Micah 5 (BOGWICC)
1 Iwe mzinda wa anthu ankhondo, sonkhanitsa anthu ako ankhondo,pakuti anthu atizungulira kuti alimbane nafe.Adzakantha ndi ndodo pa chibwanocha wolamulira wa Israeli. 2 “Koma iwe Betelehemu Efurata,ngakhale uli wonyozeka pakati pa mafuko a Yuda,mwa iwe mudzatulukamunthu amene adzalamulira Israeli,amene chiyambi chake nʼchakalekale,nʼchamasiku amakedzana.” 3 Nʼchifukwa chake Israeli adzasiyidwampaka pa nthawi imene mayi amene ali woyembekezera adzachire.Ndipo abale ake onse otsalira adzabwererakudzakhala pamodzi ndi Aisraeli. 4 Iye adzalimbika, ndipo adzaweta nkhosa zakemwa mphamvu ya Yehova,mu ulemerero wa dzina la Yehova Mulungu wake.Ndipo iwo adzakhala mu mtendere,pakuti ukulu wake udzakhala ponseponse pa dziko lapansi. 5 Ndipo Iye adzakhala mtendere wawo.Asiriya akadzalowa mʼdziko lathundi kuyamba kuthira nkhondo malo athu otetezedwa,tidzawadzutsira abusa asanu ndi awiri,ngakhalenso atsogoleri asanu ndi atatu. 6 Iwo adzagonjetsa dziko la Asiriya ndi lupanga,dziko la Nimurodi adzalilamulira mwankhondo.Adzatipulumutsa kwa Asiriyaakadzafika mʼmalire a mʼdziko lathukudzatithira nkhondo. 7 Otsalira a Yakobo adzakhalapakati pa mitundu yambiri ya anthungati mame ochokera kwa Yehova,ngati mvumbi pa udzu,omwe sulamulidwa ndi munthukapena kudikira lamulo la anthu. 8 Otsala a Yakobo adzakhala pakati pa mitundu ya anthu,mʼgulu la anthu a mitundu yambiri,ngati mkango pakati pa nyama za mʼnkhalango.Ngati mwana wa mkango pakati pa gulu la nkhosa,amene pozidutsa amazidya ndi kuzikhadzula,ndipo palibe angathe kuzilanditsa. 9 Mudzagonjetsa adani anu,ndipo adani anu onse adzawonongeka. 10 Yehova akuti,“Tsiku limenelo ndidzawononga akavalo anu onsendi kuphwasula magaleta anu. 11 Ndidzawononga mizinda ya mʼdziko mwanundi kugwetsa malinga anu onse. 12 Ndidzawononga ufiti wanundipo sikudzakhalanso anthu owombeza mawula. 13 Ndidzawononga mafano anu osemapamodzi ndi miyala yanu yopatulika imene ili pakati panu;simudzagwadiranso zinthu zopangandi manja anu. 14 Ndidzazula mitengo ya mafano a Asera imene ili pakati panu,ndipo ndidzawononga mizinda yanu. 15 Ndidzayilanga mwaukali ndi mokwiyamitundu imene sinandimvere Ine.”
