Isaiah 42 (BOGWICC)

1 “Nayu mtumiki wanga, amene ndimamuchirikiza,amene ndamusankha, amenenso ndimakondwera naye.Ndayika Mzimu wanga mwa Iyeyo,ndipo adzaweruza anthu a mitundu yonse mwachilungamo. 2 Iye sadzafuwula, sadzamveka mawu,kapena mawu ake kumveka mʼmisewu. 3 Bango lophwanyika sadzalithyola,ndipo moto wozilala sadzawuzimitsa.Motero adzaonetsa kuti chilungamo ndicho choonadi; 4 sadzafowoka kapena kukhumudwampaka atakhazikitsa chilungamo pa dziko lapansi,ndi mpaka mayiko a mʼmbali mwa nyanja atafika poyembekezera malangizo ake.” 5 Yehova Mulunguamene analenga zamlengalenga ndi kuziyalika,amene analenga dziko lapansi ndi zonse zimene zimabereka,amenenso amapereka mpweya kwa anthu ake okhala mʼdzikomo,ndi moyo kwa onse oyendamo, akuti, 6 “Ine Yehova, ndakuyitana chifukwa Ine ndine wolungama;ndikugwira dzanja ndipondidzakuteteza.Ndakupereka kukhala pangano langa kwa anthundi kuwunika kwa anthu a mitundu ina. 7 Udzatsekula maso a anthu osaona,udzamasula anthu a mʼndendendi kutulutsa mʼndende anthu okhala mu mdima. 8 “Ine ndine Yehova: dzina langa ndi limenelo!Sindidzapereka ulemerero wanga kwa wina aliyensekapena matamando anga kwa mafano. 9 Taonani, zinthu zimene ndinalosera kale zachitikadi,ndipo ndikuwuzani zinthu zatsopano;zinthuzo zisanaonekereIne ndakudziwitsani.” 10 Imbirani Yehova nyimbo yatsopano,mutamandeni inu okhala mʼdziko lonse lapansi,inu amene mumayenda pa nyanja, nyanja ikokome ndi zonse zili mʼmenemo.Inu okhala pa zilumba tamandani Yehova. 11 Chipululu ndi mizinda yake zikweze mawu awo;midzi ya Akedara ikondwere.Anthu a ku Sela ayimbe mwachimwemwe;afuwule kuchokera pamwamba pa mapiri. 12 Atamande Yehovandipo alalike matamando ake kwa anthu apazilumba zonse. 13 Yehova adzapita ku nkhondo ngati munthu wamphamvu,adzawutsa ukali wake ngati munthu wankhondo;akukuwa ndiponso akufuwula mfuwu wankhondondipo adzagonjetsa adani ake. 14 Yehova akuti, “Ndakhala ndili chete kwa nthawi yayitali,ndakhala ndili phee osachita kanthu.Koma tsopano, ngati mayi pa nthawi yochira,ndi kubuwula ndi kupuma modukizadukiza ndipo ndili wefuwefu. 15 Ndidzawononga mapiri ndi zitundandipo ndidzawumitsa zomera zawo zonse;ndidzasandutsa mitsinje kukhala zilumbandipo ndidzawumitsa maiwe. 16 Ndidzatsogolera anthu osaona mʼmisewu imene sanayidziwe,ndidzawatsogolera mʼnjira zimene sanayendepo;ndidzasandutsa mdima wa kutsogolo kwawo kuti ukhale kuwalandipo ndidzasalaza malo osalala.Zimenezi ndizo ndidzachite;sindidzawataya. 17 Koma onse amene amadalira mafanoamene amanena kwa mafanowo kuti, ‘ndinu milungu yathu,’ndidzawachititsa manyazi kotheratu. 18 “Imvani, agonthi inu;yangʼanani osaona inu, kuti muone! 19 Ali wosaona ndani, si mtumiki wanga kodi?Ndipo ndani ali wosamva ngati mthenga amene ndamutuma?Kodi ndani ali wosaona ngati uja ndinachita naye pangano,kapena wosaona ndani ngati mtumiki wa Yehova? 20 Iwe waona zinthu zambiri, koma sunazisamale;makutu ako ndi otsekuka koma sumva kanthu.” 21 Chinamukomera Yehovachifukwa cha chilungamo chake,kapena lamulo lake kukhala lalikulu ndi lopambana. 22 Koma awa ndi anthu amene afunkhidwa ndi kuwalanda zinthu zawo,onsewa anawakola mʼmaenjekapena akuwabisa mʼndende.Tsono asanduka chofunkhapopanda wina wowapulumutsakapena kunena kuti,“Abwezeni kwawo.” 23 Kodi ndani wa inu amene adzamvetsera zimenezikapena kutchera khutu ndi kumva za mʼtsogolomo? 24 Ndani anapereka Yakobo kwa ofunkha,ndi Israeli kwa anthu akuba?Kodi si Yehova,amene ife tamuchimwirayu?Pakuti sanathe kutsatira njira zake;ndipo sanamvere malangizo ake. 25 Motero anawakwiyira kwambiri,nawavutitsa ndi nkhondo.Anayatsa moto ponseponse mowazungulira komabe iwo sanamvetse;motowo unawapsereza, koma iwo sanatengepo phunziro ayi.

