Isaiah 43 (BOGWICC)

1 Koma tsopano, Yehovaamene anakulenga, iwe Yakobo,amene anakuwumba, iwe Israeli akuti,“Usaope, pakuti ndakuwombola;Ndinakuyitanitsa mokutchula dzina lako, ndiwe wanga. 2 Pamene ukuwoloka nyanja,ndidzakhala nawe;ndipo pamene ukuwoloka mitsinje,sidzakukokolola.Pamene ukudutsa pa moto,sudzapsa;lawi la moto silidzakutentha. 3 Chifukwa Ine Yehova, Mulungu wako,Woyera wa Israeli, ndine Mpulumutsi wako.Ndinapereka Igupto pofuna kuti ndiwombole iwe,ndinapereka Kusi ndi Seba mʼmalo mwa iwe. 4 Popeza kuti ndiwe wamtengowapatali wolemekezeka ndi wapamtima panga,ndipo chifukwa ndimakukonda,ndidzapereka anthu mʼmalo mwa iwe,ndidzapereka mitundu ya anthu pofuna kuwombola moyo wako. 5 Usachite mantha, pakuti Ine ndili nawe;ndidzabweretsa ana ako kuchokera kummawa,ndipo ndidzakusonkhanitsani kuchokera kumadzulo. 6 Ndidzawuza a kumpoto kuti, ‘Amasuleni,’ndidzawuza akummwera kuti, ‘Musawagwire.’Bweretsani ana anga aamuna kuchokera ku mayiko akutali,ana anga a akazi kuchokera kumalekezero a dziko lapansi; 7 onsewo amadziwika ndi dzina langa;ndinawalenga chifukwa cha ulemerero wanga,ndinawawumba, inde ndinawapanga.” 8 Tulutsa anthu amene ali nawo maso koma sakupenya,anthu amene ali nawo makutu koma sakumva. 9 Mitundu yonse ya anthu isonkhane pamodzi,anthu a mitundu ina akhale pamodzi pabwalo la milandu.Ndani wa iwo amene ananeneratu zimenezi?Ndani wa iwo anatifotokozerapo zinthu zakalekale?Abweretu ndi mboni zawo kuti adzatsimikizire kuti ananena zoona,kuti anthu ena amve ndi kunena kuti, “Ndi zoona.” 10 Yehova akunena kuti, “Inu Aisraeli ndinu mboni zanga,ndi mtumiki wanga amene ndinakusankha,kuti mundidziwe ndi kundikhulupirira, ndipo mudzamvetsa kuti Mulungu ndine ndekha.Patsogolo panga sipanapangidwepo mulungu wina,ngakhale pambuyo pangasipadzakhalaponso wina.” 11 Akutero Yehova, “Ine, Inetu ndine Yehova,ndipo palibe Mpulumutsi wina koma Ine ndekha. 12 Ndine amene ndinaneneratu, amene ndinakupulumutsa;ndine, osati mulungu wina wachilendo pakati panu amene ndinalengezeratu.Inu ndinu mboni zanga, kuti Ine ndine Mulungu,” akutero Yehova. 13 “Ine ndine Mulungu kuyambira nthawi yamakedzana, ndipo ndidzakhalabe Mulungu ku nthawi zonse.Palibe amene angathe kuthawa mʼmanja mwanga,ndipo chimene ndachita palibe angathe kuchisintha.” 14 Yehova akuti,Mpulumutsi wanu, Woyerayo wa Israeli akuti,“Chifukwa cha inu ndidzatuma gulu lankhondo kukalimbana ndi Babulonindi kukupulumutsani.Ndidzagwetsa zitseko zonse za mzindawo, ndipo kukondwa kwa anthu ake kudzasanduka kulira. 15 Ine ndine Yehova, Woyera wanu uja,Mlengi wa Israeli. Ine ndine Mfumu yanu.” 16 Yehovaanapanga njira pa nyanja,anapanga njira pakati pa madzi amphamvu. 17 Iye anasonkhanitsa magaleta, akavalo,gulu lankhondo ndi asilikali amphamvu,ndipo onse anagwa pamenepo, osadzukansoanazimitsidwa kutheratu ngati chingwe cha nyale. Yehova ameneyu akuti, 18 “Iwalani zinthu zakale;ndipo musaganizirenso zinthu zimene zinachitika kale. 19 Taonani, Ine ndikuchita zinthu zatsopano!Tsopano zayamba kale kuoneka; kodi simukuziona?Ine ndikulambula msewu mʼchipululundi kupanga mitsinje mʼdziko lowuma. 20 Nyama zakuthengo, nkhandwe ndi akadzidzizinandilemekeza.Ndidzayendetsa mitsinje mʼdziko lowumakuti ndiwapatse madzi anthu angaosankhidwa. 21 Anthu amene ndinadziwumbira ndekhakuti aziyimba nyimbo yotamanda Ine. 22 “Komatu simunapemphera kwa Ine, Inu a mʼbanja la Yakobo,munatopa nane, Inu Aisraeli. 23 Simunabweretse kwa Ine nkhosa za nsembe zopsereza,kapena kundilemekeza ndi nsembe zanu.Ine sindinakulemetseni pomakupemphani zopereka za chakudyakapena kukutopetsani pomakupemphani nsembe zofukiza. 24 Simunandigulire bango lonunkhirakapena kundipatsa Ine mafuta okwanira a nsembe zanu.Koma inu mwandilemetsa Ine ndi machimo anundipo mwanditopetsa Ine ndi zolakwa zanu. 25 “Ine, Inetu, ndi amene ndimafafanizazolakwa zanu, chifukwa cha Ine mwini,ndipo sindidzakumbukiranso machimo anu. 26 Mundikumbutse zakale,ndipo titsutsane nkhaniyi pamodzi;fotokozani mlandu wanu kuti muonetse kuti ndinu osalakwa. 27 Kholo lanu loyamba linachimwa;ndipo Atsogoleri anu achipembedzo anandiwukira. 28 Chifukwa chake Ine ndidzanyazitsa akuluakulu a Nyumba yanu ya mapemphero,ndipo ndidzapereka Yakobo kuti awonongedwendi Israeli kuti achitidwe chipongwe.”

