Nehemiah 9 (BOGWICC)

1 Pa tsiku la 24 la mwezi womwewo, Aisraeli anasonkhana pamodzi ndi kusala chakudya, kuvala ziguduli ndi kudzithira dothi pa mutu. 2 Aisraeliwa anadzipatula pakati pa anthu a mitundu ina ndipo anayimirira nayamba kuwulula machimo awo ndi zolakwa za makolo awo. 3 Anthuwo anayimirira pomwepo, ndipo anamva mawu a mʼbuku la malamulo a Yehova akuwerengedwa kwa maora enanso atatu ndipo anakhala maora ena atatu akuwulula machimo awo ndi kupembedza Yehova Mulungu wawo. 4 Pa makwerero okhalapo alevi anayimirirapo anthu awa: Yesuwa, Bani, Kadimieli, Sebaniya, Buni, Serebiya, Bani ndi Kenani. Iwowa ankapemphera mokweza mawu kwa Yehova Mulungu wawo. 5 Ndipo Alevi awa: Yesuwa, Kadimieli, Bani, Hasabaneya, Serebiya, Hodiya, Sebaniya ndi Petahiya anati: “Imirirani ndipo mutamande Yehova Mulungu wanu, amene ndi wamuyaya.”“Litamandike dzina lake laulemerero limene liposa madalitso ndi matamando onse. 6 Inu nokha ndiye Yehova. Munalenga kumwamba, ngakhale kumwambamwamba, zolengedwa zonse zimene zili mʼmenemo. Munalenga dziko ndi zonse zokhalamo, nyanja ndi zonse zili mʼmenemo. Zonse mumazisunga ndi moyo ndipo zonse za kumwamba zimakupembedzani. 7 “Inu ndinu Yehova Mulungu amene munasankha Abramu ndi kumutulutsa mʼdziko la Uri wa ku Kaldeya ndi kumutcha dzina lake Abrahamu. 8 Inu munaona kuti mtima wake unali wokhulupirika kwa inu, ndipo munapangana naye pangano lakuti mudzapereka kwa zidzukulu zake dziko la Akanaani Ahiti, Aamori, Aperezi, Ayebusi ndi Agirigasi. Inu mwasunga lonjezo lanu chifukwa ndinu wolungama. 9 “Munaona kuzunzika kwa makolo athu ku Igupto. Munamva kufuwula kwawo pa Nyanja Yofiira. 10 Inu munachita zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa kutsutsana ndi Farao, pamaso pa Farao, nduna zake ndi anthu onse a mʼdziko lake, pakuti Inu munadziwa kuti anazunza makolo athu. Inu munadzipangira nokha dzina, monga zilili mpaka lero lino. 11 Inu munagawa nyanja anthu anu akupenya, kotero kuti anadutsa powuma, koma munamiza mʼmadzi akuya anthu amene ankawalondola monga mmene uchitira mwala mʼmadzi ozama. 12 Masana munkawunikira ndi chipilala cha mtambo ndipo usiku munkawunikira ndi chipilala cha moto njira yonse imene ankayendamo. 13 “Munatsika pa Phiri la Sinai, ndipo munawayankhula kuchokera kumwamba. Munawapatsa malangizo olungama, ziphunzitso zoona ndiponso malamulo abwino. 14 Inu munawadziwitsa kuti tsiku lanu la Sabata ndi loyera ndipo munawapatsa malamulo ndi ziphunzitso. 15 Pamene anali ndi njala munawapatsa buledi wochokera kumwamba. Pamene anali ndi ludzu munawapatsa madzi otuluka mʼthanthwe. Munawawuza kuti apite kukalanda dziko limene munalonjeza kuti mudzawapatsa.” 16 “Koma makolo athu anadzikuza ndi kuwumitsa khosi, ndipo iwo sanamvere malamulo anu. 17 Anakana kumvera ndipo sanakumbukire zodabwitsa zimene munachita pakati pawo. Koma iwo anawumitsa khosi, nakuwukirani podzisankhira okha mtsogoleri kuti awatsogolere kubwerera ku ukapolo ku dziko la Igupto. Koma ndinu Mulungu wokhululukira, wokoma mtima ndi wachifundo wosapsa mtima msanga ndi wachikondi chachikulu chosasinthika. Choncho Inu simunawasiye. 18 Ngakhale pamene iwo anadziwumbira fano la mwana wangʼombe ndi kuti, ‘Uyu ndi mulungu wanu amene anakutulutsani mʼdziko la Igupto,’ kapena pamene anachita chipongwe choopsa. 19 “Koma Inu ndi chifundo chanu chachikulu, simunawasiye mʼchipululu. Chipilala cha mtambo sichinasiye kuwatsogolera pa njira yawo masana ndipo chipilala cha moto sichinasiye kuwatsogolera pa njira yawo usiku. 20 Inu munawapatsa mzimu wanu wabwino kuti uwalangize. Inu simunawamane chakudya cha mana chija, ndipo munawapatsa madzi akumwa. 