Ecclesiastes 9 (BOGWICC)

1 Ndinalingalira zonse ndanenazi ndipo ndinapeza kuti anthu olungama ndi anthu anzeru ali mʼmanja mwa Mulungu pamodzi ndi zimene amachita, koma palibe amene amadziwa zimene zikumudikira mʼtsogolo mwake, kaya chikondi kapena chidani. 2 Onsewa mathero awo ndi amodzi, anthu olungama ndi anthu oyipa, abwino ndi oyipa, oyera ndi odetsedwa, amene amapereka nsembe ndi amene sapereka nsembe.Zomwe zimachitikira munthu wabwino,zimachitikiranso munthu wochimwa,zomwe zimachitikira amene amalumbira,zimachitikiranso amene amaopa kulumbira. 3 Choyipa chimene chili mʼzonse zochitika pansi ndi ichi: Mathero a zonse ndi amodzi. Ndithu, mitima ya anthu ndi yodzaza ndi zoyipa, ndipo mʼmitima mwawo muli zamisala pamene ali ndi moyo, potsiriza pake iwo amakakhala pamodzi ndi anthu akufa. 4 Aliyense amene ali ndi moyo amakhala ndi chiyembekezo, pajatu galu wamoyo aposa mkango wakufa! 5 Pakuti amoyo amadziwa kuti adzafa,koma akufa sadziwa kanthu;alibe mphotho ina yowonjezera,ndipo palibe amene amawakumbukira. 6 Chikondi chawo, chidani chawondiponso nsanje yawo, zonse zinatha kalekale;sadzakhalanso ndi gawopa zonse zochitika pansi pano. 7 Pita, kadye chakudya chako mokondwera ndi kumwa vinyo wako ndi mtima wosangalala, pakuti tsopano Mulungu akukondwera ndi zochita zako. 8 Uzivala zovala zoyera nthawi zonse, uzidzola mafuta mʼmutu mwako nthawi zonse. 9 Uzikondwerera moyo pamodzi ndi mkazi wako amene umamukonda, masiku onse a moyo uno wopanda phindu, amene Mulungu wakupatsa pansi pano. Pakuti mkaziyo ndiye gawo la moyo wako pa ntchito yako yolemetsa pansi pano. 10 Ntchito iliyonse imene ukuyigwira, uyigwire ndi mphamvu zako zonse, pakuti ku manda kumene ukupita kulibe kugwira ntchito, kulibe malingaliro, chidziwitso ndiponso nzeru. 11 Ine ndinaonanso chinthu china pansi pano:opambana pa kuthamanga si aliwiro,kapena opambana pa nkhondo si amphamvu,ndiponso okhala ndi chakudya si anzeru,kapena okhala ndi chuma si odziwa zambiri,kapena okomeredwa mtima si ophunzira;koma mwayi umangowagwera onsewa pa nthawi yake. 12 Kungoti palibe munthu amene amadziwa kuti nthawi yake idzafika liti:monga momwe nsomba zimagwidwira mu ukonde,kapena mmene mbalame zimakodwera mu msampha,chimodzimodzinso anthu amakodwa mu msampha pa nthawi yoyipa,pamene tsoka limawagwera mosayembekezera. 13 Ine ndinaonanso pansi pano chitsanzo ichi cha nzeru chimene chinandikhudza kwambiri: 14 Panali mzinda waungʼono umene unali ndi anthu owerengeka. Ndipo mfumu yamphamvu inabwera kudzawuthira nkhondo, inawuzungulira ndi kumanga mitumbira yankhondo. 15 Tsono mu mzindamo munali munthu wosauka koma wanzeru, ndipo anapulumutsa mzindawo ndi nzeru zakezo. Koma palibe amene anakumbukira munthu wosaukayo. 16 Choncho ine ndinati, “Nzeru ndi yopambana mphamvu.” Koma nzeru ya munthu wosauka imanyozedwa, ndipo palibe amene amalabadirako za mawu ake. 17 Mawu oyankhula mofatsa a munthu wanzeru, anthu amawasamalira kwambirikupambana kufuwula kwa mfumu ya zitsiru. 18 Nzeru ndi yabwino kupambana zida zankhondo,koma wochimwa mmodzi amawononga zinthu zambiri zabwino.

