Proverbs 14 (BOGWICC)

1 Mkazi wanzeru amamanga banja lake,koma mkazi wopusa amalimasula ndi manja ake omwe. 2 Amene amayenda molungama amaopa Yehova,koma amene njira zake ndi zoyipa amanyoza Yehova. 3 Kuyankhula kwa chitsiru kumamuyitanira ndodo pa msana,koma milomo ya munthu wanzeru imamuteteza. 4 Pakasowa ngʼombe zolima gome limakhala lopanda chakudya,koma pakakhala ngʼombe zamphamvu zakudya zimachulukanso. 5 Mboni yokhulupirika sinama,koma mboni yonyenga imayankhula zabodza. 6 Wonyoza anzake amafunafuna nzeru koma osayipeza,koma munthu womvetsa bwino amadziwa zinthu msanga. 7 Khala kutali ndi munthu wopusachifukwa sudzapeza mawu a nzeru. 8 Nzeru za munthu wochenjera zagona pakuzindikira njira zake.Koma uchitsiru wa zitsiru umapusitsidwa ndi chinyengo chawo chomwe. 9 Zitsiru zimanyoza za kulapa machimo, awo,koma kufuna kwabwino kumapezeka mwa anthu olungama. 10 Mtima uliwonse umadziwa wokha zowawa zake,ndipo palibe wina aliyense angadziwe kukondwa kwake. 11 Nyumba ya munthu woyipa idzapasuka,koma tenti ya munthu wowongoka mtima idzakhazikika. 12 Pali njira ina yooneka ngati yabwino kwa munthu,koma kumatsiriziro kwake ndi ku imfa. 13 Ngakhale poseka mtima utha kumva kuwawa,ndipo mathero achimwemwe akhoza kukhala chisoni. 14 Munthu wosakhulupirika adzalandira zogwirizana ndi ntchito yake,koma munthu wabwino adzalandira mphotho ya ntchito yake. 15 Munthu wopusa amakhulupirira chilichonse,koma munthu wochenjera amaganizira bwino mayendedwe ake. 16 Munthu wanzeru amaopa Mulungu ndipo amapewa zoyipa,koma munthu wopusa ndi wokula mtima amakhala wosasamala. 17 Munthu wopsa mtima msanga amachita zinthu za uchitsiru,ndipo anthu amadana ndi munthu wachinyengo. 18 Anthu opusa amalandira uchitsiru,koma anthu ochenjera amavekedwa chipewa cha ulemerero wa kudziwa zinthu. 19 Anthu oyipa adzagwada pamaso pa anthu abwino,ndipo anthu oyipa adzapempha thandizo kwa anthu olungama. 20 Munthu wosauka ngakhale anansi ake omwe amamuda,koma munthu wolemera ali ndi abwenzi ambiri. 21 Wonyoza mnansi wake ndi wochimwakoma ndi wodala amene amachitira chifundo anthu osowa. 22 Kodi amene amakonzekera zoyipa sasochera?Koma amene amakonzekera zabwino anthu amawaonetsa chikondi ndi kukhulupirika. 23 Ntchito iliyonse imakhala ndi phindu,koma kuyankhulayankhula kumabweretsa umphawi. 24 Chipewa chaulemu cha anthu a nzeru ndi chuma chawo chomwe,koma malipiro a zitsiru ndi uchitsiru. 25 Mboni yokhulupirika imapulumutsa miyoyo,koma mboni yabodza imaphetsa. 26 Amene amaopa Yehova ali ndi chitetezo chokwanirandipo iye adzakhala pothawira pa ana ake. 27 Kuopa Yehova ndiye kasupe wamoyo,kumathandiza munthu kuti apewe msampha wa imfa. 28 Gulu lalikulu la anthu ndiye ulemerero wa mfumu,koma popanda anthu kalonga amawonongeka. 29 Munthu wosapsa mtima msanga amamvetsa zinthu kwambiri,koma munthu wopsa mtima msanga amaonetsa uchitsiru wake. 30 Mtima wodekha umapatsa thupi moyo,koma nsanje imawoletsa mafupa. 31 Amene amapondereza mʼmphawi amanyoza mlengi wake,koma wochitira chifundo munthu wosowa amalemekeza Mulungu. 32 Anthu oyipa adzakanthidwa chifukwa cha ntchito zawo zomwe,koma olungama adzatetezedwa mwa imfa yawo. 33 Nzeru zimakhala mu mtima mwa anthu omvetsa zinthu,koma nzeru sipezeka mu mtima mwa zitsiru. 34 Chilungamo chimakweza mtundu wa anthu,koma uchimo umachititsa manyazi mtundu uliwonse. 35 Mfumu imasangalatsidwa ndi wantchito wanzeru,koma imachitira ukali wantchito wochititsa manyazi.

