Isaiah 3 (BOGWICC)

1 Taonani tsopano, AmbuyeYehova Wamphamvuzonse,ali pafupi kuchotsa mu Yerusalemu ndi mu Yudazinthu pamodzi ndi thandizo;adzachotsa chakudya chonse ndi madzi onse, 2 anthu amphamvu ndi asilikali ankhondo,oweruza ndi aneneri,anthu olosera ndi akuluakulu, 3 atsogoleri a ankhondo makumi asanu ndi anthu olemekezeka,aphungu ndi anthu amatsenga ndi akatswiri pa za kulosera. 4 Ndidzawayikira anyamata kuti akhale mafumu awo;ana akhanda ndiwo adzawalamulire. 5 Anthu adzazunzana,munthu ndi munthu mnzake, mnansi ndi mnansi wake.Anthu wamba adzanyozaakuluakulu. 6 Munthu adzagwira mʼbale wakemʼnyumba ya abambo awo, ndipo adzati,“Iwe uli nawo mwinjiro, ndiye ukhale mtsogoleri wathu;lamulira malo opasuka ano!” 7 Koma tsiku limenelo mʼbale wakeyo adzafuwula kuti,“Ayi, mavuto oterewa ndilibe mankhwala ake.Ndilibe chakudya kapena chovala mʼnyumba mwanga;musasankhe ine kukhala mtsogoleri wa anthu.” 8 Yerusalemu akudzandira,Yuda akugwa;zokamba zawo ndi ntchito zawo nʼzotsutsana ndi Yehova,sakulabadira ulemerero wa Mulungu. 9 Maonekedwe a nkhope zawo amawatsutsa;amaonetsera poyera tchimo lawo ngati Sodomu;salibisa tchimo lawolo.Tsoka kwa iwoodziputira okha mavuto. 10 Nena kwa olungama kuti zonse zidzawayendera bwino,pakuti adzakondwera ndi phindu la ntchito zawo. 11 Tsoka kwa anthu oyipa! Mavuto ali pa iwo!Adzalandira malipiro a zimene manja awo anachita. 12 Achinyamata akupondereza anthu anga,ndipo amene akuwalamulira ndi akazi.Aa, anthu anga, atsogoleri anu akukusocheretsani;akukuchotsani pa njira yanu. 13 Yehova wakhala pamalo pake mʼbwalo la milandu;wakonzeka kuti aweruze anthu ake. 14 Yehova akuwazenga milanduakuluakulu ndi atsogoleri a anthu ake:“Ndinu amene mwawononga munda wanga wa mpesa;nyumba zanu zadzaza ndi zolanda kwa amphawi. 15 Nʼchifukwa chiyani inu mukupsinja anthu anga,nʼkudyera masuku pamutu amphawi?”Akutero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse. 16 Yehova akunena kuti,“Akazi a ku Ziyoni ngodzikuza kwambiri,akuyenda atakweza makosi awo,akukopa amuna ndi maso awoakuyenda monyangʼamaakuliza zigwinjiri za mʼmiyendo yawo 17 Nʼchifukwa chake Ambuye, adzatulutsa zipere pa mitu ya akazi a ku Ziyoniwo;Yehova adzachititsa dazi mitu yawo.” 18 Tsiku limenelo Ambuye adzawachotsera zodzikongoletsera zawo: za mʼmiyendo, za ku mutu za mʼkhosi, 19 ndolo ndi zibangiri, nsalu zophimba pa nkhope, 20 maduku, zigwinjiri za mʼmiyendo ndi malamba, mabotolo a zonunkhira ndi zithumwa, 21 mphete ndi zipini, 22 zovala za pa mphwando, zipewa ndi mwinjiro, zikwama, 23 magalasi oyangʼanira, zovala zosalala, nduwira ndiponso nsalu za mʼmapewa. 24 Mʼmalo mwa kununkhira azidzanunkha,mʼmalo mwa lamba, adzavala chingwe;mʼmalo mwa tsitsi lopesa bwino, adzakhala ndi dazi;mʼmalo mwa zovala zabwino, adzavala chiguduli;mʼmalo mwa kunyadira kukongola adzachita manyazi. 25 Iwe Yerusalemu anthu ako aamuna adzaphedwa ndi lupanga,asilikali ako adzafera ku nkhondo. 26 Pa zipata za Ziyoni padzakhala kubuma ndi kulira;Iweyo udzasakazidwa nʼkukhala pansi, ukugubuduzika pa fumbi.

