Proverbs 17 (BOGWICC)

1 Nʼkwabwino kudya mkute koma pali mtendere,kuposa kuchita madyerero mʼnyumba mʼmene muli mikangano. 2 Kapolo wanzeru adzalamulira mwana wochititsa manyazi,ndipo kapoloyo adzagawana nawo cholowa ngati mmodzi mwa abale. 3 Siliva amamuyesa mʼngʼanjo ndipo golide amamuyesa mʼngʼanjo,koma Yehova amayesa mitima. 4 Munthu woyipa amamvera malangizo oyipa;munthu wabodza amatchera khutu mawu osakaza. 5 Iye amene amalalatira mʼmphawi amanyoza mlengi wake;amene amakondwerera tsoka la mnzake sadzakhala osalangidwa. 6 Zidzukulu ndiye ulemu wa anthu okalamba,ndipo makolo ndiye ulemerero wa ana. 7 Kuyankhula bwino sikuyenerana ndi chitsiru,nanji kuyankhula bodza kungayenerane kodi ndi mfumu? 8 Chiphuphu chili ngati mankhwala amwayi kwa wochiperekayo;kulikonse kumene amapita zinthu zimamuyendera. 9 Iye amene amakhululukira zolakwa za wina, amafunitsitsa chikondi;wobwerezabwereza nkhani amapha chibwenzi. 10 Munthu wanzeru amamva kamodzi kokha,munthu wopanda nzeru ndi samvamkunkhu. 11 Munthu woyipa maganizo ake ali pa kuwukira basi;ndipo bwana adzamutumizira wamthenga wankhanza. 12 Nʼkwabwino kukumana ndi chimbalangondo cholandidwa ana akekusiyana ndi kukumana ndi chitsiru mu uchitsiru wake. 13 Ngati munthu abwezera choyipa kusinthana ndi zabwino,ndiye choyipa sichidzachoka mʼnyumba mwake. 14 Chiyambi cha mikangano chili ngati kukhamulira madzi,choncho uzichokapo mkangano usanayambe. 15 Kumasula munthu wolakwa kapena kumanga munthu wosalakwa,zonse ziwirizi Yehova zimamunyansa. 16 Ndalama zogulira nzeru zili ndi phindu lanji mʼmanja mwa chitsirupoti iyeyo mutu wake sumayenda bwino? 17 Bwenzi lako limakukonda nthawi zonse,ndipo mʼbale wako anabadwa kuti azikuthandiza pamavuto. 18 Munthu wopanda nzeru amavomereza zopereka chikolendipo iyeyo amasanduka chikole cha mnansi wake. 19 Wokonda zolakwa amakonda mkangano,ndipo wokonda kuyankhula zonyada amadziyitanira chiwonongeko. 20 Munthu wamtima woyipa zinthu sizimuyendera bwino;ndipo woyankhula zachinyengo amagwa mʼmavuto. 21 Mwana wopusa amamvetsa chisoni abambo ake,abambo a chitsiru sakhala ndi chimwemwe. 22 Mtima wosangalala uli ngati mankhwala abwino,koma mtima wokhumudwa umafowoketsa mafupa. 23 Munthu woyipa amalandira chiphuphu chamserikuti apotoze chiweruzo cholungama. 24 Munthu wozindikira zinthu, maso ake amakhala pa nzeru,koma chitsiru chimwazamwaza maso ake pa dziko lonse lapansi. 25 Mwana wopusa amamvetsa chisoni abambo akendipo amapweteketsa mtima amayi ake. 26 Sibwino kulipitsa munthu wosalakwa,kapena kulanga anthu osalakwa. 27 Munthu wosunga pakamwa ndiye wodziwa zinthu,ndipo wodekha mtima ndiye womvetsa bwino zinthu. 28 Ngakhale chitsiru chimakhala ngati chanzeru chikakhala chete;ndipo chikatseka pakamwa chimakhala ngati munthu wochenjera.

