Jeremiah 10 (BOGWICC)

1 Inu Aisraeli, imvani zimene Yehova akunena. 2 Yehova akuti,“Musatsatire makhalidwe a anthu a mitundu inakapena kuchita mantha ndi zizindikiro zamlengalenga,ngakhale anthu a mitundu ina amachita nazo mantha. 3 Pakuti miyambo ya mitundu inayo ndiyachabechabe.Iwo amakadula mtengo ku nkhalangondipo mmisiri amawusema ndi sompho. 4 Amakongoletsa chosemacho ndi siliva ndi golide;kenaka amachikhomerera ndi misomalikuti chisagwedezeke. 5 Mafano awo ali ngati mtengo wakanjedza woopsezera mbalame mʼmunda wa minkhaka.Mafanowo sangathe nʼkuyankhula komwendipo ayenera kunyamulidwapopeza sangathe nʼkuyenda komwe.Musachite nawo manthapopeza sangathe kukuchitani choyipandiponso alibe mphamvu yochitira chabwino chilichonse.” 6 Palibe wofanana nanu, Inu Yehova;Inu ndinu wamkulu,ndipo dzina lanu lili ndi mphamvu yayikulu. 7 Ndani amene angaleke kukuopani,inu Mfumu ya mitundu ya anthu?Chimenechi ndicho chokuyenerani.Pakati pa anthu anzeru onse komanso mafumu onsea mitundu ya anthu,palibe wina wofanana nanu. 8 Onsewo ndi opusa ndi opanda nzeru;malangizo awo amawatenga kuchokera kwa mafano achabechabe opanga ndi mitengo. 9 Siliva wosula amabwera naye kuchokera ku Tarisisindipo golide amachokera naye ku Ufazi.Mafanowo ndi ntchito ya anthu aluso ndi odziwa kuzokota golide.Tsono mafanowo amawaveka zovala za mtundu wamtambo ndi pepo.Yonseyo ndi ntchito ya anthu a luso. 10 Koma Yehova ndiye Mulungu woona;Iyeyo ndiye Mulungu wamoyo, Mfumu yamuyaya.Akakwiya, dziko limagwedezeka;anthu a mitundu ina sangathe kupirira ukali wakewo. 11 “Awuze anthu awa kuti, ‘Milungu iyi, imene sinalenge dziko lakumwamba ndi dziko lapansi, idzawonongeka pa dziko lapansi ndi pansi pa thambo.’ ” 12 Koma Mulungu analenga dziko lapansi ndi mphamvu zake;Iye anapanga dziko lonse ndi nzeru zakendipo anayala thambo mwaluso lake. 13 Iye akayankhula, kumamveka mkokomo wamadzi akumwamba;Iyeyo amabweretsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi.Amabweretsa mphenzi pamodzi ndi mvulandi kutulutsa mphepo yamkuntho kumalo kumene osungirako. 14 Anthu onse ndi opusa ndiponso opanda nzeru;mmisiri aliyense wosula golide akuchita manyazi ndi mafano ake.Mafano akewo ndi abodza;alibe moyo mʼkati mwawo. 15 Mafanowo ndi achabechabe, zinthu zosekedwa nazo.Pamene anthuwo azidzaweruzidwa, mafanowo adzawonongedwa. 16 Koma Yehova amene ndi Cholowa cha Yakobo sali ngati mafanowo.Iyeyu ndi Mlengi wa zinthu zonsekuphatikizapo Israeli, mtundu umene anawusankha kuti ukhale anthu ake.Dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse. 17 Sonkhanitsani katundu wanu,inu amene mukukhala mʼlinga la ankhondo. 18 Pakuti Yehova akuti,“Tsopano Ine ndidzachotsa anthu onseamene akukhala mʼdziko lino;adzakhala pa mavutompaka adzamvetsa.” 19 Aliyense ankangoti, “Mayo ine, chifukwa cha kupweteka kwanga!Chilonda changa nʼchachikulu!”Koma ine ndinkaganiza kuti, “Ndithu, ili ndi vuto langa basi,choncho ndingolipirira.” 20 Tenti yanga yawonongeka,zingwe zake zonse zaduka.Ana anga andisiya ndipo kulibenso.Palibenso amene adzandimangire tenti,kapena kufunyulula nsalu yake. 21 Abusa ndi opusandipo sanapemphe nzeru kwa Yehova;choncho palibe chimene anapindulandipo nkhosa zawo zonse zabalalika. 22 Tamvani! kukubwera mphekesera,phokoso lalikulu la gulu la a ankhondo likumveka kuchokera kumpoto!Lidzasandutsa bwinja mizinda ya ku Yuda,malo okhala nkhandwe. 23 Inu Yehova, ndikudziwa kuti moyo umene munthu ali nawo si wake;munthuyo sangathe kuwongolera mayendedwe ake. 24 Inu Yehova, langizeni, komatu mwachilungamo,osati ndi mkwiyo wanu,mungandiwononge kotheratu. 25 Tsanulirani ukali wanu pa mitundu ya anthu amene sakudziwani,ndiye kuti mitundu ya anthu amene satama pa dzina lanu mopemba.Iwo aja anasakaza Yakobo;amusakaza kotheratundipo awononga dziko lake.

