Ezekiel 7 (BOGWICC)

1 Yehova anandipatsa uthenga uwu kuti, 2 “Iwe mwana wa munthu, Ine Ambuye Yehova ndikuwuza dziko la Israeli kuti:“Chimaliziro! Chimaliziro chafikaku ngodya zinayi za dziko. 3 Chimaliziro chili pa iwe tsopano.Mkwiyo wanga ndidzawuthira pa iwe.Ndidzakuweruza molingana ndi machitidwe akondi kukulanga chifukwa cha zonyansa zako. 4 Ine sindidzakumvera chisonikapena kukuleka.Ndidzakulanga ndithu chifukwa cha ntchito zako zoyipakomanso chifukwa cha miyambo yako yonyansa imene ili pakati pako.Pamenepo udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.” 5 “Zimene ndikunena Ine Ambuye Yehova ndi izi:“Chiwonongeko! Chiwonongeko chimene sichinamvekepo!Taona chikubwera! 6 Chimaliziro chafika!Chimaliziro chafika!Chiwonongeko chakugwera.Taona chafika! 7 Inu anthu okhala mʼdziko,chiwonongeko chakugwerani.Nthawi yafika, tsiku layandikira; tsiku la chisokonezo osati la chimwemwe pa mapiri. 8 Ine ndili pafupi kukukwiyirani,ndipo ukali wanga udzathera pa iwe;Ine ndidzakuweruza molingana ndi machitidwe akondiponso ndidzakulanga chifukwa cha miyambo yako yonyansa. 9 Ine sindidzakumvera chisonikapena kukuleka.Ndidzakulanga malingana ndi ntchito zakondiponso chifukwa cha miyambo yako yonyansa pakati pako.‘Pamenepo udzadziwa kuti Ine Yehova ndine amene ndimakantha.’ 10 “Taona, tsikulo!Taona, lafika!Chiwonongeko chako chabwera.Ndodo yaphuka mphundu za maluwa.Kudzitama kwaphuka. 11 Chiwawa chasanduka ndodoyowakwapulira chifukwa cha kuyipa kwawo.Palibe mwa anthu amenewo amene adzatsale.Palibe ndi mmodzi yemwe mwa unyinji wawo.Palibiretu ndipo sipadzapezekamunthu wowalira maliro. 12 Nthawi yafika!Tsiku layandikira!Munthu wogula asakondwerendipo wogulitsa asamve chisoni,popeza ukali wanga uli pa gulu lonse. 13 Wogulitsa sadzazipezanso zinthuzimene anagulitsa kwa winachinkana onse awiri akanali ndi moyo,pakuti chilango chidzagwera onsewondipo sichingasinthike.Chifukwa cha machimo awo, palibe aliyenseamene adzapulumutsa moyo wake. 14 “Lipenga lalira,ndipo zonse zakonzeka.Koma palibe ndi mmodzi yemwe amene akupita ku nkhondo,pakuti mkwiyo wanga uli pa gulu lonse. 15 Ku bwalo kuli kumenyanandipo mʼkati muli mliri ndi njala.Anthu okhala ku midziadzafa ndi nkhondo.Iwo okhala ku mizindaadzafa ndi mliri ndi njala. 16 Onse amene adzapulumukandi kumakakhala ku mapiri,azidzalira ngati nkhunda za ku zigwa.Aliyense azidzabuwula chifukwa cha machimo ake. 17 Dzanja lililonse lidzalefuka,ndipo bondo lililonse lidzalobodoka ngati madzi. 18 Iwo adzavala zigudulindipo adzagwidwa ndi mantha.Adzakhala ndi nkhope zamanyazindipo mitu yawo adzameta mpala. 19 “Iwo adzataya siliva wawo mʼmisewundipo golide wawo adzakhala chinthu chonyansa.Siliva ndi golide wawosizidzatha kuwapulumutsapa tsiku la ukali wa Yehova.Chuma chawochi sichidzawathandiza kuthetsa njala,kapena kukhala okhuta,pakuti ndicho chinawagwetsa mʼmachimo. 20 Iwo ankanyadira zodzikongoletsera zawo zamakakandipo ankazigwiritsa ntchito kupanga mafano awo onyansa ndi zonyansa zawo zina.Nʼchifukwa chake Ine ndidzazisandutsakukhala zowanyansa. 21 Ndidzazipereka kwa alendo kuti azifunkhe.Anthu oyipa a dziko lapansi adzazilandandi kudziyipitsa. 22 Ine ndidzawalekerera anthuwondipo adzayipitsa malo anga apamtima.Adzalowamo ngati mbalandi kuyipitsamo. 23 “Konzani maunyolo,chifukwa dziko ladzaza ndi anthu opha anzawondipo mzinda wadzaza ndi chiwawa. 24 Ndidzabweretsa mitundu ya anthu oyipitsitsakuti idzalande nyumba zawo.Ndidzathetsa kunyada kwa anthu amphamvupamene anthu akunja adzalowa mʼmalo awo achipembedzo ndi kuyipitsamo. 25 Nkhawa ikadzawafikiraadzafunafuna mtendere koma osawupeza. 26 Tsoka lidzatsatana ndi tsoka linzake,ndipo mphekesera idzatsatana ndi mphekesera inzake.Iwo adzayesa kufuna masomphenya kuchokera kwa mneneri.Adzasowa ansembe owaphunzitsa malamulo,ndipo anthu akuluakulu sadzakhalanso ndi uphungu. 27 Mfumu idzalira,kalonga adzagwidwa ndi mantha.Manja a anthu a mʼdzikomo azidzangonjenjemera ndi mantha.Ine ndidzawalanga molingana ndi machitidwe awo,ndipo ndidzawaweruza molingana ndi momwe anaweruzira anzawo.Choncho adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”

