Lamentations 3 (BOGWICC)

1 Ine ndine munthu amene ndaona masautsondi ndodo ya ukali wake. 2 Wandipititsa kutali ndipo wandiyendetsamu mdima osati mʼkuwala; 3 zoonadi anandikantha ndi dzanja lakemobwerezabwereza tsiku lonse. 4 Wakalambitsa khungu langa ndi mnofu wanga,ndipo waphwanya mafupa anga. 5 Wandizinga ndi kundizungulirandi zowawa ndi zolemetsa. 6 Wandikhazika mu mdimangati amene anafa kale. 7 Wandimangira khoma kotero kuti sindingathawe,wandimanga ndi maunyolo. 8 Ngakhale pamene ndifuwula kapena kupempha chithandizo,amakana pemphero langa. 9 Wanditsekera njira yanga ndi miyala yosema;ndipo wakhotetsa tinjira tanga. 10 Wandidikirira ngati chimbalangondo,wandibisalira ngati mkango. 11 Wandikokera pambali ndi kundingʼambangʼamba,ndipo wandisiya wopanda thandizo. 12 Wakoka uta wakendipo walunjikitsa mivi yake pa ine. 13 Walasa mtima wangandi mivi ya mʼphodo mwake. 14 Ndinakhala choseketsa cha anthu anga onse;amandinyodola mʼnyimbo zawo tsiku lonse. 15 Wandidyetsa zowawandipo wandimwetsa ndulu. 16 Wathyola mano anga ndi miyala;wandiviviniza mʼfumbi; 17 Wandichotsera mtendere;ndayiwala kuti kupeza bwino nʼchiyani. 18 Choncho ndikuti, “Ulemerero wanga wachokandi zonse zimene ndimayembekeza kwa Yehova.” 19 Kukumbukira masautso anga ndi kusowa pokhala,zili ngati zowawa ndi ndulu. 20 Ine ndikuzikumbukira bwino izi,ndipo moyo wanga wathedwa mʼkati mwanga. 21 Komabe ndimakumbukira zimenezi,nʼchifukwa chake ndili ndi chiyembekezo. 22 Ife sitinawonongekeretu chifukwa chikondi cha Yehova ndi chachikulu,ndi chifundo chake ndi chosatha. 23 Zimaoneka zatsopano mmawa uliwonse;kukhulupirika kwanu nʼkwakukulu. 24 Mu mtima mwanga ndimati, “Yehova ndiye zanga zonse;motero ndimamuyembekezera.” 25 Yehova ndi wabwino kwa amene amayembekezera Iye,kwa munthu amene amafunafuna Iyeyo; 26 nʼkwabwino kudikira chipulumutso chaYehova modekha. 27 Nʼkwabwino kuti munthu asenze golipamene ali wamngʼono. 28 Akhale chete pa yekha,chifukwa Yehova wamusenzetsa golilo. 29 Abise nkhope yake mʼfumbimwina chiyembekezo nʼkukhalapobe. 30 Apereke tsaya lake kwa iye amene angamumenye,ndipo amuchititse manyazi. 31 Chifukwa Ambuye satayiratuanthu nthawi zonse. 32 Ngakhale amabweretsa zowawa, Iye adzawachitira chifundo,chifukwa chikondi chake ndi chosatha. 