In Other Versions

Jeremiah 10 in the ANGEFD

Jeremiah 10 in the ANTPNG2D

Jeremiah 10 in the AS21

Jeremiah 10 in the BAGH

Jeremiah 10 in the BBPNG

Jeremiah 10 in the BBT1E

Jeremiah 10 in the BDS

Jeremiah 10 in the BEV

Jeremiah 10 in the BHAD

Jeremiah 10 in the BIB

Jeremiah 10 in the BLPT

Jeremiah 10 in the BNT

Jeremiah 10 in the BNTABOOT

Jeremiah 10 in the BNTLV

Jeremiah 10 in the BOATCB

Jeremiah 10 in the BOATCB2

Jeremiah 10 in the BOBCV

Jeremiah 10 in the BOCNT

Jeremiah 10 in the BOECS

Jeremiah 10 in the BOHCB

Jeremiah 10 in the BOHCV

Jeremiah 10 in the BOHLNT

Jeremiah 10 in the BOHNTLTAL

Jeremiah 10 in the BOICB

Jeremiah 10 in the BOILNTAP

Jeremiah 10 in the BOITCV

Jeremiah 10 in the BOKCV

Jeremiah 10 in the BOKCV2

Jeremiah 10 in the BOKHWOG

Jeremiah 10 in the BOKSSV

Jeremiah 10 in the BOLCB

Jeremiah 10 in the BOLCB2

Jeremiah 10 in the BOMCV

Jeremiah 10 in the BONAV

Jeremiah 10 in the BONCB

Jeremiah 10 in the BONLT

Jeremiah 10 in the BONUT2

Jeremiah 10 in the BOPLNT

Jeremiah 10 in the BOSCB

Jeremiah 10 in the BOSNC

Jeremiah 10 in the BOTLNT

Jeremiah 10 in the BOVCB

Jeremiah 10 in the BOYCB

Jeremiah 10 in the BPBB

Jeremiah 10 in the BPH

Jeremiah 10 in the BSB

Jeremiah 10 in the CCB

Jeremiah 10 in the CUV

Jeremiah 10 in the CUVS

Jeremiah 10 in the DBT

Jeremiah 10 in the DGDNT

Jeremiah 10 in the DHNT

Jeremiah 10 in the DNT

Jeremiah 10 in the ELBE

Jeremiah 10 in the EMTV

Jeremiah 10 in the ESV

Jeremiah 10 in the FBV

Jeremiah 10 in the FEB

Jeremiah 10 in the GGMNT

Jeremiah 10 in the GNT

Jeremiah 10 in the HARY

Jeremiah 10 in the HNT

Jeremiah 10 in the IRVA

Jeremiah 10 in the IRVB

Jeremiah 10 in the IRVG

Jeremiah 10 in the IRVH

Jeremiah 10 in the IRVK

Jeremiah 10 in the IRVM

Jeremiah 10 in the IRVM2

Jeremiah 10 in the IRVO

Jeremiah 10 in the IRVP

Jeremiah 10 in the IRVT

Jeremiah 10 in the IRVT2

Jeremiah 10 in the IRVU

Jeremiah 10 in the ISVN

Jeremiah 10 in the JSNT

Jeremiah 10 in the KAPI

Jeremiah 10 in the KBT1ETNIK

Jeremiah 10 in the KBV

Jeremiah 10 in the KJV

