Galatians 5 (BOGWICC)

1 Khristu anatimasula kuti tikhale mfulu. Tsono chirimikani, ndipo musakodwenso mʼgoli la ukapolo. 2 Chonde mvetsetsani! Ine Paulo, ndikukuwuzani kuti mukalola kuchita mdulidwe, Khristu simupindula nayenso konse. 3 Ndikubwerezanso kuwuza munthu aliyense wovomereza kuchita mdulidwe kuti ayeneranso kutsata Malamulo onse. 4 Inu amene mukufuna kulungamitsidwa ndi lamulo mwachotsedwa mwa Khristu; munagwa kusiyana nacho chisomo. 5 Koma mwachikhulupiriro, ife tikudikira mwachidwi kudzera mwa Mzimu, chilungamo chimene tikuyembekeza. 6 Pakuti mwa Khristu Yesu mdulidwe kapena kusachita mdulidwe zilibe phindu. Chinthu chokhacho chimene chimafunika ndi chikhulupiriro chogwira ntchito mwachikondi. 7 Inu munkathamanga mpikisano wanu wabwino. Anakuletsani ndani kuti musamverenso choonadi? 8 Kukopeka kwanu kumeneku sikuchokera kwa Iye amene anakuyitanani. 9 “Yisiti wapangʼono amagwira ntchito mu buledi yense.” 10 Ine ndikutsimikiza mwa Ambuye kuti inu simudzasiyana nane maganizo. Iye amene akukusokonezani adzalangidwa, kaya iyeyo ndiye ndani. 11 Abale, ngati ine ndikulalikirabe za mdulidwe, nʼchifukwa chiyani ndikusautsidwabe? Ngati ndikanakhala kuti sindikulalikira chipulumutso cha mtanda, palibe amene akanakhumudwa. 12 Kunena za amene akukuvutani, ndikanakonda akanangodzithena okha! 13 Inu abale, Mulungu anakuyitanani kuti mukhale mfulu. Koma musagwiritse ntchito ufulu wanuwo kuchita zoyipa zachikhalidwe cha uchimo cha thupi lanu, koma mutumikirane wina ndi mnzake mwachikondi. 14 Pakuti malamulo onse akuphatikizidwa mu lamulo ili, “Konda mnansi wako monga iwe mwini.” 15 Ngati mupitiriza kulumana ndi kukhadzulana, samalani kuti mungawonongane. 16 Choncho ine ndikuti, mulole kuti Mzimu akutsogolereni ndipo simudzachita zofuna za thupi lanu la uchimo. 17 Pakuti thupi lanu la uchimo limalakalaka zimene ndi zotsutsana ndi Mzimu, ndi Mzimu zimene ndi zotsutsana ndi thupi lanu la uchimo. Ziwirizi zimadana, kotero kuti simungachite zimene mukufuna. 18 Koma ngati Mzimu akutsogolerani, ndiye kuti simuli pansi pa lamulo. 19 Ntchito za thupi lanu la uchimo zimaonekera poyera ndi izi: dama, zodetsa ndi kuchita zonyansa; 20 kupembedza mafano ndi ufiti; kudana, kukangana, kupsa mtima, kudzikonda, kugawikana, mipatuko 21 ndi nsanje, kuledzera, mchezo ndi zina zotere. Ine ndikukuchenjezani monga ndinachita poyamba paja kuti amene amachita zimenezi sadzalandira ufumu wa Mulungu. 22 Koma chipatso cha Mzimu Woyera ndi chikondi, chimwemwe, mtendere, kuleza mtima, chifundo, kukoma mtima, kukhulupirika, 23 kufatsa ndi kudziretsa. Palibe lamulo loletsa zimenezi. 24 Amene ali ake a Khristu Yesu anapachika pa mtanda thupi lawo la uchimo pamodzi ndi zokhumba zawo ndi zolakalaka zawo. 25 Popeza timakhala ndi moyo mwa Mzimu Woyera, tiyeni tiyende pamodzi ndi Mzimu Woyera. 26 Tisakhale odzitukumula, oputana ndi ochitirana nsanje.