In Other Versions

Proverbs 14 in the ANGEFD

Proverbs 14 in the ANTPNG2D

Proverbs 14 in the AS21

Proverbs 14 in the BAGH

Proverbs 14 in the BBPNG

Proverbs 14 in the BBT1E

Proverbs 14 in the BDS

Proverbs 14 in the BEV

Proverbs 14 in the BHAD

Proverbs 14 in the BIB

Proverbs 14 in the BLPT

Proverbs 14 in the BNT

Proverbs 14 in the BNTABOOT

Proverbs 14 in the BNTLV

Proverbs 14 in the BOATCB

Proverbs 14 in the BOATCB2

Proverbs 14 in the BOBCV

Proverbs 14 in the BOCNT

Proverbs 14 in the BOECS

Proverbs 14 in the BOHCB

Proverbs 14 in the BOHCV

Proverbs 14 in the BOHLNT

Proverbs 14 in the BOHNTLTAL

Proverbs 14 in the BOICB

Proverbs 14 in the BOILNTAP

Proverbs 14 in the BOITCV

Proverbs 14 in the BOKCV

Proverbs 14 in the BOKCV2

Proverbs 14 in the BOKHWOG

Proverbs 14 in the BOKSSV

Proverbs 14 in the BOLCB

Proverbs 14 in the BOLCB2

Proverbs 14 in the BOMCV

Proverbs 14 in the BONAV

Proverbs 14 in the BONCB

Proverbs 14 in the BONLT

Proverbs 14 in the BONUT2

Proverbs 14 in the BOPLNT

Proverbs 14 in the BOSCB

Proverbs 14 in the BOSNC

Proverbs 14 in the BOTLNT

Proverbs 14 in the BOVCB

Proverbs 14 in the BOYCB

Proverbs 14 in the BPBB

Proverbs 14 in the BPH

Proverbs 14 in the BSB

Proverbs 14 in the CCB

Proverbs 14 in the CUV

Proverbs 14 in the CUVS

Proverbs 14 in the DBT

Proverbs 14 in the DGDNT

Proverbs 14 in the DHNT

Proverbs 14 in the DNT

Proverbs 14 in the ELBE

Proverbs 14 in the EMTV

Proverbs 14 in the ESV

Proverbs 14 in the FBV

Proverbs 14 in the FEB

Proverbs 14 in the GGMNT

Proverbs 14 in the GNT

Proverbs 14 in the HARY

Proverbs 14 in the HNT

Proverbs 14 in the IRVA

Proverbs 14 in the IRVB

Proverbs 14 in the IRVG

Proverbs 14 in the IRVH

Proverbs 14 in the IRVK

Proverbs 14 in the IRVM

Proverbs 14 in the IRVM2

Proverbs 14 in the IRVO

Proverbs 14 in the IRVP

Proverbs 14 in the IRVT

Proverbs 14 in the IRVT2

Proverbs 14 in the IRVU

Proverbs 14 in the ISVN

Proverbs 14 in the JSNT

Proverbs 14 in the KAPI

Proverbs 14 in the KBT1ETNIK

Proverbs 14 in the KBV

Proverbs 14 in the KJV

Proverbs 14 in the KNFD

Proverbs 14 in the LBA

Proverbs 14 in the LBLA

Proverbs 14 in the LNT

Proverbs 14 in the LSV

Proverbs 14 in the MAAL

Proverbs 14 in the MBV

Proverbs 14 in the MBV2

Proverbs 14 in the MHNT

Proverbs 14 in the MKNFD

Proverbs 14 in the MNG

Proverbs 14 in the MNT

Proverbs 14 in the MNT2

Proverbs 14 in the MRS1T

Proverbs 14 in the NAA

Proverbs 14 in the NASB

Proverbs 14 in the NBLA

Proverbs 14 in the NBS

Proverbs 14 in the NBVTP

Proverbs 14 in the NET2

Proverbs 14 in the NIV11

Proverbs 14 in the NNT

Proverbs 14 in the NNT2

Proverbs 14 in the NNT3

Proverbs 14 in the PDDPT

Proverbs 14 in the PFNT

Proverbs 14 in the RMNT

Proverbs 14 in the SBIAS

Proverbs 14 in the SBIBS

Proverbs 14 in the SBIBS2

Proverbs 14 in the SBICS

Proverbs 14 in the SBIDS

Proverbs 14 in the SBIGS

Proverbs 14 in the SBIHS

Proverbs 14 in the SBIIS

Proverbs 14 in the SBIIS2

Proverbs 14 in the SBIIS3

Proverbs 14 in the SBIKS

Proverbs 14 in the SBIKS2

Proverbs 14 in the SBIMS

Proverbs 14 in the SBIOS

Proverbs 14 in the SBIPS

Proverbs 14 in the SBISS

Proverbs 14 in the SBITS

Proverbs 14 in the SBITS2

Proverbs 14 in the SBITS3

Proverbs 14 in the SBITS4

Proverbs 14 in the SBIUS

Proverbs 14 in the SBIVS

Proverbs 14 in the SBT

Proverbs 14 in the SBT1E

Proverbs 14 in the SCHL

Proverbs 14 in the SNT

Proverbs 14 in the SUSU

Proverbs 14 in the SUSU2

Proverbs 14 in the SYNO

Proverbs 14 in the TBIAOTANT

Proverbs 14 in the TBT1E

Proverbs 14 in the TBT1E2

Proverbs 14 in the TFTIP

Proverbs 14 in the TFTU

Proverbs 14 in the TGNTATF3T

Proverbs 14 in the THAI

Proverbs 14 in the TNFD

Proverbs 14 in the TNT

Proverbs 14 in the TNTIK

Proverbs 14 in the TNTIL

Proverbs 14 in the TNTIN

Proverbs 14 in the TNTIP

Proverbs 14 in the TNTIZ

Proverbs 14 in the TOMA

Proverbs 14 in the TTENT

Proverbs 14 in the UBG

Proverbs 14 in the UGV

Proverbs 14 in the UGV2

Proverbs 14 in the UGV3

Proverbs 14 in the VBL

Proverbs 14 in the VDCC

Proverbs 14 in the YALU

Proverbs 14 in the YAPE

Proverbs 14 in the YBVTP

Proverbs 14 in the ZBP