Deuteronomy 14 (BOGWICC)

1 Inu ndinu ana a Yehova Mulungu wanu. Osamadzichekacheka kapena kudzimeta pamphumi chifukwa cha abale anu amene amwalira, 2 pakuti ndinu anthu opatulika a Yehova Mulungu wanu. Pakati pa anthu onse pa dziko lonse lapansi, Yehova wasankha inu kuti chikhale chuma chake chamtengo wapatali. 3 Musamadye chinthu chilichonse chonyansa. 4 Nyama zomwe mukhoza kudya ndi izi: ngʼombe, nkhosa, mbuzi, 5 mbawala, gwape, mphoyo, mphalapala, ngoma, nyumbu ndi mbalale. 6 Nyama iliyonse imene ili ndi chipondero chogawikana pakati ndi yobzikula mukhoza kudya. 7 Komabe pakati pa nyama zimene zimabzikula kapena zogawikana zipondero, zimene simukuyenera kudya ndi ngamira, kalulu ndi mbira. Zimenezi ngakhale zimabzikula, zipondero zake sizogawikana, choncho ndi zodetsedwa, musadye. 8 Nkhumba simabzikula ndi yodetsedwanso ngakhale ili ndi zipondero zogawikana. Musamadye nyama yake kapena kukhudza imene yafa. 9 Mwa zamoyo zonse zimene zimakhala mʼmadzi, mukhoza kudya chilichonse chimene chili ndi minga ya pa msana ndi mamba. 10 Koma chilichonse chimene chilibe minga ya pa msana ndi mamba musadye pakuti nʼchodetsedwa. 11 Mukhoza kudya mbalame iliyonse yoyenera kudya. 12 Koma simukuyenera kudya izi: mphungu, nkhwazi, mwimba, 13 nankapakapa, akamtema, akhungubwi a mitundu yonse, ndi mtundu uliwonse wa miphamba, 14 mtundu uliwonse wa khwangwala, 15 kadzidzi wamphondo, kadzidzi wodzuma, chipudo, mtundu uliwonse wa akabawi, 16 kadzidzi wamngʼono, chiswankhono ndi mantchichi, 17 tsekwe, vuwo, dembo, 18 indwa, zimeza za mitundu yonse, nsadzu ndi mleme. 19 Zowuluka zonse za miyendo inayi ndi zodetsedwa. Musamadye zimenezi. 20 Koma chowuluka chilichonse choyenera kudya mukhoza kudya. 21 Musamadye chilichonse chimene mwachipeza chofaifa. Mukhoza kupatsa mlendo amene akukhala mu mzinda wina uliwonse wa mizinda yanu. Iyeyo akhoza kudya kapena mukhoza kugulitsa kwa wina aliyense amene sali wa mtundu wanu. Koma inu ndinu anthu opatulika a Yehova Mulungu wanu.Musamaphike mwana wambuzi mu mkaka wa mayi wake. 22 Muzionetsetsa kuti mukupatula chakhumi pa zokolola zanu chaka chilichonse. 23 Muzidyera chakhumi cha tirigu wanu, vinyo wanu watsopano ndi mafuta, ndi ana oyamba kubadwa a ngʼombe zanu pamaso pa Yehova Mulungu wanu pa malo amene adzasankhe ngati kokhalako dzina lake, kuti muphunzire kuopa Yehova Mulungu wanu. 24 Koma ngati malo amenewa ali kutali kwambiri ndipo kuti inu mwadalitsidwa ndi Yehova Mulungu wanu, ndipo simungathe kunyamula chakhumi chanu (chifukwa chakuti malo amene Yehova adzasankha kukayikako dzina lake ali kutali kwambiri), 25 ndiye musinthitse chakhumi chanucho ndi siliva, ndipo mutenge silivayo ndi kupita naye kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhe. 26 Gwiritsani ntchito silivayo kugula chilichonse chimene muchifuna monga ngʼombe, nkhosa, vinyo kapena zakumwa zina zosasitsa, kapena china chilichonse chimene muchifuna. Ndipo inu ndi anthu a pa banja panu mudzazidyera komweko pamaso pa Yehova Mulungu wanu ndi kukondwera. 27 Alevi okhala mʼmizinda yanu musaleke kuwathandiza popeza alibe gawo lawo la chuma kapena cholowa chawochawo. 28 Kumapeto kwa zaka zitatu zilizonse muzibweretsa zakhumi zonse pa zokolola za chaka chimenecho ndi kuzisunga mʼmidzi yanu, 29 kuti Alevi (amene alibe gawo lawo la chuma kapena cholowa chawochawo), alendo, ana ndi akazi amasiye, amene akukhala mʼmizinda yanu akhoza kubwera kudzadya ndi kukhuta. Ndipo kuti akutero Yehova Mulungu wanu akudalitseni pa ntchito zanu zonse.

