Deuteronomy 21 (BOGWICC)

1 Ngati munthu apezeka ataphedwa mʼmunda mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani kukhala lanu koma inu osadziwa amene wamupha, 2 akuluakulu anu ndi oweruza adzapite ndi kuyeza kutalikirana kuchokera pamene pali mtembowo ndi mizinda yoyandikira. 3 Kenaka akuluakulu a mzinda wapafupi kwambiri ndi mtembowo adzatenge ngʼombe imene sinagwirepo ntchito kapena kuvalapo goli 4 ndi kuyikusira ku chigwa chimene sichinalimidwepo ndiponso kumene kuli mtsinje woyenda. Ku chigwa kumeneko ayenera kukayithyola khosi ngʼombeyo. 5 Ansembe, ana a Aaroni, adzapite patsogolo pangʼono, popeza ndiwo amene Yehova Mulungu wanu anawasankha kuti azitumikira, kupereka mdalitso mʼdzina la Yehova ndi kugamula milandu yonse yamikangano ndi yovulazana. 6 Kenaka akuluakulu a mzinda wapafupi kwambiri ndi mtembowo adzasamba mʼmanja pamwamba pa ngʼombe yothyoledwa khosi ija, 7 nadzatsimikiza kuti, “Manja athu sanakhetse magazi awa ndipo sitinaonerere kuphedwako. 8 Yehova, landirani nsembe yopepesa ya anthu anu Aisraeli amene munawapulumutsa, ndipo muwakhululukire tchimo la kupha munthu wosalakwa.” Mukatero ndiye kuti adzapezeka kuti ndi osalakwa. 9 Kotero mudzadzichotsera nokha tchimo lokhetsa magazi wosalakwa, popeza mwachita zoyenera pamaso pa Yehova. 10 Mukapita kukachita nkhondo ndi adani anu, Yehova Mulungu wanu nawapereka adani anuwo mʼmanja mwanu muwagwira ukapolo, 11 ndiye ngati muona mkazi wokongola pakati pa ogwidwawo nakutengani mtima, mukhoza kumutenga kuti akhale mkazi wanu. 12 Mumutengere ku nyumba kwanu, kumumeta tsitsi lake, mumuwenge zikhadabo zake 13 ndipo avulidwe zovala zimene anagwidwa nazo. Atakhala mʼnyumba mwanu nalira maliro a abambo ndi amayi ake kwa mwezi wathunthu, ndiye mukhoza kupita kwa iye ndi kukhala mwamuna wake ndipo iyeyo adzakhala mkazi wanu. 14 Ngati simukukondweretsedwa naye, muloleni kuti apite kumene afuna. Musamugulitse kapena kumuzunza ngati kapolo, popeza mwamuchotsa ulemu. 15 Ngati munthu ali ndi akazi awiri, nakonda wina koposa mnzake, onsewa ndikubereka ana aamuna koma woyamba nakhala mwana wa mkazi amene samukondayo, 16 akamagawa chuma chake akanali moyo kwa ana akewo, asapereke ufulu wa mwana woyamba kubadwa kwa mwana wamwamuna wa mkazi amene amamukonda mʼmalo mwa mwana wake woyamba kubadwa weniweni amene ndi mwana wamkazi amene samukonda. 17 Iye ayenera kuonetsa kuti mwana wake wamwamuna wa mkazi wosakondedwayo ndiye woyamba kubadwa pomupatsa miyeso iwiri ya zonse zimene ali nazo. Mwana wamwamuna ameneyo ndiye chizindikiro cha mphamvu za abambo ake. Ufulu wokhala mwana wamwamuna woyamba ndi wake. 18 Ngati munthu ali ndi mwana wamwamuna wosamvera ndi wowukira amene samvera a abambo ake ndi amayi ake akamuweruza, 19 abambo ndi amayi ake amugwire ndi kupita naye kwa akuluakulu ku chipata cha mzinda wake ndipo 20 akawawuze akuluakuluwo kuti, “Mwana wathu wamwamunayu ndi wosamva ndi wowukira. Iyeyu satimvera. Ndi mwana wadyera komanso ndi chidakwa.” 21 Pamenepo anthu onse a mu mzinda wake adzamuphe ndi miyala. Muyenera kuchotsa zoyipa pakati panu. Aisraeli onse adzamva zimenezi ndipo adzachita mantha. 22 Ngati munthu wopezeka ndi mlandu wopha mnzake waphedwa ndipo mtembo wake wapachikidwa pamtengo, 23 musasiye mtembowo pa mtengopo usiku wonse. Muonetsetse kuti mwakawukwirira tsiku lomwelo, chifukwa aliyense wopachikidwa pamtengo ndi wotembereredwa ndi Mulungu. Musayipitse dziko limene Yehova Mulungu wanu akupatsani ngati cholowa chanu.

