Jeremiah 19 (BOGWICC)

1 Yehova anandiwuza kuti, “Pita ukagule mʼphika wadothi kwa munthu wowumba. Utenge akuluakulu ena a anthuwa ndi ansembe 2 ndipo mupite ku Chigwa cha Hinomu chimene chili pafupi ndi pa chipata cha mapale. Pamenepo ukalengeze mawu amene ndikakuwuze. 3 Ukanene kuti, ‘Imvani mawu a Yehova, inu mafumu a ku Yuda ndi anthu a ku Yerusalemu. Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akuti: Tamverani! Ine ndibweretsa mavuto pa malo pano mwakuti aliyense amene adzamve adzadzidzimuka. 4 Pakuti anthu andikana Ine ndipo ayipitsa malo ano. Afukiza lubani pa malo ano kwa milungu imene iwo ngakhale makolo awo ngakhalenso mafumu a ku Yuda sanayidziwe. Iwo adzaza malowa ndi magazi a anthu osalakwa. 5 Amanga nsanja zopembedzerapo Baala, kuperekapo ana awo kuti akhale nsembe zopsereza kwa Baala, chinthu chimene Ine sindinalamule kapena kuchiyankhula, ngakhalenso kuchiganizira. 6 Nʼchifukwa chake taonani, masiku akubwera, akutero Yehova, pamene anthu sadzatchulanso malo ano kuti Tofeti kapena Chigwa cha Hinomu, koma Chophera anthu. 7 “ ‘Pamalo pano ndidzasokoneza maganizo a anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu. Ndidzachititsa kuti adani awo awaphe ku nkhondo. Ndidzawakanthitsa kwa anthu amene akuwazonda. Mitembo yawo ndidzayipereka kwa mbalame za mlengalenga ndi zirombo za kutchire kuti ikhale chakudya chawo. 8 Mzinda uno ndidzawusakaza ndi kuwusandutsa chinthu chochititsa mantha ndi chonyansa. Onse odutsamo adzadabwa ndi kupukusa mitu yawo chifukwa cha kuwonongeka kwake. 9 Adani awo adzawuzinga mzindawo kufuna kuwapha motero kuti anthu a mʼkatimo adzafika pomadyana wina ndi mnzake. Adzadya ana awo aamuna ndi ana awo aakazi.’ 10 “Tsono iwe udzaphwanye mtsukowo anthu amene udzapite nawowo akuona, 11 ndipo ukawawuze kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse akuti, Ine ndidzaphwanya dziko lino ndi mzinda uno ngati momwe wowumba amaphwanyira mbiya yake ndipo sangathe kuyikonzanso. Adzayika anthu akufa ku Tofeti chifukwa padzasowa malo ena owayika. 12 Umu ndi mmene ndidzachitire ndi malo ano pamodzi ndi anthu okhalamo, akutero Yehova. Ndidzasandutsa mzindawu kukhala ngati Tofeti. 13 Nyumba za mu Yerusalemu ndi za mafumu a ku Yuda ndidzazisandutsa ngati za ku Tofeti chifukwa ndi nyumba zimene pa madenga ake ankafukiza lubani kwa zolengedwa zamlengalenga ndi kuthira nsembe zachakumwa kwa milungu ina.’ ” 14 Kenaka Yeremiya anabwerako ku Tofeti, kumene Yehova anamutuma kuti akanenere, nakayimirira mʼbwalo la Nyumba ya Yehova ndi kuwawuza anthu kuti, 15 “Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akuti, ‘Tamverani! Ine ndidzabweretsa masautso amene ndinanena aja pa mzinda uno ndi pa mizinda yozungulira, chifukwa anthu ake ndi nkhutukumve ndipo sanamvere mawu anga.’ ”