In Other Versions

Ezekiel 7 in the ANGEFD

Ezekiel 7 in the ANTPNG2D

Ezekiel 7 in the AS21

Ezekiel 7 in the BAGH

Ezekiel 7 in the BBPNG

Ezekiel 7 in the BBT1E

Ezekiel 7 in the BDS

Ezekiel 7 in the BEV

Ezekiel 7 in the BHAD

Ezekiel 7 in the BIB

Ezekiel 7 in the BLPT

Ezekiel 7 in the BNT

Ezekiel 7 in the BNTABOOT

Ezekiel 7 in the BNTLV

Ezekiel 7 in the BOATCB

Ezekiel 7 in the BOATCB2

Ezekiel 7 in the BOBCV

Ezekiel 7 in the BOCNT

Ezekiel 7 in the BOECS

Ezekiel 7 in the BOHCB

Ezekiel 7 in the BOHCV

Ezekiel 7 in the BOHLNT

Ezekiel 7 in the BOHNTLTAL

Ezekiel 7 in the BOICB

Ezekiel 7 in the BOILNTAP

Ezekiel 7 in the BOITCV

Ezekiel 7 in the BOKCV

Ezekiel 7 in the BOKCV2

Ezekiel 7 in the BOKHWOG

Ezekiel 7 in the BOKSSV

Ezekiel 7 in the BOLCB

Ezekiel 7 in the BOLCB2

Ezekiel 7 in the BOMCV

Ezekiel 7 in the BONAV

Ezekiel 7 in the BONCB

Ezekiel 7 in the BONLT

Ezekiel 7 in the BONUT2

Ezekiel 7 in the BOPLNT

Ezekiel 7 in the BOSCB

Ezekiel 7 in the BOSNC

Ezekiel 7 in the BOTLNT

Ezekiel 7 in the BOVCB

Ezekiel 7 in the BOYCB

Ezekiel 7 in the BPBB

Ezekiel 7 in the BPH

Ezekiel 7 in the BSB

Ezekiel 7 in the CCB

Ezekiel 7 in the CUV

Ezekiel 7 in the CUVS

Ezekiel 7 in the DBT

Ezekiel 7 in the DGDNT

Ezekiel 7 in the DHNT

Ezekiel 7 in the DNT

Ezekiel 7 in the ELBE

Ezekiel 7 in the EMTV

Ezekiel 7 in the ESV

Ezekiel 7 in the FBV

Ezekiel 7 in the FEB

Ezekiel 7 in the GGMNT

Ezekiel 7 in the GNT

Ezekiel 7 in the HARY

Ezekiel 7 in the HNT

Ezekiel 7 in the IRVA

Ezekiel 7 in the IRVB

Ezekiel 7 in the IRVG

Ezekiel 7 in the IRVH

Ezekiel 7 in the IRVK

Ezekiel 7 in the IRVM

Ezekiel 7 in the IRVM2

Ezekiel 7 in the IRVO

Ezekiel 7 in the IRVP

Ezekiel 7 in the IRVT

Ezekiel 7 in the IRVT2

Ezekiel 7 in the IRVU

Ezekiel 7 in the ISVN

Ezekiel 7 in the JSNT

Ezekiel 7 in the KAPI

Ezekiel 7 in the KBT1ETNIK

Ezekiel 7 in the KBV

Ezekiel 7 in the KJV

