Deuteronomy 25 (BOGWICC)

1 Anthu akasemphana mawu, ayenera kupita ku bwalo la milandu ndipo woweruza adzaweruza mlanduwo. Adzamasula wosalakwa nalanga wolakwa. 2 Munthu akapezeka wolakwa ayenera kukwapulidwa, woweruza amugoneke pansi wolakwayo ndipo akwapulidwe pamaso pake zikoti zochuluka molingana ndi mlandu wake, 3 koma asamukwapule zikoti zopitirira makumi anayi. Akakwapulidwa kupitirira apo ndiye kuti mʼbale wanuyo anyozeka pamaso panu. 4 Musamange ngʼombe pakamwa pamene ikupuntha tirigu. 5 Ngati abale akukhala pamodzi ndipo wina mwa iwo akamwalira wosasiya mwana wamwamuna, mkazi wamasiyeyo asakakwatiwe ndi mlendo. Mʼbale wake wa mwamuna wakeyo amukwatire kukwaniritsa chimene akuyenera kuchita kwa mlamu wakeyo. 6 Mwana wamwamuna woyamba amene mayiyo angabereke ayenera kutenga dzina la mwamuna wake womwalirayo kuti dzina lake lisafafanizike mu Israeli. 7 Komabe, ngati munthu sakufuna kukwatira mkazi wa mʼbale wakeyo, mkaziyo ayenera kupita kwa akuluakulu ku chipata cha mzinda ndi kukanena kuti, “Mʼbale wake wa mwamuna wanga akukana kupitiriza dzina la mʼbale wake mu Israeli. Iye akukana kulowa chokolo.” 8 Pamenepo akuluakulu a mu mzinda wawowo adzamuyitanitsa nakamba naye. Ngati alimbikirabe kunena kuti, “Ine sindikufuna kumukwatira mkaziyu,” 9 mkazi wamasiye wa mʼbale wakeyo adzapita kwa iye pamaso pa akuluakuluwo namuvula nsapato imodzi, adzamulavulire kumaso nʼkunena kuti, “Izi ndi zimene amachitira munthu amene safuna kupitiriza mbiri ya banja la mʼbale wake.” 10 Mbiri ya banja la munthu ameneyo idzadziwika mu Israeli kuti ndi Banja la Wovulidwa nsapato. 11 Ngati anthu awiri akuchita ndewu ndipo mkazi wa mmodzi wa iwo abwera kudzaleretsa mwamuna wake kwa mnzakeyo natambasula dzanja lake kugwira ku maliseche kwa winayo, 12 muyenera kumudula dzanja, osamumvera chisoni. 13 Musamakhale ndi miyeso iwiri yosiyana mʼthumba mwanu, wolemera ndi wopepuka. 14 Musamakhale ndi milingo iwiri yosiyana mʼnyumba mwanu, waukulu ndi waungʼono. 15 Muyenera kukhala ndi miyeso ndi milingo yoyenera ndi yosanyenga kuti mukhalitse mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani. 16 Pakuti Yehova Mulungu wanu amanyansidwa ndi aliyense wochita za chinyengo zoterezi. 17 Kumbukirani zimene Aamaleki anakuchitirani pamene munali pa ulendo wochokera ku Igupto. 18 Pamene munali otopa ndi ofowoka, iwo anakumana nanu pa ulendo wanu ndi kukantha onse otsalira mʼmbuyo ndipo iwo sanaope Mulungu. 19 Pamene Yehova Mulungu wanu akupumulitsani kwa adani onse okuzungulirani mʼdziko limene akupatsani inu ngati cholowa chanu, mudzawafafanize Aamaleki, asadzawakumbukirenso pa dziko lapansi. Musadzayiwale chimenechi!