In Other Versions

Deuteronomy 14 in the ANGEFD

Deuteronomy 14 in the ANTPNG2D

Deuteronomy 14 in the AS21

Deuteronomy 14 in the BAGH

Deuteronomy 14 in the BBPNG

Deuteronomy 14 in the BBT1E

Deuteronomy 14 in the BDS

Deuteronomy 14 in the BEV

Deuteronomy 14 in the BHAD

Deuteronomy 14 in the BIB

Deuteronomy 14 in the BLPT

Deuteronomy 14 in the BNT

Deuteronomy 14 in the BNTABOOT

Deuteronomy 14 in the BNTLV

Deuteronomy 14 in the BOATCB

Deuteronomy 14 in the BOATCB2

Deuteronomy 14 in the BOBCV

Deuteronomy 14 in the BOCNT

Deuteronomy 14 in the BOECS

Deuteronomy 14 in the BOHCB

Deuteronomy 14 in the BOHCV

Deuteronomy 14 in the BOHLNT

Deuteronomy 14 in the BOHNTLTAL

Deuteronomy 14 in the BOICB

Deuteronomy 14 in the BOILNTAP

Deuteronomy 14 in the BOITCV

Deuteronomy 14 in the BOKCV

Deuteronomy 14 in the BOKCV2

Deuteronomy 14 in the BOKHWOG

Deuteronomy 14 in the BOKSSV

Deuteronomy 14 in the BOLCB

Deuteronomy 14 in the BOLCB2

Deuteronomy 14 in the BOMCV

Deuteronomy 14 in the BONAV

Deuteronomy 14 in the BONCB

Deuteronomy 14 in the BONLT

Deuteronomy 14 in the BONUT2

Deuteronomy 14 in the BOPLNT

Deuteronomy 14 in the BOSCB

Deuteronomy 14 in the BOSNC

Deuteronomy 14 in the BOTLNT

Deuteronomy 14 in the BOVCB

Deuteronomy 14 in the BOYCB

Deuteronomy 14 in the BPBB

Deuteronomy 14 in the BPH

Deuteronomy 14 in the BSB

Deuteronomy 14 in the CCB

Deuteronomy 14 in the CUV

Deuteronomy 14 in the CUVS

Deuteronomy 14 in the DBT

Deuteronomy 14 in the DGDNT

Deuteronomy 14 in the DHNT

Deuteronomy 14 in the DNT

Deuteronomy 14 in the ELBE

Deuteronomy 14 in the EMTV

Deuteronomy 14 in the ESV

Deuteronomy 14 in the FBV

Deuteronomy 14 in the FEB

Deuteronomy 14 in the GGMNT

Deuteronomy 14 in the GNT

Deuteronomy 14 in the HARY

Deuteronomy 14 in the HNT

Deuteronomy 14 in the IRVA

Deuteronomy 14 in the IRVB

Deuteronomy 14 in the IRVG

Deuteronomy 14 in the IRVH

Deuteronomy 14 in the IRVK

Deuteronomy 14 in the IRVM

Deuteronomy 14 in the IRVM2

Deuteronomy 14 in the IRVO

Deuteronomy 14 in the IRVP

Deuteronomy 14 in the IRVT

Deuteronomy 14 in the IRVT2

Deuteronomy 14 in the IRVU

Deuteronomy 14 in the ISVN

Deuteronomy 14 in the JSNT

Deuteronomy 14 in the KAPI

Deuteronomy 14 in the KBT1ETNIK

Deuteronomy 14 in the KBV

Deuteronomy 14 in the KJV

