Genesis 4 (BOGWICC)

1 Adamu anagona malo amodzi ndi Hava mkazi wake ndipo mkaziyo anakhala woyembekezera nabala Kaini, ndipo anati, “Ndi thandizo la Yehova ndapeza mwana wamwamuna.” 2 Kenaka anabereka mʼbale wake Abele.Abele anali woweta nkhosa ndipo Kaini anali mlimi. 3 Patapita nthawi, Kaini anatenga zipatso za ku munda nakazipereka kwa Yehova monga nsembe. 4 Nayenso Abele anatenga ana ankhosa oyamba kubadwa pamodzi ndi mafuta ake nakazipereka ngati nsembe kwa Yehova. Yehova anakondwera ndi Abele ndi nsembe yake. 5 Koma sanakondwere ndi Kaini ndi nsembe yake. Kotero Kaini anakwiya kwambiri ndipo nkhope yake inagwa. 6 Choncho Yehova anati kwa Kaini, “Chifukwa chiyani wakwiya ndipo bwanji nkhope yako yagwa? 7 Ukanachita zabwino sindikanakulandira kodi? Koma tsopano wachita zoyipa ndipo tchimo likukudikira pa khomo pako, likufuna kukugwira; koma iwe uyenera kugonjetsa tchimolo.” 8 Tsiku lina Kaini anati kwa mʼbale wake Abele, “Tiye tipite ku munda.” Ndipo ali ku mundako, Kaini anawukira mʼbale wake namupha. 9 Ndipo Yehova anamufunsa Kaini kuti, “Ali kuti mʼbale wako Abele?”Iye anayankha kuti, “Sindikudziwa. Kodi ine ndine wosunga mʼbale wanga?” 10 Yehova anati, “Kodi wachita chiyani? Tamvera! Magazi a mʼbale wako akulirira kwa Ine kuchokera mʼnthaka. 11 Ndipo tsopano ndiwe wotembereredwa ndipo wachotsedwa mʼdziko limene nthaka yake inatsekula pakamwa pake kulandira magazi a mʼbale wako amene unakhetsa. 12 Udzalima munda koma nthakayo sidzakupatsanso zokolola zake. Udzakhala wosakhazikika; womangoyendayenda pa dziko lapansi.” 13 Kaini anati kwa Yehova, “Chilango changa ndi chachikulu kuposera mphamvu zanga. 14 Lero mukundipirikitsa pa dziko ndi pamaso panu; ndidzakhala wosakhazikika, woyendayenda, ndipo aliyense amene adzandipeze adzandipha.” 15 Koma Yehova anamuwuza kuti, “Sizidzatero ayi; aliyense amene adzaphe Kaini adzalangidwa ndi kulipiritsidwa kasanu ndi kawiri.” Pamenepo Yehova anayika chizindikiro pa Kaini kuti aliyense womupeza asamuphe. 16 Ndipo Kaini anachoka pamaso pa Yehova nakakhala ku dziko la Nodi, kummawa kwa Edeni. 17 Kaini anagona malo amodzi ndi mkazi wake ndipo mkaziyo anakhala woyembekezera nabala Enoki. Kaini nthawi imeneyo nʼkuti akumanga mzinda ndipo anawutcha dzina la mwana wake Enoki. 18 Enoki anabereka Iradi; Iradi anabereka Mehuyaeli, ndipo Mehuyaeli anabereka Metusela, ndipo Metusela anabereka Lameki. 19 Lameki anakwatira akazi awiri, wina dzina lake linali Ada ndi winayo dzina lake linali Zila. 20 Ada anabereka Yabala; iyeyu anali kholo la onse okhala mʼmatenti ndi oweta ziweto. 21 Dzina la mʼbale wake linali Yubala; iyeyu anali kholo la onse oyimba zeze ndi chitoliro. 22 Zila nayenso anali ndi mwana wamwamuna, dzina lake Tubala-Kaini. Iyeyu anali kholo la amisiri onse osula zida za mkuwa ndi chitsulo. Mlongo wake wa Tubala-Kaini anali Naama. 23 Lameki anawuza akazi akewo kuti,“Ada ndi Zila, ndimvereni;inu akazi anga imvani mawu anga.Ine ndinapha munthu chifukwa anandipweteka.Ndinapha mnyamatayo chifukwa anandimenya. 24 Ngati wopha Kaini amulipsira kasanu nʼkawiri,ndiye kuti wopha ine Lameki adzamulipsira kokwanira 77.” 25 Adamu anagonanso malo amodzi ndi mkazi wake, ndipo anabereka mwana wamwamuna namutcha Seti, kutanthauza kuti, “Mulungu wandipatsa mwana wina mʼmalo mwa Abele, popeza Kaini anamupha.” 26 Seti naye anali ndi mwana wa mwamuna, ndipo anamutcha Enosi.Pa nthawi imeneyi anthu anayamba kupemphera mʼdzina la Yehova.

