Leviticus 21 (BOGWICC)

1 Yehova anawuza Mose kuti, “Yankhula ndi ansembe, ana a Aaroni, ndipo uwawuze kuti, ‘Wansembe asadzidetse pokhudza munthu wakufa pakati pa abale ake. 2 Koma akhoza kukhudza thupi lakufa la amayi ake, abambo ake, mwana wake wamwamuna, mwana wake wamkazi, mchimwene wake, 3 kapena mlongo wake wosakwatiwa amene amadalira iye chifukwa sanakwatiwe. Iye akhoza kudzidetsa pokhudza thupi lakufa la mchemwali wake wosakwatiwa yekha. 4 Koma wansembe asadzidetse chifukwa cha anthu amene ali nawo pa ubale obwera chifukwa cha ukwati. 5 “ ‘Ansembe asamete tsitsi kumutu kwawo kapena mʼmphepete mwa ndevu zawo, kapenanso kudzichekacheka pa thupi lawo. 6 Ayenera kukhala oyera pamaso pa Mulungu wawo ndipo asachititse manyazi dzina la Mulungu wawo. Popeza amapereka nsembe zotentha pa moto kwa Yehova, chakudya cha Mulungu wawo, iwo azikhala woyera. 7 “ ‘Asakwatire akazi amene adzidetsa ndi chiwerewere kapena akazi amene amuna awo awasudzula, chifukwa ansembe ndi oyera pamaso pa Mulungu wawo. 8 Iwo akhale oyera chifukwa amapereka nsembe kwa Mulungu wanu. Muziwaona kuti ndi oyera, popeza Ine Yehova amene ndimawayeretsa ndine woyera, nawonso akhale oyera. 9 “ ‘Ngati mwana wamkazi wa wansembe adziyipitsa pochita zachiwerewere, ndiye kuti iye akuchititsa manyazi abambo ake; mwanayo atenthedwe pa moto. 10 “ ‘Munthu amene ali mkulu wa ansembe pakati pa abale ake, amene anamudzoza pomutsanulira mafuta pamutu pake, ndiponso amene anapatulidwa pomuveka zovala zaunsembe, asalekerere tsitsi lake kapena kungʼamba zovala zake kusonyeza kuti ali pa chisoni. 11 Asalowe mʼnyumba mmene muli munthu wakufa ngakhale womwalirayo ndi amayi ake kapena abambo ake. 12 Asadzidetse potulukira kunja kwa malo opatulika popeza mafuta womupatula kukhala wansembe ali pamutu pake. Ine ndine Yehova. 13 “ ‘Iye akwatire namwali wosadziwa mwamuna. 14 Asakwatire mkazi wamasiye, mkazi wosudzulidwa, kapena mkazi wachiwerewere, koma akwatire namwali wosadziwa mwamuna pakati pa anthu a mtundu wake, 15 kuti mtundu wake usakhale wodetsedwa pakati pa abale popeza ndine Yehova, amene ndimamuyeretsa.’ ” 16 Yehova anawuza Mose kuti, 17 “Muwuze Aaroni kuti, ‘Munthu aliyense mwa zidzukulu zake ku mibado yawo yonse ikubwera akakhala ndi chilema asabwere kudzapereka nsembe kwa Mulungu wake. 18 Munthu aliyense wachilema motere: munthu wakhungu kapena wolumala miyendo, munthu wolumala nkhope kapena waziwalo zambiri, 19 munthu wa phazi lolumala kapena dzanja lolumala, 20 kapena munthu wokhota msana kapena wamfupi kwambiri, kapena wolumala maso, munthu wa nthenda yonyerenyetsa, kapena wamphere, kapenanso wophwanyika mavalo, sayenera kusendera pafupi. 21 Mdzukulu aliyense wa Aaroni wansembe, amene ali ndi chilema asadzayandikire kukapereka nsembe zopsereza kwa Yehova. Popeza kuti ali ndi chilema, asayandikire kudzapereka nsembe ya chakudya kwa Mulungu wake. 22 Koma iye angathe kudya chakudya chopatulika kwambiri chija, ngakhalenso chakudya chotsala pa nsembe zopatulika. 23 Koma chifukwa cha kulumala kwake, sayenera kuyandikira katani kapena kufika pa guwa kuti angadetse malo anga wopatulika. Ine ndine Yehova, amene ndimawayeretsa.’ ” 24 Choncho Mose anawuza Aaroni ndi ana ake pamodzi ndi Aisraeli onse zimenezi.

