Romans 5 (BOGWICC)

1 Tsopano popeza tayesedwa olungama mwa chikhulupiriro, tili ndi mtendere ndi Mulungu kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu. 2 Iyeyo ndiye amene anatsekulira njira mwachikhulupiriro yolowera mʼchisomo mʼmene takhazikikamo. Ndipo tikukondwerera chiyembekezo cha ulemerero wa Mulungu. 3 Koma si pokhapo ayi, koma ife tikukondweranso mʼmasautso athu chifukwa tikudziwa kuti masautso amatiphunzitsa kupirira. 4 Ndipo kupirira kumabweretsa makhalidwe, makhalidwe amabweretsa chiyembekezo. 5 Ndipo chiyembekezo chimenechi sichitikhumudwitsa chifukwa Mulungu mwa Mzimu Woyera, amene Iye anatipatsa, wadzaza mʼmitima mwathu ndi chikondi chake. 6 Pakuti pa nthawi yake, tikanali ochimwa, Khristu anatifera anthu osapembedzafe. 7 Sizichitika kawirikawiri kuti munthu wina afere munthu wolungama, ngakhale kuti chifukwa cha munthu wabwino wina atha kulimba mtima kumufera. 8 Koma Mulungu anaonetsa chikondi chake kwa ife chifukwa pamene tinali ochimwabe, Khristu anatifera. 9 Popeza chifukwa cha magazi ake ife tapezeka olungama pamaso pa Mulungu, Iyeyo adzatipulumutsa koposa kotani ku mkwiyo wa Mulungu. 10 Pakuti pamene tinali adani a Mulungu, tinayanjanitsidwa ndi Iye kudzera mu imfa ya Mwana wake. Nanga tidzapulumutsidwa bwanji kudzera mʼmoyo wake, titayanjanitsidwa naye? 11 Sikuti izi zili chomwechi chabe, koma timakondweranso mwa Mulungu kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu. Kudzera mwa Iye, ife tsopano tayanjanitsidwa ndi Mulungu. 12 Choncho monga momwe tchimo linalowa mʼdziko lapansi kudzera mwa munthu mmodzi, ndi imfa kudzera mu tchimo, mʼnjirayi imfa inafika kwa anthu onse pakuti onse anachimwa. 13 Pakuti Malamulo asanaperekedwe, tchimo linali mʼdziko lapansi. Koma pamene palibe Malamulo, tchimo silitengedwa kukhala tchimo. 14 Komabe, imfa inalamulira kuyambira nthawi ya Adamu mpaka nthawi ya Mose. Inalamulira ngakhalenso pa iwo amene sanachimwe posamvera Malamulo monga anachitira Adamu. Adamuyo amene anali chifaniziro cha wina amene ankabwera. 15 Koma sitingafananitse mphatso yaulereyo ndi kuchimwa kwa anthu. Pakuti ngati anthu ambiri anafa chifukwa cha kuchimwa kwa munthu mmodziyo, kuli koposa bwanji nanga chisomo cha Mulungu ndi mphatso zomwe zinabwera ndi chisomo cha munthu mmodzi, Yesu Khristu, ndi kusefukira kwa ambiri! 16 Ndiponso, mphatso ya Mulungu sifanana ndi zotsatira za kuchimwa kwa munthu mmodzi. Chiweruzo chinatsatira tchimo la munthu mmodzi ndi kubweretsa kutsutsidwa koma mphatso inatsatira zolakwa zambiri ndi kubweretsa kulungamitsidwa. 17 Pakuti ngati, chifukwa cha kulakwa kwa munthu mmodziyo, imfa inalamulira kudzera mwa munthu mmodziyo, kuli koposa bwanji nanga kwa iwo amene adzalandira chisomo chochuluka ndi mphatso yachilungamo, adzalamulira mʼmoyo kudzera mwa munthu mmodzi, Yesu Khristu. 18 Choncho monga tchimo limodzi linabweretsa kutsutsika pa anthu onse, chimodzimodzinso ntchito imodzi yolungama inabweretsa chilungamo kwa anthu onse ndi kuwapatsa moyo. 19 Pakuti kusamvera kwa munthu mmodzi kunasandutsa anthu ambiri kukhala ochimwa, chimodzimodzinso anthu ambiri adzasanduka olungama kudzera mwa munthu mmodzinso. 20 Malamulo a Mulungu anaperekedwa ndi cholinga chakuti anthu onse azindikire kuchuluka kwa machimo awo. Koma pamene machimo anachuluka, chisomo chinachuluka koposa. 21 Choncho monga momwe tchimo linkalamulira anthu ndi kubweretsa imfa pa iwo, chomwecho kunali koyenera kuti chisomo chilamulire pobweretsa chilungamo kwa anthu, ndi kuwafikitsa ku moyo wosatha mwa Yesu Khristu Ambuye athu.

