Exodus 19 (BOGWICC)

1 Ana a Israeli aja anafika ku chipululu cha Sinai pa tsiku loyamba la mwezi wachitatu chichokere mʼdziko la Igupto. 2 Atachoka ku Refidimu, anafika ku Sinai, ndipo Aisraeli anamangako misasa yawo moyangʼanana ndi phirilo. 3 Mose anakwera ku phiri kukakumana ndi Mulungu ndipo Yehova anamuyitana nati, “Ukawuze zidzukulu za Yakobo, ana onse a Israeli kuti, 4 ‘Inu eni munaona zimene ndinawachitira Aigupto ndiponso mmene ndinakunyamulirani, monga mmene chiwombankhanga chimanyamulira ana ake pa mapiko,’ ndikukubweretsani kwa Ine. 5 Tsopano, ngati mumveradi mawu anga ndi kusunga pangano langa, mudzakhala chuma changa chapamtima pakati pa mitundu yonse. Ngakhale kuti dziko lonse lapansi ndi langa, 6 inu mudzakhala ansembe achifumu ndi mtundu woyera mtima. Awa ndi mawu amene uyenera kuwawuza Aisraeli.” 7 Ndipo Mose anabwerera ndi kuyitanitsa akuluakulu. Atabwera anawafotokozera mawu amene Yehova anamulamulira kuti adzanene. 8 Anthu onse anayankha pamodzi kuti, “Ife tidzachita zonse zimene Yehova wanena.” Choncho Mose anabweza yankho lawo kwa Yehova. 9 Yehova anati kwa Mose, “Ine ndibwera kwa iwe mu mtambo wakuda kuti anthu adzandimve ndikuyankhula ndi iwe. Choncho adzakukhulupirira nthawi zonse.” Kenaka Mose anawuza Yehova zimene anthu ananena. 10 Ndipo Yehova anati kwa Mose, “Pita kwa anthu onse ndi kuwayeretsa lero ndi mawa. Achape zovala zawo 11 ndipo akhale atakonzeka pofika tsiku lachitatu, chifukwa tsiku limenelo Yehova adzatsika pa phiri la Sinai anthu onse akuona. 12 Uwalembere malire anthuwo kuzungulira phirilo ndipo uwawuze kuti, ‘Samalani musakwere phirilo kapena kukhudza tsinde lake. Aliyense wokhudza phiri adzaphedwa ndithu. 13 Aliyense wokhudza phiri adzaphedwa ndi miyala kapena kumulasa ndi mivi. Palibe amene adzamukhudze. Palibe munthu amene adzaloledwa kukhala ndi moyo ngakhale nyama. Iwo adzayenera kuphedwa.’ Koma anthu adzapita ku phirilo akadzamva kulira kwa lipenga la nyanga yankhosa.” 14 Tsono Mose anatsika phiri lija nafika kwa anthu aja ndi kuwayeretsa. Iwo anachapa zovala zawo. 15 Kenaka iye anati kwa anthu, “Konzekerani tsiku lachitatu, musagone pamodzi ndi mkazi.” 16 Mʼmamawa wa tsiku lachitatu kunali mabingu, ziphaliwali ndi mtambo wakuda umene unaphimba phiri, ndiponso lipenga lolira kwambiri. Aliyense ku misasa kuja ananjenjemera ndi mantha. 17 Ndipo Mose anatsogolera anthu kutuluka mʼmisasa kukakumana ndi Mulungu, ndipo anayima mʼmunsi mwa phiri. 18 Phiri la Sinai linakutidwa ndi utsi, chifukwa Yehova anatsika ndi moto pa phiripo. Utsi unakwera ngati wochokera mʼngʼanjo yamoto ndipo phiri lonse linagwedezeka kwambiri. 19 Liwu la lipenga linkakulirakulira. Tsono Mose anayankhula ndipo Yehova anamuyankha ndi mabingu. 20 Yehova anatsika nafika pamwamba pa phiri la Sinai, ndipo anayitana Mose kuti apite pa phiripo. Choncho Mose anakwera, 21 ndipo Yehova anati kwa iye, “Tsika ukawachenjeze anthu kuti asayesere kudutsa malire kuti adzandione chifukwa ambiri a iwo adzafa. 22 Ngakhale ansembe amene amatumikira pamaso pa Yehova ayenera kudziyeretsa kuopa kuti ndingadzawalange.” 23 Mose anati kwa Yehova, “Anthu sangakwere phiri la Sinai chifukwa inu munatichenjeza. Lembani malire kuzungulira phiri ndipo mulipatule kuti likhale loyera.” 24 Yehova anayankha, “Tsika ukamutenge Aaroni. Koma ansembe ndi anthu asayesere kubzola malire kuti abwere kwa Yehova chifukwa Iye adzawalanga.” 25 Ndipo Mose anatsika ndi kukawawuza anthuwo.

