Ezekiel 9 (BOGWICC)
1 Pambuyo pake Yehova anandiyankhula mofuwula kuti, “Bwerani pafupi, inu odzalanga mzindawu, aliyense ali ndi chida chake mʼmanja.” 2 Ndipo ndinaona anthu asanu ndi mmodzi akubwera kuchokera ku chipata chakumtunda chimene chimaloza kumpoto, aliyense ali ndi chida choopsa cha nkhondo mʼdzanja lake. Pagulu pawopa panali munthu wovala chovala chabafuta, atatenga zolembera pambali pake. Iwo analowa ndi kuyima pambali pa guwa lamkuwa. 3 Tsono ulemerero wa Mulungu wa Israeli unakwera kuchokera pamwamba pa akerubi, pamene unali, ndipo unafika pa chiwundo cha Nyumba ya Mulungu. Pamenepo Yehova anayitana munthu amene anavala chovala chabafuta uja amene anatenga zolembera pambali pake 4 ndipo anamuwuza kuti, “Pita mu mzinda wonse wa Yerusalemu ndi kuyika chizindikiro pamphumi pa anthu amene akumva chisoni ndi kulira chifukwa cha zinthu zonse zonyansa zimene zikuchitika mu mzindamo.” 5 Kenaka ndinamva Yehova akuwuza anthu ena aja kuti, “Mutsateni mu mzinda wonse ndipo mukakanthe aliyense mopanda kumvera chisoni kapena chifundo. 6 Mukaphe kotheratu anthu okalamba, anyamata ndi atsikana, makanda ndi akazi koma musakakhudze wina aliyense amene ali ndi chizindikiro. Muyambire ku Nyumba yanga yopatulika.” Motero iwo anayamba ndi akuluakulu amene anali kutsogolo kwa Nyumba ya Mulungu. 7 Ndipo Yehova anawawuza kuti, “Ipitsani Nyumba ya Mulungu ndipo mudzaze mabwalo ake ndi anthu akufa. Pitani.” Choncho iwo anapita nayamba kupha anthu mu mzinda monse. 8 Pamene iwo ankapha anthu, ine ndinatsala ndekha. Tsono ndinadzigwetsa chafufumimba ndi kufuwula kuti, “Aa, Ambuye Yehova! Kodi mwawakwiyiratu anthu a ku Yerusalemu motero kuti mudzawononga kotheratu anthu onse otsala ku Israeli?” 9 Iye anandiyankha kuti, “Tchimo la Aisraeli ndi Yuda ndi lalikulu kwambiri; dziko ladzaza ndi zophana ndipo mu mzinda mwadzaza ndi zosalungama. Iwo akunena kuti, ‘Yehova walisiya dziko lake; Yehova sakuona.’ 10 Choncho sindidzawamvera chisoni kapena kuwaleka, koma Ine ndidzawalanga potsata zochita zawo.” 11 Ndipo munthu wovala chovala chabafuta uja atatenga zolembera pambali pake anadzafotokozera Yehova kuti, “Ndachita monga munandilamulira.”
In Other Versions
Ezekiel 9 in the ANGEFD
Ezekiel 9 in the ANTPNG2D
Ezekiel 9 in the AS21
Ezekiel 9 in the BAGH
Ezekiel 9 in the BBPNG
Ezekiel 9 in the BBT1E
Ezekiel 9 in the BDS
Ezekiel 9 in the BEV
Ezekiel 9 in the BHAD
Ezekiel 9 in the BIB
Ezekiel 9 in the BLPT
Ezekiel 9 in the BNT
Ezekiel 9 in the BNTABOOT
Ezekiel 9 in the BNTLV
Ezekiel 9 in the BOATCB
Ezekiel 9 in the BOATCB2
Ezekiel 9 in the BOBCV
Ezekiel 9 in the BOCNT
Ezekiel 9 in the BOECS
Ezekiel 9 in the BOHCB
Ezekiel 9 in the BOHCV
Ezekiel 9 in the BOHLNT
Ezekiel 9 in the BOHNTLTAL
Ezekiel 9 in the BOICB
Ezekiel 9 in the BOILNTAP
Ezekiel 9 in the BOITCV
Ezekiel 9 in the BOKCV
Ezekiel 9 in the BOKCV2
Ezekiel 9 in the BOKHWOG
Ezekiel 9 in the BOKSSV
Ezekiel 9 in the BOLCB
Ezekiel 9 in the BOLCB2
