Nehemiah 6 (BOGWICC)

1 Pamenepo Sanibalati, Tobiya, Gesemu Mwarabu ndi adani athu anamva kuti ndatsiriza ntchito yomanganso khoma ndi kuti palibe mpata umene watsala ngakhale kuti pa nthawi imeneyi ndinali ndisanayike zitseko pa zipata. 2 Sanibalati ndi Gesemu, ananditumizira uthenga uwu: “Bwerani tidzakumane pa mudzi wina ku chigwa cha Ono.”Koma iwo anakonzekera kuti akandichite chiwembu kumeneko. 3 Choncho ine ndinatuma amithenga ndi yankho ili: “Ine ndikugwira ntchito yayikulu kuno ndipo sindingathe kubwera kumeneko. Kodi ntchito iyime pofuna kuti ndibwere kumeneko?” 4 Ananditumizira uthenga umodzimodzi omwewu kanayi ndipo ndinawayankha chimodzimodzi. 5 Tsono kachisanu, Sanibalati anatumiza wantchito wake ndi kalata yosamata. 6 Mu kalatamo munali mawu akuti,“Pali mphekesera pakati pa mitundu ya anthu, ndiponso Gesemu akunena zomwezo kuti inu ndi Ayuda onse mufuna kuwukira boma. Nʼchifukwa chake mukumanga khoma. Mphekeserazo zikutinso inu mukufuna kudzakhala mfumu yawo. 7 Mwayikanso kale aneneri amene adzalengeza za iwe mu Yerusalemu kuti ‘Mu Yuda muli mfumu!’ Tsono nkhani iyi imveka ndithu kwa mfumu. Choncho bwerani kuti tidzakambirane.” 8 Ine ndinatumiza yankho ili: “Pa zimene mukunenazo, palibe chimene chinachitikapo. Inu mukungozipeka mʼmutu mwanu.” 9 Apa adani athu onsewa ankangofuna kutiopseza. Iwo ankaganiza kuti “Tichita mantha ndi kuleka kugwira ntchito.”Tsono ndinapemphera kuti, “Inu Mulungu ndilimbitseni mtima.” 10 Tsiku lina ndinapita ku nyumba ya Semaya mwana wa Delaya mwana wa Mehatabeli. Tsono anandiwuza kuti, “Tiyeni tikakumanire ku Nyumba ya Mulungu. Tikabisale mʼmenemo ndi kutseka zitseko chifukwa akubwera kudzakuphani. Ndithu usiku uno akubwera kudzakuphani.” 11 Koma ndinayankha kuti, “Kodi munthu ngati ine nʼkuthawa? Kapena munthu wofanana ndi ine nʼkupita ku Nyumba ya Mulungu kuti apulumutse moyo wake? Ayi, ine sindipita!” 12 Ndinazindikira kuti Mulungu sanamutume koma kuti anayankhula mawu oloserawa motsutsana nane chifukwa Tobiya ndi Sanibalati anamulemba ntchitoyi. 13 Iye analembedwa ntchitoyi ndi cholinga choti ine ndichite mantha, ndithawe. Ndikanatero ndiye kuti ndikanachimwira Yehova ndiponso iwowo akanandiyipitsira mbiri yanga ndi kumandinyoza. 14 Tsono ndinapemphera kuti, “Inu Mulungu wanga, kumbukirani Tobiya ndi Sanibalati chifukwa cha zimene achita. Kumbukiraninso mneneri wamkazi Nowadiya ndi aneneri amene akhala akufuna kundiopseza.” 15 Ndipo khoma linatsirizidwa kumanga pa tsiku la 25 la mwezi wa Eluli. Linamangidwa pa masiku okwana 52. 16 Adani athu onse atamva izi, mitundu yonse ya anthu yozungulira inachita mantha ndi kuchita manyazi. Iwo anazindikira kuti ntchitoyo inachitika ndi thandizo la Mulungu wathu. 17 Komanso masiku amenewo anthu olemekezeka a ku Yuda ankalemberana naye makalata ambiri ndi Tobiyayo, 18 pakuti anthu ambiri a ku Yuda anali atalumbira kale kuti adzagwira naye ntchito popeza anali mkamwini wa Sekaniya mwana wa Ara, ndipo mwana wake Yehohanani anakwatira mwana wamkazi wa Mesulamu mwana wa Berekiya. 19 Kuwonjezera apo, anthu ankasimba za ntchito zake zabwino ine ndili pomwepo ndipo anakamuwululira mawu anga. Choncho Tobiyayo ankatumiza makalata ondiopseza.

