Jeremiah 6 (BOGWICC)

1 “Thawani, inu anthu a ku Benjamini!Tulukani mu Yerusalemu!Lizani lipenga ku Tekowa!Kwezani mbendera ku Beti-Hakeremu!Pakuti tsoka lalikulu likubwera kuchokera kumpoto,ndipo chiwonongekocho nʼchachikulu. 2 Kodi mzinda wa Ziyoni suli ngati msipu wokongola kwambiri,kumene abusa amafikako ndi ziweto zawo? 3 Abusa ndi nkhosa zawo adzabwera kudzalimbana nawo;adzamanga matenti awo mowuzinga,ndipo aliyense adzakhazika anthu ake pamalo pake.” 4 Adzanena kuti, “Konzekani kuwuthira nkhondo mzindawo!Nyamukani, kuti tiwuthire nkhondo mzindawu masana ano.Koma tili ndi tsoka, dzuwa lapendeka,ndipo zithunzithunzi za kumadzulo zikunka zitalika. 5 Tsono nyamukani kuti tiwuthire nkhondo mzindawu usiku unondi kuwononga malinga ake!” 6 Yehova Wamphamvuzonse akuti,“Dulani mitengondipo mumange mitumbira yankhondo kulimbana ndi Yerusalemu.Mzinda umenewu uyenera kulangidwa;wadzaza ndi kuponderezana. 7 Monga momwe chitsime chimatulutsira madzindi mmenenso Yerusalemu amatulutsira zoyipa zake.Chiwawa ndi chiwonongeko ndi zomwe zimamveka mu mzindamo;nthenda yake ndi mabala ake ndimaziona nthawi zonse. 8 Iwe Yerusalemu, tengapo phunziro,kuopa kuti chikondi changa pa iwe chingakuchokerendi kusandutsa dziko lako kukhala bwinjamopanda munthu wokhalamo.” 9 Yehova Wamphamvuzonse anandiwuza kuti,“Adani adzawakunkha ndithu anthu otsala a Israeli,monga momwe amachitira populula mphesa.Tsono iwe yesetsa kupulumutsa amene ungathemonga mmene amachitira munthu wokolola mphesa.” 10 Kodi ndiyankhule ndi yani ndi kumuchenjeza?Ndinene mawu ochenjeza kwa yani kuti amve?Makutu awo ndi otsekekakotero kuti sangathe kumva.Mawu a Yehova ndi onyansa kwa iwo;sasangalatsidwa nawo. 11 Koma ine ndadzazidwa ndi mkwiyo wa Yehova,ndipo ndatopa ndi kusunga mkwiyo wa Yehova. Yehova anandiwuza kuti, “Tsono ndidzawutulutsira mkwiyo umenewu pa ana oyenda mʼmisewundi pa achinyamata amene asonkhana pamodzi;pakutinso mwamuna ndi mkazi wake adzatengedwa,pamodzi ndi okalamba amene ali ndi zaka zochuluka. 12 Nyumba zawo adzazipereka kwa ena,pamodzi ndi minda yawo ndi akazi awo.Ndidzatambasula dzanja langa kukanthaanthu okhala mʼdzikomo,”akutero Yehova. 13 “Kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu,onse ali ndi dyera lofuna kupeza phindu mwa kuba;aneneri pamodzi ndi ansembe omwe,onse amachita zachinyengo. 14 Amapoletsa zilonda za anthu angapamwamba pokha.Iwo amanena kuti, ‘Mtendere, mtendere,’pamene palibe mtendere. 