21 Munawasunga zaka makumi anayi mʼchipululu ndipo sanasowe kanthu kalikonse. Zovala zawo sizinathe kapena mapazi awo kutupa.” 22 “Inu munawapatsa mafumu ndi mayiko mʼmanja mwawo. Munawagawiranso mayiko achilendo akutali kwambiri. Munabwera nawo mʼdziko la Sihoni mfumu ya Hesiboni ndi dziko la Ogi mfumu ya Basani kuti alowemo nʼkulitenga kukhala lawo. 23 Munachulukitsa ana awo aamuna ngati nyenyezi za mlengalenga. Ndipo munawabweretsa mʼdziko limene munawuza makolo awo kuti alilowe ndi kulitenga. 24 Choncho zidzukulu zawo zinapita ndi kukalandira dzikolo. Inu munagonjetsa pamaso pawo, Akanaani amene amakhala mʼdzikolo. Inde munapereka mʼmanja mwawo mafumu awo pamodzi ndi anthu a mʼdzikomo kuti achite nawo monga angafunire. 25 Iwo analanda mizinda yotetezedwa ndi dziko lachonde. Anatenganso nyumba zodzaza ndi zinthu zonse zabwino, zitsime zokumbidwa kale, mitengo ya mphesa, mitengo ya olivi ndi mitengo yambiri ya zipatso. Ndipo anadya nakhuta ndipo anali athanzi. Choncho ankakondwa chifukwa cha ubwino wanu wopambana. 26 “Komabe iwo anakhala osamvera ndipo anakuwukirani nafulatira malamulo anu. Anapha aneneri anu, amene anakawadandaulira kuti abwerere kwa Inu. Anachita chipongwe choopsa. 27 Pamene anazunzidwa anafuwulira kwa Inu, ndipo Inu munawamvera muli kumwambako. Ndipo mwa chifundo chanu chachikulu munkawapatsa atsogoleri amene ankawapulumutsa mʼmanja mwa adani awo.” 28 “Koma akangokhala pa mtendere ankayambanso kuchita zoyipa pamaso panu. Choncho munkawapereka mʼmanja mwa adani awo amene ankawalamulira. Komabe pamene ankabwerera ndi kumalira kwa Inu, Inu munkawamva muli kumwambako. Chifukwa cha chifundo chanu chochuluka, nthawi zonse munkawapulumutsa. 29 “Inu munkawachenjeza kuti abwerere ndi kuyamba kutsata malamulo anu. Koma iwo ankadzitukumula ndipo sankamvera malamulo anu. Iwo anachimwira malangizo anu amene munati ‘Amapatsa moyo kwa munthu wowamvera.’ Iwo ankakufulatirani, nawumitsa makosi awo osafuna kukumverani. 30 Munapirira nawo kwa zaka zambiri. Munkawachenjeza ndi Mzimu wanu kudzera mwa aneneri anu, koma iwo sankakumverani. Choncho munawapereka mʼmanja mwa anthu a mayiko ena. 31 Komabe mwachifundo chanu chachikulu simuwatheretu kapena kuwataya pakuti ndinu Mulungu wokoma mtima ndi wachifundo. 32 “Nʼchifukwa chake, tsono, Inu Mulungu wathu, Mulungu wamkulu, wamphamvu ndi woopsa kwambiri mumasunga pangano ndi chikondi chosasinthika. Musalole kuti mavuto onse amene atigwera ife, mafumu athu, atsogoleri athu, ansembe athu, aneneri athu, makolo athu ndi anthu ena onse kuyambira nthawi ya mafumu a ku Asiriya mpaka lero aoneke ochepa pamaso panu. 33 Koma Inu mwakhala wolungama pa zonse zimene zakhala zikutichitikira. Mwachita zokhulupirika, koma ife tachita zolakwa. 34 Ndipotu mafumu athu, atsogoleri athu, ansembe athu ndi makolo athu sanatsatire mawu anu. Iwo sanalabadire za malamulo anu ngakhale mawu anu owachenjeza amene munawapatsa. 35 Ngakhale ankadzilamulira okha, nʼkumalandira zabwino zochuluka mʼdziko lalikulu ndi lachonde limene munawapatsa, koma iwo sanakutumikireni kapena kusiya ntchito zawo zoyipa. 36 “Tsono, taonani! Ife lero ndife akapolo, ndife akapolo mʼdziko limene munapereka kwa makolo athu kuti azidya zipatso zake ndi zabwino zake zonse. 37 Tsono chifukwa cha machimo athu, mafumu amene munawayika kuti azitilamulira angodzilemeretsa ndi chuma chambiri cha dzikoli. Iwo ali ndi mphamvu zolamulira matupi athu ndi ngʼombe zathu momwe afunira. Zedi, ife tili mʼmavuto aakulu.” 38 “Chifukwa cha zonsezi, ife tikuchita mgwirizano wokhazikika, pochita kulemba, ndipo atsogoleri athu, Alevi athu ndi ansembe athu asindikiza chidindo chawo pa mgwirizanowo.”

