Ecclesiastes 2 (BOGWICC)
1 Ine ndinaganiza mu mtima mwanga, “Tsopano ndiyese zosangalatsa kuti ndipeze zomwe ndi zabwino.” Koma izi zinaonekanso kuti ndi zopandapake. 2 “Kuseka,” ndinati, “imeneyo ndi misala. Ndipo kodi chisangalalo chimabweretsa phindu lanji?” 3 Ndinayesa kudzisangalatsa ndi vinyo, koma umenewu unali uchitsiru, pamenepo nʼkuti maganizo anga akutsogozedwa ndi nzeru. Ine ndinkati mwina kapena njira yotero nʼkukhala yopambana, imene anthu amatsata pofuna kusangalala pa masiku owerengeka a moyo wawo. 4 Ndinagwira ntchito zikuluzikulu: Ndinadzimangira nyumba ndi kuwoka mipesa. 5 Ndinalima madimba ndi minda yamitengo; ndipo ndinadzalamo mitengo ya zipatso za mitundu yonse. 6 Ndinakumba mayiwe osungiramo madzi woti ndizithirira minda ya mitengo yodzalidwa ija. 7 Ndinagula akapolo aamuna ndi akapolo aakazi, ndiponso ndinali ndi akapolo ena omwe anabadwira mʼnyumba mwanga. Ndinalinso ndi ngʼombe ndi nkhosa zambiri kupambana aliyense mu Yerusalemu amene analipo ndisanabadwe. 8 Ndinadzikundikira siliva ndi golide, ndiponso chuma chochokera kwa mafumu ndi madera awo. Ndinali ndi amuna ndi akazi oyimba ndiponso azikazi; zinthu zokondweretsa mtima wa munthu. 9 Ndinali munthu wotchuka kupambana wina aliyense mu Yerusalemu amene analipo ndisanabadwe. Mu zonsezi nzeru zanga zinali nane. 10 Sindinadzimane chilichonse chimene maso anga anachifuna;mtima wanga sindinawumane zokondweretsa.Mtima wanga unakondwera ndi ntchito yanga yonse,ndipo iyi ndiyo inali mphotho ya ntchito zanga zonse zolemetsa. 11 Koma pamene ndinayamba kuyangʼanayangʼana zonse zimene ndinachita ndi manja anga,ndi zimene ndinazivutikira kuti ndizipeze,zonsezi zinali zopandapake; kungodzivuta chabe,palibe chomwe ndinapindula pansi pano. 12 Kenaka maganizo anga anayamba kulingalira zakuti nzeru nʼchiyani,komanso kuti misala ndi uchitsiru nʼchiyani.Kodi munthu wodzalowa ufumu tsopanoyo angachite chiyanichoposa chimene chinachitidwa kale? 13 Ndinaona kuti nzeru ndi yopambana uchitsiru,monga momwe kuwala kumapambanira mdima. 14 Munthu wanzeru amayenda maso ali patsogolo,pamene chitsiru chimayenda mʼchimbulimbuli;koma ndinazindikira kuti chomwechimawachitikira onsewo ndi chimodzi. 15 Pamenepo ndinalingalira mu mtima mwanga,“Zochitikira chitsiru zidzandichitikiranso ine.Nanga tsono phindu langa nʼchiyani pakukhala wanzeru?”Ndinati mu mtima mwanga,“Ichinso ndi chopandapake.” 16 Pakuti munthu wanzeru, pamodzinso ndi chitsiru sadzakumbukiridwa nthawi yayitali;mʼmasiku amʼtsogolo awiriwo adzayiwalika.Mmene chimafera chitsiru ndi mmenenso amafera wanzeru! 17 Kotero ndinadana nawo moyo chifukwa ntchito zimene zimagwiridwa pansi pano ndi zosautsa kwa ine. Ntchito zonsezo ndi zopandapake, nʼkungodzivuta chabe. 18 Ine ndinadana nazo ntchito zonse zimene ndinazigwira pansi pano, chifukwa ndinayenera kudzazisiyira wina amene adzalowa mʼmalo mwanga. 19 Ndipo ndani amadziwa kuti munthu ameneyo adzakhala wanzeru kapena chitsiru? Komabe munthuyo adzakhala wolamulira zonse zimene ndinazichita pansi pano mwa nzeru zanga. Izinso ndi zopandapake. 20 Motero ndinayamba kutaya mtima chifukwa cha ntchito zonse zimene ndinazivutikira pansi pano. 21 Pakuti munthu atha kugwira ntchito yake mwanzeru, chidziwitso ndi luntha, ndipo kenaka nʼkusiyira wina amene sanakhetserepo thukuta. Izinso ndi zopandapake ndiponso tsoka lalikulu. 22 Kodi munthu amapindulanji pa ntchito zonse zolemetsa ndi zodetsa nkhawa zimene amazichita pansi pano? 23 Masiku ake onse amakhala achisoni, ntchito yake imakhala yovuta; ngakhale usiku womwe, mtima wake supumula. Izinso ndi zopandapake. 24 Kwa munthu palibe chabwino china kuposa kudya, kumwa ndi kukondwerera ntchito zake. Izinso ndaona kuti ndi zochokera kwa Mulungu, 25 pakuti popanda Iye, ndani angadye ndi kupeza chisangalalo? 26 Munthu amene amakondweretsa Mulungu, Mulunguyo amamusandutsa wanzeru, wozindikira ndi wachisangalalo, koma wochimwa, Mulungu amamupatsa ntchito yosonkhanitsa ndi kusunga chuma kuti adzachipereke kwa amene Mulunguyo amakondwera naye. Izinso ndi zopandapake, nʼkungodzivuta chabe.
