Jeremiah 21 (BOGWICC)

1 Mfumu Zedekiya inatuma Pasuri mwana wa Malikiya ndi wansembe Zefaniya mwana wa Maseya kwa Yeremiya. 2 Iwo amati akanene kwa Yeremiya mawu akuti, “Tinenere kwa Yehova chifukwa Nebukadinezara mfumu ya Babuloni akutithira nkhondo. Mwina mwake Yehova nʼkutichitira zodabwitsa kuti Nebukadinezarayo achoke kwathu kuno.” 3 Koma Yehova anawuza Yeremiya kuti ayankhe Pasuri ndi Zefaniya kuti, “Kamuwuzeni Zedekiya kuti, 4 ‘Yehova, Mulungu wa Israeli akuti ndikulandeni zida zimene zili mʼmanja mwanu zimene mukugwiritsa ntchito polimbana ndi mfumu ya ku Babuloni ndi ankhondo ake amene akuzingani kunja kwa lingali. Ndipo ndidzasonkhanitsa zidazo mʼkati mwa mzindawu. 5 Ineyo mwini wakene ndi mkono wotambasula ndi dzanja lamphamvu, ndidzachita nanu nkhondo ndili wokwiya, wokalipa ndi waukali. 6 Ndidzakantha amene amakhala mu mzinda muno, anthu pamodzi ndi zirombo, ndipo zidzafa ndi mliri woopsa. 7 Pambuyo pake, ndidzapereka Zedekiya mfumu ya ku Yuda, nduna zake pamodzi ndi anthu a mu mzinda muno amene adzapulumuke pa nthawi ya mliri, lupanga ndi njala kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni ndi kwa adani awo amene ankafuna kuwapha. Iye adzawapha ndi lupanga. Sadzawachitira chifundo kapena kuwamvera chisoni kapenanso kuwakomera mtima.’ 8 “Yehova anati ndiwawuzenso anthu amenewa kuti asankhe pakati pa moyo ndi imfa. 9 Aliyense amene akhale mu mzinda muno adzaphedwa ndi lupanga, njala kapena mliri. Koma aliyense amene apite kukadzipereka kwa Ababuloni amene akuzinganiwa adzakhala ndi moyo, adzapulumuka. 10 Ine ndatsimikiza kuchitira mzinda uno choyipa osati chabwino, akutero Yehova. Udzaperekedwa mʼdzanja la mfumu ya ku Babuloni, ndipo iyeyo adzawutentha ndi moto. 11 “Komanso, uwuze banja laufumu la Yuda kuti, ‘Imva mawu a Yehova; 12 inu a mʼbanja la Davide, Yehova akuti,“ ‘Weruzani mwachilungamo mmawa uliwonse;pulumutsani mʼdzanja la wozunzaaliyense amene walandidwa katundu wake,kuopa kuti ukali wanga ungabukendi kuyaka ngati moto wosazimitsikachifukwa cha zoyipa zimene mwachita. 13 Ndidzalimbana nanu,inu amene mukukhala pamwamba pa chigwa,inu okhala ngati thanthwe lapachidikha,akutero Yehova.Inu amene mumanena kuti, ‘Ndani amene angabwere kudzalimbana nafe?Ndani amene angathe kulowa mʼmalinga mwathu?’ 14 Ndidzakulangani molingana ndi ntchito zanu,akutero Yehova.Ndidzatentha nkhalango zanu;moto udzapsereza zonse zimene zakuzungulirani.’ ”