In Other Versions

Exodus 19 in the ANGEFD

Exodus 19 in the ANTPNG2D

Exodus 19 in the AS21

Exodus 19 in the BAGH

Exodus 19 in the BBPNG

Exodus 19 in the BBT1E

Exodus 19 in the BDS

Exodus 19 in the BEV

Exodus 19 in the BHAD

Exodus 19 in the BIB

Exodus 19 in the BLPT

Exodus 19 in the BNT

Exodus 19 in the BNTABOOT

Exodus 19 in the BNTLV

Exodus 19 in the BOATCB

Exodus 19 in the BOATCB2

Exodus 19 in the BOBCV

Exodus 19 in the BOCNT

Exodus 19 in the BOECS

Exodus 19 in the BOHCB

Exodus 19 in the BOHCV

Exodus 19 in the BOHLNT

Exodus 19 in the BOHNTLTAL

Exodus 19 in the BOICB

Exodus 19 in the BOILNTAP

Exodus 19 in the BOITCV

Exodus 19 in the BOKCV

Exodus 19 in the BOKCV2

Exodus 19 in the BOKHWOG

Exodus 19 in the BOKSSV

Exodus 19 in the BOLCB

Exodus 19 in the BOLCB2

Exodus 19 in the BOMCV

Exodus 19 in the BONAV

Exodus 19 in the BONCB

Exodus 19 in the BONLT

Exodus 19 in the BONUT2

Exodus 19 in the BOPLNT

Exodus 19 in the BOSCB

Exodus 19 in the BOSNC

Exodus 19 in the BOTLNT

Exodus 19 in the BOVCB

Exodus 19 in the BOYCB

Exodus 19 in the BPBB

Exodus 19 in the BPH

Exodus 19 in the BSB

Exodus 19 in the CCB

Exodus 19 in the CUV

Exodus 19 in the CUVS

Exodus 19 in the DBT

Exodus 19 in the DGDNT

Exodus 19 in the DHNT

Exodus 19 in the DNT

Exodus 19 in the ELBE

Exodus 19 in the EMTV

Exodus 19 in the ESV

Exodus 19 in the FBV

Exodus 19 in the FEB

Exodus 19 in the GGMNT

Exodus 19 in the GNT

Exodus 19 in the HARY

Exodus 19 in the HNT

Exodus 19 in the IRVA

Exodus 19 in the IRVB

Exodus 19 in the IRVG

Exodus 19 in the IRVH

Exodus 19 in the IRVK

Exodus 19 in the IRVM

Exodus 19 in the IRVM2

Exodus 19 in the IRVO

Exodus 19 in the IRVP

Exodus 19 in the IRVT

Exodus 19 in the IRVT2

Exodus 19 in the IRVU

Exodus 19 in the ISVN

Exodus 19 in the JSNT

Exodus 19 in the KAPI

Exodus 19 in the KBT1ETNIK

Exodus 19 in the KBV

Exodus 19 in the KJV

Exodus 19 in the KNFD

Exodus 19 in the LBA

Exodus 19 in the LBLA

Exodus 19 in the LNT

Exodus 19 in the LSV

Exodus 19 in the MAAL

Exodus 19 in the MBV

Exodus 19 in the MBV2

Exodus 19 in the MHNT

Exodus 19 in the MKNFD

Exodus 19 in the MNG

Exodus 19 in the MNT

Exodus 19 in the MNT2

Exodus 19 in the MRS1T

Exodus 19 in the NAA

Exodus 19 in the NASB

Exodus 19 in the NBLA

Exodus 19 in the NBS

Exodus 19 in the NBVTP

Exodus 19 in the NET2

Exodus 19 in the NIV11

Exodus 19 in the NNT

Exodus 19 in the NNT2

Exodus 19 in the NNT3

Exodus 19 in the PDDPT

Exodus 19 in the PFNT

Exodus 19 in the RMNT

Exodus 19 in the SBIAS

Exodus 19 in the SBIBS

Exodus 19 in the SBIBS2

Exodus 19 in the SBICS

Exodus 19 in the SBIDS

Exodus 19 in the SBIGS

Exodus 19 in the SBIHS

Exodus 19 in the SBIIS

Exodus 19 in the SBIIS2

Exodus 19 in the SBIIS3

Exodus 19 in the SBIKS

Exodus 19 in the SBIKS2

Exodus 19 in the SBIMS

Exodus 19 in the SBIOS

Exodus 19 in the SBIPS

Exodus 19 in the SBISS

Exodus 19 in the SBITS

Exodus 19 in the SBITS2

Exodus 19 in the SBITS3

Exodus 19 in the SBITS4

Exodus 19 in the SBIUS

Exodus 19 in the SBIVS

Exodus 19 in the SBT

Exodus 19 in the SBT1E

Exodus 19 in the SCHL

Exodus 19 in the SNT

Exodus 19 in the SUSU

Exodus 19 in the SUSU2

Exodus 19 in the SYNO

Exodus 19 in the TBIAOTANT

Exodus 19 in the TBT1E

Exodus 19 in the TBT1E2

Exodus 19 in the TFTIP

Exodus 19 in the TFTU

Exodus 19 in the TGNTATF3T

Exodus 19 in the THAI

Exodus 19 in the TNFD

Exodus 19 in the TNT

Exodus 19 in the TNTIK

Exodus 19 in the TNTIL

Exodus 19 in the TNTIN

Exodus 19 in the TNTIP

Exodus 19 in the TNTIZ

Exodus 19 in the TOMA

Exodus 19 in the TTENT

Exodus 19 in the UBG

Exodus 19 in the UGV

Exodus 19 in the UGV2

Exodus 19 in the UGV3

Exodus 19 in the VBL

Exodus 19 in the VDCC

Exodus 19 in the YALU

Exodus 19 in the YAPE

Exodus 19 in the YBVTP

Exodus 19 in the ZBP