In Other Versions
Ecclesiastes 2 in the ANGEFD
Ecclesiastes 2 in the ANTPNG2D
Ecclesiastes 2 in the AS21
Ecclesiastes 2 in the BAGH
Ecclesiastes 2 in the BBPNG
Ecclesiastes 2 in the BBT1E
Ecclesiastes 2 in the BDS
Ecclesiastes 2 in the BEV
Ecclesiastes 2 in the BHAD
Ecclesiastes 2 in the BIB
Ecclesiastes 2 in the BLPT
Ecclesiastes 2 in the BNT
Ecclesiastes 2 in the BNTABOOT
Ecclesiastes 2 in the BNTLV
Ecclesiastes 2 in the BOATCB
Ecclesiastes 2 in the BOATCB2
Ecclesiastes 2 in the BOBCV
Ecclesiastes 2 in the BOCNT
Ecclesiastes 2 in the BOECS
Ecclesiastes 2 in the BOHCB
Ecclesiastes 2 in the BOHCV
Ecclesiastes 2 in the BOHLNT
Ecclesiastes 2 in the BOHNTLTAL
Ecclesiastes 2 in the BOICB
Ecclesiastes 2 in the BOILNTAP
Ecclesiastes 2 in the BOITCV
Ecclesiastes 2 in the BOKCV
Ecclesiastes 2 in the BOKCV2
Ecclesiastes 2 in the BOKHWOG
Ecclesiastes 2 in the BOKSSV
Ecclesiastes 2 in the BOLCB
Ecclesiastes 2 in the BOLCB2
Ecclesiastes 2 in the BOMCV
Ecclesiastes 2 in the BONAV
Ecclesiastes 2 in the BONCB
Ecclesiastes 2 in the BONLT
Ecclesiastes 2 in the BONUT2
Ecclesiastes 2 in the BOPLNT
Ecclesiastes 2 in the BOSCB
Ecclesiastes 2 in the BOSNC
Ecclesiastes 2 in the BOTLNT
Ecclesiastes 2 in the BOVCB
Ecclesiastes 2 in the BOYCB
Ecclesiastes 2 in the BPBB
Ecclesiastes 2 in the BPH
Ecclesiastes 2 in the BSB
Ecclesiastes 2 in the CCB
Ecclesiastes 2 in the CUV
Ecclesiastes 2 in the CUVS
Ecclesiastes 2 in the DBT
Ecclesiastes 2 in the DGDNT
Ecclesiastes 2 in the DHNT
Ecclesiastes 2 in the DNT
Ecclesiastes 2 in the ELBE
Ecclesiastes 2 in the EMTV
Ecclesiastes 2 in the ESV
Ecclesiastes 2 in the FBV
Ecclesiastes 2 in the FEB
Ecclesiastes 2 in the GGMNT
Ecclesiastes 2 in the GNT
Ecclesiastes 2 in the HARY
Ecclesiastes 2 in the HNT
Ecclesiastes 2 in the IRVA
Ecclesiastes 2 in the IRVB
Ecclesiastes 2 in the IRVG
Ecclesiastes 2 in the IRVH
Ecclesiastes 2 in the IRVK
Ecclesiastes 2 in the IRVM
Ecclesiastes 2 in the IRVM2
Ecclesiastes 2 in the IRVO
Ecclesiastes 2 in the IRVP
Ecclesiastes 2 in the IRVT
Ecclesiastes 2 in the IRVT2
Ecclesiastes 2 in the IRVU
Ecclesiastes 2 in the ISVN
Ecclesiastes 2 in the JSNT
Ecclesiastes 2 in the KAPI
Ecclesiastes 2 in the KBT1ETNIK
Ecclesiastes 2 in the KBV
Ecclesiastes 2 in the KJV