15 Kodi amachita manyazi akamachita zonyansazo?Ayi, sachita manyazi ndi pangʼono pomwe;sadziwa ndi kugwetsa nkhope komwe.Choncho iwo adzagwera pakati pa anzawo amene agwa kale;adzagwa pansi tsiku limene ndidzawalange,”akutero Yehova. 16 Yehova akuti,“Imani pa mphambano ndipo mupenye;kumeneko ndiye kuli njira zakale,funsani kumene kuli njira yabwino. Yendani mʼmenemo,ndipo mudzapeza mpumulo wa miyoyo yanu.Koma inu munati, ‘Ife sitidzayenda njira imeneyo.’ 17 Ine ndinakupatsani alonda oti akuyangʼanirenindipo ndinati, ‘Imvani kulira kwa lipenga!’koma inu munati, ‘Sitidzamvera.’ 18 Nʼchifukwa chake imvani, inu anthu a mitundu ina;yangʼanitsitsani, inu amene mwasonkhana pano,chimene chidzawachitikire anthuwo. 19 Imvani, inu anthu okhala pa dziko lapansi,ndikubweretsa masautso pa anthu awa.Zimenezi ndi mphotho ya ntchito zawo.Iwowa sanamvere mawu angandipo anakana lamulo langa. 20 Kodi pali phindu lanji ngakhale mubwere ndi lubani kuchokera ku Seba,kapena zonunkhira zina kuchokera ku dziko lakutali?Nsembe zanu zopsereza Ine sindidzalandira;nsembe zanu sizindikondweretsa.” 21 Choncho Yehova akuti,“Ndidzayika zokhumudwitsa pamaso pa anthu awa.Abambo ndi ana awo aamuna onse adzapunthwa ndi kugwa;anansi awo ndi abwenzi awo adzawonongeka.” 22 Yehova akunena kuti,“Taonani, gulu lankhondo likubwerakuchokera kumpoto;mtundu wa anthu amphamvu wanyamukakuchokera kumathero a dziko lapansi. 23 Atenga mauta ndi mikondo;ndi anthu ankhanza ndi opanda chifundo.Phokoso lawo lili ngati mkokomo wa nyanja.Akwera pa akavalo awondipo akonzekera ngati anthu ankhondo,kudzakuthirani nkhondo anthu a ku Ziyoni.” 24 A ku Ziyoni akuti “Ife tamva mbiri yawo,ndipo manja anthu alefukiratu.Nkhawa yatigwira,ndipo tikumva ululu ngati mayi pa nthawi yake yochira. 25 Musapite ku mindakapena kuyenda mʼmisewu,pakuti mdani ali ndi lupanga,ndipo ponseponse anthu akuchita mantha. 26 Inu anthu anga, valani zigudulindipo gubudukani pa phulusa;lirani mwamphamvungati munthu wolirira mwana wake mmodzi yekha,pakuti mwadzidzidzi wowonongayoadzabwera kudzatipha. 27 “Iwe Yeremiya, ndakuyika kuti ukhale choyesera zitsulo.Uwayese anthu angamonga ungayesere chitsulokuti uwone makhalidwe awo. 28 Onsewo ali ndi khalidwe lokanika ndi lowukirandipo akunka nanena zamiseche.Iwo ndi olimba ngati mkuwa ndi chitsulo.Onse amangochita zoyipa zokhazokha. 29 Moto mu mvukuto ukuyaka kwambiri;mtovu watha kusungunuka ndi moto.Koma ntchito yosungunulayo sikupindulachifukwa zoyipa sizikuchokapo. 30 Iwo ali ngati siliva wotayidwa,chifukwa Yehova wawakana.”