In Other Versions

Deuteronomy 21 in the ANGEFD

Deuteronomy 21 in the ANTPNG2D

Deuteronomy 21 in the AS21

Deuteronomy 21 in the BAGH

Deuteronomy 21 in the BBPNG

Deuteronomy 21 in the BBT1E

Deuteronomy 21 in the BDS

Deuteronomy 21 in the BEV

Deuteronomy 21 in the BHAD

Deuteronomy 21 in the BIB

Deuteronomy 21 in the BLPT

Deuteronomy 21 in the BNT

Deuteronomy 21 in the BNTABOOT

Deuteronomy 21 in the BNTLV

Deuteronomy 21 in the BOATCB

Deuteronomy 21 in the BOATCB2

Deuteronomy 21 in the BOBCV

Deuteronomy 21 in the BOCNT

Deuteronomy 21 in the BOECS

Deuteronomy 21 in the BOHCB

Deuteronomy 21 in the BOHCV

Deuteronomy 21 in the BOHLNT

Deuteronomy 21 in the BOHNTLTAL

Deuteronomy 21 in the BOICB

Deuteronomy 21 in the BOILNTAP

Deuteronomy 21 in the BOITCV

Deuteronomy 21 in the BOKCV

Deuteronomy 21 in the BOKCV2

Deuteronomy 21 in the BOKHWOG

Deuteronomy 21 in the BOKSSV

Deuteronomy 21 in the BOLCB

Deuteronomy 21 in the BOLCB2

Deuteronomy 21 in the BOMCV

Deuteronomy 21 in the BONAV

Deuteronomy 21 in the BONCB

Deuteronomy 21 in the BONLT

Deuteronomy 21 in the BONUT2

Deuteronomy 21 in the BOPLNT

Deuteronomy 21 in the BOSCB

Deuteronomy 21 in the BOSNC

Deuteronomy 21 in the BOTLNT

Deuteronomy 21 in the BOVCB

Deuteronomy 21 in the BOYCB

Deuteronomy 21 in the BPBB

Deuteronomy 21 in the BPH

Deuteronomy 21 in the BSB

Deuteronomy 21 in the CCB

Deuteronomy 21 in the CUV

Deuteronomy 21 in the CUVS

Deuteronomy 21 in the DBT

Deuteronomy 21 in the DGDNT

Deuteronomy 21 in the DHNT

Deuteronomy 21 in the DNT

Deuteronomy 21 in the ELBE

Deuteronomy 21 in the EMTV

Deuteronomy 21 in the ESV

Deuteronomy 21 in the FBV

Deuteronomy 21 in the FEB

Deuteronomy 21 in the GGMNT

Deuteronomy 21 in the GNT

Deuteronomy 21 in the HARY

Deuteronomy 21 in the HNT

Deuteronomy 21 in the IRVA

Deuteronomy 21 in the IRVB

Deuteronomy 21 in the IRVG

Deuteronomy 21 in the IRVH

Deuteronomy 21 in the IRVK

Deuteronomy 21 in the IRVM

Deuteronomy 21 in the IRVM2

Deuteronomy 21 in the IRVO

Deuteronomy 21 in the IRVP

Deuteronomy 21 in the IRVT

Deuteronomy 21 in the IRVT2

Deuteronomy 21 in the IRVU

Deuteronomy 21 in the ISVN

Deuteronomy 21 in the JSNT

Deuteronomy 21 in the KAPI

Deuteronomy 21 in the KBT1ETNIK

Deuteronomy 21 in the KBV

Deuteronomy 21 in the KJV