In Other Versions

Isaiah 42 in the ANGEFD

Isaiah 42 in the ANTPNG2D

Isaiah 42 in the AS21

Isaiah 42 in the BAGH

Isaiah 42 in the BBPNG

Isaiah 42 in the BBT1E

Isaiah 42 in the BDS

Isaiah 42 in the BEV

Isaiah 42 in the BHAD

Isaiah 42 in the BIB

Isaiah 42 in the BLPT

Isaiah 42 in the BNT

Isaiah 42 in the BNTABOOT

Isaiah 42 in the BNTLV

Isaiah 42 in the BOATCB

Isaiah 42 in the BOATCB2

Isaiah 42 in the BOBCV

Isaiah 42 in the BOCNT

Isaiah 42 in the BOECS

Isaiah 42 in the BOHCB

Isaiah 42 in the BOHCV

Isaiah 42 in the BOHLNT

Isaiah 42 in the BOHNTLTAL

Isaiah 42 in the BOICB

Isaiah 42 in the BOILNTAP

Isaiah 42 in the BOITCV

Isaiah 42 in the BOKCV

Isaiah 42 in the BOKCV2

Isaiah 42 in the BOKHWOG

Isaiah 42 in the BOKSSV

Isaiah 42 in the BOLCB

Isaiah 42 in the BOLCB2

Isaiah 42 in the BOMCV

Isaiah 42 in the BONAV

Isaiah 42 in the BONCB

Isaiah 42 in the BONLT

Isaiah 42 in the BONUT2

Isaiah 42 in the BOPLNT

Isaiah 42 in the BOSCB

Isaiah 42 in the BOSNC

Isaiah 42 in the BOTLNT

Isaiah 42 in the BOVCB

Isaiah 42 in the BOYCB

Isaiah 42 in the BPBB

Isaiah 42 in the BPH

Isaiah 42 in the BSB

Isaiah 42 in the CCB

Isaiah 42 in the CUV

Isaiah 42 in the CUVS

Isaiah 42 in the DBT

Isaiah 42 in the DGDNT

Isaiah 42 in the DHNT

Isaiah 42 in the DNT

Isaiah 42 in the ELBE

Isaiah 42 in the EMTV

Isaiah 42 in the ESV

Isaiah 42 in the FBV

Isaiah 42 in the FEB

Isaiah 42 in the GGMNT

Isaiah 42 in the GNT

Isaiah 42 in the HARY

Isaiah 42 in the HNT

Isaiah 42 in the IRVA

Isaiah 42 in the IRVB

Isaiah 42 in the IRVG

Isaiah 42 in the IRVH

Isaiah 42 in the IRVK

Isaiah 42 in the IRVM

Isaiah 42 in the IRVM2

Isaiah 42 in the IRVO

Isaiah 42 in the IRVP

Isaiah 42 in the IRVT

Isaiah 42 in the IRVT2

Isaiah 42 in the IRVU

Isaiah 42 in the ISVN

Isaiah 42 in the JSNT

Isaiah 42 in the KAPI

Isaiah 42 in the KBT1ETNIK

Isaiah 42 in the KBV

Isaiah 42 in the KJV

Isaiah 42 in the KNFD

Isaiah 42 in the LBA

Isaiah 42 in the LBLA

Isaiah 42 in the LNT

Isaiah 42 in the LSV

Isaiah 42 in the MAAL

Isaiah 42 in the MBV

Isaiah 42 in the MBV2

Isaiah 42 in the MHNT

Isaiah 42 in the MKNFD

Isaiah 42 in the MNG

Isaiah 42 in the MNT

Isaiah 42 in the MNT2

Isaiah 42 in the MRS1T

Isaiah 42 in the NAA

Isaiah 42 in the NASB

Isaiah 42 in the NBLA

Isaiah 42 in the NBS

Isaiah 42 in the NBVTP

Isaiah 42 in the NET2

Isaiah 42 in the NIV11

Isaiah 42 in the NNT

Isaiah 42 in the NNT2

Isaiah 42 in the NNT3

Isaiah 42 in the PDDPT

Isaiah 42 in the PFNT

Isaiah 42 in the RMNT

Isaiah 42 in the SBIAS

Isaiah 42 in the SBIBS

Isaiah 42 in the SBIBS2

Isaiah 42 in the SBICS

Isaiah 42 in the SBIDS

Isaiah 42 in the SBIGS

Isaiah 42 in the SBIHS

Isaiah 42 in the SBIIS

Isaiah 42 in the SBIIS2

Isaiah 42 in the SBIIS3

Isaiah 42 in the SBIKS

Isaiah 42 in the SBIKS2

Isaiah 42 in the SBIMS

Isaiah 42 in the SBIOS

Isaiah 42 in the SBIPS

Isaiah 42 in the SBISS

Isaiah 42 in the SBITS

Isaiah 42 in the SBITS2

Isaiah 42 in the SBITS3

Isaiah 42 in the SBITS4

Isaiah 42 in the SBIUS

Isaiah 42 in the SBIVS

Isaiah 42 in the SBT

Isaiah 42 in the SBT1E

Isaiah 42 in the SCHL

Isaiah 42 in the SNT

Isaiah 42 in the SUSU

Isaiah 42 in the SUSU2

Isaiah 42 in the SYNO

Isaiah 42 in the TBIAOTANT

Isaiah 42 in the TBT1E

Isaiah 42 in the TBT1E2

Isaiah 42 in the TFTIP

Isaiah 42 in the TFTU

Isaiah 42 in the TGNTATF3T

Isaiah 42 in the THAI

Isaiah 42 in the TNFD

Isaiah 42 in the TNT

Isaiah 42 in the TNTIK

Isaiah 42 in the TNTIL

Isaiah 42 in the TNTIN

Isaiah 42 in the TNTIP

Isaiah 42 in the TNTIZ

Isaiah 42 in the TOMA

Isaiah 42 in the TTENT

Isaiah 42 in the UBG

Isaiah 42 in the UGV

Isaiah 42 in the UGV2

Isaiah 42 in the UGV3

Isaiah 42 in the VBL

Isaiah 42 in the VDCC

Isaiah 42 in the YALU

Isaiah 42 in the YAPE

Isaiah 42 in the YBVTP

Isaiah 42 in the ZBP