In Other Versions

Deuteronomy 25 in the ANGEFD

Deuteronomy 25 in the ANTPNG2D

Deuteronomy 25 in the AS21

Deuteronomy 25 in the BAGH

Deuteronomy 25 in the BBPNG

Deuteronomy 25 in the BBT1E

Deuteronomy 25 in the BDS

Deuteronomy 25 in the BEV

Deuteronomy 25 in the BHAD

Deuteronomy 25 in the BIB

Deuteronomy 25 in the BLPT

Deuteronomy 25 in the BNT

Deuteronomy 25 in the BNTABOOT

Deuteronomy 25 in the BNTLV

Deuteronomy 25 in the BOATCB

Deuteronomy 25 in the BOATCB2

Deuteronomy 25 in the BOBCV

Deuteronomy 25 in the BOCNT

Deuteronomy 25 in the BOECS

Deuteronomy 25 in the BOHCB

Deuteronomy 25 in the BOHCV

Deuteronomy 25 in the BOHLNT

Deuteronomy 25 in the BOHNTLTAL

Deuteronomy 25 in the BOICB

Deuteronomy 25 in the BOILNTAP

Deuteronomy 25 in the BOITCV

Deuteronomy 25 in the BOKCV

Deuteronomy 25 in the BOKCV2

Deuteronomy 25 in the BOKHWOG

Deuteronomy 25 in the BOKSSV

Deuteronomy 25 in the BOLCB

Deuteronomy 25 in the BOLCB2

Deuteronomy 25 in the BOMCV

Deuteronomy 25 in the BONAV

Deuteronomy 25 in the BONCB

Deuteronomy 25 in the BONLT

Deuteronomy 25 in the BONUT2

Deuteronomy 25 in the BOPLNT

Deuteronomy 25 in the BOSCB

Deuteronomy 25 in the BOSNC

Deuteronomy 25 in the BOTLNT

Deuteronomy 25 in the BOVCB

Deuteronomy 25 in the BOYCB

Deuteronomy 25 in the BPBB

Deuteronomy 25 in the BPH

Deuteronomy 25 in the BSB

Deuteronomy 25 in the CCB

Deuteronomy 25 in the CUV

Deuteronomy 25 in the CUVS

Deuteronomy 25 in the DBT

Deuteronomy 25 in the DGDNT

Deuteronomy 25 in the DHNT

Deuteronomy 25 in the DNT

Deuteronomy 25 in the ELBE

Deuteronomy 25 in the EMTV

Deuteronomy 25 in the ESV

Deuteronomy 25 in the FBV

Deuteronomy 25 in the FEB

Deuteronomy 25 in the GGMNT

Deuteronomy 25 in the GNT

Deuteronomy 25 in the HARY

Deuteronomy 25 in the HNT

Deuteronomy 25 in the IRVA

Deuteronomy 25 in the IRVB

Deuteronomy 25 in the IRVG

Deuteronomy 25 in the IRVH

Deuteronomy 25 in the IRVK

Deuteronomy 25 in the IRVM

Deuteronomy 25 in the IRVM2

Deuteronomy 25 in the IRVO

Deuteronomy 25 in the IRVP

Deuteronomy 25 in the IRVT

Deuteronomy 25 in the IRVT2

Deuteronomy 25 in the IRVU

Deuteronomy 25 in the ISVN

Deuteronomy 25 in the JSNT

Deuteronomy 25 in the KAPI

Deuteronomy 25 in the KBT1ETNIK

Deuteronomy 25 in the KBV

Deuteronomy 25 in the KJV

Deuteronomy 25 in the KNFD

Deuteronomy 25 in the LBA

Deuteronomy 25 in the LBLA

Deuteronomy 25 in the LNT

Deuteronomy 25 in the LSV

Deuteronomy 25 in the MAAL

Deuteronomy 25 in the MBV

Deuteronomy 25 in the MBV2

Deuteronomy 25 in the MHNT

Deuteronomy 25 in the MKNFD

Deuteronomy 25 in the MNG

Deuteronomy 25 in the MNT

Deuteronomy 25 in the MNT2

Deuteronomy 25 in the MRS1T

Deuteronomy 25 in the NAA

Deuteronomy 25 in the NASB

Deuteronomy 25 in the NBLA

Deuteronomy 25 in the NBS

Deuteronomy 25 in the NBVTP

Deuteronomy 25 in the NET2

Deuteronomy 25 in the NIV11

Deuteronomy 25 in the NNT

Deuteronomy 25 in the NNT2

Deuteronomy 25 in the NNT3

Deuteronomy 25 in the PDDPT

Deuteronomy 25 in the PFNT

Deuteronomy 25 in the RMNT

Deuteronomy 25 in the SBIAS

Deuteronomy 25 in the SBIBS

Deuteronomy 25 in the SBIBS2

Deuteronomy 25 in the SBICS

Deuteronomy 25 in the SBIDS

Deuteronomy 25 in the SBIGS

Deuteronomy 25 in the SBIHS

Deuteronomy 25 in the SBIIS

Deuteronomy 25 in the SBIIS2

Deuteronomy 25 in the SBIIS3

Deuteronomy 25 in the SBIKS

Deuteronomy 25 in the SBIKS2

Deuteronomy 25 in the SBIMS

Deuteronomy 25 in the SBIOS

Deuteronomy 25 in the SBIPS

Deuteronomy 25 in the SBISS

Deuteronomy 25 in the SBITS

Deuteronomy 25 in the SBITS2

Deuteronomy 25 in the SBITS3

Deuteronomy 25 in the SBITS4

Deuteronomy 25 in the SBIUS

Deuteronomy 25 in the SBIVS

Deuteronomy 25 in the SBT

Deuteronomy 25 in the SBT1E

Deuteronomy 25 in the SCHL

Deuteronomy 25 in the SNT

Deuteronomy 25 in the SUSU

Deuteronomy 25 in the SUSU2

Deuteronomy 25 in the SYNO

Deuteronomy 25 in the TBIAOTANT

Deuteronomy 25 in the TBT1E

Deuteronomy 25 in the TBT1E2

Deuteronomy 25 in the TFTIP

Deuteronomy 25 in the TFTU

Deuteronomy 25 in the TGNTATF3T

Deuteronomy 25 in the THAI

Deuteronomy 25 in the TNFD

Deuteronomy 25 in the TNT

Deuteronomy 25 in the TNTIK

Deuteronomy 25 in the TNTIL

Deuteronomy 25 in the TNTIN

Deuteronomy 25 in the TNTIP

Deuteronomy 25 in the TNTIZ

Deuteronomy 25 in the TOMA

Deuteronomy 25 in the TTENT

Deuteronomy 25 in the UBG

Deuteronomy 25 in the UGV

Deuteronomy 25 in the UGV2

Deuteronomy 25 in the UGV3

Deuteronomy 25 in the VBL

Deuteronomy 25 in the VDCC

Deuteronomy 25 in the YALU

Deuteronomy 25 in the YAPE

Deuteronomy 25 in the YBVTP

Deuteronomy 25 in the ZBP