In Other Versions

Genesis 4 in the ANGEFD

Genesis 4 in the ANTPNG2D

Genesis 4 in the AS21

Genesis 4 in the BAGH

Genesis 4 in the BBPNG

Genesis 4 in the BBT1E

Genesis 4 in the BDS

Genesis 4 in the BEV

Genesis 4 in the BHAD

Genesis 4 in the BIB

Genesis 4 in the BLPT

Genesis 4 in the BNT

Genesis 4 in the BNTABOOT

Genesis 4 in the BNTLV

Genesis 4 in the BOATCB

Genesis 4 in the BOATCB2

Genesis 4 in the BOBCV

Genesis 4 in the BOCNT

Genesis 4 in the BOECS

Genesis 4 in the BOHCB

Genesis 4 in the BOHCV

Genesis 4 in the BOHLNT

Genesis 4 in the BOHNTLTAL

Genesis 4 in the BOICB

Genesis 4 in the BOILNTAP

Genesis 4 in the BOITCV

Genesis 4 in the BOKCV

Genesis 4 in the BOKCV2

Genesis 4 in the BOKHWOG

Genesis 4 in the BOKSSV

Genesis 4 in the BOLCB

Genesis 4 in the BOLCB2

Genesis 4 in the BOMCV

Genesis 4 in the BONAV

Genesis 4 in the BONCB

Genesis 4 in the BONLT

Genesis 4 in the BONUT2

Genesis 4 in the BOPLNT

Genesis 4 in the BOSCB

Genesis 4 in the BOSNC

Genesis 4 in the BOTLNT

Genesis 4 in the BOVCB

Genesis 4 in the BOYCB

Genesis 4 in the BPBB

Genesis 4 in the BPH

Genesis 4 in the BSB

Genesis 4 in the CCB

Genesis 4 in the CUV

Genesis 4 in the CUVS

Genesis 4 in the DBT

Genesis 4 in the DGDNT

Genesis 4 in the DHNT

Genesis 4 in the DNT

Genesis 4 in the ELBE

Genesis 4 in the EMTV

Genesis 4 in the ESV

Genesis 4 in the FBV

Genesis 4 in the FEB

Genesis 4 in the GGMNT

Genesis 4 in the GNT

Genesis 4 in the HARY

Genesis 4 in the HNT

Genesis 4 in the IRVA

Genesis 4 in the IRVB

Genesis 4 in the IRVG

Genesis 4 in the IRVH

Genesis 4 in the IRVK

Genesis 4 in the IRVM

Genesis 4 in the IRVM2

Genesis 4 in the IRVO

Genesis 4 in the IRVP

Genesis 4 in the IRVT

Genesis 4 in the IRVT2

Genesis 4 in the IRVU

Genesis 4 in the ISVN

Genesis 4 in the JSNT

Genesis 4 in the KAPI

Genesis 4 in the KBT1ETNIK

Genesis 4 in the KBV

Genesis 4 in the KJV

Genesis 4 in the KNFD

Genesis 4 in the LBA

Genesis 4 in the LBLA

Genesis 4 in the LNT

Genesis 4 in the LSV

Genesis 4 in the MAAL

Genesis 4 in the MBV

Genesis 4 in the MBV2

Genesis 4 in the MHNT

Genesis 4 in the MKNFD

Genesis 4 in the MNG

Genesis 4 in the MNT

Genesis 4 in the MNT2

Genesis 4 in the MRS1T

Genesis 4 in the NAA

Genesis 4 in the NASB

Genesis 4 in the NBLA

Genesis 4 in the NBS

Genesis 4 in the NBVTP

Genesis 4 in the NET2

Genesis 4 in the NIV11

Genesis 4 in the NNT

Genesis 4 in the NNT2

Genesis 4 in the NNT3

Genesis 4 in the PDDPT

Genesis 4 in the PFNT

Genesis 4 in the RMNT

Genesis 4 in the SBIAS

Genesis 4 in the SBIBS

Genesis 4 in the SBIBS2

Genesis 4 in the SBICS

Genesis 4 in the SBIDS

Genesis 4 in the SBIGS

Genesis 4 in the SBIHS

Genesis 4 in the SBIIS

Genesis 4 in the SBIIS2

Genesis 4 in the SBIIS3

Genesis 4 in the SBIKS

Genesis 4 in the SBIKS2

Genesis 4 in the SBIMS

Genesis 4 in the SBIOS

Genesis 4 in the SBIPS

Genesis 4 in the SBISS

Genesis 4 in the SBITS

Genesis 4 in the SBITS2

Genesis 4 in the SBITS3

Genesis 4 in the SBITS4

Genesis 4 in the SBIUS

Genesis 4 in the SBIVS

Genesis 4 in the SBT

Genesis 4 in the SBT1E

Genesis 4 in the SCHL

Genesis 4 in the SNT

Genesis 4 in the SUSU

Genesis 4 in the SUSU2

Genesis 4 in the SYNO

Genesis 4 in the TBIAOTANT

Genesis 4 in the TBT1E

Genesis 4 in the TBT1E2

Genesis 4 in the TFTIP

Genesis 4 in the TFTU

Genesis 4 in the TGNTATF3T

Genesis 4 in the THAI

Genesis 4 in the TNFD

Genesis 4 in the TNT

Genesis 4 in the TNTIK

Genesis 4 in the TNTIL

Genesis 4 in the TNTIN

Genesis 4 in the TNTIP

Genesis 4 in the TNTIZ

Genesis 4 in the TOMA

Genesis 4 in the TTENT

Genesis 4 in the UBG

Genesis 4 in the UGV

Genesis 4 in the UGV2

Genesis 4 in the UGV3

Genesis 4 in the VBL

Genesis 4 in the VDCC

Genesis 4 in the YALU

Genesis 4 in the YAPE

Genesis 4 in the YBVTP

Genesis 4 in the ZBP