Deuteronomy 14 in the KNFD

Deuteronomy 14 in the LBA

Deuteronomy 14 in the LBLA

Deuteronomy 14 in the LNT

Deuteronomy 14 in the LSV

Deuteronomy 14 in the MAAL

Deuteronomy 14 in the MBV

Deuteronomy 14 in the MBV2

Deuteronomy 14 in the MHNT

Deuteronomy 14 in the MKNFD

Deuteronomy 14 in the MNG

Deuteronomy 14 in the MNT

Deuteronomy 14 in the MNT2

Deuteronomy 14 in the MRS1T

Deuteronomy 14 in the NAA

Deuteronomy 14 in the NASB

Deuteronomy 14 in the NBLA

Deuteronomy 14 in the NBS

Deuteronomy 14 in the NBVTP

Deuteronomy 14 in the NET2

Deuteronomy 14 in the NIV11

Deuteronomy 14 in the NNT

Deuteronomy 14 in the NNT2

Deuteronomy 14 in the NNT3

Deuteronomy 14 in the PDDPT

Deuteronomy 14 in the PFNT

Deuteronomy 14 in the RMNT

Deuteronomy 14 in the SBIAS

Deuteronomy 14 in the SBIBS

Deuteronomy 14 in the SBIBS2

Deuteronomy 14 in the SBICS

Deuteronomy 14 in the SBIDS

Deuteronomy 14 in the SBIGS

Deuteronomy 14 in the SBIHS

Deuteronomy 14 in the SBIIS

Deuteronomy 14 in the SBIIS2

Deuteronomy 14 in the SBIIS3

Deuteronomy 14 in the SBIKS

Deuteronomy 14 in the SBIKS2

Deuteronomy 14 in the SBIMS

Deuteronomy 14 in the SBIOS

Deuteronomy 14 in the SBIPS

Deuteronomy 14 in the SBISS

Deuteronomy 14 in the SBITS

Deuteronomy 14 in the SBITS2

Deuteronomy 14 in the SBITS3

Deuteronomy 14 in the SBITS4

Deuteronomy 14 in the SBIUS

Deuteronomy 14 in the SBIVS

Deuteronomy 14 in the SBT

Deuteronomy 14 in the SBT1E

Deuteronomy 14 in the SCHL

Deuteronomy 14 in the SNT

Deuteronomy 14 in the SUSU

Deuteronomy 14 in the SUSU2

Deuteronomy 14 in the SYNO

Deuteronomy 14 in the TBIAOTANT

Deuteronomy 14 in the TBT1E

Deuteronomy 14 in the TBT1E2

Deuteronomy 14 in the TFTIP

Deuteronomy 14 in the TFTU

Deuteronomy 14 in the TGNTATF3T

Deuteronomy 14 in the THAI

Deuteronomy 14 in the TNFD

Deuteronomy 14 in the TNT

Deuteronomy 14 in the TNTIK

Deuteronomy 14 in the TNTIL

Deuteronomy 14 in the TNTIN

Deuteronomy 14 in the TNTIP

Deuteronomy 14 in the TNTIZ

Deuteronomy 14 in the TOMA

Deuteronomy 14 in the TTENT

Deuteronomy 14 in the UBG

Deuteronomy 14 in the UGV

Deuteronomy 14 in the UGV2

Deuteronomy 14 in the UGV3

Deuteronomy 14 in the VBL

Deuteronomy 14 in the VDCC

Deuteronomy 14 in the YALU

Deuteronomy 14 in the YAPE

Deuteronomy 14 in the YBVTP

Deuteronomy 14 in the ZBP