Revelation 14 (BOGWICC)

1 Kenaka ndinaona patsogolo panga panali Mwana Wankhosa, atayimirira pa Phiri la Ziyoni, ndipo Iye anali pamodzi ndi anthu 144,000 amene pa mphumi pawo panalembedwa dzina la Mwana Wankhosayo ndi la Atate ake. 2 Ndipo ndinamva liwu lochokera kumwamba ngati mkokomo wa madzi ambiri, ndiponso ngati kugunda kwamphamvu kwa bingu. Liwu limene ndinamvalo linali ngati a anthu akuyimba azeze awo. 3 Anthuwo ankayimba nyimbo yatsopano patsogolo pa mpando waufumu ndi zamoyo zinayi zija ndi akuluakulu aja. Palibe ndi mmodzi yemwe amene anatha kuphunzira nyimboyo kupatula anthu 144,000 aja amene anawomboledwa pa dziko lapansi. 4 Awa ndiwo amene sanadzidetse koma anadzisunga ndipo sanadziyipitse ndi akazi. Anthu amenewa ndiwo ankatsatira Mwana Wankhosa kulikonse kumene ankapita. Ndiwo amene anagulidwa pakati pa anthu a dziko lapansi kuti akhale oyambirira kuperekedwa kwa Mulungu ndi kwa Mwana Wankhosa. 5 Iwo sananenepo bodza ndipo alibe cholakwa. 6 Kenaka ndinaona mngelo wina akuwuluka mu mlengalenga ndipo anali ndi Uthenga Wabwino wamuyaya woti akalalikire kwa anthu okhala pa dziko lapansi, kwa a mtundu uliwonse, a fuko lililonse, a chiyankhulo chilichonse ndi kwa anthu onse. 7 Mngeloyo anayankhula mokweza mawu kuti, “Wopani Mulungu ndi kumutamanda, chifukwa nthawi yoweruza anthu yafika. Mumupembedze Iye amene analenga thambo, dziko lapansi, nyanja ndi akasupe amadzi.” 8 Mngelo wachiwiri anatsatana naye ndipo anati, “Wagwa! Wagwa Babuloni womveka uja, amene anachititsa anthu a mitundu yonse kumwa vinyo wa zilakolako zake zachigololo.” 9 Mngelo wachitatu anatsatana nawo ndi mawu ofuwula anati, “Ngati wina apembedza chirombo chija ndi fano lake ndi kulembedwa chizindikiro pa mphumi kapena pa dzanja, 10 nayenso adzamwa vinyo waukali wa Mulungu, umene wathiridwa popanda kuchepetsa mphamvu zake mʼchikho cha ukali wa Mulungu. Munthuyo adzazunzidwa ndi moto wamiyala yasulufure pamaso pa angelo oyera ndi pa Mwana Wankhosa. 11 Ndipo utsi wa moto wowazunzawo udzakwera kumwamba mpaka muyaya. Sikudzakhala kupumula usana ndi usiku kwa amene anapembedza chirombo chija ndi fano lake kapena kwa aliyense amene analembedwa chizindikiro cha dzina lake lija.” 12 Pamenepa ndi pofunika kupirira kwa anthu oyera mtima amene amasunga malamulo a Mulungu ndi kukhalabe okhulupirika kwa Yesu. 13 Kenaka ndinamva mawu kuchokera kumwamba akuti, “Lemba kuti, Odala anthu amene akufa ali mwa Ambuye kuyambira tsopano mpaka mʼtsogolo.”“Inde,” akutero Mzimu, “akapumule ntchito zawo zotopetsa pakuti ntchito zawo zidzawatsata.” 14 Ndinayangʼana patsogolo panga ndinaona mtambo woyera patakhalapo wina ngati Mwana wa Munthu, kumutu atavala chipewa chaufumu chagolide ndipo mʼdzanja mwake munali chikwakwa chakunthwa. 15 Tsono mngelo wina anatuluka mʼNyumba ya Mulungu nafuwula mwamphamvu kwa uja wokhala pa mtamboyu. Mngeloyo anati, “Tenga chikwakwa chako ndipo kolola, pakuti nthawi yokolola ya dziko la pansi yakwana” 16 Choncho wokhala pa mtambo uja anayamba kukolola dzinthu pa dziko lapansi ndi chikwakwa chakecho. 17 Mngelo wina anatuluka mʼNyumba ya Mulungu kumwamba ndipo nayenso anali ndi chikwakwa chakunthwa. 18 Kenaka mngelo winanso amene amalamulira moto, anatuluka kuchokera ku guwa lansembe nayitana mwamphamvu mngelo uja amene anali ndi chikwakwa chakunthwa chija, nati, “Tenga chikwakwa chako chakunthwacho yamba kudula mphesa za mʼmunda wamphesa wa pa dziko lapansi, pakuti mphesa zapsa kale.” 19 Pamenepo mngeloyo anayambadi kugwiritsa ntchito chikwakwa chake nadula mphesa za dziko lapansi, naziponya mʼchopondera mphesa chachikulu cha ukali woopsa wa Mulungu. 20 Mphesazo zinapondedwa mʼchopondera mphesa kunja kwa mzinda. Mʼchopondera mphesamo munatuluka magazi amene anayenderera ngati mtsinje, kuzama kwake mita ndi theka ndipo kutalika kwake makilomita 300.

