Proverbs 26 (BOGWICC)
1 Ngati chisanu choti mbee nthawi yachilimwe kapena mvula nthawi yokolola,ndi momwe zilili ndi ulemu wowulandira chitsiru. 2 Ngati timba wokhalira kuwuluka kapena namzeze wokhalira kuzungulirazungulira,ndi mmenenso limachitira temberero lopanda chifukwa, silichitika. 3 Mkwapulo ndi wokwapulira kavalo, chitsulo ndi cha mʼkamwa mwa bulu,choncho ndodo ndi yoyenera ku msana wa chitsiru. 4 Usayankhe chitsiru monga mwa uchitsiru wake,kuopa kuti ungadzakhale ngati chitsirucho. 5 Koma nthawi zina umuyankhe monga mwa uchitsiru wake,kuopa kuti angamadziyese yekha wanzeru. 6 Kutuma chitsiru kuti akapereke uthengakuli ngati kudzidula mapazi ndipo kumakuyitanira mavuto. 7 Monga miyendo ya munthu wolumala imene ilibe mphamvundi mmene ulili mwambi mʼkamwa mwa chitsiru. 8 Kupereka ulemu kwa chitsiruzili ngati kukulunga mwala mʼlegeni. 9 Monga umachitira mtengo waminga wobaya mʼdzanja la chidakwandi mmene ulili mwambi mʼkamwa mwa chitsiru. 10 Munthu amene amalemba ntchito chitsiru chongoyendayenda,ali ngati woponya mivi amene angolasa anthu chilaselase. 11 Chitsiru chimene chimabwerezabwereza uchitsiru wakechili ngati galu amene amabwerera ku masanzi ake. 12 Munthu wa uchitsiru aliko bwino popeza pali chiyembekezokuposana ndi munthu amene amadziyesa yekha kuti ndi wanzeru. 13 Munthu waulesi amati, “Mu msewu muli mkango,mkango woopsa ukuyendayenda mʼmisewu!” 14 Monga chitseko chimapita uku ndi uku pa zolumikizira zake,momwemonso munthu waulesi amangotembenukatembenuka pa bedi lake. 15 Munthu waulesi akapisa dzanja lake mu mʼbale;zimamutopetsa kuti alifikitse pakamwa pake. 16 Munthu waulesi amadziyesa yekha wanzerukuposa anthu asanu ndi awiri amene amayankha mochenjera. 17 Munthu wongolowera mikangano imene si yakeali ngati munthu wogwira makutu a galu wongodziyendera. 18 Monga munthu wamisala ameneakuponya sakali zamoto kapena mivi yoopsa, 19 ndi momwe alili munthu wonamiza mnzake,amene amati, “Ndimangoseka chabe!” 20 Pakasowa nkhuni, moto umazima;chomwechonso pakasowa anthu amiseche mkangano umatha. 21 Monga alili makala pa moto wonyeka kapena mmene zimachitira nkhuni pa moto,ndi mmene alili munthu wolongolola poyambitsa mikangano. 22 Mawu a munthu wamiseche ali ngati chakudya chokoma;chimene chimatsikira mʼmimba mwa munthu. 23 Monga mmene chiziro chimakutira chiwiya chadothindi mmene mawu oshashalika amabisira mtima woyipa. 24 Munthu wachidani amayankhula zabwinopamene mu mtima mwake muli chinyengo. 25 Ngakhale wotereyu mawu ake ali okoma, koma usamukhulupirire,pakuti mu mtima mwake mwadzaza zonyansa. 26 Ngakhale amabisa chidani mochenjera,koma kuyipa kwakeko kudzaonekera poyera pa gulu la anthu. 27 Ngati munthu akumba dzenje, adzagweramo yekha;ngati munthu agubuduza mwala, udzamupsinja iye mwini. 28 Munthu wonama amadana ndi amene anawapweteka,ndipo pakamwa poshashalika pamabweretsa chiwonongeko.