In Other Versions

Jeremiah 6 in the ANGEFD

Jeremiah 6 in the ANTPNG2D

Jeremiah 6 in the AS21

Jeremiah 6 in the BAGH

Jeremiah 6 in the BBPNG

Jeremiah 6 in the BBT1E

Jeremiah 6 in the BDS

Jeremiah 6 in the BEV

Jeremiah 6 in the BHAD

Jeremiah 6 in the BIB

Jeremiah 6 in the BLPT

Jeremiah 6 in the BNT

Jeremiah 6 in the BNTABOOT

Jeremiah 6 in the BNTLV

Jeremiah 6 in the BOATCB

Jeremiah 6 in the BOATCB2

Jeremiah 6 in the BOBCV

Jeremiah 6 in the BOCNT

Jeremiah 6 in the BOECS

Jeremiah 6 in the BOHCB

Jeremiah 6 in the BOHCV

Jeremiah 6 in the BOHLNT

Jeremiah 6 in the BOHNTLTAL

Jeremiah 6 in the BOICB

Jeremiah 6 in the BOILNTAP

Jeremiah 6 in the BOITCV

Jeremiah 6 in the BOKCV

Jeremiah 6 in the BOKCV2

Jeremiah 6 in the BOKHWOG

Jeremiah 6 in the BOKSSV

Jeremiah 6 in the BOLCB

Jeremiah 6 in the BOLCB2

Jeremiah 6 in the BOMCV

Jeremiah 6 in the BONAV

Jeremiah 6 in the BONCB

Jeremiah 6 in the BONLT

Jeremiah 6 in the BONUT2

Jeremiah 6 in the BOPLNT

Jeremiah 6 in the BOSCB

Jeremiah 6 in the BOSNC

Jeremiah 6 in the BOTLNT

Jeremiah 6 in the BOVCB

Jeremiah 6 in the BOYCB

Jeremiah 6 in the BPBB

Jeremiah 6 in the BPH

Jeremiah 6 in the BSB

Jeremiah 6 in the CCB

Jeremiah 6 in the CUV

Jeremiah 6 in the CUVS

Jeremiah 6 in the DBT

Jeremiah 6 in the DGDNT

Jeremiah 6 in the DHNT

Jeremiah 6 in the DNT

Jeremiah 6 in the ELBE

Jeremiah 6 in the EMTV

Jeremiah 6 in the ESV

Jeremiah 6 in the FBV

Jeremiah 6 in the FEB

Jeremiah 6 in the GGMNT

Jeremiah 6 in the GNT

Jeremiah 6 in the HARY

Jeremiah 6 in the HNT

Jeremiah 6 in the IRVA

Jeremiah 6 in the IRVB

Jeremiah 6 in the IRVG

Jeremiah 6 in the IRVH

Jeremiah 6 in the IRVK

Jeremiah 6 in the IRVM

Jeremiah 6 in the IRVM2

Jeremiah 6 in the IRVO

Jeremiah 6 in the IRVP

Jeremiah 6 in the IRVT

Jeremiah 6 in the IRVT2

Jeremiah 6 in the IRVU

Jeremiah 6 in the ISVN

Jeremiah 6 in the JSNT

Jeremiah 6 in the KAPI

Jeremiah 6 in the KBT1ETNIK

Jeremiah 6 in the KBV

Jeremiah 6 in the KJV

Jeremiah 6 in the KNFD

Jeremiah 6 in the LBA

Jeremiah 6 in the LBLA

Jeremiah 6 in the LNT

Jeremiah 6 in the LSV

Jeremiah 6 in the MAAL

Jeremiah 6 in the MBV

Jeremiah 6 in the MBV2

Jeremiah 6 in the MHNT

Jeremiah 6 in the MKNFD

Jeremiah 6 in the MNG

Jeremiah 6 in the MNT

Jeremiah 6 in the MNT2

Jeremiah 6 in the MRS1T

Jeremiah 6 in the NAA

Jeremiah 6 in the NASB

Jeremiah 6 in the NBLA

Jeremiah 6 in the NBS

Jeremiah 6 in the NBVTP

Jeremiah 6 in the NET2

Jeremiah 6 in the NIV11

Jeremiah 6 in the NNT

Jeremiah 6 in the NNT2

Jeremiah 6 in the NNT3

Jeremiah 6 in the PDDPT

Jeremiah 6 in the PFNT

Jeremiah 6 in the RMNT

Jeremiah 6 in the SBIAS

Jeremiah 6 in the SBIBS

Jeremiah 6 in the SBIBS2

Jeremiah 6 in the SBICS

Jeremiah 6 in the SBIDS

Jeremiah 6 in the SBIGS

Jeremiah 6 in the SBIHS

Jeremiah 6 in the SBIIS

Jeremiah 6 in the SBIIS2

Jeremiah 6 in the SBIIS3

Jeremiah 6 in the SBIKS

Jeremiah 6 in the SBIKS2

Jeremiah 6 in the SBIMS

Jeremiah 6 in the SBIOS

Jeremiah 6 in the SBIPS

Jeremiah 6 in the SBISS

Jeremiah 6 in the SBITS

Jeremiah 6 in the SBITS2

Jeremiah 6 in the SBITS3

Jeremiah 6 in the SBITS4

Jeremiah 6 in the SBIUS

Jeremiah 6 in the SBIVS

Jeremiah 6 in the SBT

Jeremiah 6 in the SBT1E

Jeremiah 6 in the SCHL

Jeremiah 6 in the SNT

Jeremiah 6 in the SUSU

Jeremiah 6 in the SUSU2

Jeremiah 6 in the SYNO

Jeremiah 6 in the TBIAOTANT

Jeremiah 6 in the TBT1E

Jeremiah 6 in the TBT1E2

Jeremiah 6 in the TFTIP

Jeremiah 6 in the TFTU

Jeremiah 6 in the TGNTATF3T

Jeremiah 6 in the THAI

Jeremiah 6 in the TNFD

Jeremiah 6 in the TNT

Jeremiah 6 in the TNTIK

Jeremiah 6 in the TNTIL

Jeremiah 6 in the TNTIN

Jeremiah 6 in the TNTIP

Jeremiah 6 in the TNTIZ

Jeremiah 6 in the TOMA

Jeremiah 6 in the TTENT

Jeremiah 6 in the UBG

Jeremiah 6 in the UGV

Jeremiah 6 in the UGV2

Jeremiah 6 in the UGV3

Jeremiah 6 in the VBL

Jeremiah 6 in the VDCC

Jeremiah 6 in the YALU

Jeremiah 6 in the YAPE

Jeremiah 6 in the YBVTP

Jeremiah 6 in the ZBP