Ezekiel 7 in the KNFD

Ezekiel 7 in the LBA

Ezekiel 7 in the LBLA

Ezekiel 7 in the LNT

Ezekiel 7 in the LSV

Ezekiel 7 in the MAAL

Ezekiel 7 in the MBV

Ezekiel 7 in the MBV2

Ezekiel 7 in the MHNT

Ezekiel 7 in the MKNFD

Ezekiel 7 in the MNG

Ezekiel 7 in the MNT

Ezekiel 7 in the MNT2

Ezekiel 7 in the MRS1T

Ezekiel 7 in the NAA

Ezekiel 7 in the NASB

Ezekiel 7 in the NBLA

Ezekiel 7 in the NBS

Ezekiel 7 in the NBVTP

Ezekiel 7 in the NET2

Ezekiel 7 in the NIV11

Ezekiel 7 in the NNT

Ezekiel 7 in the NNT2

Ezekiel 7 in the NNT3

Ezekiel 7 in the PDDPT

Ezekiel 7 in the PFNT

Ezekiel 7 in the RMNT

Ezekiel 7 in the SBIAS

Ezekiel 7 in the SBIBS

Ezekiel 7 in the SBIBS2

Ezekiel 7 in the SBICS

Ezekiel 7 in the SBIDS

Ezekiel 7 in the SBIGS

Ezekiel 7 in the SBIHS

Ezekiel 7 in the SBIIS

Ezekiel 7 in the SBIIS2

Ezekiel 7 in the SBIIS3

Ezekiel 7 in the SBIKS

Ezekiel 7 in the SBIKS2

Ezekiel 7 in the SBIMS

Ezekiel 7 in the SBIOS

Ezekiel 7 in the SBIPS

Ezekiel 7 in the SBISS

Ezekiel 7 in the SBITS

Ezekiel 7 in the SBITS2

Ezekiel 7 in the SBITS3

Ezekiel 7 in the SBITS4

Ezekiel 7 in the SBIUS

Ezekiel 7 in the SBIVS

Ezekiel 7 in the SBT

Ezekiel 7 in the SBT1E

Ezekiel 7 in the SCHL

Ezekiel 7 in the SNT

Ezekiel 7 in the SUSU

Ezekiel 7 in the SUSU2

Ezekiel 7 in the SYNO

Ezekiel 7 in the TBIAOTANT

Ezekiel 7 in the TBT1E

Ezekiel 7 in the TBT1E2

Ezekiel 7 in the TFTIP

Ezekiel 7 in the TFTU

Ezekiel 7 in the TGNTATF3T

Ezekiel 7 in the THAI

Ezekiel 7 in the TNFD

Ezekiel 7 in the TNT

Ezekiel 7 in the TNTIK

Ezekiel 7 in the TNTIL

Ezekiel 7 in the TNTIN

Ezekiel 7 in the TNTIP

Ezekiel 7 in the TNTIZ

Ezekiel 7 in the TOMA

Ezekiel 7 in the TTENT

Ezekiel 7 in the UBG

Ezekiel 7 in the UGV

Ezekiel 7 in the UGV2

Ezekiel 7 in the UGV3

Ezekiel 7 in the VBL

Ezekiel 7 in the VDCC

Ezekiel 7 in the YALU

Ezekiel 7 in the YAPE

Ezekiel 7 in the YBVTP

Ezekiel 7 in the ZBP