Galatians 4 (BOGWICC)

1 Chimene ndikunena ndi chakuti, ngati mlowamʼmalo akali wamngʼono, sasiyana ndi kapolo, ngakhale kuti chuma chonse ndi chake. 2 Mwanayo ayenera kumvera omulera ndiponso anthu oyangʼanira chuma mpaka nthawi imene abambo ake anakhazikitsa. 3 Chomwechonso, ife pamene tinali ana, tinali akapolo a miyambo ya dziko lapansi. 4 Koma nthawi itakwana, Mulungu anatumiza Mwana wake, wobadwa mwa mayi, wobadwa pansi pa lamulo, 5 kudzawombola amene anali pansi pa lamulo, kuti tilandiridwe monga ana. 6 Ndipo popeza ndinu ana, Mulungu anatumiza Mzimu wa Mwana wake kuti alowe mʼmitima mwathu, Mzimu amene amafuwula kuti, “Abba, Atate.” 7 Choncho sindiwenso kapolo, koma mwana wa Mulungu. Tsono popeza ndiwe mwana wake, Mulungu wakusandutsanso mlowamʼmalo. 8 Koma poyamba pamene simunkamudziwa Mulungu, munali akapolo a zimene mwachilengedwe si milungu. 9 Koma tsopano pakuti mukumudziwa Mulungu, kapena ndinene kuti Mulungu akukudziwani, nʼchifukwa chiyani mukubwereranso ku miyambo yofowoka ndi yomvetsa chisoni? Kodi mukufuna musandukenso akapolo? 10 Mumasunga masiku, miyezi ndi nyengo ndi zaka. 11 Ine ndikuopa kuti mwina ntchito zanga pa inu ndinagwira pachabe. 12 Abale, ndikukudandaulirani, mukhale ngati ine, popeza ine ndinakhala ngati inu. Inu simunandilakwire. 13 Monga inu mukudziwa ndinkakulalikirani Uthenga Wabwino ndili wofowoka. 14 Ngakhale kuti matendawo anali ngati mayesero kwa inu, simunandinyoze kapena kunyansidwa nane. Komatu inu munandilandira ngati kuti ndinali mngelo wa Mulungu, ngati kuti ndinali Khristu Yesu mwini. 15 Kodi chimwemwe chanu chonse chija chili kuti? Ine nditha kuchitira umboni kuti, ngati kukanatheka, inu mukanakolowola maso anu ndi kundipatsa. 16 Kodi tsopano ine ndasanduka mdani wanu chifukwa ndakuwuzani choonadi? 17 Anthu amenewo akuchita changu kuti akukopeni, koma changu chawocho sichabwino. Chimene iwo akufuna ndi chakuti akuchotseni inu kwa ife, kuti mukachite changu powathandiza iwowo. 18 Nʼkwabwino kuchita changu, ngati cholingacho chili chabwino ndi kukhala otero nthawi zonse osati pokhapo pamene ine ndili ndi inu. 19 Ana anga okondedwa, inu amene ine ndikukumveraninso zowawa za kubereka kufikira Khristu atawumbidwa mwa inu, 20 ine ndikanakonda ndikanakhala nanu tsopano kuti ndisinthe mawu anga, chifukwa ndathedwa nanu nzeru. 21 Tandiwuzani, inu, abale amene mukufuna kukhala pansi pa lamulo, kodi simukudziwa chimene lamulo limanena? 22 Pakuti zinalembedwa kuti Abrahamu anali ndi ana aamuna awiri, wina mayi wake anali kapolo ndipo wina mayi wake anali mfulu. 23 Mwana wake wobadwa mwa kapolo anabadwa mwathupi; koma mwana wake wobadwa mwa mfulu anabadwa monga mwa lonjezo. 24 Zinthu izi zinali ngati fanizo, pakuti amayi awiriwa akuyimira mapangano awiri. Pangano limodzi ndi lochokera mʼPhiri la Sinai, ndiye Hagara, ndipo amabereka ana amene ndi akapolo. 25 Tsono Hagara, akuyimira Phiri la Sinai ku Arabiya amene afanizidwa ndi mzinda wa Yerusalemu wa lero, chifukwa ali mu ukapolo pamodzi ndi ana ake. 26 Koma Yerusalemu wakumwamba ndiye mfulu, ndipo ndiye mayi wathu. 27 Pakuti kwalembedwa kuti,“Sangalala, iwe mayi wosabala,amene sunabalepo mwana;imba nthungululu ndi kufuwula mwachimwemwe,iwe amene sunamvepo ululu wa pobereka;chifukwa mkazi wosiyidwa adzakhala ndi ana ambirikuposa mkazi wokwatiwa.” 28 Tsono inu abale, ndinu ana alonjezo ngati Isake. 29 Nthawi imeneyo mwana wobadwa mwathupi anazunza mwana wobadwa mwamphamvu za Mzimu. Zili chimodzimodzinso lero. 30 Kodi Malemba akuti chiyani? “Muchotse kapoloyo pamodzi ndi mwana wake, chifukwa mwana wa kapolo sadzagawana chuma ndi mwana wamfulu.” 31 Chifukwa chake, abale, ife sindife ana akapolo, koma ana a mfulu.