In Other Versions

Revelation 14 in the ANGEFD

Revelation 14 in the ANTPNG2D

Revelation 14 in the AS21

Revelation 14 in the BAGH

Revelation 14 in the BBPNG

Revelation 14 in the BBT1E

Revelation 14 in the BDS

Revelation 14 in the BEV

Revelation 14 in the BHAD

Revelation 14 in the BIB

Revelation 14 in the BLPT

Revelation 14 in the BNT

Revelation 14 in the BNTABOOT

Revelation 14 in the BNTLV

Revelation 14 in the BOATCB

Revelation 14 in the BOATCB2

Revelation 14 in the BOBCV

Revelation 14 in the BOCNT

Revelation 14 in the BOECS

Revelation 14 in the BOHCB

Revelation 14 in the BOHCV

Revelation 14 in the BOHLNT

Revelation 14 in the BOHNTLTAL

Revelation 14 in the BOICB

Revelation 14 in the BOILNTAP

Revelation 14 in the BOITCV

Revelation 14 in the BOKCV

Revelation 14 in the BOKCV2

Revelation 14 in the BOKHWOG

Revelation 14 in the BOKSSV

Revelation 14 in the BOLCB

Revelation 14 in the BOLCB2

Revelation 14 in the BOMCV

Revelation 14 in the BONAV

Revelation 14 in the BONCB

Revelation 14 in the BONLT

Revelation 14 in the BONUT2

Revelation 14 in the BOPLNT

Revelation 14 in the BOSCB

Revelation 14 in the BOSNC

Revelation 14 in the BOTLNT

Revelation 14 in the BOVCB

Revelation 14 in the BOYCB

Revelation 14 in the BPBB

Revelation 14 in the BPH

Revelation 14 in the BSB

Revelation 14 in the CCB

Revelation 14 in the CUV

Revelation 14 in the CUVS

Revelation 14 in the DBT

Revelation 14 in the DGDNT

Revelation 14 in the DHNT

Revelation 14 in the DNT

Revelation 14 in the ELBE

Revelation 14 in the EMTV

Revelation 14 in the ESV

Revelation 14 in the FBV

Revelation 14 in the FEB

Revelation 14 in the GGMNT

Revelation 14 in the GNT

Revelation 14 in the HARY

Revelation 14 in the HNT

Revelation 14 in the IRVA

Revelation 14 in the IRVB

Revelation 14 in the IRVG

Revelation 14 in the IRVH

Revelation 14 in the IRVK

Revelation 14 in the IRVM

Revelation 14 in the IRVM2

Revelation 14 in the IRVO

Revelation 14 in the IRVP

Revelation 14 in the IRVT

Revelation 14 in the IRVT2

Revelation 14 in the IRVU

Revelation 14 in the ISVN

Revelation 14 in the JSNT

Revelation 14 in the KAPI

Revelation 14 in the KBT1ETNIK

Revelation 14 in the KBV

Revelation 14 in the KJV

Revelation 14 in the KNFD

Revelation 14 in the LBA

Revelation 14 in the LBLA

Revelation 14 in the LNT

Revelation 14 in the LSV

Revelation 14 in the MAAL

Revelation 14 in the MBV

Revelation 14 in the MBV2

Revelation 14 in the MHNT

Revelation 14 in the MKNFD

Revelation 14 in the MNG

Revelation 14 in the MNT

Revelation 14 in the MNT2

Revelation 14 in the MRS1T

Revelation 14 in the NAA

Revelation 14 in the NASB

Revelation 14 in the NBLA

Revelation 14 in the NBS

Revelation 14 in the NBVTP

Revelation 14 in the NET2

Revelation 14 in the NIV11

Revelation 14 in the NNT

Revelation 14 in the NNT2

Revelation 14 in the NNT3

Revelation 14 in the PDDPT

Revelation 14 in the PFNT

Revelation 14 in the RMNT

Revelation 14 in the SBIAS

Revelation 14 in the SBIBS

Revelation 14 in the SBIBS2

Revelation 14 in the SBICS

Revelation 14 in the SBIDS

Revelation 14 in the SBIGS

Revelation 14 in the SBIHS

Revelation 14 in the SBIIS

Revelation 14 in the SBIIS2

Revelation 14 in the SBIIS3

Revelation 14 in the SBIKS

Revelation 14 in the SBIKS2

Revelation 14 in the SBIMS

Revelation 14 in the SBIOS

Revelation 14 in the SBIPS

Revelation 14 in the SBISS

Revelation 14 in the SBITS

Revelation 14 in the SBITS2

Revelation 14 in the SBITS3

Revelation 14 in the SBITS4

Revelation 14 in the SBIUS

Revelation 14 in the SBIVS

Revelation 14 in the SBT

Revelation 14 in the SBT1E

Revelation 14 in the SCHL

Revelation 14 in the SNT

Revelation 14 in the SUSU

Revelation 14 in the SUSU2

Revelation 14 in the SYNO

Revelation 14 in the TBIAOTANT

Revelation 14 in the TBT1E

Revelation 14 in the TBT1E2

Revelation 14 in the TFTIP

Revelation 14 in the TFTU

Revelation 14 in the TGNTATF3T

Revelation 14 in the THAI

Revelation 14 in the TNFD

Revelation 14 in the TNT

Revelation 14 in the TNTIK

Revelation 14 in the TNTIL

Revelation 14 in the TNTIN

Revelation 14 in the TNTIP

Revelation 14 in the TNTIZ

Revelation 14 in the TOMA

Revelation 14 in the TTENT

Revelation 14 in the UBG

Revelation 14 in the UGV

Revelation 14 in the UGV2

Revelation 14 in the UGV3

Revelation 14 in the VBL

Revelation 14 in the VDCC

Revelation 14 in the YALU

Revelation 14 in the YAPE

Revelation 14 in the YBVTP

Revelation 14 in the ZBP