In Other Versions

Proverbs 17 in the ANGEFD

Proverbs 17 in the ANTPNG2D

Proverbs 17 in the AS21

Proverbs 17 in the BAGH

Proverbs 17 in the BBPNG

Proverbs 17 in the BBT1E

Proverbs 17 in the BDS

Proverbs 17 in the BEV

Proverbs 17 in the BHAD

Proverbs 17 in the BIB

Proverbs 17 in the BLPT

Proverbs 17 in the BNT

Proverbs 17 in the BNTABOOT

Proverbs 17 in the BNTLV

Proverbs 17 in the BOATCB

Proverbs 17 in the BOATCB2

Proverbs 17 in the BOBCV

Proverbs 17 in the BOCNT

Proverbs 17 in the BOECS

Proverbs 17 in the BOHCB

Proverbs 17 in the BOHCV

Proverbs 17 in the BOHLNT

Proverbs 17 in the BOHNTLTAL

Proverbs 17 in the BOICB

Proverbs 17 in the BOILNTAP

Proverbs 17 in the BOITCV

Proverbs 17 in the BOKCV

Proverbs 17 in the BOKCV2

Proverbs 17 in the BOKHWOG

Proverbs 17 in the BOKSSV

Proverbs 17 in the BOLCB

Proverbs 17 in the BOLCB2

Proverbs 17 in the BOMCV

Proverbs 17 in the BONAV

Proverbs 17 in the BONCB

Proverbs 17 in the BONLT

Proverbs 17 in the BONUT2

Proverbs 17 in the BOPLNT

Proverbs 17 in the BOSCB

Proverbs 17 in the BOSNC

Proverbs 17 in the BOTLNT

Proverbs 17 in the BOVCB

Proverbs 17 in the BOYCB

Proverbs 17 in the BPBB

Proverbs 17 in the BPH

Proverbs 17 in the BSB

Proverbs 17 in the CCB

Proverbs 17 in the CUV

Proverbs 17 in the CUVS

Proverbs 17 in the DBT

Proverbs 17 in the DGDNT

Proverbs 17 in the DHNT

Proverbs 17 in the DNT

Proverbs 17 in the ELBE

Proverbs 17 in the EMTV

Proverbs 17 in the ESV

Proverbs 17 in the FBV

Proverbs 17 in the FEB

Proverbs 17 in the GGMNT

Proverbs 17 in the GNT

Proverbs 17 in the HARY

Proverbs 17 in the HNT

Proverbs 17 in the IRVA

Proverbs 17 in the IRVB

Proverbs 17 in the IRVG

Proverbs 17 in the IRVH

Proverbs 17 in the IRVK

Proverbs 17 in the IRVM

Proverbs 17 in the IRVM2

Proverbs 17 in the IRVO

Proverbs 17 in the IRVP

Proverbs 17 in the IRVT

Proverbs 17 in the IRVT2

Proverbs 17 in the IRVU

Proverbs 17 in the ISVN

Proverbs 17 in the JSNT

Proverbs 17 in the KAPI

Proverbs 17 in the KBT1ETNIK

Proverbs 17 in the KBV

Proverbs 17 in the KJV

Proverbs 17 in the KNFD

Proverbs 17 in the LBA

Proverbs 17 in the LBLA

Proverbs 17 in the LNT

Proverbs 17 in the LSV

Proverbs 17 in the MAAL

Proverbs 17 in the MBV

Proverbs 17 in the MBV2

Proverbs 17 in the MHNT

Proverbs 17 in the MKNFD

Proverbs 17 in the MNG

Proverbs 17 in the MNT

Proverbs 17 in the MNT2

Proverbs 17 in the MRS1T

Proverbs 17 in the NAA

Proverbs 17 in the NASB

Proverbs 17 in the NBLA

Proverbs 17 in the NBS

Proverbs 17 in the NBVTP

Proverbs 17 in the NET2

Proverbs 17 in the NIV11

Proverbs 17 in the NNT

Proverbs 17 in the NNT2

Proverbs 17 in the NNT3

Proverbs 17 in the PDDPT

Proverbs 17 in the PFNT

Proverbs 17 in the RMNT

Proverbs 17 in the SBIAS

Proverbs 17 in the SBIBS

Proverbs 17 in the SBIBS2

Proverbs 17 in the SBICS

Proverbs 17 in the SBIDS

Proverbs 17 in the SBIGS

Proverbs 17 in the SBIHS

Proverbs 17 in the SBIIS

Proverbs 17 in the SBIIS2

Proverbs 17 in the SBIIS3

Proverbs 17 in the SBIKS

Proverbs 17 in the SBIKS2

Proverbs 17 in the SBIMS

Proverbs 17 in the SBIOS

Proverbs 17 in the SBIPS

Proverbs 17 in the SBISS

Proverbs 17 in the SBITS

Proverbs 17 in the SBITS2

Proverbs 17 in the SBITS3

Proverbs 17 in the SBITS4

Proverbs 17 in the SBIUS

Proverbs 17 in the SBIVS

Proverbs 17 in the SBT

Proverbs 17 in the SBT1E

Proverbs 17 in the SCHL

Proverbs 17 in the SNT

Proverbs 17 in the SUSU

Proverbs 17 in the SUSU2

Proverbs 17 in the SYNO

Proverbs 17 in the TBIAOTANT

Proverbs 17 in the TBT1E

Proverbs 17 in the TBT1E2

Proverbs 17 in the TFTIP

Proverbs 17 in the TFTU

Proverbs 17 in the TGNTATF3T

Proverbs 17 in the THAI

Proverbs 17 in the TNFD

Proverbs 17 in the TNT

Proverbs 17 in the TNTIK

Proverbs 17 in the TNTIL

Proverbs 17 in the TNTIN

Proverbs 17 in the TNTIP

Proverbs 17 in the TNTIZ

Proverbs 17 in the TOMA

Proverbs 17 in the TTENT

Proverbs 17 in the UBG

Proverbs 17 in the UGV

Proverbs 17 in the UGV2

Proverbs 17 in the UGV3

Proverbs 17 in the VBL

Proverbs 17 in the VDCC

Proverbs 17 in the YALU

Proverbs 17 in the YAPE

Proverbs 17 in the YBVTP

Proverbs 17 in the ZBP