Zechariah 9 (BOGWICC)

1 Mawu a Yehova odzudzula dziko la Hadirakindi mzinda wa Damasikopakuti maso a anthu ndiponso mafuko onse a Israeliali pa Yehova— 2 ndiponso mzinda wa Hamati, umene ukuchita malire ndi dzikoli,komanso pa Turo ndi Sidoni, ngakhale kuti iwo ndi anzeru kwambiri. 3 Ndipo Turo anadzimangira linga;wadziwunjikira siliva ngati fumbi,ndi golide ngati zinyalala za mʼmisewu. 4 Taonani Ambuye adzamulanda chuma chakechondi kuwononga mphamvu zake mʼnyanja,ndipo adzapserera ndi moto. 5 Mzinda wa Asikeloni udzaona zimenezi, nʼkuchita mantha;Gaza adzanjenjemera ndi ululu,chimodzimodzinso Ekroni, chifukwa chiyembekezo chake chidzatheratu.Mfumu ya ku Gaza idzaphedwandipo Asikeloni adzakhala opanda anthu. 6 Mu Asidodi mudzakhala mlendo,ndipo ndidzathetsa kunyada kwa Afilisti. 7 Ndidzachotsa nyama ya magazi mʼkamwa mwawo,chakudya choletsedwa mʼmano mwawo.Amene atsala adzakhala anthu a Mulungu wathu,adzasanduka atsogoleri mu Yuda,ndipo Ekroni adzakhala ngati Ayebusi. 8 Koma Ine ndidzalondera Nyumba yangandi kuyiteteza kwa ankhondo osakaza.Palibenso mdani amene adzagonjetse anthu anga,pakuti tsopano ndikuwayangʼanira. 9 Sangalala kwambiri, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni!Fuwula, mwana wamkazi wa Yerusalemu!Taona, mfumu yako ikubwera kwa iwe,yolungama ndi yogonjetsa adani,yodzichepetsa ndi yokwera pa bulu,pa mwana wamphongo wa bulu. 10 Ndidzachotsa magaleta ankhondo ku Efereimundi akavalo ankhondo ku Yerusalemu,ndipo uta wankhondo udzathyoka.Mfumuyo idzabweretsa mtendere pakati pa mitundu ya anthu.Ulamuliro wake udzayambira ku nyanja ina mpaka ku nyanja ina,ndipo kuchokera ku Mtsinje (Yufurate) mpaka ku malekezero a dziko lapansi. 11 Tsono kunena za iwe, chifukwa cha magazi a pangano lako ndi Ine,ndidzamasula amʼndende ako, ndidzawatulutsa mʼdzenje lopanda madzi. 12 Bwererani ku malo anu otetezedwa, inu amʼndende achiyembekezo;ngakhale tsopano ndikulengeza kuti ndidzakubwezerani zabwino mowirikiza. 13 Ndidzakoka Yuda monga ndimakokera uta wanga,ndipo Efereimu ndiye muvi wake.Ndidzadzutsa ana ako iwe Ziyoni,kulimbana ndi ana ako iwe Grisi,ndipo ndidzakusandutsa iwe lupanga la munthu wankhondo. 14 Pamenepo Yehova adzaonekera kwa anthu ake;mivi yake idzangʼanima ngati chingʼaningʼani.Ambuye Yehova adzaliza lipenga;ndipo adzayenda mu mkuntho wochokera kummwera, 15 ndipo Yehova Wamphamvuzonse adzawateteza.Iwo adzawonongandipo adzagonjetsa ndi miyala ya legeni.Adzamwa magazi ndi kubangula ngati amwa vinyo;magazi adzayenderera ngati a mʼmbale yowazira magazipa ngodya za guwa lansembe. 16 Tsiku limenelo Yehova Mulungu wawo adzawapulumutsapakuti anthu ake ali ngati nkhosa.Adzanyezimira mʼdziko lakengati miyala yokongola pa chipewa chaufumu. 17 Taonani chikoka ndi kukongola kwawo!Tirigu adzasangalatsa anyamata,ndi vinyo watsopano anamwali.