In Other Versions

Nehemiah 9 in the ANGEFD

Nehemiah 9 in the ANTPNG2D

Nehemiah 9 in the AS21

Nehemiah 9 in the BAGH

Nehemiah 9 in the BBPNG

Nehemiah 9 in the BBT1E

Nehemiah 9 in the BDS

Nehemiah 9 in the BEV

Nehemiah 9 in the BHAD

Nehemiah 9 in the BIB

Nehemiah 9 in the BLPT

Nehemiah 9 in the BNT

Nehemiah 9 in the BNTABOOT

Nehemiah 9 in the BNTLV

Nehemiah 9 in the BOATCB

Nehemiah 9 in the BOATCB2

Nehemiah 9 in the BOBCV

Nehemiah 9 in the BOCNT

Nehemiah 9 in the BOECS

Nehemiah 9 in the BOHCB

Nehemiah 9 in the BOHCV

Nehemiah 9 in the BOHLNT

Nehemiah 9 in the BOHNTLTAL

Nehemiah 9 in the BOICB

Nehemiah 9 in the BOILNTAP

Nehemiah 9 in the BOITCV

Nehemiah 9 in the BOKCV

Nehemiah 9 in the BOKCV2

Nehemiah 9 in the BOKHWOG

Nehemiah 9 in the BOKSSV

Nehemiah 9 in the BOLCB

Nehemiah 9 in the BOLCB2

Nehemiah 9 in the BOMCV

Nehemiah 9 in the BONAV

Nehemiah 9 in the BONCB

Nehemiah 9 in the BONLT

Nehemiah 9 in the BONUT2

Nehemiah 9 in the BOPLNT

Nehemiah 9 in the BOSCB

Nehemiah 9 in the BOSNC

Nehemiah 9 in the BOTLNT

Nehemiah 9 in the BOVCB

Nehemiah 9 in the BOYCB

Nehemiah 9 in the BPBB

Nehemiah 9 in the BPH

Nehemiah 9 in the BSB

Nehemiah 9 in the CCB

Nehemiah 9 in the CUV

Nehemiah 9 in the CUVS

Nehemiah 9 in the DBT

Nehemiah 9 in the DGDNT

Nehemiah 9 in the DHNT

Nehemiah 9 in the DNT

Nehemiah 9 in the ELBE

Nehemiah 9 in the EMTV

Nehemiah 9 in the ESV

Nehemiah 9 in the FBV

Nehemiah 9 in the FEB

Nehemiah 9 in the GGMNT

Nehemiah 9 in the GNT

Nehemiah 9 in the HARY

Nehemiah 9 in the HNT

Nehemiah 9 in the IRVA

Nehemiah 9 in the IRVB

Nehemiah 9 in the IRVG

Nehemiah 9 in the IRVH

Nehemiah 9 in the IRVK

Nehemiah 9 in the IRVM

Nehemiah 9 in the IRVM2

Nehemiah 9 in the IRVO

Nehemiah 9 in the IRVP

Nehemiah 9 in the IRVT

Nehemiah 9 in the IRVT2

Nehemiah 9 in the IRVU

Nehemiah 9 in the ISVN

Nehemiah 9 in the JSNT

Nehemiah 9 in the KAPI

Nehemiah 9 in the KBT1ETNIK

Nehemiah 9 in the KBV

Nehemiah 9 in the KJV

