Isaiah 45 (BOGWICC)

1 Yehova akuyankhula ndi wodzozedwa wakeKoresi amene anamugwira dzanja lamanjakuti agonjetse mitundu ya anthundi kuwalanda mafumu zida zawo zankhondo,ndi kutsekula zitsekokuti zipatazo zisadzatsekedwenso ndi ichi: 2 Ine ndidzayenda patsogolo pako,ndi kusalaza mapiri;ndidzaphwanya zitseko za mkuwandi kuthyola mipiringidzo ya chitsulo. 3 Ndidzakupatsa chuma chobisika mu mdima,katundu wa pamalo obisika,kotero kuti udziwe kuti Ine ndine YehovaMulungu wa Israeli, amene ndakuyitana pokutchula dzina. 4 Chifukwa cha mtumiki wanga Yakobo,chifukwa cha wosankhidwa wanga Israeli,Ine ndakuyitana pokutchula dzinandipo ndakupatsa dzina laulemungakhale iwe sukundidziwa Ine. 5 Ine ndine Yehova ndipo palibenso wina;kupatula Ine palibenso Mulungu wina.Ndidzakupatsa mphamvu,ngakhale sukundidziwa Ine, 6 kotero kuti kuchokera kummawa mpaka kumadzuloanthu adzadziwa kuti palibe wina koma Ine ndekha.Ine ndine Yehova,ndipo palibenso wina. 7 Ndimalenga kuwala ndi mdima,ndimabweretsa madalitso ndi tsoka;ndine Yehova, amene ndimachita zonsezi. 8 “Iwe thambo gwetsa mvula kuchokera kumwamba;mitambo ivumbwe mivumbi ya chilungamo.Dziko lapansi litsekuke,ndipo chipulumutso chiphuke kutichilungamo chimereponso;Ine Yehova, ndine ndalenga zimenezi. 9 “Tsoka kwa wokangana ndi mlengi wake,ngakhale kuti ali ngati phale chabe pakati pa mapale anzake.Kodi dongo lingafunse munthu wowumba kuti,‘Kodi ukuwumba chiyani?’Kodi ntchito yako inganene kuti,‘Ulibe luso?’ 10 Tsoka kwa wofunsa abambo ake kuti,‘Kodi munabereka chiyani?’Kapena amayi ake kuti,‘Kodi mufuna kubereka chiyani?’ 11 “YehovaWoyerayo wa Israeli, ndiponso Mlengi wake akunena,zokhudza zinthu zimene zikubwera ndi izi:Kodi iwe ukundifunsa za ana anga,kapena kundilamula pa zokhudza ntchito zanga? 12 Ndine amene ndinapanga dziko lapansindikulenga munthu kuti akhalemo.Ine ndi manja anga ndinayalika thambo;ndimalamulira zolengedwa zonse za mlengalenga. 13 Ndine amene ndidzawutsa Koresi kuti chilungamo changa chikwaniritsidwe:ndipo ndidzawongolera njira zake zonse.Iye adzamanganso mzinda wangandi kumasula anthu anga amene ali mu ukapolo,wopanda kupereka ndalama kapena mphotho,akutero Yehova Wamphamvuzonse.” 14 Yehova akuti,“Chuma cha ku Igupto ndi chuma cha malonda cha Kusi chidzakhala chanu.Anthu amphamvu zawo ndi athanzi a ku Sebaadzabwera kwa inundipo adzakhala anthu anu;iwo adzidzakutsatani pambuyo panuali mʼmaunyolo.Adzakugwadiranindi kukupemphani, ponena kuti,‘Ndithudi Mulungu ali ndi inu, ndipo palibenso wina;palibenso mulungu wina.’ ” 15 Zoonadi inu muli ndi Mulungu wobisikaamene ali Mulungu ndi Mpulumutsi wa Israeli. 16 Onse amene amapanga mafano adzawachititsa manyazi ndi kuwanyozetsa.Adzakhala osokonezeka maganizo. 17 Koma Yehova adzapulumutsa Israelindi chipulumutso chamuyaya;simudzachitanso manyazi kapena kunyozekampaka kalekale. 18 Yehovaanalenga zinthu zakumwamba,Iye ndiye Mulungu;amene akulenga dziko lapansi,ndi kulikhazikitsa,sanalipange kuti likhale lopanda kanthu,koma analipanga kuti anthu akhalemo.Iyeyu akunena kuti:Ine ndine Yehova,ndipo palibenso wina. 19 Ine sindinayankhule mwachinsinsi,pamalo ena a mdima;Ine sindinaziwuze zidzukulu za Yakobo kuti,“Ndifunefuneni ku malo kopanda kanthu.”Ine Yehova, ndimayankhula zoona;ndikunena zolungama. 20 Yehova akuti, “Sonkhanani pamodzi ndipo mubwere;yandikirani, inu amene munapulumuka pothawa nkhondo kwa anthu a mitundu ina.Ndinu opanda nzeru amene mumanyamula mafano a mitengo,amene mumapemphera kwa milungu imene singathe kupulumutsa. 21 Fotokozani mlandu wanu,mupatsane nzeru nonse pamodzi.Kodi ndani ananeneratu zimenezi kalekale?Ndani anazifotokozeratu zimenezi nthawi yamakedzana?Kodi si Ineyo Yehova?Ndipo palibenso Mulungu wina kupatula Ine,Mulungu wolungama ndi Wopulumutsa,palibenso wina kupatula Ine. 22 “Tembenukirani kwa Ine kuti mupulumuke,inu anthu onse a pa dziko lapansi,pakuti Ine ndine Mulungu ndipo palibenso wina. 23 Ndalumbira ndekha,pakamwa panga patulutsa mawu owona,mawu amene sadzasinthika konse akuti,bondo lililonse lidzagwada pamaso panga;anthu onse adzalumbira potchula dzina langa. 24 Iwo adzanene kwa Ine kuti,‘Chilungamo ndi mphamvu zimapezeka mwa Yehova yekha.’ ”Onse amene anamuwukira Iyeadzabwera kwa Iye ndipo adzachita manyazi. 25 Koma mwa Yehova zidzukulu zonse za Israelizidzapambana ndi kupeza ulemerero.