33 Pakuti sabweretsa masautso mwadala,kapena zowawa kwa ana a anthu. 34 Kuphwanya ndi phazia mʼndende onse a mʼdziko, 35 kukaniza munthu ufulu wakepamaso pa Wammwambamwamba, 36 kumana munthu chiweruzo cholungama—kodi Ambuye saona zonsezi? 37 Kodi ndani angayankhule zinthu nʼkuchitikangati Ambuye sanavomereze? 38 Kodi zovuta ndi zabwino sizitulukamʼkamwa mwa Wammwambamwamba? 39 Kodi nʼchifukwa chiyani munthu aliyense wamoyo amadandaulaakalangidwa chifukwa cha machimo ake? 40 Tiyeni tisanthule ndi kuyesa njira zathu,ndipo tiyeni tibwerere kwa Yehova. 41 Tiyeni tikweze mitima yathu ndi manja athukwa Mulungu kumwamba ndipo tinene kuti: 42 “Ife tachimwa ndi kuwukirandipo inu simunakhululuke. 43 “Mwadzikuta ndi mkwiyo ndi kutilondola ndipomwatitha mopanda chifundo. 44 Mwadzikuta mu mtambokotero mapemphero athu sakukufikani. 45 Mwatisandutsa zinyatsi ndi zinyalalapakati pa mitundu ya anthu. 46 “Adani anthu atitsekulira pakamwa. 47 Ife tadzazidwa ndi mantha pakuti tagwa mʼdzenje,tapasuka ndi kuwonongedwa.” 48 Misozi mʼmaso mwanga ikungoti mbwembwembwechifukwa anthu anga akuwonongedwa. 49 Misozi idzatsika kosalekeza,ndipo sidzasiya, 50 mpaka Yehova ayangʼane pansikuchokera kumwamba ndi kuona. 51 Mtima wanga ukupweteka poona zimenezichifukwa cha akazi onse a mu mzinda. 52 Akundisaka ngati mbalame,amene anali adani anga, popanda chifukwa. 53 Ayesa kundipha pondiponya mʼdzenjendi kundiponya miyala; 54 madzi anamiza mutu wangandipo ndinkaganiza kuti imfa yayandikira. 55 Ndinayitana dzina lanu Inu Yehova,kuchokera mʼdzenje lozama. 56 Inu munamva kudandaula kwanga. “Mundimverekulira kwanga kopempha thandizo.” 57 Munafika pafupi pamene ndinakuyitanani,ndipo munati, “Usaope.” 58 Inu Ambuye munandiwombola ku mlandu wanga;munapulumutsa moyo wanga. 59 Yehova, mwaona zoyipa zimene andichitira.Mundiweruzire ndinu! 60 Mwaona kuzama kwa kubwezera kwawo,chiwembu chawo chonse pa ine. 61 Inu Yehova mwamva kunyoza kwawo,chiwembu chawo chonse pa ine, 62 manongʼonongʼo a adani angaondiwukira ine tsiku lonse. 63 Tawaonani! Kaya ali pansi kapena kuyimirira,akundinyoza mu nyimbo zawo. 64 Inu Yehova, muwabwezere chowayenera,chifukwa cha zimene manja awo achita. 65 Phimbani mitima yawo,ndipo matemberero anu akhale pa iwo! 66 Muwalondole mwaukali ndipomuwawonongeretu pa dziko lapansi.

