Jeremiah 41 (BOGWICC)

1 Pa mwezi wachisanu ndi chiwiri Ismaeli mwana wa Netaniya, mdzukulu wa Elisama amene anali wa banja laufumu ndiponso mmodzi wa atsogoleri a ankhondo a mfumu, anabwera ku Mizipa kwa Gedaliya mwana wa Ahikamu ndi anthu khumi. Pamene ankadya naye kumeneko, 2 Ismaeli mwana wa Netaniya pamodzi ndi anthu khumi aja anayimirira ndi kupha ndi lupanga Gedaliya mwana wa Ahikamu, mdzukulu wa Safani. Choncho anapha munthu amene mfumu ya ku Babuloni inamusankha kukhala bwanamkubwa wa dzikolo. 3 Ismaeli anaphanso Ayuda onse amene anali pamodzi ndi Gedaliya ku Mizipa, kuphatikizanso asilikali a Ababuloni amene anali ku Mizipako. 4 Mmawa mwake, anthu asanadziwe kuti Gedaliya waphedwa, 5 kunafika anthu 80 ochekera ku Sekemu, Silo ndi Samariya, amene anali atameta ndevu zawo, atangʼamba zovala zawo ndi kudzichekacheka. Iwowa anatenga chopereka cha ufa ndi lubani kuti adzapereke ku Nyumba ya Yehova. 6 Ismaeli mwana wa Netaniya anachoka ku Mizipa akulira kupita kukakumana nawo. Atakumana nawo, iye anati, “Bwerani mudzaonane ndi Gedaliya mwana wa Ahikamu.” 7 Atafika pakati pa mzinda, Ismaeli mwana wa Netaniya pamodzi ndi anthu amene anali naye anawapha anthuwo ndi kuwaponya mʼchitsime. 8 Koma anthu khumi a gululo anawuza Ismaeli kuti, “Musatiphe! Tili ndi tirigu ndi barele, mafuta ndi uchi, zimene tabisa mʼmunda.” Choncho anawasiya ndipo sanawaphere pamodzi ndi anzawo aja. 9 Tsono chitsime chimene anaponyamo mitembo ya anthu amene anawaphawo pamodzi ndi mtembo wa Gedaliya chinali chimene mfumu Asa anachikumba poopsedwa ndi Baasa mfumu ya Israeli. Ismaeli mwana wa Netaliya anachidzaza ndi mitembo. 10 Pambuyo pake Ismaeli anatenga ukapolo anthu ena onse amene anali ku Mizipa: ana aakazi a mfumu pamodzi ndi ena onse amene anatsalira kumeneko, amene Nebuzaradani mtsogoleri wa asilikali olonda mfumu anapatsa Gedaliya mwana wa Ahikamu kuti akhale bwanamkubwa wawo. Ismaeli mwana wa Netaliya anatenga ukapolo anthuwa ndi kuwoloka nawo kumapita ku dziko la Aamoni. 11 Pamene Yohanani mwana wa Kareya ndi atsogoleri onse a ankhondo amene anali naye pamodzi anamva zoyipa zonse zimene Ismaeli mwana wa Netaniya anachita, 12 anatenga ankhondo awo onse kupita kukamenyana ndi Ismaeli mwana wa Netaniya. Anakamupeza kufupi ndi chidziwe chachikulu cha ku Gibiyoni. 13 Pamene anthu onse amene Ismaeli anawagwira anaona Yohanani mwana wa Kareya pamodzi ndi atsogoleri a ankhondo amene anali naye, anasangalala. 14 Anthu onse amene Ismaeli anawagwira ukapolo ku Mizipa anabwerera ndi kupita kwa Yohanani mwana wa Kareya. 15 Koma Ismaeli pamodzi ndi anthu ake asanu ndi atatu, anathawa Yohanani ndi kuthawira kwa Aamoni. 16 Kenaka Yohanani mwana wa Kareya pamodzi ndi atsogoleri onse a ankhondo amene anali naye anatsogolera anthu onse otsala a ku Mizipa amene anawapulumutsa kwa Ismaeli mwana wa Netaniya atapha Gedaliya mwana wa Ahikamu. Anthu amenewa anali: asilikali, akazi, ana ndi amuna ofulidwa otumikira mfumu amene anawatenga ku Gibiyoni. 17 Ndipo ananyamuka nayima ku Geruti Kimuhamu pafupi ndi Betelehemu pa ulendo wawo wopita ku Igupto 18 kuthawa Ababuloni. Iwo anaopa Ababuloniwo chifukwa Ismaeli mwana wa Netaniya anapha Gedaliya mwana wa Ahikamu, amene mfumu ya ku Babuloni inamuyika kukhala bwanamkubwa wa dzikolo.

