Proverbs 24 (BOGWICC)

1 Usachitire nsanje anthu oyipa,usalakalake kuti uzikhala nawo, 2 pakuti mitima yawo imalingalira chiwawa,ndipo pakamwa pawo pamayankhula zoyambitsa mavuto. 3 Nyumba imamangidwa ndi anthu anzeru,ndipo imakhazikika ndi anthu odziwa zinthu; 4 Munthu wodziwa zinthu angathe kudzaza zipinda zakendi chuma chamtengowapatali ndiponso chabwino. 5 Munthu wodziwa zinthu ali ndi mphamvu yayikulu kuposa munthu wanyonga zambiri,ndipo munthu wachidziwitso amaposa munthu wamphamvu. 6 Pafunika malangizo kuti ukamenye nkhondo.Pakakhala aphungu ambiri kupambana kumakhalapo. 7 Nzeru ndi chinthu chapatali kwambiri kwa chitsiru;chilibe choti chiyankhule pabwalo la milandu pa chipata. 8 Amene amakonzekera kuchita zoyipaadzatchedwa mvundulamadzi. 9 Kukonzekera kuchita za uchitsiru ndi tchimo,ndipo munthu wonyoza amanyansa anthu. 10 Ngati utaya mtima nthawi ya mavuto ndiye kutimphamvu yako ndi yochepadi! 11 Uwapulumutse amene akutengedwa kuti akaphedwe;uwalanditse amene akuyenda movutika kupita kokaphedwa. 12 Ukanena kuti, “Koma ife sitinadziwe kanthu za izi,”kodi Iye amene amasanthula mtima sazindikira zimenezi?Kodi Iye amene amateteza moyo wako sazidziwa zimenezi?Kodi Iye sadzalipira munthu malingana ndi ntchito zake? 13 Mwana wanga, uzidya uchi popeza ndi wabwino;uchi wochokera mʼchisa cha njuchi ndi wokoma ukawulawa. 14 Udziwe kuti nzeru ndi yoteronso pa moyo wako;ngati uyipeza nzeruyo, zinthu zidzakuyendera bwino mʼtsogolo,ndipo chiyembekezo chako sichidzapita pachabe. 15 Usachite zachifwamba nyumba ya munthu wolungama ngati munthu woyipa.Usachite nayo nkhondo nyumba yake; 16 paja munthu wolungama akagwa kasanu nʼkawiri amadzukiriranso.Koma woyipa adzathedwa tsoka likadzawafikira. 17 Usamakondwera ndi kugwa kwa mdani wako.Mtima wako usamasangalale iye akapunthwa. 18 Kuopa kuti Yehova ataziona zimenezi nayipidwa nazo,angaleke kukwiyira mdaniyo. 19 Usavutike mtima chifukwa cha anthu ochita zoyipakapena kuchitira nsanje anthu oyipa, 20 paja munthu woyipa alibe tsogolo.Moyo wa anthu oyipa adzawuzimitsa ngati nyale. 21 Mwana wanga, uziopa Yehova ndi mfumu,ndipo usamagwirizana ndi anthu owachitira mwano, 22 awiri amenewa amagwetsa tsoka mwadzidzidzi.Ndani angadziwe mavuto amene angagwetse? 23 Malangizo enanso a anthu anzeru ndi awa:Kukondera poweruza mlandu si chinthu chabwino: 24 Aliyense amene amawuza munthu wolakwa kuti, “Iwe ndi munthu wosalakwa,”anthu a mitundu yonse adzamutemberera, ndi mitundu ya anthu idzayipidwa naye. 25 Koma olanga anthu oyipa zinthu zidzawayendera bwinondipo madalitso ochuluka adzakhala pa iwo. 26 Woyankhula mawu owonandiye amaonetsa chibwenzi chenicheni. 27 Ugwiriretu ntchito zako zonse,makamaka za ku mundandipo pambuyo pake uyambe kumanga nyumba. 28 Usakhale mboni yotsutsa mnzako popanda chifukwa,kapena kugwiritsa ntchito pakamwa pako kunena zachinyengo. 29 Usanene kuti, “Ine ndidzamuchitira iye monga momwe wandichitira ine;ndidzamubwezera munthu ameneyo zimene anandichitira.” 30 Ndinkayenda mʼmbali mwa munda wa munthu waulesindinadutsa munda wamphesa wa munthu wopanda nzeru. 31 Ndinapeza kuti paliponse mʼmundamo munali mutamera minga,mʼnthaka imeneyo munali mutamera khwisa,ndipo mpanda wake wamiyala unali utawonongeka. 32 Tsono nditaona ndinayamba kuganizira mu mtima mwangandipo ndinatolapo phunziro ili: 33 Ukati, “Bwanji ndigone pangʼono,” kapena “Ndiwodzereko pangʼono,”kapenanso “Ndipinde manja pangʼono kuti ndipumule,” 34 umphawi udzafika pa iwe ngati mbalandipo usiwa udzakupeza ngati munthu wachifwamba.