In Other Versions

Leviticus 21 in the ANGEFD

Leviticus 21 in the ANTPNG2D

Leviticus 21 in the AS21

Leviticus 21 in the BAGH

Leviticus 21 in the BBPNG

Leviticus 21 in the BBT1E

Leviticus 21 in the BDS

Leviticus 21 in the BEV

Leviticus 21 in the BHAD

Leviticus 21 in the BIB

Leviticus 21 in the BLPT

Leviticus 21 in the BNT

Leviticus 21 in the BNTABOOT

Leviticus 21 in the BNTLV

Leviticus 21 in the BOATCB

Leviticus 21 in the BOATCB2

Leviticus 21 in the BOBCV

Leviticus 21 in the BOCNT

Leviticus 21 in the BOECS

Leviticus 21 in the BOHCB

Leviticus 21 in the BOHCV

Leviticus 21 in the BOHLNT

Leviticus 21 in the BOHNTLTAL

Leviticus 21 in the BOICB

Leviticus 21 in the BOILNTAP

Leviticus 21 in the BOITCV

Leviticus 21 in the BOKCV

Leviticus 21 in the BOKCV2

Leviticus 21 in the BOKHWOG

Leviticus 21 in the BOKSSV

Leviticus 21 in the BOLCB

Leviticus 21 in the BOLCB2

Leviticus 21 in the BOMCV

Leviticus 21 in the BONAV

Leviticus 21 in the BONCB

Leviticus 21 in the BONLT

Leviticus 21 in the BONUT2

Leviticus 21 in the BOPLNT

Leviticus 21 in the BOSCB

Leviticus 21 in the BOSNC

Leviticus 21 in the BOTLNT

Leviticus 21 in the BOVCB

Leviticus 21 in the BOYCB

Leviticus 21 in the BPBB

Leviticus 21 in the BPH

Leviticus 21 in the BSB

Leviticus 21 in the CCB

Leviticus 21 in the CUV

Leviticus 21 in the CUVS

Leviticus 21 in the DBT

Leviticus 21 in the DGDNT

Leviticus 21 in the DHNT

Leviticus 21 in the DNT

Leviticus 21 in the ELBE

Leviticus 21 in the EMTV

Leviticus 21 in the ESV

Leviticus 21 in the FBV

Leviticus 21 in the FEB

Leviticus 21 in the GGMNT

Leviticus 21 in the GNT

Leviticus 21 in the HARY

Leviticus 21 in the HNT

Leviticus 21 in the IRVA

Leviticus 21 in the IRVB

Leviticus 21 in the IRVG

Leviticus 21 in the IRVH

Leviticus 21 in the IRVK

Leviticus 21 in the IRVM

Leviticus 21 in the IRVM2

Leviticus 21 in the IRVO

Leviticus 21 in the IRVP

Leviticus 21 in the IRVT

Leviticus 21 in the IRVT2

Leviticus 21 in the IRVU

Leviticus 21 in the ISVN

Leviticus 21 in the JSNT

Leviticus 21 in the KAPI

Leviticus 21 in the KBT1ETNIK

Leviticus 21 in the KBV

Leviticus 21 in the KJV

Leviticus 21 in the KNFD

Leviticus 21 in the LBA

Leviticus 21 in the LBLA

Leviticus 21 in the LNT

Leviticus 21 in the LSV

Leviticus 21 in the MAAL

Leviticus 21 in the MBV

Leviticus 21 in the MBV2

Leviticus 21 in the MHNT

Leviticus 21 in the MKNFD

Leviticus 21 in the MNG

Leviticus 21 in the MNT

Leviticus 21 in the MNT2

Leviticus 21 in the MRS1T

Leviticus 21 in the NAA

Leviticus 21 in the NASB

Leviticus 21 in the NBLA

Leviticus 21 in the NBS

Leviticus 21 in the NBVTP

Leviticus 21 in the NET2

Leviticus 21 in the NIV11

Leviticus 21 in the NNT

Leviticus 21 in the NNT2

Leviticus 21 in the NNT3

Leviticus 21 in the PDDPT

Leviticus 21 in the PFNT

Leviticus 21 in the RMNT

Leviticus 21 in the SBIAS

Leviticus 21 in the SBIBS

Leviticus 21 in the SBIBS2

Leviticus 21 in the SBICS

Leviticus 21 in the SBIDS

Leviticus 21 in the SBIGS

Leviticus 21 in the SBIHS

Leviticus 21 in the SBIIS

Leviticus 21 in the SBIIS2

Leviticus 21 in the SBIIS3

Leviticus 21 in the SBIKS

Leviticus 21 in the SBIKS2

Leviticus 21 in the SBIMS

Leviticus 21 in the SBIOS

Leviticus 21 in the SBIPS

Leviticus 21 in the SBISS

Leviticus 21 in the SBITS

Leviticus 21 in the SBITS2

Leviticus 21 in the SBITS3

Leviticus 21 in the SBITS4

Leviticus 21 in the SBIUS

Leviticus 21 in the SBIVS

Leviticus 21 in the SBT

Leviticus 21 in the SBT1E

Leviticus 21 in the SCHL

Leviticus 21 in the SNT

Leviticus 21 in the SUSU

Leviticus 21 in the SUSU2

Leviticus 21 in the SYNO

Leviticus 21 in the TBIAOTANT

Leviticus 21 in the TBT1E

Leviticus 21 in the TBT1E2

Leviticus 21 in the TFTIP

Leviticus 21 in the TFTU

Leviticus 21 in the TGNTATF3T

Leviticus 21 in the THAI

Leviticus 21 in the TNFD

Leviticus 21 in the TNT

Leviticus 21 in the TNTIK

Leviticus 21 in the TNTIL

Leviticus 21 in the TNTIN

Leviticus 21 in the TNTIP

Leviticus 21 in the TNTIZ

Leviticus 21 in the TOMA

Leviticus 21 in the TTENT

Leviticus 21 in the UBG

Leviticus 21 in the UGV

Leviticus 21 in the UGV2

Leviticus 21 in the UGV3

Leviticus 21 in the VBL

Leviticus 21 in the VDCC

Leviticus 21 in the YALU

Leviticus 21 in the YAPE

Leviticus 21 in the YBVTP

Leviticus 21 in the ZBP