In Other Versions

Isaiah 45 in the ANGEFD

Isaiah 45 in the ANTPNG2D

Isaiah 45 in the AS21

Isaiah 45 in the BAGH

Isaiah 45 in the BBPNG

Isaiah 45 in the BBT1E

Isaiah 45 in the BDS

Isaiah 45 in the BEV

Isaiah 45 in the BHAD

Isaiah 45 in the BIB

Isaiah 45 in the BLPT

Isaiah 45 in the BNT

Isaiah 45 in the BNTABOOT

Isaiah 45 in the BNTLV

Isaiah 45 in the BOATCB

Isaiah 45 in the BOATCB2

Isaiah 45 in the BOBCV

Isaiah 45 in the BOCNT

Isaiah 45 in the BOECS

Isaiah 45 in the BOHCB

Isaiah 45 in the BOHCV

Isaiah 45 in the BOHLNT

Isaiah 45 in the BOHNTLTAL

Isaiah 45 in the BOICB

Isaiah 45 in the BOILNTAP

Isaiah 45 in the BOITCV

Isaiah 45 in the BOKCV

Isaiah 45 in the BOKCV2

Isaiah 45 in the BOKHWOG

Isaiah 45 in the BOKSSV

Isaiah 45 in the BOLCB

Isaiah 45 in the BOLCB2

Isaiah 45 in the BOMCV

Isaiah 45 in the BONAV

Isaiah 45 in the BONCB

Isaiah 45 in the BONLT

Isaiah 45 in the BONUT2

Isaiah 45 in the BOPLNT

Isaiah 45 in the BOSCB

Isaiah 45 in the BOSNC

Isaiah 45 in the BOTLNT

Isaiah 45 in the BOVCB

Isaiah 45 in the BOYCB

Isaiah 45 in the BPBB

Isaiah 45 in the BPH

Isaiah 45 in the BSB

Isaiah 45 in the CCB

Isaiah 45 in the CUV

Isaiah 45 in the CUVS

Isaiah 45 in the DBT

Isaiah 45 in the DGDNT

Isaiah 45 in the DHNT

Isaiah 45 in the DNT

Isaiah 45 in the ELBE

Isaiah 45 in the EMTV

Isaiah 45 in the ESV

Isaiah 45 in the FBV

Isaiah 45 in the FEB

Isaiah 45 in the GGMNT

Isaiah 45 in the GNT

Isaiah 45 in the HARY

Isaiah 45 in the HNT

Isaiah 45 in the IRVA

Isaiah 45 in the IRVB

Isaiah 45 in the IRVG

Isaiah 45 in the IRVH

Isaiah 45 in the IRVK

Isaiah 45 in the IRVM

Isaiah 45 in the IRVM2

Isaiah 45 in the IRVO

Isaiah 45 in the IRVP

Isaiah 45 in the IRVT

Isaiah 45 in the IRVT2

Isaiah 45 in the IRVU

Isaiah 45 in the ISVN

Isaiah 45 in the JSNT

Isaiah 45 in the KAPI

Isaiah 45 in the KBT1ETNIK

Isaiah 45 in the KBV

Isaiah 45 in the KJV