Ecclesiastes 2 in the KNFD
Ecclesiastes 2 in the LBA
Ecclesiastes 2 in the LBLA
Ecclesiastes 2 in the LNT
Ecclesiastes 2 in the LSV
Ecclesiastes 2 in the MAAL
Ecclesiastes 2 in the MBV
Ecclesiastes 2 in the MBV2
Ecclesiastes 2 in the MHNT
Ecclesiastes 2 in the MKNFD
Ecclesiastes 2 in the MNG
Ecclesiastes 2 in the MNT
Ecclesiastes 2 in the MNT2
Ecclesiastes 2 in the MRS1T
Ecclesiastes 2 in the NAA
Ecclesiastes 2 in the NASB
Ecclesiastes 2 in the NBLA
Ecclesiastes 2 in the NBS
Ecclesiastes 2 in the NBVTP
Ecclesiastes 2 in the NET2
Ecclesiastes 2 in the NIV11
Ecclesiastes 2 in the NNT
Ecclesiastes 2 in the NNT2
Ecclesiastes 2 in the NNT3
Ecclesiastes 2 in the PDDPT
Ecclesiastes 2 in the PFNT
Ecclesiastes 2 in the RMNT
Ecclesiastes 2 in the SBIAS
Ecclesiastes 2 in the SBIBS
Ecclesiastes 2 in the SBIBS2
Ecclesiastes 2 in the SBICS
Ecclesiastes 2 in the SBIDS
Ecclesiastes 2 in the SBIGS
Ecclesiastes 2 in the SBIHS
Ecclesiastes 2 in the SBIIS
Ecclesiastes 2 in the SBIIS2
Ecclesiastes 2 in the SBIIS3
Ecclesiastes 2 in the SBIKS
Ecclesiastes 2 in the SBIKS2
Ecclesiastes 2 in the SBIMS
Ecclesiastes 2 in the SBIOS
Ecclesiastes 2 in the SBIPS
Ecclesiastes 2 in the SBISS
Ecclesiastes 2 in the SBITS
Ecclesiastes 2 in the SBITS2
Ecclesiastes 2 in the SBITS3
Ecclesiastes 2 in the SBITS4
Ecclesiastes 2 in the SBIUS
Ecclesiastes 2 in the SBIVS
Ecclesiastes 2 in the SBT
Ecclesiastes 2 in the SBT1E
Ecclesiastes 2 in the SCHL
Ecclesiastes 2 in the SNT
Ecclesiastes 2 in the SUSU
Ecclesiastes 2 in the SUSU2
Ecclesiastes 2 in the SYNO
Ecclesiastes 2 in the TBIAOTANT
Ecclesiastes 2 in the TBT1E
Ecclesiastes 2 in the TBT1E2
Ecclesiastes 2 in the TFTIP
Ecclesiastes 2 in the TFTU
Ecclesiastes 2 in the TGNTATF3T
Ecclesiastes 2 in the THAI
Ecclesiastes 2 in the TNFD
Ecclesiastes 2 in the TNT
Ecclesiastes 2 in the TNTIK
Ecclesiastes 2 in the TNTIL
Ecclesiastes 2 in the TNTIN
Ecclesiastes 2 in the TNTIP
Ecclesiastes 2 in the TNTIZ
Ecclesiastes 2 in the TOMA
Ecclesiastes 2 in the TTENT
Ecclesiastes 2 in the UBG
Ecclesiastes 2 in the UGV
Ecclesiastes 2 in the UGV2
Ecclesiastes 2 in the UGV3
Ecclesiastes 2 in the VBL
Ecclesiastes 2 in the VDCC
Ecclesiastes 2 in the YALU
Ecclesiastes 2 in the YAPE
Ecclesiastes 2 in the YBVTP
Ecclesiastes 2 in the ZBP