In Other Versions
Proverbs 26 in the ANGEFD
Proverbs 26 in the ANTPNG2D
Proverbs 26 in the AS21
Proverbs 26 in the BAGH
Proverbs 26 in the BBPNG
Proverbs 26 in the BBT1E
Proverbs 26 in the BDS
Proverbs 26 in the BEV
Proverbs 26 in the BHAD
Proverbs 26 in the BIB
Proverbs 26 in the BLPT
Proverbs 26 in the BNT
Proverbs 26 in the BNTABOOT
Proverbs 26 in the BNTLV
Proverbs 26 in the BOATCB
Proverbs 26 in the BOATCB2
Proverbs 26 in the BOBCV
Proverbs 26 in the BOCNT
Proverbs 26 in the BOECS
Proverbs 26 in the BOHCB
Proverbs 26 in the BOHCV
Proverbs 26 in the BOHLNT
Proverbs 26 in the BOHNTLTAL
Proverbs 26 in the BOICB
Proverbs 26 in the BOILNTAP
Proverbs 26 in the BOITCV
Proverbs 26 in the BOKCV
Proverbs 26 in the BOKCV2
Proverbs 26 in the BOKHWOG
Proverbs 26 in the BOKSSV
Proverbs 26 in the BOLCB
Proverbs 26 in the BOLCB2
Proverbs 26 in the BOMCV
Proverbs 26 in the BONAV
Proverbs 26 in the BONCB
Proverbs 26 in the BONLT
Proverbs 26 in the BONUT2
Proverbs 26 in the BOPLNT
Proverbs 26 in the BOSCB
Proverbs 26 in the BOSNC
Proverbs 26 in the BOTLNT
Proverbs 26 in the BOVCB
Proverbs 26 in the BOYCB
Proverbs 26 in the BPBB
Proverbs 26 in the BPH
Proverbs 26 in the BSB
Proverbs 26 in the CCB
Proverbs 26 in the CUV
Proverbs 26 in the CUVS
Proverbs 26 in the DBT
Proverbs 26 in the DGDNT
Proverbs 26 in the DHNT
Proverbs 26 in the DNT
Proverbs 26 in the ELBE
Proverbs 26 in the EMTV
Proverbs 26 in the ESV
Proverbs 26 in the FBV
Proverbs 26 in the FEB
Proverbs 26 in the GGMNT
Proverbs 26 in the GNT
Proverbs 26 in the HARY
Proverbs 26 in the HNT
Proverbs 26 in the IRVA
Proverbs 26 in the IRVB
Proverbs 26 in the IRVG
Proverbs 26 in the IRVH
Proverbs 26 in the IRVK
Proverbs 26 in the IRVM
Proverbs 26 in the IRVM2
Proverbs 26 in the IRVO
Proverbs 26 in the IRVP
Proverbs 26 in the IRVT
Proverbs 26 in the IRVT2
Proverbs 26 in the IRVU
Proverbs 26 in the ISVN
Proverbs 26 in the JSNT
Proverbs 26 in the KAPI
Proverbs 26 in the KBT1ETNIK
Proverbs 26 in the KBV
Proverbs 26 in the KJV
Proverbs 26 in the KNFD
Proverbs 26 in the LBA
Proverbs 26 in the LBLA
Proverbs 26 in the LNT
Proverbs 26 in the LSV
Proverbs 26 in the MAAL
Proverbs 26 in the MBV
Proverbs 26 in the MBV2
Proverbs 26 in the MHNT
Proverbs 26 in the MKNFD
Proverbs 26 in the MNG
Proverbs 26 in the MNT
Proverbs 26 in the MNT2
Proverbs 26 in the MRS1T
Proverbs 26 in the NAA
Proverbs 26 in the NASB
Proverbs 26 in the NBLA
Proverbs 26 in the NBS
Proverbs 26 in the NBVTP
Proverbs 26 in the NET2
Proverbs 26 in the NIV11
Proverbs 26 in the NNT
Proverbs 26 in the NNT2
Proverbs 26 in the NNT3
Proverbs 26 in the PDDPT
Proverbs 26 in the PFNT
Proverbs 26 in the RMNT
Proverbs 26 in the SBIAS
Proverbs 26 in the SBIBS
Proverbs 26 in the SBIBS2
Proverbs 26 in the SBICS
Proverbs 26 in the SBIDS
Proverbs 26 in the SBIGS
Proverbs 26 in the SBIHS
Proverbs 26 in the SBIIS
Proverbs 26 in the SBIIS2
Proverbs 26 in the SBIIS3
Proverbs 26 in the SBIKS
Proverbs 26 in the SBIKS2
Proverbs 26 in the SBIMS
Proverbs 26 in the SBIOS
Proverbs 26 in the SBIPS
Proverbs 26 in the SBISS
Proverbs 26 in the SBITS
Proverbs 26 in the SBITS2
Proverbs 26 in the SBITS3
Proverbs 26 in the SBITS4
Proverbs 26 in the SBIUS
Proverbs 26 in the SBIVS
Proverbs 26 in the SBT
Proverbs 26 in the SBT1E
Proverbs 26 in the SCHL
Proverbs 26 in the SNT
Proverbs 26 in the SUSU
Proverbs 26 in the SUSU2
Proverbs 26 in the SYNO
Proverbs 26 in the TBIAOTANT
Proverbs 26 in the TBT1E
Proverbs 26 in the TBT1E2
Proverbs 26 in the TFTIP
Proverbs 26 in the TFTU
Proverbs 26 in the TGNTATF3T
Proverbs 26 in the THAI
Proverbs 26 in the TNFD
Proverbs 26 in the TNT
Proverbs 26 in the TNTIK
Proverbs 26 in the TNTIL
Proverbs 26 in the TNTIN
Proverbs 26 in the TNTIP
Proverbs 26 in the TNTIZ
Proverbs 26 in the TOMA
Proverbs 26 in the TTENT
Proverbs 26 in the UBG
Proverbs 26 in the UGV
Proverbs 26 in the UGV2
Proverbs 26 in the UGV3
Proverbs 26 in the VBL
Proverbs 26 in the VDCC
Proverbs 26 in the YALU
Proverbs 26 in the YAPE
Proverbs 26 in the YBVTP
Proverbs 26 in the ZBP