In Other Versions

Galatians 5 in the ANGEFD

Galatians 5 in the ANTPNG2D

Galatians 5 in the AS21

Galatians 5 in the BAGH

Galatians 5 in the BBPNG

Galatians 5 in the BBT1E

Galatians 5 in the BDS

Galatians 5 in the BEV

Galatians 5 in the BHAD

Galatians 5 in the BIB

Galatians 5 in the BLPT

Galatians 5 in the BNT

Galatians 5 in the BNTABOOT

Galatians 5 in the BNTLV

Galatians 5 in the BOATCB

Galatians 5 in the BOATCB2

Galatians 5 in the BOBCV

Galatians 5 in the BOCNT

Galatians 5 in the BOECS

Galatians 5 in the BOHCB

Galatians 5 in the BOHCV

Galatians 5 in the BOHLNT

Galatians 5 in the BOHNTLTAL

Galatians 5 in the BOICB

Galatians 5 in the BOILNTAP

Galatians 5 in the BOITCV

Galatians 5 in the BOKCV

Galatians 5 in the BOKCV2

Galatians 5 in the BOKHWOG

Galatians 5 in the BOKSSV

Galatians 5 in the BOLCB

Galatians 5 in the BOLCB2

Galatians 5 in the BOMCV

Galatians 5 in the BONAV

Galatians 5 in the BONCB

Galatians 5 in the BONLT

Galatians 5 in the BONUT2

Galatians 5 in the BOPLNT

Galatians 5 in the BOSCB

Galatians 5 in the BOSNC

Galatians 5 in the BOTLNT

Galatians 5 in the BOVCB

Galatians 5 in the BOYCB

Galatians 5 in the BPBB

Galatians 5 in the BPH

Galatians 5 in the BSB

Galatians 5 in the CCB

Galatians 5 in the CUV

Galatians 5 in the CUVS

Galatians 5 in the DBT

Galatians 5 in the DGDNT

Galatians 5 in the DHNT

Galatians 5 in the DNT

Galatians 5 in the ELBE

Galatians 5 in the EMTV

Galatians 5 in the ESV

Galatians 5 in the FBV

Galatians 5 in the FEB

Galatians 5 in the GGMNT

Galatians 5 in the GNT

Galatians 5 in the HARY

Galatians 5 in the HNT

Galatians 5 in the IRVA

Galatians 5 in the IRVB

Galatians 5 in the IRVG

Galatians 5 in the IRVH

Galatians 5 in the IRVK

Galatians 5 in the IRVM

Galatians 5 in the IRVM2

Galatians 5 in the IRVO

Galatians 5 in the IRVP

Galatians 5 in the IRVT

Galatians 5 in the IRVT2

Galatians 5 in the IRVU

Galatians 5 in the ISVN

Galatians 5 in the JSNT

Galatians 5 in the KAPI

Galatians 5 in the KBT1ETNIK

Galatians 5 in the KBV

Galatians 5 in the KJV

Galatians 5 in the KNFD

Galatians 5 in the LBA

Galatians 5 in the LBLA

Galatians 5 in the LNT

Galatians 5 in the LSV

Galatians 5 in the MAAL

Galatians 5 in the MBV

Galatians 5 in the MBV2

Galatians 5 in the MHNT

Galatians 5 in the MKNFD

Galatians 5 in the MNG

Galatians 5 in the MNT

Galatians 5 in the MNT2

Galatians 5 in the MRS1T

Galatians 5 in the NAA

Galatians 5 in the NASB

Galatians 5 in the NBLA

Galatians 5 in the NBS

Galatians 5 in the NBVTP

Galatians 5 in the NET2

Galatians 5 in the NIV11

Galatians 5 in the NNT

Galatians 5 in the NNT2

Galatians 5 in the NNT3

Galatians 5 in the PDDPT

Galatians 5 in the PFNT

Galatians 5 in the RMNT

Galatians 5 in the SBIAS

Galatians 5 in the SBIBS

Galatians 5 in the SBIBS2

Galatians 5 in the SBICS

Galatians 5 in the SBIDS

Galatians 5 in the SBIGS

Galatians 5 in the SBIHS

Galatians 5 in the SBIIS

Galatians 5 in the SBIIS2

Galatians 5 in the SBIIS3

Galatians 5 in the SBIKS

Galatians 5 in the SBIKS2

Galatians 5 in the SBIMS

Galatians 5 in the SBIOS

Galatians 5 in the SBIPS

Galatians 5 in the SBISS

Galatians 5 in the SBITS

Galatians 5 in the SBITS2

Galatians 5 in the SBITS3

Galatians 5 in the SBITS4

Galatians 5 in the SBIUS

Galatians 5 in the SBIVS

Galatians 5 in the SBT

Galatians 5 in the SBT1E

Galatians 5 in the SCHL

Galatians 5 in the SNT

Galatians 5 in the SUSU

Galatians 5 in the SUSU2

Galatians 5 in the SYNO

Galatians 5 in the TBIAOTANT

Galatians 5 in the TBT1E

Galatians 5 in the TBT1E2

Galatians 5 in the TFTIP

Galatians 5 in the TFTU

Galatians 5 in the TGNTATF3T

Galatians 5 in the THAI

Galatians 5 in the TNFD

Galatians 5 in the TNT

Galatians 5 in the TNTIK

Galatians 5 in the TNTIL

Galatians 5 in the TNTIN

Galatians 5 in the TNTIP

Galatians 5 in the TNTIZ

Galatians 5 in the TOMA

Galatians 5 in the TTENT

Galatians 5 in the UBG

Galatians 5 in the UGV

Galatians 5 in the UGV2

Galatians 5 in the UGV3

Galatians 5 in the VBL

Galatians 5 in the VDCC

Galatians 5 in the YALU

Galatians 5 in the YAPE

Galatians 5 in the YBVTP

Galatians 5 in the ZBP