In Other Versions

Isaiah 3 in the ANGEFD

Isaiah 3 in the ANTPNG2D

Isaiah 3 in the AS21

Isaiah 3 in the BAGH

Isaiah 3 in the BBPNG

Isaiah 3 in the BBT1E

Isaiah 3 in the BDS

Isaiah 3 in the BEV

Isaiah 3 in the BHAD

Isaiah 3 in the BIB

Isaiah 3 in the BLPT

Isaiah 3 in the BNT

Isaiah 3 in the BNTABOOT

Isaiah 3 in the BNTLV

Isaiah 3 in the BOATCB

Isaiah 3 in the BOATCB2

Isaiah 3 in the BOBCV

Isaiah 3 in the BOCNT

Isaiah 3 in the BOECS

Isaiah 3 in the BOHCB

Isaiah 3 in the BOHCV

Isaiah 3 in the BOHLNT

Isaiah 3 in the BOHNTLTAL

Isaiah 3 in the BOICB

Isaiah 3 in the BOILNTAP

Isaiah 3 in the BOITCV

Isaiah 3 in the BOKCV

Isaiah 3 in the BOKCV2

Isaiah 3 in the BOKHWOG

Isaiah 3 in the BOKSSV

Isaiah 3 in the BOLCB

Isaiah 3 in the BOLCB2

Isaiah 3 in the BOMCV

Isaiah 3 in the BONAV

Isaiah 3 in the BONCB

Isaiah 3 in the BONLT

Isaiah 3 in the BONUT2

Isaiah 3 in the BOPLNT

Isaiah 3 in the BOSCB

Isaiah 3 in the BOSNC

Isaiah 3 in the BOTLNT

Isaiah 3 in the BOVCB

Isaiah 3 in the BOYCB

Isaiah 3 in the BPBB

Isaiah 3 in the BPH

Isaiah 3 in the BSB

Isaiah 3 in the CCB

Isaiah 3 in the CUV

Isaiah 3 in the CUVS

Isaiah 3 in the DBT

Isaiah 3 in the DGDNT

Isaiah 3 in the DHNT

Isaiah 3 in the DNT

Isaiah 3 in the ELBE

Isaiah 3 in the EMTV

Isaiah 3 in the ESV

Isaiah 3 in the FBV

Isaiah 3 in the FEB

Isaiah 3 in the GGMNT

Isaiah 3 in the GNT

Isaiah 3 in the HARY

Isaiah 3 in the HNT

Isaiah 3 in the IRVA

Isaiah 3 in the IRVB

Isaiah 3 in the IRVG

Isaiah 3 in the IRVH

Isaiah 3 in the IRVK

Isaiah 3 in the IRVM

Isaiah 3 in the IRVM2

Isaiah 3 in the IRVO

Isaiah 3 in the IRVP

Isaiah 3 in the IRVT

Isaiah 3 in the IRVT2

Isaiah 3 in the IRVU

Isaiah 3 in the ISVN

Isaiah 3 in the JSNT

Isaiah 3 in the KAPI

Isaiah 3 in the KBT1ETNIK

Isaiah 3 in the KBV

Isaiah 3 in the KJV

Isaiah 3 in the KNFD

Isaiah 3 in the LBA

Isaiah 3 in the LBLA

Isaiah 3 in the LNT

Isaiah 3 in the LSV

Isaiah 3 in the MAAL

Isaiah 3 in the MBV

Isaiah 3 in the MBV2

Isaiah 3 in the MHNT

Isaiah 3 in the MKNFD

Isaiah 3 in the MNG

Isaiah 3 in the MNT

Isaiah 3 in the MNT2

Isaiah 3 in the MRS1T

Isaiah 3 in the NAA

Isaiah 3 in the NASB

Isaiah 3 in the NBLA

Isaiah 3 in the NBS

Isaiah 3 in the NBVTP

Isaiah 3 in the NET2

Isaiah 3 in the NIV11

Isaiah 3 in the NNT

Isaiah 3 in the NNT2

Isaiah 3 in the NNT3

Isaiah 3 in the PDDPT

Isaiah 3 in the PFNT

Isaiah 3 in the RMNT

Isaiah 3 in the SBIAS

Isaiah 3 in the SBIBS

Isaiah 3 in the SBIBS2

Isaiah 3 in the SBICS

Isaiah 3 in the SBIDS

Isaiah 3 in the SBIGS

Isaiah 3 in the SBIHS

Isaiah 3 in the SBIIS

Isaiah 3 in the SBIIS2

Isaiah 3 in the SBIIS3

Isaiah 3 in the SBIKS

Isaiah 3 in the SBIKS2

Isaiah 3 in the SBIMS

Isaiah 3 in the SBIOS

Isaiah 3 in the SBIPS

Isaiah 3 in the SBISS

Isaiah 3 in the SBITS

Isaiah 3 in the SBITS2

Isaiah 3 in the SBITS3

Isaiah 3 in the SBITS4

Isaiah 3 in the SBIUS

Isaiah 3 in the SBIVS

Isaiah 3 in the SBT

Isaiah 3 in the SBT1E

Isaiah 3 in the SCHL

Isaiah 3 in the SNT

Isaiah 3 in the SUSU

Isaiah 3 in the SUSU2

Isaiah 3 in the SYNO

Isaiah 3 in the TBIAOTANT

Isaiah 3 in the TBT1E

Isaiah 3 in the TBT1E2

Isaiah 3 in the TFTIP

Isaiah 3 in the TFTU

Isaiah 3 in the TGNTATF3T

Isaiah 3 in the THAI

Isaiah 3 in the TNFD

Isaiah 3 in the TNT

Isaiah 3 in the TNTIK

Isaiah 3 in the TNTIL

Isaiah 3 in the TNTIN

Isaiah 3 in the TNTIP

Isaiah 3 in the TNTIZ

Isaiah 3 in the TOMA

Isaiah 3 in the TTENT

Isaiah 3 in the UBG

Isaiah 3 in the UGV

Isaiah 3 in the UGV2

Isaiah 3 in the UGV3

Isaiah 3 in the VBL

Isaiah 3 in the VDCC

Isaiah 3 in the YALU

Isaiah 3 in the YAPE

Isaiah 3 in the YBVTP

Isaiah 3 in the ZBP