In Other Versions

Romans 5 in the ANGEFD

Romans 5 in the ANTPNG2D

Romans 5 in the AS21

Romans 5 in the BAGH

Romans 5 in the BBPNG

Romans 5 in the BBT1E

Romans 5 in the BDS

Romans 5 in the BEV

Romans 5 in the BHAD

Romans 5 in the BIB

Romans 5 in the BLPT

Romans 5 in the BNT

Romans 5 in the BNTABOOT

Romans 5 in the BNTLV

Romans 5 in the BOATCB

Romans 5 in the BOATCB2

Romans 5 in the BOBCV

Romans 5 in the BOCNT

Romans 5 in the BOECS

Romans 5 in the BOHCB

Romans 5 in the BOHCV

Romans 5 in the BOHLNT

Romans 5 in the BOHNTLTAL

Romans 5 in the BOICB

Romans 5 in the BOILNTAP

Romans 5 in the BOITCV

Romans 5 in the BOKCV

Romans 5 in the BOKCV2

Romans 5 in the BOKHWOG

Romans 5 in the BOKSSV

Romans 5 in the BOLCB

Romans 5 in the BOLCB2

Romans 5 in the BOMCV

Romans 5 in the BONAV

Romans 5 in the BONCB

Romans 5 in the BONLT

Romans 5 in the BONUT2

Romans 5 in the BOPLNT

Romans 5 in the BOSCB

Romans 5 in the BOSNC

Romans 5 in the BOTLNT

Romans 5 in the BOVCB

Romans 5 in the BOYCB

Romans 5 in the BPBB

Romans 5 in the BPH

Romans 5 in the BSB

Romans 5 in the CCB

Romans 5 in the CUV

Romans 5 in the CUVS

Romans 5 in the DBT

Romans 5 in the DGDNT

Romans 5 in the DHNT

Romans 5 in the DNT

Romans 5 in the ELBE

Romans 5 in the EMTV

Romans 5 in the ESV

Romans 5 in the FBV

Romans 5 in the FEB

Romans 5 in the GGMNT

Romans 5 in the GNT

Romans 5 in the HARY

Romans 5 in the HNT

Romans 5 in the IRVA

Romans 5 in the IRVB

Romans 5 in the IRVG

Romans 5 in the IRVH

Romans 5 in the IRVK

Romans 5 in the IRVM

Romans 5 in the IRVM2

Romans 5 in the IRVO

Romans 5 in the IRVP

Romans 5 in the IRVT

Romans 5 in the IRVT2

Romans 5 in the IRVU

Romans 5 in the ISVN

Romans 5 in the JSNT

Romans 5 in the KAPI

Romans 5 in the KBT1ETNIK

Romans 5 in the KBV

Romans 5 in the KJV

Romans 5 in the KNFD

Romans 5 in the LBA

Romans 5 in the LBLA

Romans 5 in the LNT

Romans 5 in the LSV

Romans 5 in the MAAL

Romans 5 in the MBV

Romans 5 in the MBV2

Romans 5 in the MHNT

Romans 5 in the MKNFD

Romans 5 in the MNG

Romans 5 in the MNT

Romans 5 in the MNT2

Romans 5 in the MRS1T

Romans 5 in the NAA

Romans 5 in the NASB

Romans 5 in the NBLA

Romans 5 in the NBS

Romans 5 in the NBVTP

Romans 5 in the NET2

Romans 5 in the NIV11

Romans 5 in the NNT

Romans 5 in the NNT2

Romans 5 in the NNT3

Romans 5 in the PDDPT

Romans 5 in the PFNT

Romans 5 in the RMNT

Romans 5 in the SBIAS

Romans 5 in the SBIBS

Romans 5 in the SBIBS2

Romans 5 in the SBICS

Romans 5 in the SBIDS

Romans 5 in the SBIGS

Romans 5 in the SBIHS

Romans 5 in the SBIIS

Romans 5 in the SBIIS2

Romans 5 in the SBIIS3

Romans 5 in the SBIKS

Romans 5 in the SBIKS2

Romans 5 in the SBIMS

Romans 5 in the SBIOS

Romans 5 in the SBIPS

Romans 5 in the SBISS

Romans 5 in the SBITS

Romans 5 in the SBITS2

Romans 5 in the SBITS3

Romans 5 in the SBITS4

Romans 5 in the SBIUS

Romans 5 in the SBIVS

Romans 5 in the SBT

Romans 5 in the SBT1E

Romans 5 in the SCHL

Romans 5 in the SNT

Romans 5 in the SUSU

Romans 5 in the SUSU2

Romans 5 in the SYNO

Romans 5 in the TBIAOTANT

Romans 5 in the TBT1E

Romans 5 in the TBT1E2

Romans 5 in the TFTIP

Romans 5 in the TFTU

Romans 5 in the TGNTATF3T

Romans 5 in the THAI

Romans 5 in the TNFD

Romans 5 in the TNT

Romans 5 in the TNTIK

Romans 5 in the TNTIL

Romans 5 in the TNTIN

Romans 5 in the TNTIP

Romans 5 in the TNTIZ

Romans 5 in the TOMA

Romans 5 in the TTENT

Romans 5 in the UBG

Romans 5 in the UGV

Romans 5 in the UGV2

Romans 5 in the UGV3

Romans 5 in the VBL

Romans 5 in the VDCC

Romans 5 in the YALU

Romans 5 in the YAPE

Romans 5 in the YBVTP

Romans 5 in the ZBP