In Other Versions

Jeremiah 19 in the ANGEFD

Jeremiah 19 in the ANTPNG2D

Jeremiah 19 in the AS21

Jeremiah 19 in the BAGH

Jeremiah 19 in the BBPNG

Jeremiah 19 in the BBT1E

Jeremiah 19 in the BDS

Jeremiah 19 in the BEV

Jeremiah 19 in the BHAD

Jeremiah 19 in the BIB

Jeremiah 19 in the BLPT

Jeremiah 19 in the BNT

Jeremiah 19 in the BNTABOOT

Jeremiah 19 in the BNTLV

Jeremiah 19 in the BOATCB

Jeremiah 19 in the BOATCB2

Jeremiah 19 in the BOBCV

Jeremiah 19 in the BOCNT

Jeremiah 19 in the BOECS

Jeremiah 19 in the BOHCB

Jeremiah 19 in the BOHCV

Jeremiah 19 in the BOHLNT

Jeremiah 19 in the BOHNTLTAL

Jeremiah 19 in the BOICB

Jeremiah 19 in the BOILNTAP

Jeremiah 19 in the BOITCV

Jeremiah 19 in the BOKCV

Jeremiah 19 in the BOKCV2

Jeremiah 19 in the BOKHWOG

Jeremiah 19 in the BOKSSV

Jeremiah 19 in the BOLCB

Jeremiah 19 in the BOLCB2

Jeremiah 19 in the BOMCV

Jeremiah 19 in the BONAV

Jeremiah 19 in the BONCB

Jeremiah 19 in the BONLT

Jeremiah 19 in the BONUT2

Jeremiah 19 in the BOPLNT

Jeremiah 19 in the BOSCB

Jeremiah 19 in the BOSNC

Jeremiah 19 in the BOTLNT

Jeremiah 19 in the BOVCB

Jeremiah 19 in the BOYCB

Jeremiah 19 in the BPBB

Jeremiah 19 in the BPH

Jeremiah 19 in the BSB

Jeremiah 19 in the CCB

Jeremiah 19 in the CUV

Jeremiah 19 in the CUVS

Jeremiah 19 in the DBT

Jeremiah 19 in the DGDNT

Jeremiah 19 in the DHNT

Jeremiah 19 in the DNT

Jeremiah 19 in the ELBE

Jeremiah 19 in the EMTV

Jeremiah 19 in the ESV

Jeremiah 19 in the FBV

Jeremiah 19 in the FEB

Jeremiah 19 in the GGMNT

Jeremiah 19 in the GNT

Jeremiah 19 in the HARY

Jeremiah 19 in the HNT

Jeremiah 19 in the IRVA

Jeremiah 19 in the IRVB

Jeremiah 19 in the IRVG

Jeremiah 19 in the IRVH

Jeremiah 19 in the IRVK

Jeremiah 19 in the IRVM

Jeremiah 19 in the IRVM2

Jeremiah 19 in the IRVO

Jeremiah 19 in the IRVP

Jeremiah 19 in the IRVT

Jeremiah 19 in the IRVT2

Jeremiah 19 in the IRVU

Jeremiah 19 in the ISVN

Jeremiah 19 in the JSNT

Jeremiah 19 in the KAPI

Jeremiah 19 in the KBT1ETNIK

Jeremiah 19 in the KBV

Jeremiah 19 in the KJV

Jeremiah 19 in the KNFD

Jeremiah 19 in the LBA

Jeremiah 19 in the LBLA

Jeremiah 19 in the LNT

Jeremiah 19 in the LSV

Jeremiah 19 in the MAAL

Jeremiah 19 in the MBV

Jeremiah 19 in the MBV2

Jeremiah 19 in the MHNT

Jeremiah 19 in the MKNFD

Jeremiah 19 in the MNG

Jeremiah 19 in the MNT

Jeremiah 19 in the MNT2

Jeremiah 19 in the MRS1T

Jeremiah 19 in the NAA

Jeremiah 19 in the NASB

Jeremiah 19 in the NBLA

Jeremiah 19 in the NBS

Jeremiah 19 in the NBVTP

Jeremiah 19 in the NET2

Jeremiah 19 in the NIV11

Jeremiah 19 in the NNT

Jeremiah 19 in the NNT2

Jeremiah 19 in the NNT3

Jeremiah 19 in the PDDPT

Jeremiah 19 in the PFNT

Jeremiah 19 in the RMNT

Jeremiah 19 in the SBIAS

Jeremiah 19 in the SBIBS

Jeremiah 19 in the SBIBS2

Jeremiah 19 in the SBICS

Jeremiah 19 in the SBIDS

Jeremiah 19 in the SBIGS

Jeremiah 19 in the SBIHS

Jeremiah 19 in the SBIIS

Jeremiah 19 in the SBIIS2

Jeremiah 19 in the SBIIS3

Jeremiah 19 in the SBIKS

Jeremiah 19 in the SBIKS2

Jeremiah 19 in the SBIMS

Jeremiah 19 in the SBIOS

Jeremiah 19 in the SBIPS

Jeremiah 19 in the SBISS

Jeremiah 19 in the SBITS

Jeremiah 19 in the SBITS2

Jeremiah 19 in the SBITS3

Jeremiah 19 in the SBITS4

Jeremiah 19 in the SBIUS

Jeremiah 19 in the SBIVS

Jeremiah 19 in the SBT

Jeremiah 19 in the SBT1E

Jeremiah 19 in the SCHL

Jeremiah 19 in the SNT

Jeremiah 19 in the SUSU

Jeremiah 19 in the SUSU2

Jeremiah 19 in the SYNO

Jeremiah 19 in the TBIAOTANT

Jeremiah 19 in the TBT1E

Jeremiah 19 in the TBT1E2

Jeremiah 19 in the TFTIP

Jeremiah 19 in the TFTU

Jeremiah 19 in the TGNTATF3T

Jeremiah 19 in the THAI

Jeremiah 19 in the TNFD

Jeremiah 19 in the TNT

Jeremiah 19 in the TNTIK

Jeremiah 19 in the TNTIL

Jeremiah 19 in the TNTIN

Jeremiah 19 in the TNTIP

Jeremiah 19 in the TNTIZ

Jeremiah 19 in the TOMA

Jeremiah 19 in the TTENT

Jeremiah 19 in the UBG

Jeremiah 19 in the UGV

Jeremiah 19 in the UGV2

Jeremiah 19 in the UGV3

Jeremiah 19 in the VBL

Jeremiah 19 in the VDCC

Jeremiah 19 in the YALU

Jeremiah 19 in the YAPE

Jeremiah 19 in the YBVTP

Jeremiah 19 in the ZBP