In Other Versions

Lamentations 3 in the ANGEFD

Lamentations 3 in the ANTPNG2D

Lamentations 3 in the AS21

Lamentations 3 in the BAGH

Lamentations 3 in the BBPNG

Lamentations 3 in the BBT1E

Lamentations 3 in the BDS

Lamentations 3 in the BEV

Lamentations 3 in the BHAD

Lamentations 3 in the BIB

Lamentations 3 in the BLPT

Lamentations 3 in the BNT

Lamentations 3 in the BNTABOOT

Lamentations 3 in the BNTLV

Lamentations 3 in the BOATCB

Lamentations 3 in the BOATCB2

Lamentations 3 in the BOBCV

Lamentations 3 in the BOCNT

Lamentations 3 in the BOECS

Lamentations 3 in the BOHCB

Lamentations 3 in the BOHCV

Lamentations 3 in the BOHLNT

Lamentations 3 in the BOHNTLTAL

Lamentations 3 in the BOICB

Lamentations 3 in the BOILNTAP

Lamentations 3 in the BOITCV

Lamentations 3 in the BOKCV

Lamentations 3 in the BOKCV2

Lamentations 3 in the BOKHWOG

Lamentations 3 in the BOKSSV

Lamentations 3 in the BOLCB

Lamentations 3 in the BOLCB2

Lamentations 3 in the BOMCV

Lamentations 3 in the BONAV

Lamentations 3 in the BONCB

Lamentations 3 in the BONLT

Lamentations 3 in the BONUT2

Lamentations 3 in the BOPLNT

Lamentations 3 in the BOSCB

Lamentations 3 in the BOSNC

Lamentations 3 in the BOTLNT

Lamentations 3 in the BOVCB

Lamentations 3 in the BOYCB

Lamentations 3 in the BPBB

Lamentations 3 in the BPH

Lamentations 3 in the BSB

Lamentations 3 in the CCB

Lamentations 3 in the CUV

Lamentations 3 in the CUVS

Lamentations 3 in the DBT

Lamentations 3 in the DGDNT

Lamentations 3 in the DHNT

Lamentations 3 in the DNT

Lamentations 3 in the ELBE

Lamentations 3 in the EMTV

Lamentations 3 in the ESV

Lamentations 3 in the FBV

Lamentations 3 in the FEB

Lamentations 3 in the GGMNT

Lamentations 3 in the GNT

Lamentations 3 in the HARY

Lamentations 3 in the HNT

Lamentations 3 in the IRVA

Lamentations 3 in the IRVB

Lamentations 3 in the IRVG

Lamentations 3 in the IRVH

Lamentations 3 in the IRVK

Lamentations 3 in the IRVM

Lamentations 3 in the IRVM2

Lamentations 3 in the IRVO

Lamentations 3 in the IRVP

Lamentations 3 in the IRVT

Lamentations 3 in the IRVT2

Lamentations 3 in the IRVU

Lamentations 3 in the ISVN

Lamentations 3 in the JSNT

Lamentations 3 in the KAPI

Lamentations 3 in the KBT1ETNIK

Lamentations 3 in the KBV

Lamentations 3 in the KJV

Lamentations 3 in the KNFD

Lamentations 3 in the LBA

Lamentations 3 in the LBLA

Lamentations 3 in the LNT

Lamentations 3 in the LSV

Lamentations 3 in the MAAL

Lamentations 3 in the MBV

Lamentations 3 in the MBV2

Lamentations 3 in the MHNT

Lamentations 3 in the MKNFD

Lamentations 3 in the MNG

Lamentations 3 in the MNT

Lamentations 3 in the MNT2

Lamentations 3 in the MRS1T

Lamentations 3 in the NAA

Lamentations 3 in the NASB

Lamentations 3 in the NBLA

Lamentations 3 in the NBS

Lamentations 3 in the NBVTP

Lamentations 3 in the NET2

Lamentations 3 in the NIV11

Lamentations 3 in the NNT

Lamentations 3 in the NNT2

Lamentations 3 in the NNT3

Lamentations 3 in the PDDPT

Lamentations 3 in the PFNT

Lamentations 3 in the RMNT

Lamentations 3 in the SBIAS

Lamentations 3 in the SBIBS

Lamentations 3 in the SBIBS2

Lamentations 3 in the SBICS

Lamentations 3 in the SBIDS

Lamentations 3 in the SBIGS

Lamentations 3 in the SBIHS

Lamentations 3 in the SBIIS

Lamentations 3 in the SBIIS2

Lamentations 3 in the SBIIS3

Lamentations 3 in the SBIKS

Lamentations 3 in the SBIKS2

Lamentations 3 in the SBIMS

Lamentations 3 in the SBIOS

Lamentations 3 in the SBIPS

Lamentations 3 in the SBISS

Lamentations 3 in the SBITS

Lamentations 3 in the SBITS2

Lamentations 3 in the SBITS3

Lamentations 3 in the SBITS4

Lamentations 3 in the SBIUS

Lamentations 3 in the SBIVS

Lamentations 3 in the SBT

Lamentations 3 in the SBT1E

Lamentations 3 in the SCHL

Lamentations 3 in the SNT

Lamentations 3 in the SUSU

Lamentations 3 in the SUSU2

Lamentations 3 in the SYNO

Lamentations 3 in the TBIAOTANT

Lamentations 3 in the TBT1E

Lamentations 3 in the TBT1E2

Lamentations 3 in the TFTIP

Lamentations 3 in the TFTU

Lamentations 3 in the TGNTATF3T

Lamentations 3 in the THAI

Lamentations 3 in the TNFD

Lamentations 3 in the TNT

Lamentations 3 in the TNTIK

Lamentations 3 in the TNTIL

Lamentations 3 in the TNTIN

Lamentations 3 in the TNTIP

Lamentations 3 in the TNTIZ

Lamentations 3 in the TOMA

Lamentations 3 in the TTENT

Lamentations 3 in the UBG

Lamentations 3 in the UGV

Lamentations 3 in the UGV2

Lamentations 3 in the UGV3

Lamentations 3 in the VBL

Lamentations 3 in the VDCC

Lamentations 3 in the YALU

Lamentations 3 in the YAPE

Lamentations 3 in the YBVTP

Lamentations 3 in the ZBP