Psalms 69 (BOGWICC)

undefined Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Potsata mayimbidwe a “Akakombo.” 1 Pulumutseni Inu Mulungu,pakuti madzi afika mʼkhosi 2 Ine ndikumira mʼthope lozamamʼmene mulibe popondapo.Ndalowa mʼmadzi ozama;mafunde andimiza. 3 Ndafowoka ndikupempha chithandizo;kummero kwanga kwawuma gwaa,mʼmaso mwanga mwadakuyembekezera Mulungu wanga. 4 Iwo amene amadana nane popanda chifukwandi ochuluka kuposa tsitsi la kumutu kwanga;ambiri ndi adani anga popanda chifukwa,iwo amene akufunafuna kundiwononga.Ndikukakamizidwa kubwezerazomwe sindinabe. 5 Mukudziwa uchitsiru wanga, Inu Mulungu,kulakwa kwanga sikuli kobisika kwa Inu. 6 Iwo amene amadalira Inuasanyozedwe chifukwa cha ine,Inu Ambuye Wamphamvuzonse.Iwo amene amafunafuna Inuasachititsidwe manyazi chifukwa cha ine,Inu Mulungu wa Israeli. 7 Pakuti ndimapirira kunyozedwa chifukwa cha Inu,ndipo manyazi amaphimba nkhope yanga. 8 Ndine mlendo kwa abale anga,munthu wakudza kwa ana aamuna a amayi anga; 9 pakuti changu chochitira nyumba yanu chandiphetsandipo chipongwe cha iwo amene amanyoza Inu chandigwera. 10 Pamene ndikulira ndi kusala kudya,ndiyenera kupirira kunyozedwa; 11 pomwe ndavala chiguduli,anthu amandiseweretsa. 12 Iwo amene amakhala pa chipata amandinena,ndipo ine ndine nyimbo ya zidakwa. 13 Koma ndikupempha kwa Inu Ambuye,pa nthawi yanu yondikomera mtima;mwa chikondi chanu chachikuluInu Mulungu, mundiyankhe pondipulumutsa. 14 Mundilanditse kuchoka mʼmatope,musalole kuti ndimire,pulumutseni ine kwa iwoamene amadana nane, kuchoka mʼmadzi ozama. 15 Musalole kuti chigumula chindimeze,kuya kusandimezendipo dzenje lisatseke pakamwa pake kundimiza. 16 Ndiyankheni Inu Yehova mwa ubwino wanu wa chikondi chanu;mwa chifundo chanu chachikulu tembenukirani kwa ine. 17 Musabisire nkhope yanu mtumiki wanu,ndiyankheni msanga, pakuti ndili pa mavuto. 18 Bwerani pafupi ndi kundilanditsa;ndiwomboleni chifukwa cha adani anga. 19 Inu mukudziwa momwe ndanyozedwera,kunyozedwa ndi kuchititsidwa manyazi; adani anga onse ali pamaso panu. 20 Mnyozo waswa mtima wangandipo wandisiya wopanda thandizo lililonse;ndinafunafuna ena woti andichitire chisoni,koma panalibe ndi mmodzi yemwe woti anditonthoze, sindinapeze ndi mmodzi yemwe. 21 Iwo anayika ndulu mʼchakudya changandi kundipatsa vinyo wosasa chifukwa cha ludzu. 22 Chakudya chomwe chayikidwa patsogolo pawo chikhale msampha;chikhale chobwezera chilango ndiponso khwekhwe. 23 Maso awo adetsedwe kotero kuti asaonensondipo misana yawo ipindike mpaka kalekale. 24 Khuthulirani ukali wanu pa iwo;mkwiyo wanu woyaka moto uwathe mphamvu. 25 Malo awo akhale wopanda anthupasapezeke ndi mmodzi yemwe wokhala mʼmatenti awo. 26 Pakuti iwo amazunza amene inu munamuvulazandi kuyankhula zowawa kwa amene munawapweteka. 27 Awonjezereni kulakwa pa kulakwa kwawo,musalole kuti akhale ndi gawo pa chipulumutso chanu. 28 Iwo afufutidwe mʼbuku la amoyondipo asalembedwe pamodzi ndi olungama. 29 Ndikumva zowawa ndi kuzunzika;lolani chipulumutso chanu, Inu Mulungu, chinditeteze. 30 Ine ndidzatamanda dzina la Mulungu mʼnyimbo,ndidzalemekeza Iye ndi chiyamiko. 31 Izi zidzakondweretsa Yehova kupambana ngʼombe,kupambananso ngʼombe yayimuna, pamodzi ndi nyanga ndi ziboda zake. 32 Wosauka adzaona ndipo adzasangalala,Inu amene mumafunafuna Mulungu, mitima yanu ikhale ndi moyo! 33 Yehova amamvera anthu osowandipo sanyoza anthu ake omangidwa. 34 Kumwamba ndi dziko lapansi zitamanda Iye,nyanja ndi zonse zomwe zimayenda mʼmenemo, 35 pakuti Mulungu adzapulumutsa Ziyonindi kumanganso mizinda ya Yuda,anthu adzakhala kumeneko ndipo dzikolo lidzakhala lawo; 36 ana atumiki ake adzalitenga kukhala cholowa chawo,ndipo iwo amene amakonda dzina lake adzakhala kumeneko.