Deuteronomy 21 in the KNFD

Deuteronomy 21 in the LBA

Deuteronomy 21 in the LBLA

Deuteronomy 21 in the LNT

Deuteronomy 21 in the LSV

Deuteronomy 21 in the MAAL

Deuteronomy 21 in the MBV

Deuteronomy 21 in the MBV2

Deuteronomy 21 in the MHNT

Deuteronomy 21 in the MKNFD

Deuteronomy 21 in the MNG

Deuteronomy 21 in the MNT

Deuteronomy 21 in the MNT2

Deuteronomy 21 in the MRS1T

Deuteronomy 21 in the NAA

Deuteronomy 21 in the NASB

Deuteronomy 21 in the NBLA

Deuteronomy 21 in the NBS

Deuteronomy 21 in the NBVTP

Deuteronomy 21 in the NET2

Deuteronomy 21 in the NIV11

Deuteronomy 21 in the NNT

Deuteronomy 21 in the NNT2

Deuteronomy 21 in the NNT3

Deuteronomy 21 in the PDDPT

Deuteronomy 21 in the PFNT

Deuteronomy 21 in the RMNT

Deuteronomy 21 in the SBIAS

Deuteronomy 21 in the SBIBS

Deuteronomy 21 in the SBIBS2

Deuteronomy 21 in the SBICS

Deuteronomy 21 in the SBIDS

Deuteronomy 21 in the SBIGS

Deuteronomy 21 in the SBIHS

Deuteronomy 21 in the SBIIS

Deuteronomy 21 in the SBIIS2

Deuteronomy 21 in the SBIIS3

Deuteronomy 21 in the SBIKS

Deuteronomy 21 in the SBIKS2

Deuteronomy 21 in the SBIMS

Deuteronomy 21 in the SBIOS

Deuteronomy 21 in the SBIPS

Deuteronomy 21 in the SBISS

Deuteronomy 21 in the SBITS

Deuteronomy 21 in the SBITS2

Deuteronomy 21 in the SBITS3

Deuteronomy 21 in the SBITS4

Deuteronomy 21 in the SBIUS

Deuteronomy 21 in the SBIVS

Deuteronomy 21 in the SBT

Deuteronomy 21 in the SBT1E

Deuteronomy 21 in the SCHL

Deuteronomy 21 in the SNT

Deuteronomy 21 in the SUSU

Deuteronomy 21 in the SUSU2

Deuteronomy 21 in the SYNO

Deuteronomy 21 in the TBIAOTANT

Deuteronomy 21 in the TBT1E

Deuteronomy 21 in the TBT1E2

Deuteronomy 21 in the TFTIP

Deuteronomy 21 in the TFTU

Deuteronomy 21 in the TGNTATF3T

Deuteronomy 21 in the THAI

Deuteronomy 21 in the TNFD

Deuteronomy 21 in the TNT

Deuteronomy 21 in the TNTIK

Deuteronomy 21 in the TNTIL

Deuteronomy 21 in the TNTIN

Deuteronomy 21 in the TNTIP

Deuteronomy 21 in the TNTIZ

Deuteronomy 21 in the TOMA

Deuteronomy 21 in the TTENT

Deuteronomy 21 in the UBG

Deuteronomy 21 in the UGV

Deuteronomy 21 in the UGV2

Deuteronomy 21 in the UGV3

Deuteronomy 21 in the VBL

Deuteronomy 21 in the VDCC

Deuteronomy 21 in the YALU

Deuteronomy 21 in the YAPE

Deuteronomy 21 in the YBVTP

Deuteronomy 21 in the ZBP