In Other Versions

Ecclesiastes 9 in the ANGEFD

Ecclesiastes 9 in the ANTPNG2D

Ecclesiastes 9 in the AS21

Ecclesiastes 9 in the BAGH

Ecclesiastes 9 in the BBPNG

Ecclesiastes 9 in the BBT1E

Ecclesiastes 9 in the BDS

Ecclesiastes 9 in the BEV

Ecclesiastes 9 in the BHAD

Ecclesiastes 9 in the BIB

Ecclesiastes 9 in the BLPT

Ecclesiastes 9 in the BNT

Ecclesiastes 9 in the BNTABOOT

Ecclesiastes 9 in the BNTLV

Ecclesiastes 9 in the BOATCB

Ecclesiastes 9 in the BOATCB2

Ecclesiastes 9 in the BOBCV

Ecclesiastes 9 in the BOCNT

Ecclesiastes 9 in the BOECS

Ecclesiastes 9 in the BOHCB

Ecclesiastes 9 in the BOHCV

Ecclesiastes 9 in the BOHLNT

Ecclesiastes 9 in the BOHNTLTAL

Ecclesiastes 9 in the BOICB

Ecclesiastes 9 in the BOILNTAP

Ecclesiastes 9 in the BOITCV

Ecclesiastes 9 in the BOKCV

Ecclesiastes 9 in the BOKCV2

Ecclesiastes 9 in the BOKHWOG

Ecclesiastes 9 in the BOKSSV

Ecclesiastes 9 in the BOLCB

Ecclesiastes 9 in the BOLCB2

Ecclesiastes 9 in the BOMCV

Ecclesiastes 9 in the BONAV

Ecclesiastes 9 in the BONCB

Ecclesiastes 9 in the BONLT

Ecclesiastes 9 in the BONUT2

Ecclesiastes 9 in the BOPLNT

Ecclesiastes 9 in the BOSCB

Ecclesiastes 9 in the BOSNC

Ecclesiastes 9 in the BOTLNT

Ecclesiastes 9 in the BOVCB

Ecclesiastes 9 in the BOYCB

Ecclesiastes 9 in the BPBB

Ecclesiastes 9 in the BPH

Ecclesiastes 9 in the BSB

Ecclesiastes 9 in the CCB

Ecclesiastes 9 in the CUV

Ecclesiastes 9 in the CUVS

Ecclesiastes 9 in the DBT

Ecclesiastes 9 in the DGDNT

Ecclesiastes 9 in the DHNT

Ecclesiastes 9 in the DNT

Ecclesiastes 9 in the ELBE

Ecclesiastes 9 in the EMTV

Ecclesiastes 9 in the ESV

Ecclesiastes 9 in the FBV

Ecclesiastes 9 in the FEB

Ecclesiastes 9 in the GGMNT

Ecclesiastes 9 in the GNT

Ecclesiastes 9 in the HARY

Ecclesiastes 9 in the HNT

Ecclesiastes 9 in the IRVA

Ecclesiastes 9 in the IRVB

Ecclesiastes 9 in the IRVG

Ecclesiastes 9 in the IRVH

Ecclesiastes 9 in the IRVK

Ecclesiastes 9 in the IRVM

Ecclesiastes 9 in the IRVM2

Ecclesiastes 9 in the IRVO

Ecclesiastes 9 in the IRVP

Ecclesiastes 9 in the IRVT

Ecclesiastes 9 in the IRVT2

Ecclesiastes 9 in the IRVU

Ecclesiastes 9 in the ISVN

Ecclesiastes 9 in the JSNT

Ecclesiastes 9 in the KAPI

Ecclesiastes 9 in the KBT1ETNIK

Ecclesiastes 9 in the KBV

Ecclesiastes 9 in the KJV