In Other Versions

Psalms 69 in the ANGEFD

Psalms 69 in the ANTPNG2D

Psalms 69 in the AS21

Psalms 69 in the BAGH

Psalms 69 in the BBPNG

Psalms 69 in the BBT1E

Psalms 69 in the BDS

Psalms 69 in the BEV

Psalms 69 in the BHAD

Psalms 69 in the BIB

Psalms 69 in the BLPT

Psalms 69 in the BNT

Psalms 69 in the BNTABOOT

Psalms 69 in the BNTLV

Psalms 69 in the BOATCB

Psalms 69 in the BOATCB2

Psalms 69 in the BOBCV

Psalms 69 in the BOCNT

Psalms 69 in the BOECS

Psalms 69 in the BOHCB

Psalms 69 in the BOHCV

Psalms 69 in the BOHLNT

Psalms 69 in the BOHNTLTAL

Psalms 69 in the BOICB

Psalms 69 in the BOILNTAP

Psalms 69 in the BOITCV

Psalms 69 in the BOKCV

Psalms 69 in the BOKCV2

Psalms 69 in the BOKHWOG

Psalms 69 in the BOKSSV

Psalms 69 in the BOLCB

Psalms 69 in the BOLCB2

Psalms 69 in the BOMCV

Psalms 69 in the BONAV

Psalms 69 in the BONCB

Psalms 69 in the BONLT

Psalms 69 in the BONUT2

Psalms 69 in the BOPLNT

Psalms 69 in the BOSCB

Psalms 69 in the BOSNC

Psalms 69 in the BOTLNT

Psalms 69 in the BOVCB

Psalms 69 in the BOYCB

Psalms 69 in the BPBB

Psalms 69 in the BPH

Psalms 69 in the BSB

Psalms 69 in the CCB

Psalms 69 in the CUV

Psalms 69 in the CUVS

Psalms 69 in the DBT

Psalms 69 in the DGDNT

Psalms 69 in the DHNT

Psalms 69 in the DNT

Psalms 69 in the ELBE

Psalms 69 in the EMTV

Psalms 69 in the ESV

Psalms 69 in the FBV

Psalms 69 in the FEB

Psalms 69 in the GGMNT

Psalms 69 in the GNT

Psalms 69 in the HARY

Psalms 69 in the HNT

Psalms 69 in the IRVA

Psalms 69 in the IRVB

Psalms 69 in the IRVG

Psalms 69 in the IRVH

Psalms 69 in the IRVK

Psalms 69 in the IRVM

Psalms 69 in the IRVM2

Psalms 69 in the IRVO

Psalms 69 in the IRVP

Psalms 69 in the IRVT

Psalms 69 in the IRVT2

Psalms 69 in the IRVU

Psalms 69 in the ISVN

Psalms 69 in the JSNT

Psalms 69 in the KAPI

Psalms 69 in the KBT1ETNIK

Psalms 69 in the KBV

Psalms 69 in the KJV

Psalms 69 in the KNFD

Psalms 69 in the LBA

Psalms 69 in the LBLA

Psalms 69 in the LNT

Psalms 69 in the LSV

Psalms 69 in the MAAL

Psalms 69 in the MBV

Psalms 69 in the MBV2

Psalms 69 in the MHNT

Psalms 69 in the MKNFD

Psalms 69 in the MNG

Psalms 69 in the MNT

Psalms 69 in the MNT2

Psalms 69 in the MRS1T

Psalms 69 in the NAA

Psalms 69 in the NASB

Psalms 69 in the NBLA

Psalms 69 in the NBS

Psalms 69 in the NBVTP

Psalms 69 in the NET2

Psalms 69 in the NIV11

Psalms 69 in the NNT

Psalms 69 in the NNT2

Psalms 69 in the NNT3

Psalms 69 in the PDDPT

Psalms 69 in the PFNT

Psalms 69 in the RMNT

Psalms 69 in the SBIAS

Psalms 69 in the SBIBS

Psalms 69 in the SBIBS2

Psalms 69 in the SBICS

Psalms 69 in the SBIDS

Psalms 69 in the SBIGS

Psalms 69 in the SBIHS

Psalms 69 in the SBIIS

Psalms 69 in the SBIIS2

Psalms 69 in the SBIIS3

Psalms 69 in the SBIKS

Psalms 69 in the SBIKS2

Psalms 69 in the SBIMS

Psalms 69 in the SBIOS

Psalms 69 in the SBIPS

Psalms 69 in the SBISS

Psalms 69 in the SBITS

Psalms 69 in the SBITS2

Psalms 69 in the SBITS3

Psalms 69 in the SBITS4

Psalms 69 in the SBIUS

Psalms 69 in the SBIVS

Psalms 69 in the SBT

Psalms 69 in the SBT1E

Psalms 69 in the SCHL

Psalms 69 in the SNT

Psalms 69 in the SUSU

Psalms 69 in the SUSU2

Psalms 69 in the SYNO

Psalms 69 in the TBIAOTANT

Psalms 69 in the TBT1E

Psalms 69 in the TBT1E2

Psalms 69 in the TFTIP

Psalms 69 in the TFTU

Psalms 69 in the TGNTATF3T

Psalms 69 in the THAI

Psalms 69 in the TNFD

Psalms 69 in the TNT

Psalms 69 in the TNTIK

Psalms 69 in the TNTIL

Psalms 69 in the TNTIN

Psalms 69 in the TNTIP

Psalms 69 in the TNTIZ

Psalms 69 in the TOMA

Psalms 69 in the TTENT

Psalms 69 in the UBG

Psalms 69 in the UGV

Psalms 69 in the UGV2

Psalms 69 in the UGV3

Psalms 69 in the VBL

Psalms 69 in the VDCC

Psalms 69 in the YALU

Psalms 69 in the YAPE

Psalms 69 in the YBVTP

Psalms 69 in the ZBP