Nehemiah 9 in the KNFD

Nehemiah 9 in the LBA

Nehemiah 9 in the LBLA

Nehemiah 9 in the LNT

Nehemiah 9 in the LSV

Nehemiah 9 in the MAAL

Nehemiah 9 in the MBV

Nehemiah 9 in the MBV2

Nehemiah 9 in the MHNT

Nehemiah 9 in the MKNFD

Nehemiah 9 in the MNG

Nehemiah 9 in the MNT

Nehemiah 9 in the MNT2

Nehemiah 9 in the MRS1T

Nehemiah 9 in the NAA

Nehemiah 9 in the NASB

Nehemiah 9 in the NBLA

Nehemiah 9 in the NBS

Nehemiah 9 in the NBVTP

Nehemiah 9 in the NET2

Nehemiah 9 in the NIV11

Nehemiah 9 in the NNT

Nehemiah 9 in the NNT2

Nehemiah 9 in the NNT3

Nehemiah 9 in the PDDPT

Nehemiah 9 in the PFNT

Nehemiah 9 in the RMNT

Nehemiah 9 in the SBIAS

Nehemiah 9 in the SBIBS

Nehemiah 9 in the SBIBS2

Nehemiah 9 in the SBICS

Nehemiah 9 in the SBIDS

Nehemiah 9 in the SBIGS

Nehemiah 9 in the SBIHS

Nehemiah 9 in the SBIIS

Nehemiah 9 in the SBIIS2

Nehemiah 9 in the SBIIS3

Nehemiah 9 in the SBIKS

Nehemiah 9 in the SBIKS2

Nehemiah 9 in the SBIMS

Nehemiah 9 in the SBIOS

Nehemiah 9 in the SBIPS

Nehemiah 9 in the SBISS

Nehemiah 9 in the SBITS

Nehemiah 9 in the SBITS2

Nehemiah 9 in the SBITS3

Nehemiah 9 in the SBITS4

Nehemiah 9 in the SBIUS

Nehemiah 9 in the SBIVS

Nehemiah 9 in the SBT

Nehemiah 9 in the SBT1E

Nehemiah 9 in the SCHL

Nehemiah 9 in the SNT

Nehemiah 9 in the SUSU

Nehemiah 9 in the SUSU2

Nehemiah 9 in the SYNO

Nehemiah 9 in the TBIAOTANT

Nehemiah 9 in the TBT1E

Nehemiah 9 in the TBT1E2

Nehemiah 9 in the TFTIP

Nehemiah 9 in the TFTU

Nehemiah 9 in the TGNTATF3T

Nehemiah 9 in the THAI

Nehemiah 9 in the TNFD

Nehemiah 9 in the TNT

Nehemiah 9 in the TNTIK

Nehemiah 9 in the TNTIL

Nehemiah 9 in the TNTIN

Nehemiah 9 in the TNTIP

Nehemiah 9 in the TNTIZ

Nehemiah 9 in the TOMA

Nehemiah 9 in the TTENT

Nehemiah 9 in the UBG

Nehemiah 9 in the UGV

Nehemiah 9 in the UGV2

Nehemiah 9 in the UGV3

Nehemiah 9 in the VBL

Nehemiah 9 in the VDCC

Nehemiah 9 in the YALU

Nehemiah 9 in the YAPE

Nehemiah 9 in the YBVTP

Nehemiah 9 in the ZBP