Ezekiel 9 in the BOMCV
Ezekiel 9 in the BONAV
Ezekiel 9 in the BONCB
Ezekiel 9 in the BONLT
Ezekiel 9 in the BONUT2
Ezekiel 9 in the BOPLNT
Ezekiel 9 in the BOSCB
Ezekiel 9 in the BOSNC
Ezekiel 9 in the BOTLNT
Ezekiel 9 in the BOVCB
Ezekiel 9 in the BOYCB
Ezekiel 9 in the BPBB
Ezekiel 9 in the BPH
Ezekiel 9 in the BSB
Ezekiel 9 in the CCB
Ezekiel 9 in the CUV
Ezekiel 9 in the CUVS
Ezekiel 9 in the DBT
Ezekiel 9 in the DGDNT
Ezekiel 9 in the DHNT
Ezekiel 9 in the DNT
Ezekiel 9 in the ELBE
Ezekiel 9 in the EMTV
Ezekiel 9 in the ESV
Ezekiel 9 in the FBV
Ezekiel 9 in the FEB
Ezekiel 9 in the GGMNT
Ezekiel 9 in the GNT
Ezekiel 9 in the HARY
Ezekiel 9 in the HNT
Ezekiel 9 in the IRVA
Ezekiel 9 in the IRVB
Ezekiel 9 in the IRVG
Ezekiel 9 in the IRVH
Ezekiel 9 in the IRVK
Ezekiel 9 in the IRVM
Ezekiel 9 in the IRVM2
Ezekiel 9 in the IRVO
Ezekiel 9 in the IRVP
Ezekiel 9 in the IRVT
Ezekiel 9 in the IRVT2
Ezekiel 9 in the IRVU
Ezekiel 9 in the ISVN
Ezekiel 9 in the JSNT
Ezekiel 9 in the KAPI
Ezekiel 9 in the KBT1ETNIK
Ezekiel 9 in the KBV
Ezekiel 9 in the KJV
Ezekiel 9 in the KNFD
Ezekiel 9 in the LBA
Ezekiel 9 in the LBLA
Ezekiel 9 in the LNT
Ezekiel 9 in the LSV
Ezekiel 9 in the MAAL
Ezekiel 9 in the MBV
Ezekiel 9 in the MBV2
Ezekiel 9 in the MHNT
Ezekiel 9 in the MKNFD
Ezekiel 9 in the MNG
Ezekiel 9 in the MNT
Ezekiel 9 in the MNT2
Ezekiel 9 in the MRS1T
Ezekiel 9 in the NAA
Ezekiel 9 in the NASB
Ezekiel 9 in the NBLA
Ezekiel 9 in the NBS
Ezekiel 9 in the NBVTP
Ezekiel 9 in the NET2
Ezekiel 9 in the NIV11
Ezekiel 9 in the NNT
Ezekiel 9 in the NNT2
Ezekiel 9 in the NNT3
Ezekiel 9 in the PDDPT
Ezekiel 9 in the PFNT
Ezekiel 9 in the RMNT
Ezekiel 9 in the SBIAS
Ezekiel 9 in the SBIBS
Ezekiel 9 in the SBIBS2
Ezekiel 9 in the SBICS
Ezekiel 9 in the SBIDS
Ezekiel 9 in the SBIGS
Ezekiel 9 in the SBIHS
Ezekiel 9 in the SBIIS
Ezekiel 9 in the SBIIS2
Ezekiel 9 in the SBIIS3
Ezekiel 9 in the SBIKS
Ezekiel 9 in the SBIKS2
Ezekiel 9 in the SBIMS
Ezekiel 9 in the SBIOS
Ezekiel 9 in the SBIPS
Ezekiel 9 in the SBISS
Ezekiel 9 in the SBITS
Ezekiel 9 in the SBITS2
Ezekiel 9 in the SBITS3
Ezekiel 9 in the SBITS4
Ezekiel 9 in the SBIUS
Ezekiel 9 in the SBIVS
Ezekiel 9 in the SBT
Ezekiel 9 in the SBT1E
Ezekiel 9 in the SCHL
Ezekiel 9 in the SNT
Ezekiel 9 in the SUSU
Ezekiel 9 in the SUSU2
Ezekiel 9 in the SYNO
Ezekiel 9 in the TBIAOTANT
Ezekiel 9 in the TBT1E
Ezekiel 9 in the TBT1E2
Ezekiel 9 in the TFTIP
Ezekiel 9 in the TFTU
Ezekiel 9 in the TGNTATF3T
Ezekiel 9 in the THAI
Ezekiel 9 in the TNFD
Ezekiel 9 in the TNT
Ezekiel 9 in the TNTIK
Ezekiel 9 in the TNTIL
Ezekiel 9 in the TNTIN
Ezekiel 9 in the TNTIP
Ezekiel 9 in the TNTIZ
Ezekiel 9 in the TOMA
Ezekiel 9 in the TTENT
Ezekiel 9 in the UBG
Ezekiel 9 in the UGV
Ezekiel 9 in the UGV2
Ezekiel 9 in the UGV3
Ezekiel 9 in the VBL
Ezekiel 9 in the VDCC
Ezekiel 9 in the YALU
Ezekiel 9 in the YAPE
Ezekiel 9 in the YBVTP
Ezekiel 9 in the ZBP