Isaiah 45 in the KNFD

Isaiah 45 in the LBA

Isaiah 45 in the LBLA

Isaiah 45 in the LNT

Isaiah 45 in the LSV

Isaiah 45 in the MAAL

Isaiah 45 in the MBV

Isaiah 45 in the MBV2

Isaiah 45 in the MHNT

Isaiah 45 in the MKNFD

Isaiah 45 in the MNG

Isaiah 45 in the MNT

Isaiah 45 in the MNT2

Isaiah 45 in the MRS1T

Isaiah 45 in the NAA

Isaiah 45 in the NASB

Isaiah 45 in the NBLA

Isaiah 45 in the NBS

Isaiah 45 in the NBVTP

Isaiah 45 in the NET2

Isaiah 45 in the NIV11

Isaiah 45 in the NNT

Isaiah 45 in the NNT2

Isaiah 45 in the NNT3

Isaiah 45 in the PDDPT

Isaiah 45 in the PFNT

Isaiah 45 in the RMNT

Isaiah 45 in the SBIAS

Isaiah 45 in the SBIBS

Isaiah 45 in the SBIBS2

Isaiah 45 in the SBICS

Isaiah 45 in the SBIDS

Isaiah 45 in the SBIGS

Isaiah 45 in the SBIHS

Isaiah 45 in the SBIIS

Isaiah 45 in the SBIIS2

Isaiah 45 in the SBIIS3

Isaiah 45 in the SBIKS

Isaiah 45 in the SBIKS2

Isaiah 45 in the SBIMS

Isaiah 45 in the SBIOS

Isaiah 45 in the SBIPS

Isaiah 45 in the SBISS

Isaiah 45 in the SBITS

Isaiah 45 in the SBITS2

Isaiah 45 in the SBITS3

Isaiah 45 in the SBITS4

Isaiah 45 in the SBIUS

Isaiah 45 in the SBIVS

Isaiah 45 in the SBT

Isaiah 45 in the SBT1E

Isaiah 45 in the SCHL

Isaiah 45 in the SNT

Isaiah 45 in the SUSU

Isaiah 45 in the SUSU2

Isaiah 45 in the SYNO

Isaiah 45 in the TBIAOTANT

Isaiah 45 in the TBT1E

Isaiah 45 in the TBT1E2

Isaiah 45 in the TFTIP

Isaiah 45 in the TFTU

Isaiah 45 in the TGNTATF3T

Isaiah 45 in the THAI

Isaiah 45 in the TNFD

Isaiah 45 in the TNT

Isaiah 45 in the TNTIK

Isaiah 45 in the TNTIL

Isaiah 45 in the TNTIN

Isaiah 45 in the TNTIP

Isaiah 45 in the TNTIZ

Isaiah 45 in the TOMA

Isaiah 45 in the TTENT

Isaiah 45 in the UBG

Isaiah 45 in the UGV

Isaiah 45 in the UGV2

Isaiah 45 in the UGV3

Isaiah 45 in the VBL

Isaiah 45 in the VDCC

Isaiah 45 in the YALU

Isaiah 45 in the YAPE

Isaiah 45 in the YBVTP

Isaiah 45 in the ZBP