In Other Versions

Galatians 4 in the ANGEFD

Galatians 4 in the ANTPNG2D

Galatians 4 in the AS21

Galatians 4 in the BAGH

Galatians 4 in the BBPNG

Galatians 4 in the BBT1E

Galatians 4 in the BDS

Galatians 4 in the BEV

Galatians 4 in the BHAD

Galatians 4 in the BIB

Galatians 4 in the BLPT

Galatians 4 in the BNT

Galatians 4 in the BNTABOOT

Galatians 4 in the BNTLV

Galatians 4 in the BOATCB

Galatians 4 in the BOATCB2

Galatians 4 in the BOBCV

Galatians 4 in the BOCNT

Galatians 4 in the BOECS

Galatians 4 in the BOHCB

Galatians 4 in the BOHCV

Galatians 4 in the BOHLNT

Galatians 4 in the BOHNTLTAL

Galatians 4 in the BOICB

Galatians 4 in the BOILNTAP

Galatians 4 in the BOITCV

Galatians 4 in the BOKCV

Galatians 4 in the BOKCV2

Galatians 4 in the BOKHWOG

Galatians 4 in the BOKSSV

Galatians 4 in the BOLCB

Galatians 4 in the BOLCB2

Galatians 4 in the BOMCV

Galatians 4 in the BONAV

Galatians 4 in the BONCB

Galatians 4 in the BONLT

Galatians 4 in the BONUT2

Galatians 4 in the BOPLNT

Galatians 4 in the BOSCB

Galatians 4 in the BOSNC

Galatians 4 in the BOTLNT

Galatians 4 in the BOVCB

Galatians 4 in the BOYCB

Galatians 4 in the BPBB

Galatians 4 in the BPH

Galatians 4 in the BSB

Galatians 4 in the CCB

Galatians 4 in the CUV

Galatians 4 in the CUVS

Galatians 4 in the DBT

Galatians 4 in the DGDNT

Galatians 4 in the DHNT

Galatians 4 in the DNT

Galatians 4 in the ELBE

Galatians 4 in the EMTV

Galatians 4 in the ESV

Galatians 4 in the FBV

Galatians 4 in the FEB

Galatians 4 in the GGMNT

Galatians 4 in the GNT

Galatians 4 in the HARY

Galatians 4 in the HNT

Galatians 4 in the IRVA

Galatians 4 in the IRVB

Galatians 4 in the IRVG

Galatians 4 in the IRVH

Galatians 4 in the IRVK

Galatians 4 in the IRVM

Galatians 4 in the IRVM2

Galatians 4 in the IRVO

Galatians 4 in the IRVP

Galatians 4 in the IRVT

Galatians 4 in the IRVT2

Galatians 4 in the IRVU

Galatians 4 in the ISVN

Galatians 4 in the JSNT

Galatians 4 in the KAPI

Galatians 4 in the KBT1ETNIK

Galatians 4 in the KBV

Galatians 4 in the KJV

Galatians 4 in the KNFD

Galatians 4 in the LBA

Galatians 4 in the LBLA

Galatians 4 in the LNT

Galatians 4 in the LSV

Galatians 4 in the MAAL

Galatians 4 in the MBV

Galatians 4 in the MBV2

Galatians 4 in the MHNT

Galatians 4 in the MKNFD

Galatians 4 in the MNG

Galatians 4 in the MNT

Galatians 4 in the MNT2

Galatians 4 in the MRS1T

Galatians 4 in the NAA

Galatians 4 in the NASB

Galatians 4 in the NBLA

Galatians 4 in the NBS

Galatians 4 in the NBVTP

Galatians 4 in the NET2

Galatians 4 in the NIV11

Galatians 4 in the NNT

Galatians 4 in the NNT2

Galatians 4 in the NNT3

Galatians 4 in the PDDPT

Galatians 4 in the PFNT

Galatians 4 in the RMNT

Galatians 4 in the SBIAS

Galatians 4 in the SBIBS

Galatians 4 in the SBIBS2

Galatians 4 in the SBICS

Galatians 4 in the SBIDS

Galatians 4 in the SBIGS

Galatians 4 in the SBIHS

Galatians 4 in the SBIIS

Galatians 4 in the SBIIS2

Galatians 4 in the SBIIS3

Galatians 4 in the SBIKS

Galatians 4 in the SBIKS2

Galatians 4 in the SBIMS

Galatians 4 in the SBIOS

Galatians 4 in the SBIPS

Galatians 4 in the SBISS

Galatians 4 in the SBITS

Galatians 4 in the SBITS2

Galatians 4 in the SBITS3

Galatians 4 in the SBITS4

Galatians 4 in the SBIUS

Galatians 4 in the SBIVS

Galatians 4 in the SBT

Galatians 4 in the SBT1E

Galatians 4 in the SCHL

Galatians 4 in the SNT

Galatians 4 in the SUSU

Galatians 4 in the SUSU2

Galatians 4 in the SYNO

Galatians 4 in the TBIAOTANT

Galatians 4 in the TBT1E

Galatians 4 in the TBT1E2

Galatians 4 in the TFTIP

Galatians 4 in the TFTU

Galatians 4 in the TGNTATF3T

Galatians 4 in the THAI

Galatians 4 in the TNFD

Galatians 4 in the TNT

Galatians 4 in the TNTIK

Galatians 4 in the TNTIL

Galatians 4 in the TNTIN

Galatians 4 in the TNTIP

Galatians 4 in the TNTIZ

Galatians 4 in the TOMA

Galatians 4 in the TTENT

Galatians 4 in the UBG

Galatians 4 in the UGV

Galatians 4 in the UGV2

Galatians 4 in the UGV3

Galatians 4 in the VBL

Galatians 4 in the VDCC

Galatians 4 in the YALU

Galatians 4 in the YAPE

Galatians 4 in the YBVTP

Galatians 4 in the ZBP