the SBISS

Genesis 8 in the SBITS

Genesis 8 in the SBITS2

Genesis 8 in the SBITS3

Genesis 8 in the SBITS4

Genesis 8 in the SBIUS

Genesis 8 in the SBIVS

Genesis 8 in the SBT

Genesis 8 in the SBT1E

Genesis 8 in the SCHL

Genesis 8 in the SNT

Genesis 8 in the SUSU

Genesis 8 in the SUSU2

Genesis 8 in the SYNO

Genesis 8 in the TBIAOTANT

Genesis 8 in the TBT1E

Genesis 8 in the TBT1E2

Genesis 8 in the TFTIP

Genesis 8 in the TFTU

Genesis 8 in the TGNTATF3T

Genesis 8 in the THAI

Genesis 8 in the TNFD

Genesis 8 in the TNT

Genesis 8 in the TNTIK

Genesis 8 in the TNTIL

Genesis 8 in the TNTIN

Genesis 8 in the TNTIP

Genesis 8 in the TNTIZ

Genesis 8 in the TOMA

Genesis 8 in the TTENT

Genesis 8 in the UBG

Genesis 8 in the UGV

Genesis 8 in the UGV2

Genesis 8 in the UGV3

Genesis 8 in the VBL

Genesis 8 in the VDCC

Genesis 8 in the YALU

Genesis 8 in the YAPE

Genesis 8 in the YBVTP

Genesis 8 in the ZBP