Ecclesiastes 9 in the KNFD

Ecclesiastes 9 in the LBA

Ecclesiastes 9 in the LBLA

Ecclesiastes 9 in the LNT

Ecclesiastes 9 in the LSV

Ecclesiastes 9 in the MAAL

Ecclesiastes 9 in the MBV

Ecclesiastes 9 in the MBV2

Ecclesiastes 9 in the MHNT

Ecclesiastes 9 in the MKNFD

Ecclesiastes 9 in the MNG

Ecclesiastes 9 in the MNT

Ecclesiastes 9 in the MNT2

Ecclesiastes 9 in the MRS1T

Ecclesiastes 9 in the NAA

Ecclesiastes 9 in the NASB

Ecclesiastes 9 in the NBLA

Ecclesiastes 9 in the NBS

Ecclesiastes 9 in the NBVTP

Ecclesiastes 9 in the NET2

Ecclesiastes 9 in the NIV11

Ecclesiastes 9 in the NNT

Ecclesiastes 9 in the NNT2

Ecclesiastes 9 in the NNT3

Ecclesiastes 9 in the PDDPT

Ecclesiastes 9 in the PFNT

Ecclesiastes 9 in the RMNT

Ecclesiastes 9 in the SBIAS

Ecclesiastes 9 in the SBIBS

Ecclesiastes 9 in the SBIBS2

Ecclesiastes 9 in the SBICS

Ecclesiastes 9 in the SBIDS

Ecclesiastes 9 in the SBIGS

Ecclesiastes 9 in the SBIHS

Ecclesiastes 9 in the SBIIS

Ecclesiastes 9 in the SBIIS2

Ecclesiastes 9 in the SBIIS3

Ecclesiastes 9 in the SBIKS

Ecclesiastes 9 in the SBIKS2

Ecclesiastes 9 in the SBIMS

Ecclesiastes 9 in the SBIOS

Ecclesiastes 9 in the SBIPS

Ecclesiastes 9 in the SBISS

Ecclesiastes 9 in the SBITS

Ecclesiastes 9 in the SBITS2

Ecclesiastes 9 in the SBITS3

Ecclesiastes 9 in the SBITS4

Ecclesiastes 9 in the SBIUS

Ecclesiastes 9 in the SBIVS

Ecclesiastes 9 in the SBT

Ecclesiastes 9 in the SBT1E

Ecclesiastes 9 in the SCHL

Ecclesiastes 9 in the SNT

Ecclesiastes 9 in the SUSU

Ecclesiastes 9 in the SUSU2

Ecclesiastes 9 in the SYNO

Ecclesiastes 9 in the TBIAOTANT

Ecclesiastes 9 in the TBT1E

Ecclesiastes 9 in the TBT1E2

Ecclesiastes 9 in the TFTIP

Ecclesiastes 9 in the TFTU

Ecclesiastes 9 in the TGNTATF3T

Ecclesiastes 9 in the THAI

Ecclesiastes 9 in the TNFD

Ecclesiastes 9 in the TNT

Ecclesiastes 9 in the TNTIK

Ecclesiastes 9 in the TNTIL

Ecclesiastes 9 in the TNTIN

Ecclesiastes 9 in the TNTIP

Ecclesiastes 9 in the TNTIZ

Ecclesiastes 9 in the TOMA

Ecclesiastes 9 in the TTENT

Ecclesiastes 9 in the UBG

Ecclesiastes 9 in the UGV

Ecclesiastes 9 in the UGV2

Ecclesiastes 9 in the UGV3

Ecclesiastes 9 in the VBL

Ecclesiastes 9 in the VDCC

Ecclesiastes 9 in the YALU

Ecclesiastes 9 in the YAPE

Ecclesiastes 9 in the YBVTP

Ecclesiastes 9 in the ZBP