In Other Versions

Proverbs 24 in the ANGEFD

Proverbs 24 in the ANTPNG2D

Proverbs 24 in the AS21

Proverbs 24 in the BAGH

Proverbs 24 in the BBPNG

Proverbs 24 in the BBT1E

Proverbs 24 in the BDS

Proverbs 24 in the BEV

Proverbs 24 in the BHAD

Proverbs 24 in the BIB

Proverbs 24 in the BLPT

Proverbs 24 in the BNT

Proverbs 24 in the BNTABOOT

Proverbs 24 in the BNTLV

Proverbs 24 in the BOATCB

Proverbs 24 in the BOATCB2

Proverbs 24 in the BOBCV

Proverbs 24 in the BOCNT

Proverbs 24 in the BOECS

Proverbs 24 in the BOHCB

Proverbs 24 in the BOHCV

Proverbs 24 in the BOHLNT

Proverbs 24 in the BOHNTLTAL

Proverbs 24 in the BOICB

Proverbs 24 in the BOILNTAP

Proverbs 24 in the BOITCV

Proverbs 24 in the BOKCV

Proverbs 24 in the BOKCV2

Proverbs 24 in the BOKHWOG

Proverbs 24 in the BOKSSV

Proverbs 24 in the BOLCB

Proverbs 24 in the BOLCB2

Proverbs 24 in the BOMCV

Proverbs 24 in the BONAV

Proverbs 24 in the BONCB

Proverbs 24 in the BONLT

Proverbs 24 in the BONUT2

Proverbs 24 in the BOPLNT

Proverbs 24 in the BOSCB

Proverbs 24 in the BOSNC

Proverbs 24 in the BOTLNT

Proverbs 24 in the BOVCB

Proverbs 24 in the BOYCB

Proverbs 24 in the BPBB

Proverbs 24 in the BPH

Proverbs 24 in the BSB

Proverbs 24 in the CCB

Proverbs 24 in the CUV

Proverbs 24 in the CUVS

Proverbs 24 in the DBT

Proverbs 24 in the DGDNT

Proverbs 24 in the DHNT

Proverbs 24 in the DNT

Proverbs 24 in the ELBE

Proverbs 24 in the EMTV

Proverbs 24 in the ESV

Proverbs 24 in the FBV

Proverbs 24 in the FEB

Proverbs 24 in the GGMNT

Proverbs 24 in the GNT

Proverbs 24 in the HARY

Proverbs 24 in the HNT

Proverbs 24 in the IRVA

Proverbs 24 in the IRVB

Proverbs 24 in the IRVG

Proverbs 24 in the IRVH

Proverbs 24 in the IRVK

Proverbs 24 in the IRVM

Proverbs 24 in the IRVM2

Proverbs 24 in the IRVO

Proverbs 24 in the IRVP

Proverbs 24 in the IRVT

Proverbs 24 in the IRVT2

Proverbs 24 in the IRVU

Proverbs 24 in the ISVN

Proverbs 24 in the JSNT

Proverbs 24 in the KAPI

Proverbs 24 in the KBT1ETNIK

Proverbs 24 in the KBV

Proverbs 24 in the KJV

Proverbs 24 in the KNFD

Proverbs 24 in the LBA

Proverbs 24 in the LBLA

Proverbs 24 in the LNT

Proverbs 24 in the LSV

Proverbs 24 in the MAAL

Proverbs 24 in the MBV

Proverbs 24 in the MBV2

Proverbs 24 in the MHNT

Proverbs 24 in the MKNFD

Proverbs 24 in the MNG

Proverbs 24 in the MNT

Proverbs 24 in the MNT2

Proverbs 24 in the MRS1T

Proverbs 24 in the NAA

Proverbs 24 in the NASB

Proverbs 24 in the NBLA

Proverbs 24 in the NBS

Proverbs 24 in the NBVTP

Proverbs 24 in the NET2

Proverbs 24 in the NIV11

Proverbs 24 in the NNT

Proverbs 24 in the NNT2

Proverbs 24 in the NNT3

Proverbs 24 in the PDDPT

Proverbs 24 in the PFNT

Proverbs 24 in the RMNT

Proverbs 24 in the SBIAS

Proverbs 24 in the SBIBS

Proverbs 24 in the SBIBS2

Proverbs 24 in the SBICS

Proverbs 24 in the SBIDS

Proverbs 24 in the SBIGS

Proverbs 24 in the SBIHS

Proverbs 24 in the SBIIS

Proverbs 24 in the SBIIS2

Proverbs 24 in the SBIIS3

Proverbs 24 in the SBIKS

Proverbs 24 in the SBIKS2

Proverbs 24 in the SBIMS

Proverbs 24 in the SBIOS

Proverbs 24 in the SBIPS

Proverbs 24 in the SBISS

Proverbs 24 in the SBITS

Proverbs 24 in the SBITS2

Proverbs 24 in the SBITS3

Proverbs 24 in the SBITS4

Proverbs 24 in the SBIUS

Proverbs 24 in the SBIVS

Proverbs 24 in the SBT

Proverbs 24 in the SBT1E

Proverbs 24 in the SCHL

Proverbs 24 in the SNT

Proverbs 24 in the SUSU

Proverbs 24 in the SUSU2

Proverbs 24 in the SYNO

Proverbs 24 in the TBIAOTANT

Proverbs 24 in the TBT1E

Proverbs 24 in the TBT1E2

Proverbs 24 in the TFTIP

Proverbs 24 in the TFTU

Proverbs 24 in the TGNTATF3T

Proverbs 24 in the THAI

Proverbs 24 in the TNFD

Proverbs 24 in the TNT

Proverbs 24 in the TNTIK

Proverbs 24 in the TNTIL

Proverbs 24 in the TNTIN

Proverbs 24 in the TNTIP

Proverbs 24 in the TNTIZ

Proverbs 24 in the TOMA

Proverbs 24 in the TTENT

Proverbs 24 in the UBG

Proverbs 24 in the UGV

Proverbs 24 in the UGV2

Proverbs 24 in the UGV3

Proverbs 24 in the VBL

Proverbs 24 in the VDCC

Proverbs 24 in the YALU

Proverbs 24 in the YAPE

Proverbs 24 in the YBVTP

Proverbs 24 in the ZBP