In Other Versions

Zechariah 9 in the ANGEFD

Zechariah 9 in the ANTPNG2D

Zechariah 9 in the AS21

Zechariah 9 in the BAGH

Zechariah 9 in the BBPNG

Zechariah 9 in the BBT1E

Zechariah 9 in the BDS

Zechariah 9 in the BEV

Zechariah 9 in the BHAD

Zechariah 9 in the BIB

Zechariah 9 in the BLPT

Zechariah 9 in the BNT

Zechariah 9 in the BNTABOOT

Zechariah 9 in the BNTLV

Zechariah 9 in the BOATCB

Zechariah 9 in the BOATCB2

Zechariah 9 in the BOBCV

Zechariah 9 in the BOCNT

Zechariah 9 in the BOECS

Zechariah 9 in the BOHCB

Zechariah 9 in the BOHCV

Zechariah 9 in the BOHLNT

Zechariah 9 in the BOHNTLTAL

Zechariah 9 in the BOICB

Zechariah 9 in the BOILNTAP

Zechariah 9 in the BOITCV

Zechariah 9 in the BOKCV

Zechariah 9 in the BOKCV2

Zechariah 9 in the BOKHWOG

Zechariah 9 in the BOKSSV

Zechariah 9 in the BOLCB

Zechariah 9 in the BOLCB2

Zechariah 9 in the BOMCV

Zechariah 9 in the BONAV

Zechariah 9 in the BONCB

Zechariah 9 in the BONLT

Zechariah 9 in the BONUT2

Zechariah 9 in the BOPLNT

Zechariah 9 in the BOSCB

Zechariah 9 in the BOSNC

Zechariah 9 in the BOTLNT

Zechariah 9 in the BOVCB

Zechariah 9 in the BOYCB

Zechariah 9 in the BPBB

Zechariah 9 in the BPH

Zechariah 9 in the BSB

Zechariah 9 in the CCB

Zechariah 9 in the CUV

Zechariah 9 in the CUVS

Zechariah 9 in the DBT

Zechariah 9 in the DGDNT

Zechariah 9 in the DHNT

Zechariah 9 in the DNT

Zechariah 9 in the ELBE

Zechariah 9 in the EMTV

Zechariah 9 in the ESV

Zechariah 9 in the FBV

Zechariah 9 in the FEB

Zechariah 9 in the GGMNT

Zechariah 9 in the GNT

Zechariah 9 in the HARY

Zechariah 9 in the HNT

Zechariah 9 in the IRVA

Zechariah 9 in the IRVB

Zechariah 9 in the IRVG

Zechariah 9 in the IRVH

Zechariah 9 in the IRVK

Zechariah 9 in the IRVM

Zechariah 9 in the IRVM2

Zechariah 9 in the IRVO

Zechariah 9 in the IRVP

Zechariah 9 in the IRVT

Zechariah 9 in the IRVT2

Zechariah 9 in the IRVU

Zechariah 9 in the ISVN

Zechariah 9 in the JSNT

Zechariah 9 in the KAPI

Zechariah 9 in the KBT1ETNIK

Zechariah 9 in the KBV

Zechariah 9 in the KJV

Zechariah 9 in the KNFD

Zechariah 9 in the LBA

Zechariah 9 in the LBLA

Zechariah 9 in the LNT

Zechariah 9 in the LSV

Zechariah 9 in the MAAL

Zechariah 9 in the MBV

Zechariah 9 in the MBV2

Zechariah 9 in the MHNT

Zechariah 9 in the MKNFD

Zechariah 9 in the MNG

Zechariah 9 in the MNT

Zechariah 9 in the MNT2

Zechariah 9 in the MRS1T

Zechariah 9 in the NAA

Zechariah 9 in the NASB

Zechariah 9 in the NBLA

Zechariah 9 in the NBS

Zechariah 9 in the NBVTP

Zechariah 9 in the NET2

Zechariah 9 in the NIV11

Zechariah 9 in the NNT

Zechariah 9 in the NNT2

Zechariah 9 in the NNT3

Zechariah 9 in the PDDPT

Zechariah 9 in the PFNT

Zechariah 9 in the RMNT

Zechariah 9 in the SBIAS

Zechariah 9 in the SBIBS

Zechariah 9 in the SBIBS2

Zechariah 9 in the SBICS

Zechariah 9 in the SBIDS

Zechariah 9 in the SBIGS

Zechariah 9 in the SBIHS

Zechariah 9 in the SBIIS

Zechariah 9 in the SBIIS2

Zechariah 9 in the SBIIS3

Zechariah 9 in the SBIKS

Zechariah 9 in the SBIKS2

Zechariah 9 in the SBIMS

Zechariah 9 in the SBIOS

Zechariah 9 in the SBIPS

Zechariah 9 in the SBISS

Zechariah 9 in the SBITS

Zechariah 9 in the SBITS2

Zechariah 9 in the SBITS3

Zechariah 9 in the SBITS4

Zechariah 9 in the SBIUS

Zechariah 9 in the SBIVS

Zechariah 9 in the SBT

Zechariah 9 in the SBT1E

Zechariah 9 in the SCHL

Zechariah 9 in the SNT

Zechariah 9 in the SUSU

Zechariah 9 in the SUSU2

Zechariah 9 in the SYNO

Zechariah 9 in the TBIAOTANT

Zechariah 9 in the TBT1E

Zechariah 9 in the TBT1E2

Zechariah 9 in the TFTIP

Zechariah 9 in the TFTU

Zechariah 9 in the TGNTATF3T

Zechariah 9 in the THAI

Zechariah 9 in the TNFD

Zechariah 9 in the TNT

Zechariah 9 in the TNTIK

Zechariah 9 in the TNTIL

Zechariah 9 in the TNTIN

Zechariah 9 in the TNTIP

Zechariah 9 in the TNTIZ

Zechariah 9 in the TOMA

Zechariah 9 in the TTENT

Zechariah 9 in the UBG

Zechariah 9 in the UGV

Zechariah 9 in the UGV2

Zechariah 9 in the UGV3

Zechariah 9 in the VBL

Zechariah 9 in the VDCC

Zechariah 9 in the YALU

Zechariah 9 in the YAPE

Zechariah 9 in the YBVTP

Zechariah 9 in the ZBP