In Other Versions

Isaiah 43 in the ANGEFD

Isaiah 43 in the ANTPNG2D

Isaiah 43 in the AS21

Isaiah 43 in the BAGH

Isaiah 43 in the BBPNG

Isaiah 43 in the BBT1E

Isaiah 43 in the BDS

Isaiah 43 in the BEV

Isaiah 43 in the BHAD

Isaiah 43 in the BIB

Isaiah 43 in the BLPT

Isaiah 43 in the BNT

Isaiah 43 in the BNTABOOT

Isaiah 43 in the BNTLV

Isaiah 43 in the BOATCB

Isaiah 43 in the BOATCB2

Isaiah 43 in the BOBCV

Isaiah 43 in the BOCNT

Isaiah 43 in the BOECS

Isaiah 43 in the BOHCB

Isaiah 43 in the BOHCV

Isaiah 43 in the BOHLNT

Isaiah 43 in the BOHNTLTAL

Isaiah 43 in the BOICB

Isaiah 43 in the BOILNTAP

Isaiah 43 in the BOITCV

Isaiah 43 in the BOKCV

Isaiah 43 in the BOKCV2

Isaiah 43 in the BOKHWOG

Isaiah 43 in the BOKSSV

Isaiah 43 in the BOLCB

Isaiah 43 in the BOLCB2

Isaiah 43 in the BOMCV

Isaiah 43 in the BONAV

Isaiah 43 in the BONCB

Isaiah 43 in the BONLT

Isaiah 43 in the BONUT2

Isaiah 43 in the BOPLNT

Isaiah 43 in the BOSCB

Isaiah 43 in the BOSNC

Isaiah 43 in the BOTLNT

Isaiah 43 in the BOVCB

Isaiah 43 in the BOYCB

Isaiah 43 in the BPBB

Isaiah 43 in the BPH

Isaiah 43 in the BSB

Isaiah 43 in the CCB

Isaiah 43 in the CUV

Isaiah 43 in the CUVS

Isaiah 43 in the DBT

Isaiah 43 in the DGDNT

Isaiah 43 in the DHNT

Isaiah 43 in the DNT

Isaiah 43 in the ELBE

Isaiah 43 in the EMTV

Isaiah 43 in the ESV

Isaiah 43 in the FBV

Isaiah 43 in the FEB

Isaiah 43 in the GGMNT

Isaiah 43 in the GNT

Isaiah 43 in the HARY

Isaiah 43 in the HNT

Isaiah 43 in the IRVA

Isaiah 43 in the IRVB

Isaiah 43 in the IRVG

Isaiah 43 in the IRVH

Isaiah 43 in the IRVK

Isaiah 43 in the IRVM

Isaiah 43 in the IRVM2

Isaiah 43 in the IRVO

Isaiah 43 in the IRVP

Isaiah 43 in the IRVT

Isaiah 43 in the IRVT2

Isaiah 43 in the IRVU

Isaiah 43 in the ISVN

Isaiah 43 in the JSNT

Isaiah 43 in the KAPI

Isaiah 43 in the KBT1ETNIK

Isaiah 43 in the KBV

Isaiah 43 in the KJV

