Psalms 22 (BOGWICC)
undefined Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa “Mbawala yayikazi ya Mmawa.” Salimo la Davide. 1 Mulungu wanga, Mulungu wanga, nʼchifukwa chiyani mwandisiya?Chifuwa chiyani simukundithandiza ndi pangʼono pomwe?Nʼchifukwa chiyani simukumva mawu a kudandaula kwanga? 2 Inu Mulungu wanga, ine ndimalira masana, koma simuyankha,usikunso, ndipo sindikhala chete. 3 Inu ndinu Woyera, wokhala pa mpando waufumu;ndinu matamando a Israeli. 4 Pa inu makolo athu anadalira;iwo anadalira ndipo Inu munawapulumutsa. 5 Analirira kwa inu ndipo munawapulumutsa.Iwo anakhulupirira Inu ndipo simunawakhumudwitse. 6 Koma ine ndine nyongolotsi osati munthu,wosekedwa ndi wonyozedwa ndi anthu onse. 7 Onse amene amandiona amandiseka;amandiyankhulira mawu achipongwe akupukusa mitu yawo kunena kuti 8 “Iyeyu amadalira Yehova,musiyeni Yehovayo amulanditse.Musiyeni Yehova amupulumutsepopeza amakondwera mwa Yehovayo.” 9 Komabe Inu ndinu amene munandibadwitsa, munanditulutsa mʼmimba mwa amayi anga.Munachititsa kuti ndizikudaliraningakhale pa nthawi imene ndinkayamwa. 10 Chibadwire ine ndinaperekedwa kwa Inu;kuchokera mʼmimba mwa amayi anga Inu mwakhala muli Mulungu wanga. 11 Musakhale kutali ndi ine,pakuti mavuto ali pafupindipo palibe wina wondipulumutsa. 12 Ngʼombe zazimuna zandizungulira;ngʼombe zazimuna zamphamvu za ku Basani zandizinga. 13 Mikango yobangula pokadzula nyama,yatsekula kwambiri pakamwa pawo kulimbana nane. 14 Ine ndatayika pansi ngati madzindipo mafupa anga onse achoka mʼmalo mwake.Mtima wanga wasanduka phula;wasungunuka mʼkati mwanga. 15 Mphamvu zanga zauma ngati phale,ndipo lilime langa lamamatira ku nsagwada;mwandigoneka mʼfumbi la imfa. 16 Agalu andizungulira;gulu la anthu oyipa landizinga.Alasa manja ndi mapazi anga. 17 Ine nditha kuwerenga mafupa anga onse;anthu amandiyangʼanitsitsa ndi kundidzuma. 18 Iwo agawana zovala zanga pakati pawondi kuchita maere pa zovala zangazo. 19 Koma Inu Yehova, musakhale kutali;Inu mphamvu yanga, bwerani msanga kuti mudzandithandize. 20 Pulumutsani moyo wanga ku lupanga,moyo wanga wopambanawu ku mphamvu ya agalu. 21 Ndilanditseni mʼkamwa mwa mikango;pulumutseni ku nyanga za njati. 22 Ine ndidzalengeza dzina lanu kwa abale anga;ndidzakutamandani mu msonkhano. 23 Inu amene mumaopa Yehova mutamandeni!Inu zidzukulu zonse za Yakobo, mulemekezeni!Muopeni mwaulemu, inu zidzukulu zonse za Israeli! 24 Pakuti Iye sanapeputse kapena kunyozakuvutika kwa wosautsidwayo;Iye sanabise nkhope yake kwa iye.Koma anamvera kulira kwake kofuna thandizo. 25 Ndidzakutamandani pa msonkhano waukulu chifukwa cha zimene mwandichitira.Ndidzakwaniritsa lonjezo langa pamaso pa amene amaopa Inu. 26 Osauka adzadya ndipo adzakhuta;iwo amene amafunafuna Yehova adzamutamanda.Mitima yanu ikhale ndi moyo mpaka muyaya! 27 Malekezero onse a dziko lapansiadzakumbukira Yehova ndi kutembenukira kwa Iye,ndipo mabanja a mitundu ya anthuadzawerama pamaso pake, 28 pakuti ulamuliro ndi wake wa Yehovandipo Iye amalamulira anthu a mitundu yonse. 29 Anthu olemera onse a dziko lapansi adzachita phwando ndi kulambira;onse amene amapita ku fumbi adzagwada pamaso pake;iwo amene sangathe kudzisunga okha ndi moyo. 30 Zidzukulu zamʼtsogolo zidzamutumikira Iye;mibado ya mʼtsogolo idzawuzidwa za Ambuye. 31 Iwo adzalengeza za chilungamo chakekwa anthu amene pano sanabadwepakuti Iye wachita zimenezi.
