Philippians 2 (BOGWICC)

1 Ngati muli ndi chilimbikitso chilichonse chifukwa cholumikizana ndi Khristu, ngati muli ndi chitonthozo chifukwa cha chikondi chake, ngati muli ndi mtima umodzi mwa Mzimu, ndipo ngati mumakomerana mtima ndi kuchitirana chifundo, 2 tsono tsirizani chimwemwe changa pokhala amaganizo ofanana, achikondi chimodzimodzi, amodzi mu mzimu ndi acholinga chimodzinso. 3 Musachite kalikonse ndi mtima odzikonda chabe kapena odzitukumula chabe. Koma khalani odzichepetsa ndipo aliyense aziona mnzake ngati womuposa iyeyo. 4 Musamangofuna zokomera inu nokha koma aliyense azifuna zokomeranso ena. 5 Pa ubale wanu wina ndi mnzake, mukhale ndi mtima wofanana ndi wa Khristu Yesu: 6 Iyeyu, pokhala Mulungu ndithu,sanatenge kufanana ndi Mulungu kukhala chinthu choyenera kuchigwiritsa. 7 Koma anadzichepetsa kotheratunakhala ndi khalidwe ngati la kapolondi kukhala munthu ngati anthu ena onse. 8 Ndipo pokhala munthu chonchoanadzichepetsa yekhandipo anamvera mpaka imfa yake,imfa yake ya pamtanda! 9 Choncho Mulungu anamukweza Iye kukhala wapamwamba kwambiri,ndipo anamupatsa dzina loposa dzina lina lililonse 10 kuti pakumva dzina la Yesu, bondo lililonse limugwadire,kumwamba ndi pa dziko lapansi ndi pansi pa dziko, 11 ndipo lilime lililonse livomereze kuti Yesu Khristu ndi Ambuyekuchitira ulemu Mulungu Atate. 12 Tsono, abwenzi anga okondedwa, monga mwakhala omvera nthawi zonse, osati pamene ndinali nanu pokha, koma tsopano koposa pamene ndili kutali. Pitirizani kugwira ntchito ya chipulumutso chanu mwa mantha ndi kunjenjemera, 13 pakuti ndi Mulungu amene amagwira ntchito mwa inu kuti mufune ndi kuchita zimene zimamukondweretsa Iyeyo. 14 Muzichita zonse mosawiringula kapena mosatsutsapo, 15 kuti mukhale wopanda cholakwa ndi angwiro, ana a Mulungu wopanda cholakwika mu mʼbado uno wachinyengo ndi wosocheretsa. Mukatero mudzawala pakati pawo ngati nyenyezi zakumwamba 16 powawuza mawu amoyo. Ndipo ine ndidzatha kunyadira pa tsiku la Khristu kuti sindinathamange kapena kugwira ntchito pachabe. 17 Koma ngakhale ndikuthiridwa ngati nsembe ya chakumwa yoperekedwa pa nsembe ndi pa utumiki wochokera mʼchikhulupiriro chanu, ndine wokondwa ndi wosangalala pamodzi ndi inu nonse. 18 Chomwechonso, inu khalani okondwa ndi osangalala nane pamodzi. 19 Ngati Ambuye Yesu alola, ndikukhulupirira kuti ndidzamutuma Timoteyo msanga kwanuko, kuti mwina ndingadzasangalale ndikadzamva za moyo wanu. 20 Ndilibenso wina monga iyeyu amene ali ndi chidwi chenicheni pa za moyo wanu. 21 Pakuti aliyense amangofuna zokomera iye yekha osati zokomera Yesu Khristu. 22 Koma inu mukudziwa kuti Timoteyo wadzionetsa yekha, chifukwa watumikira ndi ine pa ntchito ya Uthenga Wabwino monga mwana ndi abambo ake. 23 Choncho ndikuyembekezera kumutuma msanga ndikangodziwa mmene zinthu zanga ziyendere. 24 Ndipo ndikukhulupirira kuti Ambuye akalola ine mwini ndidzafikanso kwanuko posachedwapa. 25 Koma ndikuganiza kuti nʼkofunika kuti ndikutumizireni mʼbale wanga Epafrodito, mtumiki mnzanga ndi msilikali mnzanga, amenenso ndi mtumiki wanu amene munamutumiza kuti adzandithandize pa zosowa zanga. 26 Pakuti akukulakalakani nonsenu ndipo akusauka mu mtima chifukwa munamva kuti akudwala. 27 Zoonadi ankadwala ndipo anatsala pangʼono kumwalira. Koma Mulungu anamuchitira chifundo, ndipo sanangomuchitira chifundo iye yekhayu komanso ine, kuti chisoni changa chisachuluke. 28 Choncho khumbo langa lofulumiza kumutumiza lakula, kuti pamene mumuonenso musangalale komanso kuti nkhawa yanga ichepe. 29 Mulandireni mwa Ambuye ndi chimwemwe chachikulu, ndipo anthu onga iyeyu muziwachitira ulemu. 30 Iyeyu anatsala pangʼono kufa chifukwa cha ntchito ya Khristu, anayika moyo pa chiswe kuti akwaniritse thandizo limene inu simukanatha.