Isaiah 43 in the KNFD

Isaiah 43 in the LBA

Isaiah 43 in the LBLA

Isaiah 43 in the LNT

Isaiah 43 in the LSV

Isaiah 43 in the MAAL

Isaiah 43 in the MBV

Isaiah 43 in the MBV2

Isaiah 43 in the MHNT

Isaiah 43 in the MKNFD

Isaiah 43 in the MNG

Isaiah 43 in the MNT

Isaiah 43 in the MNT2

Isaiah 43 in the MRS1T

Isaiah 43 in the NAA

Isaiah 43 in the NASB

Isaiah 43 in the NBLA

Isaiah 43 in the NBS

Isaiah 43 in the NBVTP

Isaiah 43 in the NET2

Isaiah 43 in the NIV11

Isaiah 43 in the NNT

Isaiah 43 in the NNT2

Isaiah 43 in the NNT3

Isaiah 43 in the PDDPT

Isaiah 43 in the PFNT

Isaiah 43 in the RMNT

Isaiah 43 in the SBIAS

Isaiah 43 in the SBIBS

Isaiah 43 in the SBIBS2

Isaiah 43 in the SBICS

Isaiah 43 in the SBIDS

Isaiah 43 in the SBIGS

Isaiah 43 in the SBIHS

Isaiah 43 in the SBIIS

Isaiah 43 in the SBIIS2

Isaiah 43 in the SBIIS3

Isaiah 43 in the SBIKS

Isaiah 43 in the SBIKS2

Isaiah 43 in the SBIMS

Isaiah 43 in the SBIOS

Isaiah 43 in the SBIPS

Isaiah 43 in the SBISS

Isaiah 43 in the SBITS

Isaiah 43 in the SBITS2

Isaiah 43 in the SBITS3

Isaiah 43 in the SBITS4

Isaiah 43 in the SBIUS

Isaiah 43 in the SBIVS

Isaiah 43 in the SBT

Isaiah 43 in the SBT1E

Isaiah 43 in the SCHL

Isaiah 43 in the SNT

Isaiah 43 in the SUSU

Isaiah 43 in the SUSU2

Isaiah 43 in the SYNO

Isaiah 43 in the TBIAOTANT

Isaiah 43 in the TBT1E

Isaiah 43 in the TBT1E2

Isaiah 43 in the TFTIP

Isaiah 43 in the TFTU

Isaiah 43 in the TGNTATF3T

Isaiah 43 in the THAI

Isaiah 43 in the TNFD

Isaiah 43 in the TNT

Isaiah 43 in the TNTIK

Isaiah 43 in the TNTIL

Isaiah 43 in the TNTIN

Isaiah 43 in the TNTIP

Isaiah 43 in the TNTIZ

Isaiah 43 in the TOMA

Isaiah 43 in the TTENT

Isaiah 43 in the UBG

Isaiah 43 in the UGV

Isaiah 43 in the UGV2

Isaiah 43 in the UGV3

Isaiah 43 in the VBL

Isaiah 43 in the VDCC

Isaiah 43 in the YALU

Isaiah 43 in the YAPE

Isaiah 43 in the YBVTP

Isaiah 43 in the ZBP