In Other Versions
Psalms 22 in the ANGEFD
Psalms 22 in the ANTPNG2D
Psalms 22 in the AS21
Psalms 22 in the BAGH
Psalms 22 in the BBPNG
Psalms 22 in the BBT1E
Psalms 22 in the BDS
Psalms 22 in the BEV
Psalms 22 in the BHAD
Psalms 22 in the BIB
Psalms 22 in the BLPT
Psalms 22 in the BNT
Psalms 22 in the BNTABOOT
Psalms 22 in the BNTLV
Psalms 22 in the BOATCB
Psalms 22 in the BOATCB2
Psalms 22 in the BOBCV
Psalms 22 in the BOCNT
Psalms 22 in the BOECS
Psalms 22 in the BOHCB
Psalms 22 in the BOHCV
Psalms 22 in the BOHLNT
Psalms 22 in the BOHNTLTAL
Psalms 22 in the BOICB
Psalms 22 in the BOILNTAP
Psalms 22 in the BOITCV
Psalms 22 in the BOKCV
Psalms 22 in the BOKCV2
Psalms 22 in the BOKHWOG
Psalms 22 in the BOKSSV
Psalms 22 in the BOLCB
Psalms 22 in the BOLCB2
Psalms 22 in the BOMCV
Psalms 22 in the BONAV
Psalms 22 in the BONCB
Psalms 22 in the BONLT
Psalms 22 in the BONUT2
Psalms 22 in the BOPLNT
Psalms 22 in the BOSCB
Psalms 22 in the BOSNC
Psalms 22 in the BOTLNT
Psalms 22 in the BOVCB
Psalms 22 in the BOYCB
Psalms 22 in the BPBB
Psalms 22 in the BPH
Psalms 22 in the BSB
Psalms 22 in the CCB
Psalms 22 in the CUV
Psalms 22 in the CUVS
Psalms 22 in the DBT
Psalms 22 in the DGDNT
Psalms 22 in the DHNT
Psalms 22 in the DNT
Psalms 22 in the ELBE
Psalms 22 in the EMTV
Psalms 22 in the ESV
Psalms 22 in the FBV
Psalms 22 in the FEB
Psalms 22 in the GGMNT
Psalms 22 in the GNT
Psalms 22 in the HARY
Psalms 22 in the HNT
Psalms 22 in the IRVA
Psalms 22 in the IRVB
Psalms 22 in the IRVG
Psalms 22 in the IRVH
Psalms 22 in the IRVK
Psalms 22 in the IRVM
Psalms 22 in the IRVM2
Psalms 22 in the IRVO
Psalms 22 in the IRVP
Psalms 22 in the IRVT
Psalms 22 in the IRVT2
Psalms 22 in the IRVU
Psalms 22 in the ISVN
Psalms 22 in the JSNT
Psalms 22 in the KAPI
Psalms 22 in the KBT1ETNIK
Psalms 22 in the KBV
Psalms 22 in the KJV
Psalms 22 in the KNFD
Psalms 22 in the LBA
Psalms 22 in the LBLA
Psalms 22 in the LNT
Psalms 22 in the LSV
Psalms 22 in the MAAL
Psalms 22 in the MBV
Psalms 22 in the MBV2
Psalms 22 in the MHNT
Psalms 22 in the MKNFD
Psalms 22 in the MNG
Psalms 22 in the MNT
Psalms 22 in the MNT2
Psalms 22 in the MRS1T
Psalms 22 in the NAA
Psalms 22 in the NASB
Psalms 22 in the NBLA
Psalms 22 in the NBS
Psalms 22 in the NBVTP
Psalms 22 in the NET2
Psalms 22 in the NIV11
Psalms 22 in the NNT
Psalms 22 in the NNT2
Psalms 22 in the NNT3
Psalms 22 in the PDDPT
Psalms 22 in the PFNT
Psalms 22 in the RMNT
Psalms 22 in the SBIAS
Psalms 22 in the SBIBS
Psalms 22 in the SBIBS2
Psalms 22 in the SBICS
Psalms 22 in the SBIDS
Psalms 22 in the SBIGS
Psalms 22 in the SBIHS
Psalms 22 in the SBIIS
Psalms 22 in the SBIIS2
Psalms 22 in the SBIIS3
Psalms 22 in the SBIKS
Psalms 22 in the SBIKS2
Psalms 22 in the SBIMS
Psalms 22 in the SBIOS
Psalms 22 in the SBIPS
Psalms 22 in the SBISS
Psalms 22 in the SBITS
Psalms 22 in the SBITS2
Psalms 22 in the SBITS3
Psalms 22 in the SBITS4
Psalms 22 in the SBIUS
Psalms 22 in the SBIVS
Psalms 22 in the SBT
Psalms 22 in the SBT1E
Psalms 22 in the SCHL
Psalms 22 in the SNT
Psalms 22 in the SUSU
Psalms 22 in the SUSU2
Psalms 22 in the SYNO
Psalms 22 in the TBIAOTANT
Psalms 22 in the TBT1E
Psalms 22 in the TBT1E2
Psalms 22 in the TFTIP
Psalms 22 in the TFTU
Psalms 22 in the TGNTATF3T
Psalms 22 in the THAI
Psalms 22 in the TNFD
Psalms 22 in the TNT
Psalms 22 in the TNTIK
Psalms 22 in the TNTIL
Psalms 22 in the TNTIN
Psalms 22 in the TNTIP
Psalms 22 in the TNTIZ
Psalms 22 in the TOMA
Psalms 22 in the TTENT
Psalms 22 in the UBG
Psalms 22 in the UGV
Psalms 22 in the UGV2
Psalms 22 in the UGV3
Psalms 22 in the VBL
Psalms 22 in the VDCC
Psalms 22 in the YALU
Psalms 22 in the YAPE
Psalms 22 in the YBVTP
Psalms 22 in the ZBP