In Other Versions

Nehemiah 6 in the ANGEFD

Nehemiah 6 in the ANTPNG2D

Nehemiah 6 in the AS21

Nehemiah 6 in the BAGH

Nehemiah 6 in the BBPNG

Nehemiah 6 in the BBT1E

Nehemiah 6 in the BDS

Nehemiah 6 in the BEV

Nehemiah 6 in the BHAD

Nehemiah 6 in the BIB

Nehemiah 6 in the BLPT

Nehemiah 6 in the BNT

Nehemiah 6 in the BNTABOOT

Nehemiah 6 in the BNTLV

Nehemiah 6 in the BOATCB

Nehemiah 6 in the BOATCB2

Nehemiah 6 in the BOBCV

Nehemiah 6 in the BOCNT

Nehemiah 6 in the BOECS

Nehemiah 6 in the BOHCB

Nehemiah 6 in the BOHCV

Nehemiah 6 in the BOHLNT

Nehemiah 6 in the BOHNTLTAL

Nehemiah 6 in the BOICB

Nehemiah 6 in the BOILNTAP

Nehemiah 6 in the BOITCV

Nehemiah 6 in the BOKCV

Nehemiah 6 in the BOKCV2

Nehemiah 6 in the BOKHWOG

Nehemiah 6 in the BOKSSV

Nehemiah 6 in the BOLCB

Nehemiah 6 in the BOLCB2

Nehemiah 6 in the BOMCV

Nehemiah 6 in the BONAV

Nehemiah 6 in the BONCB

Nehemiah 6 in the BONLT

Nehemiah 6 in the BONUT2

Nehemiah 6 in the BOPLNT

Nehemiah 6 in the BOSCB

Nehemiah 6 in the BOSNC

Nehemiah 6 in the BOTLNT

Nehemiah 6 in the BOVCB

Nehemiah 6 in the BOYCB

Nehemiah 6 in the BPBB

Nehemiah 6 in the BPH

Nehemiah 6 in the BSB

Nehemiah 6 in the CCB

Nehemiah 6 in the CUV

Nehemiah 6 in the CUVS

Nehemiah 6 in the DBT

Nehemiah 6 in the DGDNT

Nehemiah 6 in the DHNT

Nehemiah 6 in the DNT

Nehemiah 6 in the ELBE

Nehemiah 6 in the EMTV

Nehemiah 6 in the ESV

Nehemiah 6 in the FBV

Nehemiah 6 in the FEB

Nehemiah 6 in the GGMNT

Nehemiah 6 in the GNT

Nehemiah 6 in the HARY

Nehemiah 6 in the HNT

Nehemiah 6 in the IRVA

Nehemiah 6 in the IRVB

Nehemiah 6 in the IRVG

Nehemiah 6 in the IRVH

Nehemiah 6 in the IRVK

Nehemiah 6 in the IRVM

Nehemiah 6 in the IRVM2

Nehemiah 6 in the IRVO

Nehemiah 6 in the IRVP

Nehemiah 6 in the IRVT

Nehemiah 6 in the IRVT2

Nehemiah 6 in the IRVU

Nehemiah 6 in the ISVN

Nehemiah 6 in the JSNT

Nehemiah 6 in the KAPI

Nehemiah 6 in the KBT1ETNIK

Nehemiah 6 in the KBV

Nehemiah 6 in the KJV

Nehemiah 6 in the KNFD

Nehemiah 6 in the LBA

Nehemiah 6 in the LBLA

Nehemiah 6 in the LNT

Nehemiah 6 in the LSV

Nehemiah 6 in the MAAL

Nehemiah 6 in the MBV

Nehemiah 6 in the MBV2

Nehemiah 6 in the MHNT

Nehemiah 6 in the MKNFD

Nehemiah 6 in the MNG

Nehemiah 6 in the MNT

Nehemiah 6 in the MNT2

Nehemiah 6 in the MRS1T

Nehemiah 6 in the NAA

Nehemiah 6 in the NASB

Nehemiah 6 in the NBLA

Nehemiah 6 in the NBS

Nehemiah 6 in the NBVTP

Nehemiah 6 in the NET2

Nehemiah 6 in the NIV11

Nehemiah 6 in the NNT

Nehemiah 6 in the NNT2

Nehemiah 6 in the NNT3

Nehemiah 6 in the PDDPT

Nehemiah 6 in the PFNT

Nehemiah 6 in the RMNT

Nehemiah 6 in the SBIAS

Nehemiah 6 in the SBIBS

Nehemiah 6 in the SBIBS2

Nehemiah 6 in the SBICS

Nehemiah 6 in the SBIDS

Nehemiah 6 in the SBIGS

Nehemiah 6 in the SBIHS

Nehemiah 6 in the SBIIS

Nehemiah 6 in the SBIIS2

Nehemiah 6 in the SBIIS3

Nehemiah 6 in the SBIKS

Nehemiah 6 in the SBIKS2

Nehemiah 6 in the SBIMS

Nehemiah 6 in the SBIOS

Nehemiah 6 in the SBIPS

Nehemiah 6 in the SBISS

Nehemiah 6 in the SBITS

Nehemiah 6 in the SBITS2

Nehemiah 6 in the SBITS3

Nehemiah 6 in the SBITS4

Nehemiah 6 in the SBIUS

Nehemiah 6 in the SBIVS

Nehemiah 6 in the SBT

Nehemiah 6 in the SBT1E

Nehemiah 6 in the SCHL

Nehemiah 6 in the SNT

Nehemiah 6 in the SUSU

Nehemiah 6 in the SUSU2

Nehemiah 6 in the SYNO

Nehemiah 6 in the TBIAOTANT

Nehemiah 6 in the TBT1E

Nehemiah 6 in the TBT1E2

Nehemiah 6 in the TFTIP

Nehemiah 6 in the TFTU

Nehemiah 6 in the TGNTATF3T

Nehemiah 6 in the THAI

Nehemiah 6 in the TNFD

Nehemiah 6 in the TNT

Nehemiah 6 in the TNTIK

Nehemiah 6 in the TNTIL

Nehemiah 6 in the TNTIN

Nehemiah 6 in the TNTIP

Nehemiah 6 in the TNTIZ

Nehemiah 6 in the TOMA

Nehemiah 6 in the TTENT

Nehemiah 6 in the UBG

Nehemiah 6 in the UGV

Nehemiah 6 in the UGV2

Nehemiah 6 in the UGV3

Nehemiah 6 in the VBL

Nehemiah 6 in the VDCC

Nehemiah 6 in the YALU

Nehemiah 6 in the YAPE

Nehemiah 6 in the YBVTP

Nehemiah 6 in the ZBP