In Other Versions

Jeremiah 21 in the ANGEFD

Jeremiah 21 in the ANTPNG2D

Jeremiah 21 in the AS21

Jeremiah 21 in the BAGH

Jeremiah 21 in the BBPNG

Jeremiah 21 in the BBT1E

Jeremiah 21 in the BDS

Jeremiah 21 in the BEV

Jeremiah 21 in the BHAD

Jeremiah 21 in the BIB

Jeremiah 21 in the BLPT

Jeremiah 21 in the BNT

Jeremiah 21 in the BNTABOOT

Jeremiah 21 in the BNTLV

Jeremiah 21 in the BOATCB

Jeremiah 21 in the BOATCB2

Jeremiah 21 in the BOBCV

Jeremiah 21 in the BOCNT

Jeremiah 21 in the BOECS

Jeremiah 21 in the BOHCB

Jeremiah 21 in the BOHCV

Jeremiah 21 in the BOHLNT

Jeremiah 21 in the BOHNTLTAL

Jeremiah 21 in the BOICB

Jeremiah 21 in the BOILNTAP

Jeremiah 21 in the BOITCV

Jeremiah 21 in the BOKCV

Jeremiah 21 in the BOKCV2

Jeremiah 21 in the BOKHWOG

Jeremiah 21 in the BOKSSV

Jeremiah 21 in the BOLCB

Jeremiah 21 in the BOLCB2

Jeremiah 21 in the BOMCV

Jeremiah 21 in the BONAV

Jeremiah 21 in the BONCB

Jeremiah 21 in the BONLT

Jeremiah 21 in the BONUT2

Jeremiah 21 in the BOPLNT

Jeremiah 21 in the BOSCB

Jeremiah 21 in the BOSNC

Jeremiah 21 in the BOTLNT

Jeremiah 21 in the BOVCB

Jeremiah 21 in the BOYCB

Jeremiah 21 in the BPBB

Jeremiah 21 in the BPH

Jeremiah 21 in the BSB

Jeremiah 21 in the CCB

Jeremiah 21 in the CUV

Jeremiah 21 in the CUVS

Jeremiah 21 in the DBT

Jeremiah 21 in the DGDNT

Jeremiah 21 in the DHNT

Jeremiah 21 in the DNT

Jeremiah 21 in the ELBE

Jeremiah 21 in the EMTV

Jeremiah 21 in the ESV

Jeremiah 21 in the FBV

Jeremiah 21 in the FEB

Jeremiah 21 in the GGMNT

Jeremiah 21 in the GNT

Jeremiah 21 in the HARY

Jeremiah 21 in the HNT

Jeremiah 21 in the IRVA

Jeremiah 21 in the IRVB

Jeremiah 21 in the IRVG

Jeremiah 21 in the IRVH

Jeremiah 21 in the IRVK

Jeremiah 21 in the IRVM

Jeremiah 21 in the IRVM2

Jeremiah 21 in the IRVO

Jeremiah 21 in the IRVP

Jeremiah 21 in the IRVT

Jeremiah 21 in the IRVT2

Jeremiah 21 in the IRVU

Jeremiah 21 in the ISVN

Jeremiah 21 in the JSNT

Jeremiah 21 in the KAPI

Jeremiah 21 in the KBT1ETNIK

Jeremiah 21 in the KBV

Jeremiah 21 in the KJV

Jeremiah 21 in the KNFD

Jeremiah 21 in the LBA

Jeremiah 21 in the LBLA

Jeremiah 21 in the LNT

Jeremiah 21 in the LSV

Jeremiah 21 in the MAAL

Jeremiah 21 in the MBV

Jeremiah 21 in the MBV2

Jeremiah 21 in the MHNT

Jeremiah 21 in the MKNFD

Jeremiah 21 in the MNG

Jeremiah 21 in the MNT

Jeremiah 21 in the MNT2

Jeremiah 21 in the MRS1T

Jeremiah 21 in the NAA

Jeremiah 21 in the NASB

Jeremiah 21 in the NBLA

Jeremiah 21 in the NBS

Jeremiah 21 in the NBVTP

Jeremiah 21 in the NET2

Jeremiah 21 in the NIV11

Jeremiah 21 in the NNT

Jeremiah 21 in the NNT2

Jeremiah 21 in the NNT3

Jeremiah 21 in the PDDPT

Jeremiah 21 in the PFNT

Jeremiah 21 in the RMNT

Jeremiah 21 in the SBIAS

Jeremiah 21 in the SBIBS

Jeremiah 21 in the SBIBS2

Jeremiah 21 in the SBICS

Jeremiah 21 in the SBIDS

Jeremiah 21 in the SBIGS

Jeremiah 21 in the SBIHS

Jeremiah 21 in the SBIIS

Jeremiah 21 in the SBIIS2

Jeremiah 21 in the SBIIS3

Jeremiah 21 in the SBIKS

Jeremiah 21 in the SBIKS2

Jeremiah 21 in the SBIMS

Jeremiah 21 in the SBIOS

Jeremiah 21 in the SBIPS

Jeremiah 21 in the SBISS

Jeremiah 21 in the SBITS

Jeremiah 21 in the SBITS2

Jeremiah 21 in the SBITS3

Jeremiah 21 in the SBITS4

Jeremiah 21 in the SBIUS

Jeremiah 21 in the SBIVS

Jeremiah 21 in the SBT

Jeremiah 21 in the SBT1E

Jeremiah 21 in the SCHL

Jeremiah 21 in the SNT

Jeremiah 21 in the SUSU

Jeremiah 21 in the SUSU2

Jeremiah 21 in the SYNO

Jeremiah 21 in the TBIAOTANT

Jeremiah 21 in the TBT1E

Jeremiah 21 in the TBT1E2

Jeremiah 21 in the TFTIP

Jeremiah 21 in the TFTU

Jeremiah 21 in the TGNTATF3T

Jeremiah 21 in the THAI

Jeremiah 21 in the TNFD

Jeremiah 21 in the TNT

Jeremiah 21 in the TNTIK

Jeremiah 21 in the TNTIL

Jeremiah 21 in the TNTIN

Jeremiah 21 in the TNTIP

Jeremiah 21 in the TNTIZ

Jeremiah 21 in the TOMA

Jeremiah 21 in the TTENT

Jeremiah 21 in the UBG

Jeremiah 21 in the UGV

Jeremiah 21 in the UGV2

Jeremiah 21 in the UGV3

Jeremiah 21 in the VBL

Jeremiah 21 in the VDCC

Jeremiah 21 in the YALU

Jeremiah 21 in the YAPE

Jeremiah 21 in the YBVTP

Jeremiah 21 in the ZBP