In Other Versions

Philippians 2 in the ANGEFD

Philippians 2 in the ANTPNG2D

Philippians 2 in the AS21

Philippians 2 in the BAGH

Philippians 2 in the BBPNG

Philippians 2 in the BBT1E

Philippians 2 in the BDS

Philippians 2 in the BEV

Philippians 2 in the BHAD

Philippians 2 in the BIB

Philippians 2 in the BLPT

Philippians 2 in the BNT

Philippians 2 in the BNTABOOT

Philippians 2 in the BNTLV

Philippians 2 in the BOATCB

Philippians 2 in the BOATCB2

Philippians 2 in the BOBCV

Philippians 2 in the BOCNT

Philippians 2 in the BOECS

Philippians 2 in the BOHCB

Philippians 2 in the BOHCV

Philippians 2 in the BOHLNT

Philippians 2 in the BOHNTLTAL

Philippians 2 in the BOICB

Philippians 2 in the BOILNTAP

Philippians 2 in the BOITCV

Philippians 2 in the BOKCV

Philippians 2 in the BOKCV2

Philippians 2 in the BOKHWOG

Philippians 2 in the BOKSSV

Philippians 2 in the BOLCB

Philippians 2 in the BOLCB2

Philippians 2 in the BOMCV

Philippians 2 in the BONAV

Philippians 2 in the BONCB

Philippians 2 in the BONLT

Philippians 2 in the BONUT2

Philippians 2 in the BOPLNT

Philippians 2 in the BOSCB

Philippians 2 in the BOSNC

Philippians 2 in the BOTLNT

Philippians 2 in the BOVCB

Philippians 2 in the BOYCB

Philippians 2 in the BPBB

Philippians 2 in the BPH

Philippians 2 in the BSB

Philippians 2 in the CCB

Philippians 2 in the CUV

Philippians 2 in the CUVS

Philippians 2 in the DBT

Philippians 2 in the DGDNT

Philippians 2 in the DHNT

Philippians 2 in the DNT

Philippians 2 in the ELBE

Philippians 2 in the EMTV

Philippians 2 in the ESV

Philippians 2 in the FBV

Philippians 2 in the FEB

Philippians 2 in the GGMNT

Philippians 2 in the GNT

Philippians 2 in the HARY

Philippians 2 in the HNT

Philippians 2 in the IRVA

Philippians 2 in the IRVB

Philippians 2 in the IRVG

Philippians 2 in the IRVH

Philippians 2 in the IRVK

Philippians 2 in the IRVM

Philippians 2 in the IRVM2

Philippians 2 in the IRVO

Philippians 2 in the IRVP

Philippians 2 in the IRVT

Philippians 2 in the IRVT2

Philippians 2 in the IRVU

Philippians 2 in the ISVN

Philippians 2 in the JSNT

Philippians 2 in the KAPI

Philippians 2 in the KBT1ETNIK

Philippians 2 in the KBV

Philippians 2 in the KJV

Philippians 2 in the KNFD

Philippians 2 in the LBA

Philippians 2 in the LBLA

Philippians 2 in the LNT

Philippians 2 in the LSV

Philippians 2 in the MAAL

Philippians 2 in the MBV

Philippians 2 in the MBV2

Philippians 2 in the MHNT

Philippians 2 in the MKNFD

Philippians 2 in the MNG

Philippians 2 in the MNT

Philippians 2 in the MNT2

Philippians 2 in the MRS1T

Philippians 2 in the NAA

Philippians 2 in the NASB

Philippians 2 in the NBLA

Philippians 2 in the NBS

Philippians 2 in the NBVTP

Philippians 2 in the NET2

Philippians 2 in the NIV11

Philippians 2 in the NNT

Philippians 2 in the NNT2

Philippians 2 in the NNT3

Philippians 2 in the PDDPT

Philippians 2 in the PFNT

Philippians 2 in the RMNT

Philippians 2 in the SBIAS

Philippians 2 in the SBIBS

Philippians 2 in the SBIBS2

Philippians 2 in the SBICS

Philippians 2 in the SBIDS

Philippians 2 in the SBIGS

Philippians 2 in the SBIHS

Philippians 2 in the SBIIS

Philippians 2 in the SBIIS2

Philippians 2 in the SBIIS3

Philippians 2 in the SBIKS

Philippians 2 in the SBIKS2

Philippians 2 in the SBIMS

Philippians 2 in the SBIOS

Philippians 2 in the SBIPS

Philippians 2 in the SBISS

Philippians 2 in the SBITS

Philippians 2 in the SBITS2

Philippians 2 in the SBITS3

Philippians 2 in the SBITS4

Philippians 2 in the SBIUS

Philippians 2 in the SBIVS

Philippians 2 in the SBT

Philippians 2 in the SBT1E

Philippians 2 in the SCHL

Philippians 2 in the SNT

Philippians 2 in the SUSU

Philippians 2 in the SUSU2

Philippians 2 in the SYNO

Philippians 2 in the TBIAOTANT

Philippians 2 in the TBT1E

Philippians 2 in the TBT1E2

Philippians 2 in the TFTIP

Philippians 2 in the TFTU

Philippians 2 in the TGNTATF3T

Philippians 2 in the THAI

Philippians 2 in the TNFD

Philippians 2 in the TNT

Philippians 2 in the TNTIK

Philippians 2 in the TNTIL

Philippians 2 in the TNTIN

Philippians 2 in the TNTIP

Philippians 2 in the TNTIZ

Philippians 2 in the TOMA

Philippians 2 in the TTENT

Philippians 2 in the UBG

Philippians 2 in the UGV

Philippians 2 in the UGV2

Philippians 2 in the UGV3

Philippians 2 in the VBL

Philippians 2 in the VDCC

Philippians 2 in the YALU

Philippians 2 in the YAPE

Philippians 2 in the YBVTP

Philippians 2 in the ZBP