In Other Versions

Jeremiah 41 in the ANGEFD

Jeremiah 41 in the ANTPNG2D

Jeremiah 41 in the AS21

Jeremiah 41 in the BAGH

Jeremiah 41 in the BBPNG

Jeremiah 41 in the BBT1E

Jeremiah 41 in the BDS

Jeremiah 41 in the BEV

Jeremiah 41 in the BHAD

Jeremiah 41 in the BIB

Jeremiah 41 in the BLPT

Jeremiah 41 in the BNT

Jeremiah 41 in the BNTABOOT

Jeremiah 41 in the BNTLV

Jeremiah 41 in the BOATCB

Jeremiah 41 in the BOATCB2

Jeremiah 41 in the BOBCV

Jeremiah 41 in the BOCNT

Jeremiah 41 in the BOECS

Jeremiah 41 in the BOHCB

Jeremiah 41 in the BOHCV

Jeremiah 41 in the BOHLNT

Jeremiah 41 in the BOHNTLTAL

Jeremiah 41 in the BOICB

Jeremiah 41 in the BOILNTAP

Jeremiah 41 in the BOITCV

Jeremiah 41 in the BOKCV

Jeremiah 41 in the BOKCV2

Jeremiah 41 in the BOKHWOG

Jeremiah 41 in the BOKSSV

Jeremiah 41 in the BOLCB

Jeremiah 41 in the BOLCB2

Jeremiah 41 in the BOMCV

Jeremiah 41 in the BONAV

Jeremiah 41 in the BONCB

Jeremiah 41 in the BONLT

Jeremiah 41 in the BONUT2

Jeremiah 41 in the BOPLNT

Jeremiah 41 in the BOSCB

Jeremiah 41 in the BOSNC

Jeremiah 41 in the BOTLNT

Jeremiah 41 in the BOVCB

Jeremiah 41 in the BOYCB

Jeremiah 41 in the BPBB

Jeremiah 41 in the BPH

Jeremiah 41 in the BSB

Jeremiah 41 in the CCB

Jeremiah 41 in the CUV

Jeremiah 41 in the CUVS

Jeremiah 41 in the DBT

Jeremiah 41 in the DGDNT

Jeremiah 41 in the DHNT

Jeremiah 41 in the DNT

Jeremiah 41 in the ELBE

Jeremiah 41 in the EMTV

Jeremiah 41 in the ESV

Jeremiah 41 in the FBV

Jeremiah 41 in the FEB

Jeremiah 41 in the GGMNT

Jeremiah 41 in the GNT

Jeremiah 41 in the HARY

Jeremiah 41 in the HNT

Jeremiah 41 in the IRVA

Jeremiah 41 in the IRVB

Jeremiah 41 in the IRVG

Jeremiah 41 in the IRVH

Jeremiah 41 in the IRVK

Jeremiah 41 in the IRVM

Jeremiah 41 in the IRVM2

Jeremiah 41 in the IRVO

Jeremiah 41 in the IRVP

Jeremiah 41 in the IRVT

Jeremiah 41 in the IRVT2

Jeremiah 41 in the IRVU

Jeremiah 41 in the ISVN

Jeremiah 41 in the JSNT

Jeremiah 41 in the KAPI

Jeremiah 41 in the KBT1ETNIK

Jeremiah 41 in the KBV

Jeremiah 41 in the KJV

Jeremiah 41 in the KNFD

Jeremiah 41 in the LBA

Jeremiah 41 in the LBLA

Jeremiah 41 in the LNT

Jeremiah 41 in the LSV

Jeremiah 41 in the MAAL

Jeremiah 41 in the MBV

Jeremiah 41 in the MBV2

Jeremiah 41 in the MHNT

Jeremiah 41 in the MKNFD

Jeremiah 41 in the MNG

Jeremiah 41 in the MNT

Jeremiah 41 in the MNT2

Jeremiah 41 in the MRS1T

Jeremiah 41 in the NAA

Jeremiah 41 in the NASB

Jeremiah 41 in the NBLA

Jeremiah 41 in the NBS

Jeremiah 41 in the NBVTP

Jeremiah 41 in the NET2

Jeremiah 41 in the NIV11

Jeremiah 41 in the NNT

Jeremiah 41 in the NNT2

Jeremiah 41 in the NNT3

Jeremiah 41 in the PDDPT

Jeremiah 41 in the PFNT

Jeremiah 41 in the RMNT

Jeremiah 41 in the SBIAS

Jeremiah 41 in the SBIBS

Jeremiah 41 in the SBIBS2

Jeremiah 41 in the SBICS

Jeremiah 41 in the SBIDS

Jeremiah 41 in the SBIGS

Jeremiah 41 in the SBIHS

Jeremiah 41 in the SBIIS

Jeremiah 41 in the SBIIS2

Jeremiah 41 in the SBIIS3

Jeremiah 41 in the SBIKS

Jeremiah 41 in the SBIKS2

Jeremiah 41 in the SBIMS

Jeremiah 41 in the SBIOS

Jeremiah 41 in the SBIPS

Jeremiah 41 in the SBISS

Jeremiah 41 in the SBITS

Jeremiah 41 in the SBITS2

Jeremiah 41 in the SBITS3

Jeremiah 41 in the SBITS4

Jeremiah 41 in the SBIUS

Jeremiah 41 in the SBIVS

Jeremiah 41 in the SBT

Jeremiah 41 in the SBT1E

Jeremiah 41 in the SCHL

Jeremiah 41 in the SNT

Jeremiah 41 in the SUSU

Jeremiah 41 in the SUSU2

Jeremiah 41 in the SYNO

Jeremiah 41 in the TBIAOTANT

Jeremiah 41 in the TBT1E

Jeremiah 41 in the TBT1E2

Jeremiah 41 in the TFTIP

Jeremiah 41 in the TFTU

Jeremiah 41 in the TGNTATF3T

Jeremiah 41 in the THAI

Jeremiah 41 in the TNFD

Jeremiah 41 in the TNT

Jeremiah 41 in the TNTIK

Jeremiah 41 in the TNTIL

Jeremiah 41 in the TNTIN

Jeremiah 41 in the TNTIP

Jeremiah 41 in the TNTIZ

Jeremiah 41 in the TOMA

Jeremiah 41 in the TTENT

Jeremiah 41 in the UBG

Jeremiah 41 in the UGV

Jeremiah 41 in the UGV2

Jeremiah 41 in the UGV3

Jeremiah 41 in the VBL

Jeremiah 41 in the VDCC

Jeremiah 41 in the YALU

Jeremiah 41 in the YAPE

Jeremiah 41 in the YBVTP

Jeremiah 41 in the ZBP