In Other Versions
Micah 5 in the ANGEFD
Micah 5 in the ANTPNG2D
Micah 5 in the AS21
Micah 5 in the BAGH
Micah 5 in the BBPNG
Micah 5 in the BBT1E
Micah 5 in the BDS
Micah 5 in the BEV
Micah 5 in the BHAD
Micah 5 in the BIB
Micah 5 in the BLPT
Micah 5 in the BNT
Micah 5 in the BNTABOOT
Micah 5 in the BNTLV
Micah 5 in the BOATCB
Micah 5 in the BOATCB2
Micah 5 in the BOBCV
Micah 5 in the BOCNT
Micah 5 in the BOECS
Micah 5 in the BOHCB
Micah 5 in the BOHCV
Micah 5 in the BOHLNT
Micah 5 in the BOHNTLTAL
Micah 5 in the BOICB
Micah 5 in the BOILNTAP
Micah 5 in the BOITCV
Micah 5 in the BOKCV
Micah 5 in the BOKCV2
Micah 5 in the BOKHWOG
Micah 5 in the BOKSSV
Micah 5 in the BOLCB
Micah 5 in the BOLCB2
Micah 5 in the BOMCV
Micah 5 in the BONAV
Micah 5 in the BONCB
Micah 5 in the BONLT
Micah 5 in the BONUT2
Micah 5 in the BOPLNT
Micah 5 in the BOSCB
Micah 5 in the BOSNC
Micah 5 in the BOTLNT
Micah 5 in the BOVCB
Micah 5 in the BOYCB
Micah 5 in the BPBB
Micah 5 in the BPH
Micah 5 in the BSB
Micah 5 in the CCB
Micah 5 in the CUV
Micah 5 in the CUVS
Micah 5 in the DBT
Micah 5 in the DGDNT
Micah 5 in the DHNT
Micah 5 in the DNT
Micah 5 in the ELBE
Micah 5 in the EMTV
Micah 5 in the ESV
Micah 5 in the FBV
Micah 5 in the FEB
Micah 5 in the GGMNT
Micah 5 in the GNT
Micah 5 in the HARY
Micah 5 in the HNT
Micah 5 in the IRVA
Micah 5 in the IRVB
Micah 5 in the IRVG
Micah 5 in the IRVH
Micah 5 in the IRVK
Micah 5 in the IRVM
Micah 5 in the IRVM2
Micah 5 in the IRVO
Micah 5 in the IRVP
Micah 5 in the IRVT
Micah 5 in the IRVT2
Micah 5 in the IRVU
Micah 5 in the ISVN
Micah 5 in the JSNT
Micah 5 in the KAPI
Micah 5 in the KBT1ETNIK
Micah 5 in the KBV
Micah 5 in the KJV
Micah 5 in the KNFD
Micah 5 in the LBA
Micah 5 in the LBLA
Micah 5 in the LNT
Micah 5 in the LSV
Micah 5 in the MAAL
Micah 5 in the MBV
Micah 5 in the MBV2
Micah 5 in the MHNT
Micah 5 in the MKNFD
Micah 5 in the MNG
Micah 5 in the MNT
Micah 5 in the MNT2
Micah 5 in the MRS1T
Micah 5 in the NAA
Micah 5 in the NASB
Micah 5 in the NBLA
Micah 5 in the NBS
Micah 5 in the NBVTP
Micah 5 in the NET2
Micah 5 in the NIV11
Micah 5 in the NNT
Micah 5 in the NNT2
Micah 5 in the NNT3
Micah 5 in the PDDPT
Micah 5 in the PFNT
Micah 5 in the RMNT
Micah 5 in the SBIAS
Micah 5 in the SBIBS
Micah 5 in the SBIBS2
Micah 5 in the SBICS
Micah 5 in the SBIDS
Micah 5 in the SBIGS
Micah 5 in the SBIHS
Micah 5 in the SBIIS
Micah 5 in the SBIIS2
Micah 5 in the SBIIS3
Micah 5 in the SBIKS
Micah 5 in the SBIKS2
Micah 5 in the SBIMS
Micah 5 in the SBIOS
Micah 5 in the SBIPS
Micah 5 in the SBISS
Micah 5 in the SBITS
Micah 5 in the SBITS2
Micah 5 in the SBITS3
Micah 5 in the SBITS4
Micah 5 in the SBIUS
Micah 5 in the SBIVS
Micah 5 in the SBT
Micah 5 in the SBT1E
Micah 5 in the SCHL
Micah 5 in the SNT
Micah 5 in the SUSU
Micah 5 in the SUSU2
Micah 5 in the SYNO
Micah 5 in the TBIAOTANT
Micah 5 in the TBT1E
Micah 5 in the TBT1E2
Micah 5 in the TFTIP
Micah 5 in the TFTU
Micah 5 in the TGNTATF3T
Micah 5 in the THAI
Micah 5 in the TNFD
Micah 5 in the TNT
Micah 5 in the TNTIK
Micah 5 in the TNTIL
Micah 5 in the TNTIN
Micah 5 in the TNTIP
Micah 5 in the TNTIZ
Micah 5 in the TOMA
Micah 5 in the TTENT
Micah 5 in the UBG
Micah 5 in the UGV
Micah 5 in the UGV2
Micah 5 in the UGV3
Micah 5 in the VBL
Micah 5 in the VDCC
Micah 5 in the YALU
Micah 5 in the YAPE
Micah 5 in the YBVTP
Micah 5 in the ZBP