Jeremiah 10 in the KNFD

Jeremiah 10 in the LBA

Jeremiah 10 in the LBLA

Jeremiah 10 in the LNT

Jeremiah 10 in the LSV

Jeremiah 10 in the MAAL

Jeremiah 10 in the MBV

Jeremiah 10 in the MBV2

Jeremiah 10 in the MHNT

Jeremiah 10 in the MKNFD

Jeremiah 10 in the MNG

Jeremiah 10 in the MNT

Jeremiah 10 in the MNT2

Jeremiah 10 in the MRS1T

Jeremiah 10 in the NAA

Jeremiah 10 in the NASB

Jeremiah 10 in the NBLA

Jeremiah 10 in the NBS

Jeremiah 10 in the NBVTP

Jeremiah 10 in the NET2

Jeremiah 10 in the NIV11

Jeremiah 10 in the NNT

Jeremiah 10 in the NNT2

Jeremiah 10 in the NNT3

Jeremiah 10 in the PDDPT

Jeremiah 10 in the PFNT

Jeremiah 10 in the RMNT

Jeremiah 10 in the SBIAS

Jeremiah 10 in the SBIBS

Jeremiah 10 in the SBIBS2

Jeremiah 10 in the SBICS

Jeremiah 10 in the SBIDS

Jeremiah 10 in the SBIGS

Jeremiah 10 in the SBIHS

Jeremiah 10 in the SBIIS

Jeremiah 10 in the SBIIS2

Jeremiah 10 in the SBIIS3

Jeremiah 10 in the SBIKS

Jeremiah 10 in the SBIKS2

Jeremiah 10 in the SBIMS

Jeremiah 10 in the SBIOS

Jeremiah 10 in the SBIPS

Jeremiah 10 in the SBISS

Jeremiah 10 in the SBITS

Jeremiah 10 in the SBITS2

Jeremiah 10 in the SBITS3

Jeremiah 10 in the SBITS4

Jeremiah 10 in the SBIUS

Jeremiah 10 in the SBIVS

Jeremiah 10 in the SBT

Jeremiah 10 in the SBT1E

Jeremiah 10 in the SCHL

Jeremiah 10 in the SNT

Jeremiah 10 in the SUSU

Jeremiah 10 in the SUSU2

Jeremiah 10 in the SYNO

Jeremiah 10 in the TBIAOTANT

Jeremiah 10 in the TBT1E

Jeremiah 10 in the TBT1E2

Jeremiah 10 in the TFTIP

Jeremiah 10 in the TFTU

Jeremiah 10 in the TGNTATF3T

Jeremiah 10 in the THAI

Jeremiah 10 in the TNFD

Jeremiah 10 in the TNT

Jeremiah 10 in the TNTIK

Jeremiah 10 in the TNTIL

Jeremiah 10 in the TNTIN

Jeremiah 10 in the TNTIP

Jeremiah 10 in the TNTIZ

Jeremiah 10 in the TOMA

Jeremiah 10 in the TTENT

Jeremiah 10 in the UBG

Jeremiah 10 in the UGV

Jeremiah 10 in the UGV2

Jeremiah 10 in the UGV3

Jeremiah 10 in the VBL

Jeremiah 10 in the VDCC

Jeremiah 10 in the YALU

Jeremiah 10 in the YAPE

Jeremiah 10 in the YBVTP

Jeremiah 10 in the ZBP